ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (28) سورة: الكهف
وَٱصۡبِرۡ نَفۡسَكَ مَعَ ٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ رَبَّهُم بِٱلۡغَدَوٰةِ وَٱلۡعَشِيِّ يُرِيدُونَ وَجۡهَهُۥۖ وَلَا تَعۡدُ عَيۡنَاكَ عَنۡهُمۡ تُرِيدُ زِينَةَ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَا تُطِعۡ مَنۡ أَغۡفَلۡنَا قَلۡبَهُۥ عَن ذِكۡرِنَا وَٱتَّبَعَ هَوَىٰهُ وَكَانَ أَمۡرُهُۥ فُرُطٗا
Ndipo dzikakamize kukhala pamodzi ndi amene akupempha Mbuye wawo m’mawa ndi madzulo uku akufunafuna nkhope Yake (chiyanjo Chake), ndipo maso ako asachoke pa iwo ndi (kuyang’ana ena) ncholinga chofuna zokongoletsa za moyo wa dziko lapansi; ndipo usamumvere amene mtima wake tauiwalitsa kutikumbukira ndikumangotsatira zilakolako zake, ndipo zinthu zake nkukhala zotaika (zosalongosoka).[259]
[259] Ndime iyi idavumbulutsidwa pamene Uyaina Bun Huswaini ndi mnzake adadza kwa Mtumiki ndi kumpeza atakhala pamodzi ndi omtsatira (Maswahaba) osauka monga: Ammaru, Suhaibu ndi Bilali ndi ena onga iwo. Iwo adati kwa Mtumiki (s.a.w): “Ukadawapirikitsa anthu wambawa, ndiye kuti tikadakhala nawe nkumamvera zimene ukulalikira. Koma ife tikunyansidwa ndi ulaliki wako poona kuti nthawi zonse ukukhala ndi anthu onyozeka amene simabwana.” Choncho Qur’an idatsika kumuuza Mtumiki (s.a.w) kuti: “Usawathamangitse anthu omwe akupempha Allah m’mawa ndi madzulo ngakhale kuti ndionyozeka.”
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (28) سورة: الكهف
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق