ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: القارعة   آية:

القارعة

ٱلۡقَارِعَةُ
Kugunda kwa phokoso (la Qiyâma)!
التفاسير العربية:
مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Kodi kugunda kwa phokosolo ndi chiyani?
التفاسير العربية:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡقَارِعَةُ
Ndichiyani chingakudziwitse za kugunda kwa phokoso (la Qiyâma komwe kudzawakomole anthu)?
التفاسير العربية:
يَوۡمَ يَكُونُ ٱلنَّاسُ كَٱلۡفَرَاشِ ٱلۡمَبۡثُوثِ
Limenelo ndi tsiku limene anthu adzakhala ngati agulugufe obalalika.[475]
[475] Apa, pakutanthauza kuti anthu adzakhala ali balalabalala ngati agulugufe ndipo azidzangodziponya uku ndi uku, osadziwa kopita. Imeneyo ndi nthawi yotuluka m’manda.
التفاسير العربية:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ ٱلۡمَنفُوشِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya womwazidwa (wongouluka uku ndi uku mumlengalenga).
التفاسير العربية:
فَأَمَّا مَن ثَقُلَتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Tsono amene muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzalemere (ndikupepuka zoipa).[476]
[476] Tsiku limenelo ntchito zonse zabwino ndi zoipa zidzayesedwa ndi muyeso wa Allah, koma sitidadziwitsidwe kuti muyeso umenewo udzakhala wotani udzayesa zonse zazikulu ndi zazing’ono zomwe mpaka za mumtima.
التفاسير العربية:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Ndiye kuti iye adzakhala mu umoyo wosangalatsa (patsiku la chiweruziro).
التفاسير العربية:
وَأَمَّا مَنۡ خَفَّتۡ مَوَٰزِينُهُۥ
Ndipo yemwe muyeso wake (wa zinthu zabwino) udzapepuka (ndi kulemera zoipa),
التفاسير العربية:
فَأُمُّهُۥ هَاوِيَةٞ
Ndiye kuti mbuto yake ndi ku Hawiya.
التفاسير العربية:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا هِيَهۡ
Kodi ndi chiyani chingakudziwitse za Hawiya?
التفاسير العربية:
نَارٌ حَامِيَةُۢ
Umenewo ndi Moto woyaka mwa ukali!
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: القارعة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق