ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (30) سورة: الأنفال
وَإِذۡ يَمۡكُرُ بِكَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيُثۡبِتُوكَ أَوۡ يَقۡتُلُوكَ أَوۡ يُخۡرِجُوكَۚ وَيَمۡكُرُونَ وَيَمۡكُرُ ٱللَّهُۖ وَٱللَّهُ خَيۡرُ ٱلۡمَٰكِرِينَ
Ndipo (kumbukira) pamene omwe sadakhulupirire amakuchitira chiwembu kuti akunjate, kapena akuphe, kapena akutulutse (m’dziko lawo la Makka mwachipongwe). Ndipo amachita chiwembu, naye Allah anawononga chiwembu chawocho. Ndipo Allah ndiwokhoza koposa poononga ziwembu (za anthu oipa).[199]
[199] Apa pakutchulidwa ziwembu za Aquraish zomwe adamchitira Mtumiki (s.a.w) asanasamuke ku Makka. Iwo adasonkhana m’nyumba yochitiramo upo nayamba kukambirana za chomwe angachite naye Mneneri Muhammad, chimene chingamuonongeretu. Ena anapereka maganizo akuti akamponye m’ndende konko ku Makka popanda kumpatsa chakudya. Kapena ampatse chakudya chochepa kwambiri kufikira afe ndi njala. Ndipo ena adati koma amtseke maso ndi milomo ndi kumnjata goli m’manja kenako kumkweza pa ngamira nkukamtaya kuchipululu chamchenga kuti akafere konko.
Ena amapereka ganizo oti asankhe anyamata ochokera m’mafuko amfulu kuti onse pamodzi akammenye ndi kumupha. Ganizoli ndi lomwe anavomerezana. Koma usiku omwe adapangana kuti amuphe, ndi umene Mtumiki (s.a.w) adasamuka kunka ku Madina. potero adalephera kumupha.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (30) سورة: الأنفال
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق