ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (46) سورة: النساء
مِّنَ ٱلَّذِينَ هَادُواْ يُحَرِّفُونَ ٱلۡكَلِمَ عَن مَّوَاضِعِهِۦ وَيَقُولُونَ سَمِعۡنَا وَعَصَيۡنَا وَٱسۡمَعۡ غَيۡرَ مُسۡمَعٖ وَرَٰعِنَا لَيَّۢا بِأَلۡسِنَتِهِمۡ وَطَعۡنٗا فِي ٱلدِّينِۚ وَلَوۡ أَنَّهُمۡ قَالُواْ سَمِعۡنَا وَأَطَعۡنَا وَٱسۡمَعۡ وَٱنظُرۡنَا لَكَانَ خَيۡرٗا لَّهُمۡ وَأَقۡوَمَ وَلَٰكِن لَّعَنَهُمُ ٱللَّهُ بِكُفۡرِهِمۡ فَلَا يُؤۡمِنُونَ إِلَّا قَلِيلٗا
Mwa Ayuda alipo omwe amasintha mawu kuwachotsa m’malo mwake. Ndipo amanena (chabe ndi milomo yawo): “Tamva;” (pomwe mitima yawo ikunena): “Tanyoza.” (Ndipo akunena kuuza Mtumiki): “Imva koma wosamveredwa (ndipo pakati pakuyankhula kwawo amanena mawu akuti) ‘Raaina’ (ncholinga chomnenera kuti iye ndimbutuma), mokhotetsa malilime awo (mu zoyankhula zawo kuti akhale ngati akumunenera zabwino pomwe akumtembelera) ndi cholinga chotukwana chipembedzo (cha Chisilamu). Akadakhala kuti iwo adanena: “Tamva ndipo tamvera; ndipo imva, utiyang’anire,” (mmalo mwa kunena kwawo kwakuti: ‘Raaina’), zikadakhala zabwino ndizolingana kwa iwo. Koma Allah adawatembelera chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Sakhulupirira koma pang’ono basi.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (46) سورة: النساء
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق