কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ * - অনুবাদসমূহের সূচী


অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আয-যুখরুফ   আয়াত:

সূরা আয-যুখরুফ

حمٓ
. Hâ-Mîm.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Ndikulumbilira buku lofotokoza momveka.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّا جَعَلۡنَٰهُ قُرۡءَٰنًا عَرَبِيّٗا لَّعَلَّكُمۡ تَعۡقِلُونَ
Ndithu Ife talichita bukuli (Qur’an) kukhala chowerengedwa m’Chiarabu kuti muzindikire.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِنَّهُۥ فِيٓ أُمِّ ٱلۡكِتَٰبِ لَدَيۡنَا لَعَلِيٌّ حَكِيمٌ
Ndipo ndithu bukuli (Qur’an) lili m’manthu wa mabuku onse (Lawhi Mahfudh) limene lili kwa Ife; (ndipo ndi buku) lotukuka, la mawu anzeru.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَفَنَضۡرِبُ عَنكُمُ ٱلذِّكۡرَ صَفۡحًا أَن كُنتُمۡ قَوۡمٗا مُّسۡرِفِينَ
Kodi tisiye kukukumbutsani chifukwa chakuti ndinu anthu opyola malire (pochita zoipa)?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكَمۡ أَرۡسَلۡنَا مِن نَّبِيّٖ فِي ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo tidatumiza aneneri ambiri kwa anthu akale.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَا يَأۡتِيهِم مِّن نَّبِيٍّ إِلَّا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndipo palibe mneneri aliyense amene amawadzera koma amam’chitira chipongwe.
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَأَهۡلَكۡنَآ أَشَدَّ مِنۡهُم بَطۡشٗا وَمَضَىٰ مَثَلُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Choncho tidawaononga amene adali amphamvu kuposa iwo (Aquraish) ndipo ladutsa fanizo la (zilango zomwe zidawapeza) anthu akale.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَئِن سَأَلۡتَهُم مَّنۡ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ لَيَقُولُنَّ خَلَقَهُنَّ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo ukawafunsa: “Ndani adalenga thambo ndi nthaka?” Ndithu ayankha kuti: “Adazilenga (Allah) Mwini Mphamvu, Wodziwa.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
ٱلَّذِي جَعَلَ لَكُمُ ٱلۡأَرۡضَ مَهۡدٗا وَجَعَلَ لَكُمۡ فِيهَا سُبُلٗا لَّعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Amene wakupangirani nthaka kukhala choyala ndipo adakupangirani njira mmenemo kuti muongoke (ndikukafika kumene mukufuna).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَٱلَّذِي نَزَّلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءَۢ بِقَدَرٖ فَأَنشَرۡنَا بِهِۦ بَلۡدَةٗ مَّيۡتٗاۚ كَذَٰلِكَ تُخۡرَجُونَ
Ndiponso amene watsitsa madzi kuchokera kumwamba mwamuyeso; chifukwa cha madziwo tidaukitsa mudzi wakufa. Momwemonso inu mudzatulutsidwa (mmanda);
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَٱلَّذِي خَلَقَ ٱلۡأَزۡوَٰجَ كُلَّهَا وَجَعَلَ لَكُم مِّنَ ٱلۡفُلۡكِ وَٱلۡأَنۡعَٰمِ مَا تَرۡكَبُونَ
Ndiponso amene walenga zinthu zonse ziwiriziwiri (chachimuna ndi chachikazi). Ndipo adakupangirani zombo ndi ziweto zimene mukukwera,
আরবি তাফসীরসমূহ:
لِتَسۡتَوُۥاْ عَلَىٰ ظُهُورِهِۦ ثُمَّ تَذۡكُرُواْ نِعۡمَةَ رَبِّكُمۡ إِذَا ٱسۡتَوَيۡتُمۡ عَلَيۡهِ وَتَقُولُواْ سُبۡحَٰنَ ٱلَّذِي سَخَّرَ لَنَا هَٰذَا وَمَا كُنَّا لَهُۥ مُقۡرِنِينَ
Kuti mukhazikike mwaubwino pamisana paizo, kenako mukumbukire mtendere wa Mbuye wanu mukakhazikika pamenepo, ndipo munene: “Walemekezeka Amene watifewetsera ichi; ndipo sitikadatha kuchifewetsa ndi kuchigwiritsa ntchito.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا لَمُنقَلِبُونَ
“Ndipo ndithu ife kwa Mbuye wathu ndiko kobwerera.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلُواْ لَهُۥ مِنۡ عِبَادِهِۦ جُزۡءًاۚ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَكَفُورٞ مُّبِينٌ
Ndipo amuikira gawo mwa akapolo Ake. (Kuti ndi ana a Allah.) Ndithu munthu, ngwamsulizo woonekera poyera!
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَمِ ٱتَّخَذَ مِمَّا يَخۡلُقُ بَنَاتٖ وَأَصۡفَىٰكُم بِٱلۡبَنِينَ
Kodi wadzichitira ana achikazi mzimene wazilenga ndipo wakusankhirani inu ana achimuna?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِذَا بُشِّرَ أَحَدُهُم بِمَا ضَرَبَ لِلرَّحۡمَٰنِ مَثَلٗا ظَلَّ وَجۡهُهُۥ مُسۡوَدّٗا وَهُوَ كَظِيمٌ
Koma akauzidwa (kuti wabereka mwana wamkazi) mmodzi wa iwo chomwe amamfanizira (Allah) Wachifundo chambiri, nkhope yake imakhala yakuda ndi kudandaula kwambiri!
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَوَمَن يُنَشَّؤُاْ فِي ٱلۡحِلۡيَةِ وَهُوَ فِي ٱلۡخِصَامِ غَيۡرُ مُبِينٖ
Ha! Kodi amene waleredwa monga chokongoletsa, potsutsana iye sangathe kunena momveka? (Ameneyo ndiye mwampatsa Allah; omwe ndi ana aakazi).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلُواْ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ ٱلَّذِينَ هُمۡ عِبَٰدُ ٱلرَّحۡمَٰنِ إِنَٰثًاۚ أَشَهِدُواْ خَلۡقَهُمۡۚ سَتُكۡتَبُ شَهَٰدَتُهُمۡ وَيُسۡـَٔلُونَ
Ndipo angelo omwe ndi akapolo a (Allah) Wachifundo chambiri akuwatcha akazi. Kodi adaona kalengedwe kawo? Umboni wawo ulembedwa ndipo adzafunsidwa (pazimenezo)!
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَقَالُواْ لَوۡ شَآءَ ٱلرَّحۡمَٰنُ مَا عَبَدۡنَٰهُمۗ مَّا لَهُم بِذَٰلِكَ مِنۡ عِلۡمٍۖ إِنۡ هُمۡ إِلَّا يَخۡرُصُونَ
Ndipo (otsutsa) akunena: “Akadafuna (Allah) Wachifundo chambiri (kuti tisamapembedze mafano awa), sitikadawapembedza!” Iwo alibe kudziwa pa zimenezi (zomwe akunenazi). Koma akungonena mawu opeka.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَمۡ ءَاتَيۡنَٰهُمۡ كِتَٰبٗا مِّن قَبۡلِهِۦ فَهُم بِهِۦ مُسۡتَمۡسِكُونَ
Kapena tidawapatsa buku lina tisadapereke ili, kotero kuti iwo agwiritsitsa limenelo (ndi kugwirizana nazo zili mmenemo)?
আরবি তাফসীরসমূহ:
بَلۡ قَالُوٓاْ إِنَّا وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا عَلَىٰٓ أُمَّةٖ وَإِنَّا عَلَىٰٓ ءَاثَٰرِهِم مُّهۡتَدُونَ
Koma akunena: “Ndithu ife tidawapeza makolo athu pa chipembedzo chimenechi, ndipo ife tikutsatira mapazi awo.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكَذَٰلِكَ مَآ أَرۡسَلۡنَا مِن قَبۡلِكَ فِي قَرۡيَةٖ مِّن نَّذِيرٍ إِلَّا قَالَ مُتۡرَفُوهَآ إِنَّا وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا عَلَىٰٓ أُمَّةٖ وَإِنَّا عَلَىٰٓ ءَاثَٰرِهِم مُّقۡتَدُونَ
Ndipo momwemo, sitidatumize mchenjezi patsogolo ku mudzi uliwonse koma olemera ammenemo adanena: “Ndithu tidawapeza makolo athu pa chipembedzochi (akuchita mmene tikuchitiramu), ndipo ife titsatira mmapazi awo.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
۞ قَٰلَ أَوَلَوۡ جِئۡتُكُم بِأَهۡدَىٰ مِمَّا وَجَدتُّمۡ عَلَيۡهِ ءَابَآءَكُمۡۖ قَالُوٓاْ إِنَّا بِمَآ أُرۡسِلۡتُم بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Adanena (mneneri wawo): “Ngakhale ndakubweretserani chipembedzo chabwino kuposa chomwe mudawapeza nacho makolo anu (mupitirizabe kutsatira chipembedzo cha makolo anucho)?” Adanena: “Ife tikuzikana zimene mwatumidwa nazozi.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَٱنتَقَمۡنَا مِنۡهُمۡۖ فَٱنظُرۡ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُكَذِّبِينَ
Choncho tidawalanga iwo. Taona m’mene adalili mapeto a otsutsa aja.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِيمُ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦٓ إِنَّنِي بَرَآءٞ مِّمَّا تَعۡبُدُونَ
Ndipo (kumbuka) pamene Ibrahim adauza bambo wake ndi anthu ake (kuti): “Ndithu ine ndadzipatula ku zimene mukuzipembedzazi.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِلَّا ٱلَّذِي فَطَرَنِي فَإِنَّهُۥ سَيَهۡدِينِ
“Kupatula Amene adandilenga; ndithu Iye andiongola.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلَهَا كَلِمَةَۢ بَاقِيَةٗ فِي عَقِبِهِۦ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo adalichita liwu ili kukhala losatha ku mtundu wake, kuti abwelere (ku malankhulidwe amenewa).
আরবি তাফসীরসমূহ:
بَلۡ مَتَّعۡتُ هَٰٓؤُلَآءِ وَءَابَآءَهُمۡ حَتَّىٰ جَآءَهُمُ ٱلۡحَقُّ وَرَسُولٞ مُّبِينٞ
Koma ndidawasangalatsa awa (Aquraish) pamodzi ndi makolo awo kufikira choonadi chawadzera ndi Mtumiki wolongosola (za choonadichi).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَمَّا جَآءَهُمُ ٱلۡحَقُّ قَالُواْ هَٰذَا سِحۡرٞ وَإِنَّا بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Ndipo pamene choonadi (Qur’an) chidawadzera, adanena: “Awa ndi matsenga; ndithu ife tikuwakana.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَقَالُواْ لَوۡلَا نُزِّلَ هَٰذَا ٱلۡقُرۡءَانُ عَلَىٰ رَجُلٖ مِّنَ ٱلۡقَرۡيَتَيۡنِ عَظِيمٍ
Ndipo adatinso: “Nchifukwa ninji Qur’an iyi siidavumbulutsidwe pa munthu wamkulu mmidzi iwiriyi (Makka ndi Twaif).”
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَهُمۡ يَقۡسِمُونَ رَحۡمَتَ رَبِّكَۚ نَحۡنُ قَسَمۡنَا بَيۡنَهُم مَّعِيشَتَهُمۡ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۚ وَرَفَعۡنَا بَعۡضَهُمۡ فَوۡقَ بَعۡضٖ دَرَجَٰتٖ لِّيَتَّخِذَ بَعۡضُهُم بَعۡضٗا سُخۡرِيّٗاۗ وَرَحۡمَتُ رَبِّكَ خَيۡرٞ مِّمَّا يَجۡمَعُونَ
(Choncho Allah akunena): “Kodi iwo ndi amene akugawa mtendere wa Mbuye wako (kumpatsa amene wamfuna ndi kummana amene sakumfuna? Chikhalirecho) Ife ndi Amene timagawa pakati pawo zofunika pa moyo wawo mu moyo wadziko lapansi; ndipo tawatukula ena mwa iwo pa ulemelero pamwamba pa ena, choncho ena mwa iwo akuwachita anzawo kukhala antchito awo koma mtendere wa Mbuye wako ndi wabwino kuposa zimene akusonkhanitsa.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَوۡلَآ أَن يَكُونَ ٱلنَّاسُ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ لَّجَعَلۡنَا لِمَن يَكۡفُرُ بِٱلرَّحۡمَٰنِ لِبُيُوتِهِمۡ سُقُفٗا مِّن فِضَّةٖ وَمَعَارِجَ عَلَيۡهَا يَظۡهَرُونَ
Ndipo pakadapanda kuopera kuti anthu adzakhala gulu limodzi (lokanira Allah), ndithu tikadazichita nyumba za amene akumkana (Allah) Wachifundo chambiri kukhala ndi madenga a Siliva, ndi makwelero amene amakwelera (kukhalanso a Siliva).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلِبُيُوتِهِمۡ أَبۡوَٰبٗا وَسُرُرًا عَلَيۡهَا يَتَّكِـُٔونَ
Ndipo nyumba zawo kukhala ndi zitseko ndi makama (mabedi) omwe amayadzamira (zonsezo kukhala za Siliva).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَزُخۡرُفٗاۚ وَإِن كُلُّ ذَٰلِكَ لَمَّا مَتَٰعُ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۚ وَٱلۡأٓخِرَةُ عِندَ رَبِّكَ لِلۡمُتَّقِينَ
Ndiponso ndi zokongoletsa za golide. Koma zonsezo sikanthu ayi, ndi chisangalalo chabe cha dziko lapansi (chosakhalira kutha); ndipo tsiku lachimaliziro lomwe lili kwa Mbuye wako ndi la oopa Allah (potsatira malamulo Ake ndi kusiya zoletsedwa).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَن يَعۡشُ عَن ذِكۡرِ ٱلرَّحۡمَٰنِ نُقَيِّضۡ لَهُۥ شَيۡطَٰنٗا فَهُوَ لَهُۥ قَرِينٞ
Ndipo amene akunyozera kukumbukira (Allah) Wachifundo chambiri, timpatsa satana, kuti iye akhale bwenzi lake (lotsagana nalo).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِنَّهُمۡ لَيَصُدُّونَهُمۡ عَنِ ٱلسَّبِيلِ وَيَحۡسَبُونَ أَنَّهُم مُّهۡتَدُونَ
Ndipo iwo amawatsekereza ku njira zabwino ndi kumaganiza kuti iwo ngoongoka.
আরবি তাফসীরসমূহ:
حَتَّىٰٓ إِذَا جَآءَنَا قَالَ يَٰلَيۡتَ بَيۡنِي وَبَيۡنَكَ بُعۡدَ ٱلۡمَشۡرِقَيۡنِ فَبِئۡسَ ٱلۡقَرِينُ
Kufikira pamene adzatidzera (tsiku la Qiyâma, uku akulowetsedwa ku Moto). Adzati (kumuuza satana): “Kalanga ine! Pakati pa ine ndi iwe pakadakhala ntunda wa pakati pa kuvuma ndi kuzambwe (kutalikirana kwathu).” Ha! Taonani kuipa kwa bwenzi!
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَن يَنفَعَكُمُ ٱلۡيَوۡمَ إِذ ظَّلَمۡتُمۡ أَنَّكُمۡ فِي ٱلۡعَذَابِ مُشۡتَرِكُونَ
(Allah adzawauza kuti): “Ndipo lero sikukuthandizani kukhala limodzi kwanu m’chilango pakuti mudadzichitira nokha zoipa.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَفَأَنتَ تُسۡمِعُ ٱلصُّمَّ أَوۡ تَهۡدِي ٱلۡعُمۡيَ وَمَن كَانَ فِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Kodi ungathe kuwamveretsa agonthi, kapena ungathe kuwaongola akhungu ndi amene ali mkusokera koonekera?
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَإِمَّا نَذۡهَبَنَّ بِكَ فَإِنَّا مِنۡهُم مُّنتَقِمُونَ
Ngati titakuchotsa (padziko usadaone chilango chawo, usakhale ndi chikaiko), ndithu Ife tiwalanga iwo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَوۡ نُرِيَنَّكَ ٱلَّذِي وَعَدۡنَٰهُمۡ فَإِنَّا عَلَيۡهِم مُّقۡتَدِرُونَ
Kapena tikusonyeza zimene tidawalonjeza (uona ndi maso ako usadafe). Ndithu Ife tili ndi mphamvu pa iwo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَٱسۡتَمۡسِكۡ بِٱلَّذِيٓ أُوحِيَ إِلَيۡكَۖ إِنَّكَ عَلَىٰ صِرَٰطٖ مُّسۡتَقِيمٖ
Choncho, gwiritsa zimene zavumbulutsidwa kwa iwe, ndithu iwe uli pa njira yolunjika.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِنَّهُۥ لَذِكۡرٞ لَّكَ وَلِقَوۡمِكَۖ وَسَوۡفَ تُسۡـَٔلُونَ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi ulemelero wako ndi anthu ako; ndipo posachedwa mufunsidwa (za ulemelero umenewu).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَسۡـَٔلۡ مَنۡ أَرۡسَلۡنَا مِن قَبۡلِكَ مِن رُّسُلِنَآ أَجَعَلۡنَا مِن دُونِ ٱلرَّحۡمَٰنِ ءَالِهَةٗ يُعۡبَدُونَ
Ndipo afunse atumiki Athu amene tidawatumiza iwe usadadze: “Kodi tidapanga milungu ina kuti ipembedzedwe, osati (Allah) Wachifundo chambiri?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا مُوسَىٰ بِـَٔايَٰتِنَآ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ وَمَلَإِيْهِۦ فَقَالَ إِنِّي رَسُولُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndithu tidamtumiza Mûsa pamodzi ndi zozizwitsa Zathu kwa Farawo ndi nduna zake; ndipo adati: “Ndithu ine ndine Mtumiki wa Mbuye wa zolengedwa.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَلَمَّا جَآءَهُم بِـَٔايَٰتِنَآ إِذَا هُم مِّنۡهَا يَضۡحَكُونَ
Koma pamene adawadzera ndi zisonyezo zathu, basi iwo adali kuziseka.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَا نُرِيهِم مِّنۡ ءَايَةٍ إِلَّا هِيَ أَكۡبَرُ مِنۡ أُخۡتِهَاۖ وَأَخَذۡنَٰهُم بِٱلۡعَذَابِ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo chisonyezo chilichonse chomwe tidawasonyeza chidali chachikulu kuposa chinzake (komabe sadakhulupirire). Ndipo tidawalanga ndi chilango kuti abwelere (kwa Ife).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَقَالُواْ يَٰٓأَيُّهَ ٱلسَّاحِرُ ٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ بِمَا عَهِدَ عِندَكَ إِنَّنَا لَمُهۡتَدُونَ
Ndipo adati (kwa Mûsa): “E iwe wamatsenga! Tipemphere kwa Mbuye wako pa chomwe adakulonjeza; ndithu ife tiongoka, (tikhulupirira).”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَلَمَّا كَشَفۡنَا عَنۡهُمُ ٱلۡعَذَابَ إِذَا هُمۡ يَنكُثُونَ
Choncho, pamene tidawachotsera chilangocho, basi iwo adayamba kuswa pangano.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَنَادَىٰ فِرۡعَوۡنُ فِي قَوۡمِهِۦ قَالَ يَٰقَوۡمِ أَلَيۡسَ لِي مُلۡكُ مِصۡرَ وَهَٰذِهِ ٱلۡأَنۡهَٰرُ تَجۡرِي مِن تَحۡتِيٓۚ أَفَلَا تُبۡصِرُونَ
Ndipo Farawo adaitana anthu ake, adati: “E inu anthu anga! Kodi ulamuliro wa mu Iguputo siwanga pamodzi ndi mitsinje iyi imene ikuyenda pansi panga (pa nyumba zanga?) Kodi simukuona?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَمۡ أَنَا۠ خَيۡرٞ مِّنۡ هَٰذَا ٱلَّذِي هُوَ مَهِينٞ وَلَا يَكَادُ يُبِينُ
“Kodi kapena ine sindine woposa uyu (Mûsa) wonyozeka, ndipo sangathe kuyankhula momveka?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَلَوۡلَآ أُلۡقِيَ عَلَيۡهِ أَسۡوِرَةٞ مِّن ذَهَبٍ أَوۡ جَآءَ مَعَهُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ مُقۡتَرِنِينَ
“Nanga bwanji sadavekedwe zibangiri zagolide kapena angelo kudza pamodzi ndi iye uku akumtsatira?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَٱسۡتَخَفَّ قَوۡمَهُۥ فَأَطَاعُوهُۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَوۡمٗا فَٰسِقِينَ
Adawapeputsa anthu ake. Ndipo adamvera; iwo adali anthu otuluka mchilamulo (cha Allah).
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَلَمَّآ ءَاسَفُونَا ٱنتَقَمۡنَا مِنۡهُمۡ فَأَغۡرَقۡنَٰهُمۡ أَجۡمَعِينَ
Pamene adatikwiitsa, tidawalanga ndipo tidawamiza onse mmadzi.
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَجَعَلۡنَٰهُمۡ سَلَفٗا وَمَثَلٗا لِّلۡأٓخِرِينَ
Tidawachita (Farawo ndi anthu ake) kukhala chitsanzo cha okanira a pambuyo pawo ndikukhala mbiri kwa anthu amene akudza.
আরবি তাফসীরসমূহ:
۞ وَلَمَّا ضُرِبَ ٱبۡنُ مَرۡيَمَ مَثَلًا إِذَا قَوۡمُكَ مِنۡهُ يَصِدُّونَ
Ndipo pamene lidaperekedwa fanizo la mwana wa Mariya, pamenepo anthu anu adali kufuula (monyoza).[344]
[344] Fanizo lomwe likunenedwa apa ndi lomufanizira Isa (Yesu) ndi zomwe zikupembedzedwa kusiya Allah. Akafiri adamfanizira iye pambuyo povumbulutsidwa Ayah yakuti: “Ndithu inu ndi zomwe mukuzipembedza kusiya Allah ndi nkhuni za ku Jahannam.” Choncho adati Isa (Yesu) nayenso akalowa ku Moto chifukwa chakuti Akhrisitu amamupembedza kusiya Allah. Koma Allah adamyeretsa ponena kuti: “Ndithu awo amene ubwino wochokera kwa Ife watsogola kwa iwo, iwowo akatalikitsidwa ndi motowo” Choncho Isa (Yesu) sakalowa ku Moto chifukwa iye sadalamule anthu kuti amupembedze komanso sakudziwa kuti pali aliyense amene akupembedza iye.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَقَالُوٓاْ ءَأَٰلِهَتُنَا خَيۡرٌ أَمۡ هُوَۚ مَا ضَرَبُوهُ لَكَ إِلَّا جَدَلَۢاۚ بَلۡ هُمۡ قَوۡمٌ خَصِمُونَ
Ndipo adati: “Kodi milungu yathu ndi yabwino, kapena iye?” Sadamfanizire kwa iwe koma kufuna kutsutsana basi (kopanda kufuna choona). Koma iwo ndi anthu amtsutso.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنۡ هُوَ إِلَّا عَبۡدٌ أَنۡعَمۡنَا عَلَيۡهِ وَجَعَلۡنَٰهُ مَثَلٗا لِّبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Iye sadali kanthu koma ndi kapolo amene tidampatsa mtendere; ndipo tidamchita kukhala chitsanzo (chodabwitsa) cha ana a Israyeli.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَوۡ نَشَآءُ لَجَعَلۡنَا مِنكُم مَّلَٰٓئِكَةٗ فِي ٱلۡأَرۡضِ يَخۡلُفُونَ
Ndipo tikadafuna tikadawachita angelo kukhala pa dziko mmalo mwa inu ndi kumasiirana iwo kwa iwo (kuti mudziwe kuti angelo akugonjera malamulo a Allah. Iwo siAllah).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَإِنَّهُۥ لَعِلۡمٞ لِّلسَّاعَةِ فَلَا تَمۡتَرُنَّ بِهَا وَٱتَّبِعُونِۚ هَٰذَا صِرَٰطٞ مُّسۡتَقِيمٞ
Ndipo iye (Isa (Yesu) adzakhala chizindikiro cha Qiyâma (kuti yayandikira). Choncho musaikaikire, koma nditsatireni. Imeneyi ndi njira yolunjika.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَا يَصُدَّنَّكُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُۖ إِنَّهُۥ لَكُمۡ عَدُوّٞ مُّبِينٞ
Asakutsekerezeni satana; iye kwa inu ndi mdani woonekera.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَمَّا جَآءَ عِيسَىٰ بِٱلۡبَيِّنَٰتِ قَالَ قَدۡ جِئۡتُكُم بِٱلۡحِكۡمَةِ وَلِأُبَيِّنَ لَكُم بَعۡضَ ٱلَّذِي تَخۡتَلِفُونَ فِيهِۖ فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
Ndipo pamene Isa (Yesu) adadza ndi zisonyezo zoonekera poyera, adati: “Ndakudzerani ndi nzeru (yopindulitsa), ndikuti ndikulongosolereni zina zimene mudali kusiyana mu izo; choncho, muopeni Allah ndiponso ndimvereni.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّ ٱللَّهَ هُوَ رَبِّي وَرَبُّكُمۡ فَٱعۡبُدُوهُۚ هَٰذَا صِرَٰطٞ مُّسۡتَقِيمٞ
“Ndithu Allah ndiye Mbuye wanga ndi Mbuye wanunso; choncho mupembedzeni; imeneyi ndiyo njira yolunjika.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَٱخۡتَلَفَ ٱلۡأَحۡزَابُ مِنۢ بَيۡنِهِمۡۖ فَوَيۡلٞ لِّلَّذِينَ ظَلَمُواْ مِنۡ عَذَابِ يَوۡمٍ أَلِيمٍ
Koma magulu adasemphana pakati pawo. Ndipo kuonongeka kuchokera mu chilango cha tsiku lowawa kudzakhala pa amene adzichitira okha zoipa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّا ٱلسَّاعَةَ أَن تَأۡتِيَهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Palibe chimene akuyembekeza, koma Qiyâma basi yomwe iwadzera mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira (ali otanganidwa ndi za m’dziko).
আরবি তাফসীরসমূহ:
ٱلۡأَخِلَّآءُ يَوۡمَئِذِۭ بَعۡضُهُمۡ لِبَعۡضٍ عَدُوٌّ إِلَّا ٱلۡمُتَّقِينَ
Abwenzi tsiku limenelo adzakhala odana, wina ndi mnzake, (chifukwa chakuti adali kuthandizana pa zinthu zosalungama ndi zamachimo) kupatula oopa Allah (amene adachita chibwenzi mwa Allah, pothandizana kukwaniritsa malamulo a Allah ndi kusiya zimene Allah waletsa).
আরবি তাফসীরসমূহ:
يَٰعِبَادِ لَا خَوۡفٌ عَلَيۡكُمُ ٱلۡيَوۡمَ وَلَآ أَنتُمۡ تَحۡزَنُونَ
(Allah adzati): E inu akapolo Anga (abwino)! Palibe kuopa kwa inu lerolino ndiponso simudandaula.
আরবি তাফসীরসমূহ:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ بِـَٔايَٰتِنَا وَكَانُواْ مُسۡلِمِينَ
Amene adakhulupirira zisonyezo Zathu ndipo adali Asilamu (ogonjera Allah).
আরবি তাফসীরসমূহ:
ٱدۡخُلُواْ ٱلۡجَنَّةَ أَنتُمۡ وَأَزۡوَٰجُكُمۡ تُحۡبَرُونَ
Lowani ku Munda wamtendere, inu ndi akazi anu musangalatsidwa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
يُطَافُ عَلَيۡهِم بِصِحَافٖ مِّن ذَهَبٖ وَأَكۡوَابٖۖ وَفِيهَا مَا تَشۡتَهِيهِ ٱلۡأَنفُسُ وَتَلَذُّ ٱلۡأَعۡيُنُۖ وَأَنتُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Adzakhala akupititsidwa mbale zagolide ndi matambula (agolide); zonse zokomera moyo zidzakhala mmenemo ndi zokomera maso, ndipo inu mudzakhala mmenemo nthawi yaitali.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَتِلۡكَ ٱلۡجَنَّةُ ٱلَّتِيٓ أُورِثۡتُمُوهَا بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Ndipo umeneo ndi munda umene mwapatsidwa chifukwa cha (zabwino) zimene munkachita.
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَكُمۡ فِيهَا فَٰكِهَةٞ كَثِيرَةٞ مِّنۡهَا تَأۡكُلُونَ
Inu mupeza mmenemo zipatso zambiri zomwe muzidya.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّ ٱلۡمُجۡرِمِينَ فِي عَذَابِ جَهَنَّمَ خَٰلِدُونَ
Ndithu ochimwa (okanira) adzakhala m’chilango cha Jahannam nthawi yaitali.
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَا يُفَتَّرُ عَنۡهُمۡ وَهُمۡ فِيهِ مُبۡلِسُونَ
Sadzapatsidwa nthawi yopumula, ndipo mmenemo iwo akataya mtima (zakupeza moyo wabwino).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَمَا ظَلَمۡنَٰهُمۡ وَلَٰكِن كَانُواْ هُمُ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo sitidawapondereze koma adali kudzipondereza okha.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَنَادَوۡاْ يَٰمَٰلِكُ لِيَقۡضِ عَلَيۡنَا رَبُّكَۖ قَالَ إِنَّكُم مَّٰكِثُونَ
Ndipo (okanira) adzaitana E iwe Malik! (yemwe ndi mngelo woyang’anira moto): ‘‘Mbuye wako atipatse imfa (kuti tipumule kuchilangochi!)” Adzanena (Malik): “Ndithu inu mukhala momwemo!”
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَقَدۡ جِئۡنَٰكُم بِٱلۡحَقِّ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَكُمۡ لِلۡحَقِّ كَٰرِهُونَ
Ndithu tidakubweretserani choona; koma ambiri a inu mudali kuchida choona.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَمۡ أَبۡرَمُوٓاْ أَمۡرٗا فَإِنَّا مُبۡرِمُونَ
Kodi akonza bwino chikonzero (chawocho chomwe ndi chiwembu chofuna kumupha Mtumiki {s.a.w})? Ndithu nafenso ndife okonza chikonzero chabwino (cholepheretsa chiwembu chawocho).
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَمۡ يَحۡسَبُونَ أَنَّا لَا نَسۡمَعُ سِرَّهُمۡ وَنَجۡوَىٰهُمۚ بَلَىٰ وَرُسُلُنَا لَدَيۡهِمۡ يَكۡتُبُونَ
Kodi akuganiza kuti sitikumva zobisa zawo ndi zonong’oneza zawo? Iyayi, (tikuzimva zonse), ndipo atumiki Athu (angelo) ali nawo pamodzi; akulemba.
আরবি তাফসীরসমূহ:
قُلۡ إِن كَانَ لِلرَّحۡمَٰنِ وَلَدٞ فَأَنَا۠ أَوَّلُ ٱلۡعَٰبِدِينَ
Nena (kwa omphatikiza Allah ndi mafano): “Zikadakhala kuti (Allah) Wachifundo chambiri ali ndi mwana, ndiye kuti ine ndikadakhala woyamba kumpembedza (mwanayo).”
আরবি তাফসীরসমূহ:
سُبۡحَٰنَ رَبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ رَبِّ ٱلۡعَرۡشِ عَمَّا يَصِفُونَ
Mbuye wa kumwamba ndi pansi, Mbuye wa Arsh (Mpando wachifumu), Wapatukana ndi mbiri zimene akum’nenerazo (zoti Allah ali ndi mwana).
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَذَرۡهُمۡ يَخُوضُواْ وَيَلۡعَبُواْ حَتَّىٰ يُلَٰقُواْ يَوۡمَهُمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Asiye azingonena zachabezo ndi kusewera kufikira adzakumana ndi tsiku lawo limene akulonjezedwa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَهُوَ ٱلَّذِي فِي ٱلسَّمَآءِ إِلَٰهٞ وَفِي ٱلۡأَرۡضِ إِلَٰهٞۚ وَهُوَ ٱلۡحَكِيمُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo Iye ndiamene akupembedzedwa kumwamba, ndiponso ndi Iye Amene akupembedzedwa pansi. Iye ndi Wanzeru zakuya, Wodziwa kwambiri.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَتَبَارَكَ ٱلَّذِي لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا وَعِندَهُۥ عِلۡمُ ٱلسَّاعَةِ وَإِلَيۡهِ تُرۡجَعُونَ
Ndipo watukuka kwambiri Yemwe ufumu wa kumwamba ndi pansi ndi pakati pa zimenezi ndi Wake. Ndiponso kwa Iye ndiko kuli kudziwa kudza kwa tsiku la Qiyâma; ndipo kwa Iye Yekha ndi kumene m’dzabwezedwa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَا يَمۡلِكُ ٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ مِن دُونِهِ ٱلشَّفَٰعَةَ إِلَّا مَن شَهِدَ بِٱلۡحَقِّ وَهُمۡ يَعۡلَمُونَ
Ndipo omwe akuwapembedzawo kusiya Iye (Allah), sangathe kupulumutsa (aliyense) kupatula amene akuikira umboni choonachi, pomwe iwo akuchidziwa bwino.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَئِن سَأَلۡتَهُم مَّنۡ خَلَقَهُمۡ لَيَقُولُنَّ ٱللَّهُۖ فَأَنَّىٰ يُؤۡفَكُونَ
Ndipo ngati utawafunsa: “Ndani adawalenga?” Anena motsimikiza kuti: “Ndi Allah.” Nanga akutembenuzidwa bwanji (kusiya choona)?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَقِيلِهِۦ يَٰرَبِّ إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ قَوۡمٞ لَّا يُؤۡمِنُونَ
Ndipo zonena zake (Mneneri Muhammad{s.a.w} nthawi zonse): “E Mbuye Wanga! Ndithu awa ndi anthu osakhulupirira (nditani nao)?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَٱصۡفَحۡ عَنۡهُمۡ وَقُلۡ سَلَٰمٞۚ فَسَوۡفَ يَعۡلَمُونَ
Choncho, akhululukire, ndipo auze mawu a mtendere. Posachedwa adzadziwa!
আরবি তাফসীরসমূহ:
 
অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আয-যুখরুফ
সূরাসমূহের সূচী পৃষ্ঠার নাম্বার
 
কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ - অনুবাদসমূহের সূচী

চেওয়া ভাষা আল-কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ-খালিদ ইবরাহীম বীতালা, সংস্করণ ২০২০ খ্রি.

বন্ধ