ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (39) سورة: يس
وَٱلۡقَمَرَ قَدَّرۡنَٰهُ مَنَازِلَ حَتَّىٰ عَادَ كَٱلۡعُرۡجُونِ ٱلۡقَدِيمِ
Ndiponso mwezi; tidaukonzera malo oimirapo mpaka kukafika pomwe umabwerera ndi kukhala wochepa ndi wokhota monga nthambi ya mtengo wa kanjedza, youma komanso yokhota.[341]
[341] Ndime iyi ikufotokoza za kayendedwe ka mwezi kuti adaupangira malo 28 oimirapo. Umayamba pamalo woyamba uli wochepa ndi wokhota. Ndipo umanka nukula kuchoka pa malo ena nkufika pa malo ena mpaka kukafika pamalo pomwe umakhala wokwanira mkuwala ndi m’maonekedwe ake. Pamenepa mpamalo a 14. Tsono kuchoka apa, umayamba kuchepa pang’onopang’ono ndi kubisika mpaka utafika pa malo a 28 pomwe umabisikiratu wonse. Kayendedwe ka mwezi ndiko kamazindikiritsa anthu kutha kwa mwezi ndi chaka, pomwe kayendedwe ka dzuwa kamazindikiritsa anthu kutha kwa tsiku.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (39) سورة: يس
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق