ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (12) سورة: النساء
۞ وَلَكُمۡ نِصۡفُ مَا تَرَكَ أَزۡوَٰجُكُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّهُنَّ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَهُنَّ وَلَدٞ فَلَكُمُ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡنَۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصِينَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۚ وَلَهُنَّ ٱلرُّبُعُ مِمَّا تَرَكۡتُمۡ إِن لَّمۡ يَكُن لَّكُمۡ وَلَدٞۚ فَإِن كَانَ لَكُمۡ وَلَدٞ فَلَهُنَّ ٱلثُّمُنُ مِمَّا تَرَكۡتُمۚ مِّنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ تُوصُونَ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٖۗ وَإِن كَانَ رَجُلٞ يُورَثُ كَلَٰلَةً أَوِ ٱمۡرَأَةٞ وَلَهُۥٓ أَخٌ أَوۡ أُخۡتٞ فَلِكُلِّ وَٰحِدٖ مِّنۡهُمَا ٱلسُّدُسُۚ فَإِن كَانُوٓاْ أَكۡثَرَ مِن ذَٰلِكَ فَهُمۡ شُرَكَآءُ فِي ٱلثُّلُثِۚ مِنۢ بَعۡدِ وَصِيَّةٖ يُوصَىٰ بِهَآ أَوۡ دَيۡنٍ غَيۡرَ مُضَآرّٖۚ وَصِيَّةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَلِيمٞ
Inunso mupata gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2) achuma chimene akazi anu asiya ngati alibe mwana (kapena mdzukulu), ngati asiya mwana ndiye kuti inu mupata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) achuma chosiidwacho mutachotsapo zomwe adalamula kuti zipite kwakutikwakuti kapena ngongole zake, naonso akazi anu apata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) pa chuma chomwe mwasiya, ngati mulibe mwana (ndi mdzukulu). Koma ngati mwasiya mwana (ndi mdzukulu), (akaziwo) apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi atatu (1/8) pa chuma chomwe mwasiya mutachotsapo chomwe mudanena kuti chipite kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole (zanu). Ngati mwamuna kapena mkazi alowedwa m’malo pachuma pomwe alibe mwana (ndi mdzukulu) ngakhale makolo awiri, koma ali naye m’bale wake (wakuchikazi) kapena mlongo wake (wakuchikazinso) aliyense wa iwo apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo ngati ali ochulukirapo, ndiye kuti agawirana gawo limodzi m’magawo atatu (1/3) a chumacho pambuyo pochotsapo chomwe chidanenedwa kuti chipita kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole, popanda kupereka mavuto. Awa ndi malamulo ofunika omwe achokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri (pokhazikitsa malamulo); Woleza (pa akapolo Ake).[113]
[113] Apa akufotokoza mmene anthu ena angawagawireko chuma chamasiye.
a) Ngati atafa mkazi nkusiya mwamuna wake yekha popanda kusiya ana kapena adzukulu, mwamunayo alandire gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2) a chuma chomwe wasiya mkazi wakecho.
b) Akafa mkazi nkusiya mwamuna ndi nnwana wake kapena mdzukulu wake apa ndiye kuti mwamunayo adzalandira (1/4) gawo limodzi mwa magawo anayi achumacho.
c) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake popanda mwana kapena mdzukulu wake ndiye kuti mkaziyo adzalandira (1/4) gawo limodzi mwamagawo anayi achuma cha mwamuna wakecho. Ndipo chotsalacho achipereke kwa ena ofunika kuwagawira.
d) Akafa mwamuna nkusiya mkazi wake ndi mwana wake kapena mdzukulu wake, apa mkazi alandire (1/8) gawo limodzi mwa magawo asanu ndi atatu a chuma cha mwamunayo.
e) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena zidzukulu ndi makolo, koma nkusiya m’bale mmodzi wamwamuna kapena wamkazi wakumbali ya mayi, apa ndiye kuti m’baleyo adzalandira (1/6) gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi a chumacho. Ndipo chotsalacho adzawagawira ena oyenera kuwagawira ngati alipo. Koma ngati palibe ndiye kuti m’baleyo adzatenganso chotsalacho.
f) Akamwalira munthu popanda kusiya ana kapena adzukulu ndi makolo, koma wasiya abale akumbali yamayi, amuna kapena akazi, apa ndiye kuti abalewa adzalandira (1/3) gawo limodzi mwa magawo atatu achuma cha womwalirayo. Ndipo adzagawana pakati pawo mofanana amuna ndi akazi omwe.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (12) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق