ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (1) سورة: الكافرون

الكافرون

قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡكَٰفِرُونَ
Nena (iwe Mtumiki) (s.a.w): E inu anthu osakhulupirira![493]
[493] (Ndime 1-6) Osakhulupilira a mu mzinda wa Makka pamene adaona kuti atopa, sangathe kuzimitsa dangalira la Usilamu ndipo adamuona Mneneri (s.a.w) tsiku lililonse akuonjezera khama pa ntchito yake, chipembedzo nacho chikunkerankera mtsogolo, adapempha Muhammad (s.a.w) kuti pakhale chimvano pakati pa iwo ndi iye choti amupembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w) chaka chimodzi pamodzi naye, nayenso pa chaka chinacho asakanikirane nawo popembedza milungu yawo chaka chimodzinso. Kumeneku ndiko kuti chaka, apembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w), nayenso apembedze milungu yawo chaka chinacho. Apa ndipo pamene idavumbulutsidwa Surayi. Cholinga chake ndi ichi: Inu muli ndi milungu yanu, inenso ndili ndi Mulungu wanga. Sizingatheke kusakanikirana pakati pa milungu yanu yonama ndi Mulungu wanga woona, ngakhalenso ndi mapemphero anu onama ndi mapemphero anga owona. Inu muli ndi chipembedzo ndichikhulupiliro chanu, inenso ndili ndi chipembedzo ndi chikhulupiliro changa.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (1) سورة: الكافرون
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق