ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني آية: (42) سورة: الأنفال
إِذۡ أَنتُم بِٱلۡعُدۡوَةِ ٱلدُّنۡيَا وَهُم بِٱلۡعُدۡوَةِ ٱلۡقُصۡوَىٰ وَٱلرَّكۡبُ أَسۡفَلَ مِنكُمۡۚ وَلَوۡ تَوَاعَدتُّمۡ لَٱخۡتَلَفۡتُمۡ فِي ٱلۡمِيعَٰدِ وَلَٰكِن لِّيَقۡضِيَ ٱللَّهُ أَمۡرٗا كَانَ مَفۡعُولٗا لِّيَهۡلِكَ مَنۡ هَلَكَ عَنۢ بَيِّنَةٖ وَيَحۡيَىٰ مَنۡ حَيَّ عَنۢ بَيِّنَةٖۗ وَإِنَّ ٱللَّهَ لَسَمِيعٌ عَلِيمٌ
(Kumbukirani) pamene mudali mbali ya chigwa yoyandikira (mzinda wa Madina) pomwe iwo (ankhondo a Chikuraishi) adali mbali ya kutali ya tsidya lina (la chigwacho) pomwe aulendo amalonda adali cha kumunsi kwanu. Ngati mukadapangana nthawi yokumanirana (kuti mukumane nthawi yakutiyakuti), mukadasiyana posunga chipangano (chifukwa cha kuopa kuchuluka kwa adani anuwo). Koma (mwakumana mosayembekezera ndi ankhondo a adaniwo) kuti Allah akwaniritse chinthu chomwe nchofunika kuti chichitike, kuti awonongeke amene waonongeka (posankha kusakhulupirira) ndi umboni woonekera (umene adaukana kuutsata), ndi kuti akhale ndi moyo amene wakhala ndi moyo (amene watsata njira ya Chisilamu) ndi umboninso woonekera. Ndithudi Allah Ngwakumva zonse, Ngodziwa kwambiri.[202]
[202] M’ndime iyi mwatchulidwa gulu lankhondo la Asilamu ndi gulu lankhondo la Aquraish ndi aulendo a chuma chamalonda a Aquraish. Aquraish adavutitsa Asilamu mu Mzinda wa Makka m’nyengo yazaka khumi ndi zitatu powalanda zinthu zawo ndi kuwamenya ndi kuwapha kumene. Pambuyo pake Asilamu adathawira ku Madina nkusiya chuma chawo chonse ku Makka. Chumacho chidatengedwa ndi anthu osakhulupilira Allah a Chikuraishi. Ndipo kuonjezera pa zimenezi Akafiri (Aquraish) adali kudza ku Madina usiku kudzaononga zinthu zambiri, pambuyo pake nkuthawa. Ndipo mwa zomwe adachita ndi monga kutentha nyumba ndi ziweto. Ankachitanso zifwamba zambiri.
Patapita zaka khumi ndi zisanu, Asilamu akuvutitsidwabe, Allah adawapatsa chilolezo kuti amenyane ndi Akafiriwo monga momwe iwo adali kuwamenyera. Ndiponso kuti awalande chilichonse chimene Asilamu angathe kulanda kuti abweze zinthu zawo zomwe adawalanda. Choncho Mtumiki (s.a.w) adamva kuti pali ulendo wa Aquraish umene wanyamula chuma chambiri ndipo udzadutsa pafupi ndi mzinda wa Madina. Tero, adawakhwirizira omtsatira ake (Maswahaba) kuti apite pamodzi naye nkukauthira nkhondo ulendowo, nkuulanda chumacho.
Choncho anthu adamtsata okwana mazana atatu popanda kutenga zida zaukali za nkhondo poti sadalinge kukamenya nkhondo yeniyeni koma adalinga kukalanda chumacho basi, chomwe chidali m’manja mwa anthu ochepa a paulendo; ndipo sadalinge kukawapha. Koma wotsogolera ulendo wamalondawo, mwamwayi adamva kuti Mtumiki ndi omtsatira ake akumufunafuna kuti amulande chumacho. Pompo adasintha njira natsata njira ina yomwe siinkayendedwa kuti asakumane ndi Mtumiki.
Ndipo anatuma mthenga ku Makka kuti akawauze anthu a m’Makka kuti iwo anthu amalonda athiridwa nkhondo. Aquraish ku Makka atamva nkhani iyi, adasangalala. Adaona kuti apeza mwayi womumaliziratu Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndi omtsatira ake. Choncho adatuluka atakonzeka bwinobwino za nkhondo. Osati momwe Mtumiki ndi omtsatira ake adakonzekera. Mtumiki ndi omtsatira ake sadadziwe kuti aulendo amene iwo adali kuwadikilira awadutsa kale, ndi kuti gulu lalikulu lankhondo la Aquraish likuwadzera kudzawathira nkhondo, ndipo lafika kale pafupi nawo. Adadziwa za nkhaniyo pomwe iwo (Mtumiki ndi gulu lake) adali kutali ndi mzinda wawo wa Madina. Ndipo nkhaniyi itadziwika kwa omtsatira ake, padabuka mkangano pakati pawo. Ena adali ndi maganizo akuti alithawe gulu lankhondo la Aquraishwo, nkupitiriza kutsatira gulu lamalonda lija, pakuti adali ndi chitsimikizo chonse kuti akawagonjetsa amalondawo. Koma gulu lankhondo la Aquraish adalibe nalo chiyembekezo choligonjetsa naona kuti sikwabwino kudziika okha pachionongeko. Koma mwamwayi adakumana nalo gulu lankhondo la Aquraish mosayembekezera pomwe aulendo wa malonda aja adali kutali nawo.
Tero ili ndilo tanthauzo la Ayah ya 42.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني آية: (42) سورة: الأنفال
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق