কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ * - অনুবাদসমূহের সূচী


অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আদ-দুহা   আয়াত:

সূরা আদ-দুহা

وَٱلضُّحَىٰ
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا سَجَىٰ
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
আরবি তাফসীরসমূহ:
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
[452] M’masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo Mtumiki (s.a.w) osamutsikira chivumbulutso. Iye poona izi adali kukaika ndi kudandaula kwakukulu, nao okanira a pa Makka adali kumchita chipongwe. Adali kumunena kuti: “Kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?’’ Basi apa Allah akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha okanira aja kuti: “Sadamusiye ndipo sadakwiye naye.”
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لَّكَ مِنَ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَلَسَوۡفَ يُعۡطِيكَ رَبُّكَ فَتَرۡضَىٰٓ
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
[453] Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Allah, ndi zapadziko mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Allah adamchitira mnyengo yochepa modabwitsa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَلَمۡ يَجِدۡكَ يَتِيمٗا فَـَٔاوَىٰ
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَوَجَدَكَ ضَآلّٗا فَهَدَىٰ
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
[454] Mneneri Muhammad (s.a.w) asanapatsidwe uneneri wake ndi Allah anali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira yachiongoko.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَوَجَدَكَ عَآئِلٗا فَأَغۡنَىٰ
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَأَمَّا ٱلۡيَتِيمَ فَلَا تَقۡهَرۡ
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنۡهَرۡ
Ndiponso wopempha usamukalipire.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَأَمَّا بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثۡ
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).
আরবি তাফসীরসমূহ:
 
অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আদ-দুহা
সূরাসমূহের সূচী পৃষ্ঠার নাম্বার
 
কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ - অনুবাদসমূহের সূচী

চেওয়া ভাষা আল-কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ-খালিদ ইবরাহীম বীতালা, সংস্করণ ২০২০ খ্রি.

বন্ধ