ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: الحشر   آية:

الحشر

سَبَّحَ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۖ وَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
Zonse za kumwamba ndi za pansi zimalemekeza Allah (ndi kumuyeretsa ku khalidwe losayenera ndi ulemelero Wake). Ndipo Iye Ngopambana (salephera kanthu), Ngwaluntha (m’kakonzedwe Kake ndi m’zochita Zake).
التفاسير العربية:
هُوَ ٱلَّذِيٓ أَخۡرَجَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ مِن دِيَٰرِهِمۡ لِأَوَّلِ ٱلۡحَشۡرِۚ مَا ظَنَنتُمۡ أَن يَخۡرُجُواْۖ وَظَنُّوٓاْ أَنَّهُم مَّانِعَتُهُمۡ حُصُونُهُم مِّنَ ٱللَّهِ فَأَتَىٰهُمُ ٱللَّهُ مِنۡ حَيۡثُ لَمۡ يَحۡتَسِبُواْۖ وَقَذَفَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلرُّعۡبَۚ يُخۡرِبُونَ بُيُوتَهُم بِأَيۡدِيهِمۡ وَأَيۡدِي ٱلۡمُؤۡمِنِينَ فَٱعۡتَبِرُواْ يَٰٓأُوْلِي ٱلۡأَبۡصَٰرِ
Iye ndi Amene adatulutsa osakhulupirira ena mwa anthu a buku m’nyumba zawo mkusamusidwa koyamba (pa chilumba cha Arabu). Simunkaganizira kuti angatuluke (m’nyumba zawozo). Ndipo iwo amaganiza kuti malinga awo awateteza kwa Allah. Koma Allah adawalanga kupyolera mmene samayembekezera, ndipo adathira mantha oopsa m’mitima mwawo (potumiza Mtumiki Wake kwa iwo), adagumula nyumba zawo ndi manja awo ndi manja a okhulupirira. Choncho lingalirani (zimenezi) E inu eni nzeru! [353]
[353] Ayah imeneyi ikulongosola nkhani ya kusamutsidwa kwa Ayuda otchedwa Bani Nadhir mu mzinda wa Madina. Ayuda adasamutsidwa mu mzinda wa Madina chifukwa cha kuswa mapangano okhalirana mwa mtendere ndi Asilamu.
التفاسير العربية:
وَلَوۡلَآ أَن كَتَبَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِمُ ٱلۡجَلَآءَ لَعَذَّبَهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابُ ٱلنَّارِ
Ndipo kukadapanda kuti Allah adawalembera (pachiyambi) kusamuka (m’nyumba zawo), akadawalanga pa dziko pompano; koma chilango cha Moto chili pa iwo tsiku lachimaliziro.
التفاسير العربية:
ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ شَآقُّواْ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥۖ وَمَن يُشَآقِّ ٱللَّهَ فَإِنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo adamtsutsa Allah ndi Mthenga Wake, (kutsutsa kopyola muyeso); ndipo amene akutsutsa Allah (sangapulumuke ku chilango Chake). Ndithu Allah Ndiwolanga mwaukali.
التفاسير العربية:
مَا قَطَعۡتُم مِّن لِّينَةٍ أَوۡ تَرَكۡتُمُوهَا قَآئِمَةً عَلَىٰٓ أُصُولِهَا فَبِإِذۡنِ ٱللَّهِ وَلِيُخۡزِيَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Sim’dadule mtengo uliwonse wa zipatso za kanjedza, (inu Asilamu), kapena kuusiya uli chiimire ndi thunthu lake koma nchifuniro cha Allah ndi kuti awayalutse otuluka m’malamulo Ake.[354]
[354] (Ndime 5-7) Ndime zimenezi zikufotokoza za kagawidwe ka chuma chosiyidwa ndi adani pankhondo. Chumacho sichongogawira amene amachita nkhondo okha ayi. Kapena kugawana akulu-akulu okha monga momwe amachitira ena omwe sali Asilamu pa nkhondo zawo. Chifukwa kutero ndiye kuti chumacho chizingozungulira pakati pa anthu olemera okhaokha. Chisilamu chikulamula kuti chuma choterechi chigawidwe kwa onse kuti umphawi uwachokere onse.
التفاسير العربية:
وَمَآ أَفَآءَ ٱللَّهُ عَلَىٰ رَسُولِهِۦ مِنۡهُمۡ فَمَآ أَوۡجَفۡتُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ خَيۡلٖ وَلَا رِكَابٖ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ يُسَلِّطُ رُسُلَهُۥ عَلَىٰ مَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Ndipo chuma chimene wapereka Allah kwa Mtumiki Wake chochokera kwa iwo (Bani Nadhiri), chimenecho inu simudathamangitse mahachi kapena ngamira (pakuchipeza), koma Allah amapereka mphamvu kwa atumiki Ake zogonjetsera amene wamfuna. Ndipo Allah ali ndi Mphamvu (pa) chilichonse.
التفاسير العربية:
مَّآ أَفَآءَ ٱللَّهُ عَلَىٰ رَسُولِهِۦ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡقُرَىٰ فَلِلَّهِ وَلِلرَّسُولِ وَلِذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِ كَيۡ لَا يَكُونَ دُولَةَۢ بَيۡنَ ٱلۡأَغۡنِيَآءِ مِنكُمۡۚ وَمَآ ءَاتَىٰكُمُ ٱلرَّسُولُ فَخُذُوهُ وَمَا نَهَىٰكُمۡ عَنۡهُ فَٱنتَهُواْۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَۖ إِنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Chuma chimene Allah wachipereka kwa mtumiki Wake kuchokera kwa anthu am’midzi (yapafupi ndi mzinda wa Madina) chimenecho ncha Allah, ndi Mtumiki, ndi abale a mtumiki ndi amasiye, ndi masikini, ndiponso apaulendo; kuti chisakhale chongozungulira pakati pa olemera okha mwa inu. Ndipo chimene wakupatsani Mtumiki, chilandireni; ndipo chimene Wakuletsani chisiyeni. Muopeni Allah (potsatira malamulo Ake). Ndithu Allah Ngwaukali polanga.
التفاسير العربية:
لِلۡفُقَرَآءِ ٱلۡمُهَٰجِرِينَ ٱلَّذِينَ أُخۡرِجُواْ مِن دِيَٰرِهِمۡ وَأَمۡوَٰلِهِمۡ يَبۡتَغُونَ فَضۡلٗا مِّنَ ٱللَّهِ وَرِضۡوَٰنٗا وَيَنصُرُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلصَّٰدِقُونَ
(Chiperekedwe) kwa osauka osamuka omwe adatulutsidwa m’nyumba zawo ndi (kusiya) chuma chawo chifukwa chofuna zabwino za Allah ndi chikondi (Chake) ndi kupulumutsa (chipembedzo cha) Allah ndi Mthenga Wake (pogwiritsira ntchito matupi awo ndi chuma chawo); iwowa ndi (Asilamu) owona.
التفاسير العربية:
وَٱلَّذِينَ تَبَوَّءُو ٱلدَّارَ وَٱلۡإِيمَٰنَ مِن قَبۡلِهِمۡ يُحِبُّونَ مَنۡ هَاجَرَ إِلَيۡهِمۡ وَلَا يَجِدُونَ فِي صُدُورِهِمۡ حَاجَةٗ مِّمَّآ أُوتُواْ وَيُؤۡثِرُونَ عَلَىٰٓ أَنفُسِهِمۡ وَلَوۡ كَانَ بِهِمۡ خَصَاصَةٞۚ وَمَن يُوقَ شُحَّ نَفۡسِهِۦ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Koma amene adakhala kale mu mzinda uwu (wa Madina) ndi kukhulupirira akukonda amene adasamukira kwa iwo. Ndipo sakupeza vuto m’mitima mwawo pa zimene anzawo apatsidwa, ndipo akutsogoza zofuna za anzawo pa zawo, ngakhale iwo akuzifunitsitsa. Ndipo amene atetezedwa (ndi Allah) ku umbombo wa mitima yawo, amenewo ndiwo opambana.
التفاسير العربية:
وَٱلَّذِينَ جَآءُو مِنۢ بَعۡدِهِمۡ يَقُولُونَ رَبَّنَا ٱغۡفِرۡ لَنَا وَلِإِخۡوَٰنِنَا ٱلَّذِينَ سَبَقُونَا بِٱلۡإِيمَٰنِ وَلَا تَجۡعَلۡ فِي قُلُوبِنَا غِلّٗا لِّلَّذِينَ ءَامَنُواْ رَبَّنَآ إِنَّكَ رَءُوفٞ رَّحِيمٌ
Ndipo (okhulupirira) amene adadza pambuyo (pa Amuhajirina ndi Answari) akunena kuti: “Mbuye wathu tikhululukireni ndi anzathu amene adatitsogolera pa chikhulupiliro, ndipo musaike m’mitima mwathu njiru ndi chidani kwa amene adakhulupirira. E Mbuye wathu! Inu ndinu Wodekha, Wachisoni chosatha.”
التفاسير العربية:
۞ أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ نَافَقُواْ يَقُولُونَ لِإِخۡوَٰنِهِمُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ لَئِنۡ أُخۡرِجۡتُمۡ لَنَخۡرُجَنَّ مَعَكُمۡ وَلَا نُطِيعُ فِيكُمۡ أَحَدًا أَبَدٗا وَإِن قُوتِلۡتُمۡ لَنَنصُرَنَّكُمۡ وَٱللَّهُ يَشۡهَدُ إِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
Kodi wawaona amene achita uchiphamaso? Amene akunena kwa anzawo amene sadakhulupirire pakati pa anthu a mabuku: “Ndithu ngati (mukakamizidwa) kutuluka mu mzinda wa Madina, ndithudi tidzatuluka nanu pamodzi ndipo sitingamvere aliyense za inu mpaka muyaya; ngati mutamenyedwa nkhondo (ndi Asilamu) tidzakuthandizani. Koma Allah akuikira umboni kuti iwo ndionama (pa zimene alonjeza).
التفاسير العربية:
لَئِنۡ أُخۡرِجُواْ لَا يَخۡرُجُونَ مَعَهُمۡ وَلَئِن قُوتِلُواْ لَا يَنصُرُونَهُمۡ وَلَئِن نَّصَرُوهُمۡ لَيُوَلُّنَّ ٱلۡأَدۡبَٰرَ ثُمَّ لَا يُنصَرُونَ
Ngati atatulutsidwa, sangatuluke nawo limodzi; ngati atamenyedwa, sangawathandize ndipo ngati atawathandiza atembenuza misana (kuthawa) kenako sapulumutsidwa.
التفاسير العربية:
لَأَنتُمۡ أَشَدُّ رَهۡبَةٗ فِي صُدُورِهِم مِّنَ ٱللَّهِۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَفۡقَهُونَ
Ndithu inu (Asilamu) mukuopedwa kwambiri m’mitima mwawo kuposa mmene akumuopera Allah. Zimenezo nchifukwa chakuti iwo ndi anthu osazindikira (chilichonse).
التفاسير العربية:
لَا يُقَٰتِلُونَكُمۡ جَمِيعًا إِلَّا فِي قُرٗى مُّحَصَّنَةٍ أَوۡ مِن وَرَآءِ جُدُرِۭۚ بَأۡسُهُم بَيۡنَهُمۡ شَدِيدٞۚ تَحۡسَبُهُمۡ جَمِيعٗا وَقُلُوبُهُمۡ شَتَّىٰۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَعۡقِلُونَ
(Ayuda) sangamenyane ndi inu ali pa gulu kupatula m’midzi yotetezedwa ndi malinga, kapena kuseri kwa zipupa. Nkhondo yawo pakati pawo njaukali; ungawaganizire kuti ali pamodzi pomwe mitima yawo njosiyana; zimenezo nchifukwa chakuti iwo ndianthu opanda nzeru.
التفاسير العربية:
كَمَثَلِ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ قَرِيبٗاۖ ذَاقُواْ وَبَالَ أَمۡرِهِمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Fanizo (la Ayuda a Banu Nadhiri) lili ngati (amene adatsutsa mwa Ayuda a Qainuka) amene awatsogolera (kupeza mavuto) posachedwapa, adalawa chilango (pa dziko lapansi) cha zochita zawo (ndi kuswa mapangano). Ndipo iwo adzalandira chilango (china) chowawa kwambiri, (pa tsiku la chiweruziro).
التفاسير العربية:
كَمَثَلِ ٱلشَّيۡطَٰنِ إِذۡ قَالَ لِلۡإِنسَٰنِ ٱكۡفُرۡ فَلَمَّا كَفَرَ قَالَ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّنكَ إِنِّيٓ أَخَافُ ٱللَّهَ رَبَّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Fanizo la achinyengo (achiphamaso pakuwanyenga Banu Nadhiri kuti amupandukire Mneneri wa Allah) lili ngati satana (ponyenga munthu kusiya chikhulupiliro). Adati kwa Iye: “Mkane (Allah).” Ndipo pamene adamkana, (satana) adati: “Ine sindili ndi iwe; ndithu ine ndikuopa Allah, Mbuye wa zolengedwa.”
التفاسير العربية:
فَكَانَ عَٰقِبَتَهُمَآ أَنَّهُمَا فِي ٱلنَّارِ خَٰلِدَيۡنِ فِيهَاۚ وَذَٰلِكَ جَزَٰٓؤُاْ ٱلظَّٰلِمِينَ
Choncho mapeto a onse awiriwo, kudali kukalowa ku Moto ndi kukhala m’menemo nthawi yaitali. Iyi ndiyo mphoto ya anthu onyenga (ochenjelera anzawo).
التفاسير العربية:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَلۡتَنظُرۡ نَفۡسٞ مَّا قَدَّمَتۡ لِغَدٖۖ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَۚ إِنَّ ٱللَّهَ خَبِيرُۢ بِمَا تَعۡمَلُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Muopeni Allah (potsatira malamulo Ake ndi kusiya zimene waletsa) ndipo alingalire munthu aliyense zamawa zimene watsogoza. Ndipo muopeni Allah, ndithu Allah Ngodziwa zimene mukuchita (ndipo adzakulipirani pa zimenezo).
التفاسير العربية:
وَلَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ نَسُواْ ٱللَّهَ فَأَنسَىٰهُمۡ أَنفُسَهُمۡۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡفَٰسِقُونَ
Ndipo musakhale monga amene aiwala (zoyenera kuchitira) Allah; choncho (naye Allah) wawaiwalitsa mitima yawo (powachotsera kuzindikira zimene zingawathandize). Amenewa ndiwo olakwa kwakukulu (otuluka ku chilamulo cha Allah).
التفاسير العربية:
لَا يَسۡتَوِيٓ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِ وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡجَنَّةِۚ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَنَّةِ هُمُ ٱلۡفَآئِزُونَ
Sangafanane anthu a ku Moto, (olangidwa), ndi anthu a ku Jannah, (opeza mtendere). Anthu aku Jannah ndiwo opambana.
التفاسير العربية:
لَوۡ أَنزَلۡنَا هَٰذَا ٱلۡقُرۡءَانَ عَلَىٰ جَبَلٖ لَّرَأَيۡتَهُۥ خَٰشِعٗا مُّتَصَدِّعٗا مِّنۡ خَشۡيَةِ ٱللَّهِۚ وَتِلۡكَ ٱلۡأَمۡثَٰلُ نَضۡرِبُهَا لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَفَكَّرُونَ
Chikhala kuti tidaivumbulutsa Qur’an iyi pamwamba pa phiri, ukadaliona phirilo lili lodzichepetsa ndi kung’ambika chifukwa choopa Allah. Ndipo awa ndi mafanizo omwe tikuwapereka kwa anthu kuti aganizire.
التفاسير العربية:
هُوَ ٱللَّهُ ٱلَّذِي لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ عَٰلِمُ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِۖ هُوَ ٱلرَّحۡمَٰنُ ٱلرَّحِيمُ
Iye ndi Allah, Amene palibenso wina wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye, Wodziwa zamseri ndi zooneka. Iye Ngwachifundo chambiri, Ngwachisoni chosatha.
التفاسير العربية:
هُوَ ٱللَّهُ ٱلَّذِي لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلۡمَلِكُ ٱلۡقُدُّوسُ ٱلسَّلَٰمُ ٱلۡمُؤۡمِنُ ٱلۡمُهَيۡمِنُ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡجَبَّارُ ٱلۡمُتَكَبِّرُۚ سُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ عَمَّا يُشۡرِكُونَ
Iye ndi Allah, Amene palibenso wina wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye, Mfumu, Woyera, Mwini mtendere, Wotsimikizira (aneneri Ake mphamvu yochitira zozizwitsa,) Msungi wa chilichonse (yemwe akuona zochita za akapolo Ake;) Wamphamvu zopambana, Mgonjetsi Wotukuka muulemelero; Wamkulukulu. Wayeretsedwa Allah kuzimene akumuphatikiza nazo.
التفاسير العربية:
هُوَ ٱللَّهُ ٱلۡخَٰلِقُ ٱلۡبَارِئُ ٱلۡمُصَوِّرُۖ لَهُ ٱلۡأَسۡمَآءُ ٱلۡحُسۡنَىٰۚ يُسَبِّحُ لَهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ وَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
Iye ndi Allah; Mlengi wa (zinthu, palibe chomfanizira); Muumbi wa chilichonse, Mkonzi wa maonekedwe a zinthu, Ake ndi maina abwino, zonse za kumwamba ndi pansi zikumulemekeza Iye ndi kumyeretsa ku makhalidwe osayenerana ndi ulemelero Wake. Iye Ngopambana ndiponso Wanzeru zakuya.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: الحشر
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق