ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (9) سورة: الجمعة
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا نُودِيَ لِلصَّلَوٰةِ مِن يَوۡمِ ٱلۡجُمُعَةِ فَٱسۡعَوۡاْ إِلَىٰ ذِكۡرِ ٱللَّهِ وَذَرُواْ ٱلۡبَيۡعَۚ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Kukaitanidwa ku Swala (pemphero la Ijuma) tsiku la Ijuma, pitani mwachangu kukamtamanda Allah. Ndipo siyani malonda; zimenezo (mwalamulidwazo) nzabwino kwa inu ngati mukudziwa.[363]
[363] M’ndime imeneyi akutiphunzitsa kuti tikamva adhana (kuitana) tsiku la Ijuma, tisiye chilichonse chimene tikuchita ndi kupita mwachangu kukapemphera pemphero la Ijuma. Pempheroli ndilofunika kwa msilamu aliyense makamaka amuna. Asilamu amasonkhana m’Misikiti ikuluikulu pa tsiku limeneli pa sabata iliyonse. Ndipo pa tsiku limeneli ndipomwe Allah adakwaniritsa zolenga zake zonse. Adam adalengedwa pa tsikuli ndipo adalowetsedwa ku Jannah tsiku lomweli. Ndipo adatulutsidwa m’menemo pa tsiku la Ijuma. Mtumiki adafotokozanso za kuti Qiyâma idzadza tsiku la Ijuma.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (9) سورة: الجمعة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق