ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (1) سورة: فاطر

فاطر

ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ فَاطِرِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ جَاعِلِ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ رُسُلًا أُوْلِيٓ أَجۡنِحَةٖ مَّثۡنَىٰ وَثُلَٰثَ وَرُبَٰعَۚ يَزِيدُ فِي ٱلۡخَلۡقِ مَا يَشَآءُۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Kuyamikidwa konse nkwa Allah (Yekha) Muumbi wa thambo ndi nthaka (popanda chofanizira), amene adachita angelo kukhala atumwi eni mapiko, awiriawiri; atatuatatu; ndi anayianayi. Amaonjezera mkulenga monga momwe afunira, (palibe chimene chingakanike kwa Iye). Ndithu Allah Ngokhoza chilichonse.[338]
[338] (Ndime 1-2) Iye Allah ali ndi mphamvu pa chilichonse; chimene afuna kuti chichitike chimachitika. Ndipo palibe chimene chingakanike kulengeka ndi Iye ngati atafuna kuti chilengeke. Allah wadzitamanda m’ndime ziwirizi ndi makhalidwe Ake awiri a pamwamba. Khalidwe loyamba, ndikukhoza komwe ndikusalephera chilichonse chimene wafuna. Khalidwe Lake lachiwiri ndikupereka madalitso osiyanasiyana pa zolengedwa Zake. Allah adalenga thambo ndi nthaka popanda chofanizira, natukula thambo kumwamba popanda mzati nalikongoletsa ndi nyenyezi. Iye ndi Yemwe adayalanso nthaka naika mmenemo mmera monga chakudya cha za moyo, nang’ambamo nyanja ndi mitsinje ndi akasupe ndi zina zotero zomwe zikusonyeza mphamvu Zake zoposa ndi luso Lake. Ndime yachiwiriyi ikutiphunzitsa kuti chimene Allah wachipereka kwa munthu monga chuma kukhala ndi moyo wangwiro, kukhala ndi nzeru zakuthwa, palibe amene angazitsekereze zimenezi. Ndipo chimene Allah wam’mana munthu, palibe amene angathe kuchipereka kwa iye.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (1) سورة: فاطر
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق