ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (106) سورة: النحل
مَن كَفَرَ بِٱللَّهِ مِنۢ بَعۡدِ إِيمَٰنِهِۦٓ إِلَّا مَنۡ أُكۡرِهَ وَقَلۡبُهُۥ مُطۡمَئِنُّۢ بِٱلۡإِيمَٰنِ وَلَٰكِن مَّن شَرَحَ بِٱلۡكُفۡرِ صَدۡرٗا فَعَلَيۡهِمۡ غَضَبٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَلَهُمۡ عَذَابٌ عَظِيمٞ
Amene akukana Allah, pambuyo pomukhulupirira, (chilango chachikulu chikumuyembekezera), kupatula yemwe adakakamizidwa, uku mtima wake utakhazikika pa chikhulupiliro; koma amene akutsekulira mtima wake kusakhulupirira, mkwiyo wa Allah uli pa iwo (ndipo anthu otere) adzapata chilango chachikulu.[252]
[252] Omasulira Qur’an akunena kuti ndime iyi idatsika chifukwa cha Ammar Bun Yasir. Opembedza mafano adamgwira ndi kumuvutitsa zedi kufikira iye adawapatsa chomwe iwo ankafuna kwa iye momkakamiza kutero. Anthu adati: “Ndithudi, Ammar watuluka m’Chisilamu.” Mtumiki (s.a.w) adati: “Ndithudi, Ammar ngodzaza ndi chikhulupiliro kuyambira kumutu mpaka kumapazi. Chikhulupiliro chasakanikirana ndi minofu ndi magazi ake.” Zitatero Ammar adabwera kwa Mtumiki (s.a.w) uku akulira. Mtumiki (s.a.w) adati kwa iye: “Kodi ukupeza bwanji mtima wako?” Iye adati: “Ngokhazikika pa chikhulupiliro.” Mtumiki (s.a.w) adati: “Ngati abwereranso iwenso bwerezanso zimene wanenazo.”
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (106) سورة: النحل
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق