ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (143) سورة: البقرة
وَكَذَٰلِكَ جَعَلۡنَٰكُمۡ أُمَّةٗ وَسَطٗا لِّتَكُونُواْ شُهَدَآءَ عَلَى ٱلنَّاسِ وَيَكُونَ ٱلرَّسُولُ عَلَيۡكُمۡ شَهِيدٗاۗ وَمَا جَعَلۡنَا ٱلۡقِبۡلَةَ ٱلَّتِي كُنتَ عَلَيۡهَآ إِلَّا لِنَعۡلَمَ مَن يَتَّبِعُ ٱلرَّسُولَ مِمَّن يَنقَلِبُ عَلَىٰ عَقِبَيۡهِۚ وَإِن كَانَتۡ لَكَبِيرَةً إِلَّا عَلَى ٱلَّذِينَ هَدَى ٱللَّهُۗ وَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيُضِيعَ إِيمَٰنَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِٱلنَّاسِ لَرَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Choncho takusankhani (inu Asilamu) kukhala mpingo wabwino (wapakatikati) kuti mukhale mboni pa anthu ndi kuti Mtumiki (s.a.w) akhale mboni pa inu. Ndipo chibula (choyang’ana mbali ya ku Yerusalemu) chomwe udali nacho sitidachichite koma kuti timdziwitse (adziwike kwa anthu) amene akutsata Mtumiki (s.a.w), ndi yemwe akutembenukira m’mbuyo. Ndipo ndithudi, chidali chinthu chovuta kupatula kwa omwe Allah wawaongola. Ndipo nkosayenera kwa Allah kusokoneza Swala zanu, pakuti Allah Ngoleza kwabasi kwa anthu, Ngwachifundo chambiri. [6]
[6] Apa akutanthauza kuti pamene takutsogolerani ku njira yolunjika, takulolani inu ampingo wa Muhammad (s.a.w) kukhala anthu olungama, kulungama kosapyola nako muyeso ndiponso kopanda kuchepetsa chinthu chilichonse chazauzimu, ndi chamoyo wapadziko lino lapansi. Mpingo wa Asilamu ngwapakatikati mzokhulupilira zake zonse. Umalimbikira kugwira ntchito ya zinthu za mdziko ndiponso ya zinthu zauzimu mwakhama, chilichonse mwa zimenezi amachilimbikira mosapyoza muyeso. Limeneli ndilo tanthauzo la “mpingo wapakatikati.’’ Chisilamu sichilekelera munthu mmodzi kuti apondereze anthu ambirimbiri; ndiponso sichilekelera anthu ambiri kusalabadira za munthu mmodzi.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (143) سورة: البقرة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق