ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (1) سورة: قريش

قريش

لِإِيلَٰفِ قُرَيۡشٍ
Cholinga chakuwachita Maquraish kuti apitirize chizolowezi chawo,[486]
[486] (Ndime 1-4) Al-Kaaba, ndizachidziwikire kuti, adali malo opatulika kwa Arabu onse kuyambira nyengo ya Ibrahim (Abraham) (a.s) yemwe adamanga nyumbayi potsatira lamulo la Allah. Aquraish amene ankasunga ndi kuyang’anira Nyumba yopatulikayi, adali kupatsidwa ulemu ndi Arabu ena onse. Ndipo pa chifukwa chimenechi adali kutha kuyenda ulendo wopita ku Yemen nthawi ya dzinja, ndiponso ku Sham nthawi yachirimwe kukachita malonda ndikubwerera bwinobwino. Sadali kuputidwa ndi achifwamba m’njira, pophedwa kapena kulandidwa chuma chawo momwe ankachitiridwa Arabu ena. Pamene idamveka nkhani ya njovu kulemekezedwa kwawo kudaonjezeka kuchokera kwa mitundu yonse ya Arabu. Mu Sura imeneyi, Allah akuwakumbutsa za madalitso amenewa ndiponso akuwauza kuti adawafewetsera kayendedwe ka maulendo awo nthawi ya dzinja ndi chilimwe kuti akachite malonda ndikupeza chakudya ndi zina zofunika pa moyo wawo. Adawapatsa chitetezo posakhala ndi mantha m’njira; mantha omwe mitundu ina ya Arabu idali nawo. Madalitso onsewa ankawapeza chifukwa cha nyumba ya Al-Kaaba. Choncho kudali koyenera kwa iwo kumupembedza Mwini nyumbayo, osati mafano.
Pakadapanda nyumba Yakeyo sakadatha kumayenda maulendo mwa chitetezo, ndiponso sibwenzi kukudza aliyense ku mzindawo (Makka) chifukwa mukadakhala mulibe chodzetsa alendo.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (1) سورة: قريش
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق