ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (11) سورة: النساء
يُوصِيكُمُ ٱللَّهُ فِيٓ أَوۡلَٰدِكُمۡۖ لِلذَّكَرِ مِثۡلُ حَظِّ ٱلۡأُنثَيَيۡنِۚ فَإِن كُنَّ نِسَآءٗ فَوۡقَ ٱثۡنَتَيۡنِ فَلَهُنَّ ثُلُثَا مَا تَرَكَۖ وَإِن كَانَتۡ وَٰحِدَةٗ فَلَهَا ٱلنِّصۡفُۚ وَلِأَبَوَيۡهِ لِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُ مِمَّا تَرَكَ إِن كَانَ لَهُۥ وَلَدٞۚ فَإِن لَّمۡ يَكُن لَّهُۥ وَلَدٞ وَوَرِثَهُۥٓ أَبَوَاهُ فَلِأُمِّهِ ٱلثُّلُثُۚ فَإِن كَانَ لَهُۥٓ إِخۡوَةٞ فَلِأُمِّهِ ٱلسُّدُسُۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِي بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍۗ ءَابَآؤُكُمۡ وَأَبۡنَآؤُكُمۡ لَا تَدۡرُونَ أَيُّهُمۡ أَقۡرَبُ لَكُمۡ نَفۡعٗاۚ فَرِيضَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Allah akukulamulani za ana anu achimuna apate gawo lolingana ndi gawo la akazi awiri. Ngati akaziwo ali (opitilira) awiri, ndiye kuti adzalandira zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu (2/3) za (chumacho) chimene wasiya (womwalira), ngati mwana wamkazi ndi mmodzi, apatsidwe gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2), naonso makolo ake awiri aliyense wa iwo alandile gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achuma chosiidwacho, ngati (womwalirayo) wasiya mwana (kapena mdzukulu). Koma ngati sadasiye mwana, ndipo makolo ake awiri ndiwo awasiira, ndiye kuti mayi wake alandire gawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho, (ndipo bambo alandire 2/3). Ngati wakufayo wasiya abale, ndiye kuti mayi wake apeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achumacho. (Kugawa chumaku kuchitike) atachotsapo chimene iye adalamulira kuti adzachipereke kwakutikwakuti, kapena kulipira ngongole (zake). Atate anu ndi ana anu, simudziwa inu kuti ndani mwa iwo amene ali ndi chithandizo chapafupi kwa inu. Amenewa ndi malamulo omwe akhazikitsidwa ndi Allah. Ndithudi, Allah ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.[112]
[112] Apa akufotokoza za kagawidwe ka chuma chamasiye (mirath).
a) Ngati munthu wamwalira nkusiya ana amuna ndi akazi tero mwana wamwamuna adzapeza magawo awiri ndipo wamkazi adzapeza gawo limodzi.
b) Munthu akafa nkusiya ana akazi okha, awiri kapena ochulukirapo, anawo adzatenga magawo awiri achumacho. Ndipo onsewo alandire mofanana. Pasapezeke wotenga zochuluka kuposa wina.
Tsono gawo lomwe latsala lidzaperekedwa kwa ena oti awagawire ngati alipo. Ngati palibe, ndiye kuti gawolo lidzaperekedwanso kwa ana akaziwo.
N.B Magawo awiri m’magawo atatu (2/3), apa akutanthauza kuti chuma chonsecho amachigawa m’magawo atatu ofanana. Ndipo akaziwo nkulandira magawo awiri mwa magawo atatuwo.
c) Ngati munthu atamwalira nkusiya mwana mmodzi wamkazi, ndiye kuti chumacho achigawe magawo awiri ofanana. Gawo limodzi mwa magawo awiri aja alipereke kwa mwana wamkaziyo. Ndipo gawo lotsalalo alipereke kwa ena ofunika kuwagawira ngati alipo. Ngati palibe, aliperekenso kwa mwana yemweyo. Lamulo la adzukulu likufanana ndi lamulo la ana ngati wakufayo adalibe ana koma adzukulu ake okha.
d) Munthu akafa nkusiya ana ndi makolo ake, (tate ndi mayi), tero tate adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) a chumacho. Nayenso mayi adzapeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo chuma chotsalacho adzalandira ndi ana kapena adzukulu a muntnu wakufayo.
e) Munthu akafa nkusiya tate wake ndi mayi wake basi, popanda ana ndi adzukulu choncho apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo atatu a chumacho. Ndipo tate adzatenga magawo awiri.
f) Munthu akafa nkusiya mayi wake yekha ndi abale ake obadwa nawo kwa mayi ndi bambo mmodzi, kapena akumbali ya kwabambo okha kapena akumbali yamayi okha, apa mayi adzalandira gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi a chumacho. Anthu oyenera kuwagawira chuma chamasiye asawagawire msanga chumacho mpaka ngongole zonse za wakufayo atazibweza. Ndiponso mpaka apereke chilawo (wasiya) chomwe wakufayo adanena kuti chidzachitike. Owagawira chumawo asakhale anthu osusuka ndi chumacho. choyamba aonetsetse kuti izi zonse zakwaniritsidwa. Komatu chilawocho chisapyole pagawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho. Chikapyolera pamenepa ndiye kuti choonjezerapocho sichivomerezedwa.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (11) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق