ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (228) سورة: البقرة
وَٱلۡمُطَلَّقَٰتُ يَتَرَبَّصۡنَ بِأَنفُسِهِنَّ ثَلَٰثَةَ قُرُوٓءٖۚ وَلَا يَحِلُّ لَهُنَّ أَن يَكۡتُمۡنَ مَا خَلَقَ ٱللَّهُ فِيٓ أَرۡحَامِهِنَّ إِن كُنَّ يُؤۡمِنَّ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ وَبُعُولَتُهُنَّ أَحَقُّ بِرَدِّهِنَّ فِي ذَٰلِكَ إِنۡ أَرَادُوٓاْ إِصۡلَٰحٗاۚ وَلَهُنَّ مِثۡلُ ٱلَّذِي عَلَيۡهِنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ وَلِلرِّجَالِ عَلَيۡهِنَّ دَرَجَةٞۗ وَٱللَّهُ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ndipo akazi osiidwa (asakwatiwe) ayembekezere mpaka kuyeretsedwa kutatu kukwanire. Ndipo nkosafunika kwa iwo kubisa chimene Allah walenga m’mimba zawo, ngati akukhulupiriradi Allah ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo amuna awo ali ndi udindo wowayenereza kuwabwerera m’nthawi imeneyi ngati akufuna kuchita chimvano. Nawonso azimayi ali ndi zofunika kuchitiridwa (ndi amuna awo) monga m’mene ziliri kwa azimayiwo kuchitira amuna awo mwachilamulo cha Shariya. Koma amuna ali ndi udindo okulirapo kuposa iwo. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya. [35]
[35] Mkazi ngati amsudzula ukwati saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wina mpaka Edda yake ithe. Ndipo Edda njosiyanasiyana kwa akazi. Eddayi njotere kusiyana kwake:
1. Mkazi akasiyidwa ali ndi mimba, pamenepo ndiye kuti Edda yake imatha akangobereka. Pompo mwamuna wina akhoza kumkwatira.
2. Ngati wosiidwayo ndi mkazi yemwe sadwala matenda akumwezi
(a) chifukwa chakukalamba
(b) kapena chifukwa chakuti sanakwane zaka zoyambira kudwala kumweziko
(c) kapena chifukwa chakuti chilengedwe chake chili momwemo
(d) kapena zifukwa zina zomwe zimachititsa kuti asadwale matenda akumwezi edda yawo onsewa ndimiyezi itatu. Asakwatiwe mpaka miyezi itatu ithe kuchokera patsiku lomwe adawasudzula.
3. Ngati wosudzulidwayo ndimkazi wodwala matenda akumwezi, Edda yake imatha akamaliza “khului” zitatu. Tsono tanthauzo lakhului maulama amamasulira mosiyanasiyana. Pamazihabi a Imam Shafii tanthauzo lake ndikuyeretsedwa kutatu (twahara zitatu). Choncho kuyeretsedwa kutatuku kukatha kuyambira pomwe adamsudzula, akhoza kukwatiwa. Koma pamazihabi a Kibazi tanthauzo lake ndikudwala kumwezi katatu (hizi zitatu). Kukatha kudwala kumwezi kutatu komwe kwachitika pambuyo pamsudzulo ndiye kuti akhoza kukwatiwa. Edda ngati siinathe mkazi saloledwa kukwatiwa. Ngati atakwatiwa ali mu edda ukwatiwo suvomerezeka. Ndiye kutinso nthawi yonse yomwe mkaziyo akukhala limodzi ndi mwamunayo akuchita naye chiwerewere. Ndipo amene akubadwa mu ukwati wotere ndi ana obadwira mu chiwerewere. Akazi omwe asiidwa ukwati akuwalangiza kuti asabise mimba kuti mwanayo adzadziwike tate wake. Ngati Edda siinathe ndiponso ngati kuchuluka kwa twalaka mwamuna sadamalize, mwamunayo ali ndi ufulu wobwererana ndi mkazi ngati atafuna. Tero padzangofunika kupeza mboni ziwiri zoti zimdziwitse mkaziyo kuti mwamuna wake wabwererana naye. Mkaziyo kapenanso abale ake saloledwa kukaniza zimenezo.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (228) سورة: البقرة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق