ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (10) سورة: الأنفال
وَمَا جَعَلَهُ ٱللَّهُ إِلَّا بُشۡرَىٰ وَلِتَطۡمَئِنَّ بِهِۦ قُلُوبُكُمۡۚ وَمَا ٱلنَّصۡرُ إِلَّا مِنۡ عِندِ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ndipo Allah sadachite ichi koma kuti chikhale nkhani yabwino (yosangalatsa), ndi kuti mitima yanu ikhazikike ndi chimenecho. Ndipo palibe chipulumutso (chothandiza) koma chimene chachokera kwa Allah. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.[192]
[192] (Ndime 10-11) Asilamu adapeza lonjezo lochoka kwa Allah lakuti pa nthawi ya nkhondo adzawatumizira angelo, pamenepo mitima ya Asilamu idakhazikika kotero kuti ena mwa iwo adadzilotera nakhala ndi Janaba. Choncho panafunika kuti asambe, koma madzi panalibe. Ndipo mwadzidzidzi mvula idawavumbwira ndipo adapeza madzi osamba ndi ena ogwira nawo ntchito zina. Chigwa cha Badiri chidali chamchenga wokhawokha. Ndipo mchenga umene udali kumbali ya Asilamu udali wosayendeka. Munthu akati ayende, mapazi amangozama. Tero pamene mvulayo idavumbwa, mchengawo udagwirana nkukhala woyendeka. Zitatero Asilamu zidawayendera bwino. Koma kumbali ya Amushirikina kudali matope okhaokha. Choncho sadathe kuyenda mwachangu. Umo ndimomwe chifundo cha Allah chidalili pa Asilamu.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (10) سورة: الأنفال
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق