Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: Sura el-Bekara   Ajet:

Sura el-Bekara

الٓمٓ
Alif-Lâm-Mîm.[1]
[1] Sura iyi yayamba ndi malembo a Alifabeti, monga Alif, Laam, Miim. kusonyeza kuti Qur’an yalembedwa ndi malembo amenewa omwe anthu amawagwiritsa ntchito m’zoyankhula ndi m’zolembalemba zawo. Uku ndikuwauza osakhulupilira kuti abweretse buku lawo lolembedwa ndi malembo omwe akuwadziwawo pamene iwo amanena kuti Qur’an adangoipeka yekha Muhammadi (s.a.w) siidavumbulutsidwe ndi Allah. Choncho Allah adawachalenja kuti alembe buku lawo lofanana ndi Qur’an, koma adalephera. Choncho, kulephera kwawo ndi umboni wosonyeza kuti Qur’an ndi buku lovumbulutsidwa ndi Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ذَٰلِكَ ٱلۡكِتَٰبُ لَا رَيۡبَۛ فِيهِۛ هُدٗى لِّلۡمُتَّقِينَ
Ili ndi Buku lopanda chipeneko mkati mwake, ndichiongoko cha (anthu) oopa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡغَيۡبِ وَيُقِيمُونَ ٱلصَّلَوٰةَ وَمِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ يُنفِقُونَ
Omwe amakhulupirira zosaoneka ndi maso (monga Munda wamtendere, Moto, Angelo ndi zina zotere zomwe Allah ndi Mtumiki (s.a.w) adazifotokoza, amapemphera Swala moyenera, ndiponso amapereka m’zimene tawapatsa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ وَمَآ أُنزِلَ مِن قَبۡلِكَ وَبِٱلۡأٓخِرَةِ هُمۡ يُوقِنُونَ
Ndi amene akukhulupirira zomwe zidavumbulutsidwa kwa iwe, ndi zomwe zidavumbulutsidwa kale iwe usadadze, nakhulupiriranso motsimikiza kuti lilipo tsiku lachimaliziro.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ عَلَىٰ هُدٗى مِّن رَّبِّهِمۡۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Iwowo (omwe ali ndi chikhalidwe chotere), ali pachiongoko chochokera kwa Mbuye wawo (Allah), ndipo iwowo ndi omwe ali opambana (pokapeza ulemelero wapamwamba ku Minda ya mtendere).
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ سَوَآءٌ عَلَيۡهِمۡ ءَأَنذَرۡتَهُمۡ أَمۡ لَمۡ تُنذِرۡهُمۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Ndithu amene sadakhulupirire, nchimodzimodzi kwa iwo uwachenjeze kapena usawachenjeze sangakhulupirire.
Tefsiri na arapskom jeziku:
خَتَمَ ٱللَّهُ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ وَعَلَىٰ سَمۡعِهِمۡۖ وَعَلَىٰٓ أَبۡصَٰرِهِمۡ غِشَٰوَةٞۖ وَلَهُمۡ عَذَابٌ عَظِيمٞ
(Ali ngati kuti) Allah wawadinda chidindo chotseka mitima yawo ndi makutu awo (kotero kuti kuunika kwa chikhulupiliro sikungalowemo), ndipo m’maso mwawo muli chophimba (sangathe kuona zozizwitsa za Allah); choncho iwo adzalandira chilango chachikulu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يَقُولُ ءَامَنَّا بِٱللَّهِ وَبِٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَمَا هُم بِمُؤۡمِنِينَ
Pakati pa anthu alipo (anthu achinyengo) amene akunena: “Takhulupirira mwa Allah ndi tsiku lachimaliziro,” pomwe iwo sali okhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يُخَٰدِعُونَ ٱللَّهَ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَمَا يَخۡدَعُونَ إِلَّآ أَنفُسَهُمۡ وَمَا يَشۡعُرُونَ
Akufuna kunyenga Allah ndi amene akhulupirira, ndipo sanyenga aliyense koma okha, ndipo iwo sazindikira (kuti akudzinyenga okha).
Tefsiri na arapskom jeziku:
فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ فَزَادَهُمُ ٱللَّهُ مَرَضٗاۖ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمُۢ بِمَا كَانُواْ يَكۡذِبُونَ
M’mitima mwawo muli matenda; ndipo Allah wawaonjezera matenda. Choncho iwo adzalandira chilango chopweteka chifukwa cha bodza lawo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ لَا تُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ قَالُوٓاْ إِنَّمَا نَحۡنُ مُصۡلِحُونَ
Ndipo akauzidwa kuti: “Musaononge padziko,” amayankha kuti: “Ife ndife okonza.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَآ إِنَّهُمۡ هُمُ ٱلۡمُفۡسِدُونَ وَلَٰكِن لَّا يَشۡعُرُونَ
Dziwani kuti, ndithudi, iwo ndiwo ali oononga (pa dziko); koma sakuzindikira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ ءَامِنُواْ كَمَآ ءَامَنَ ٱلنَّاسُ قَالُوٓاْ أَنُؤۡمِنُ كَمَآ ءَامَنَ ٱلسُّفَهَآءُۗ أَلَآ إِنَّهُمۡ هُمُ ٱلسُّفَهَآءُ وَلَٰكِن لَّا يَعۡلَمُونَ
Ndipo akauzidwa kuti, “Khulupirirani monga momwe anthu ena akhulupirira,” amayankha kuti: “Kodi tikhulupirire monga momwe zakhulupirira zitsiru?” Dziwani kuti, ndithudi, iwo ndi omwe ali zitsiru, koma sakudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا لَقُواْ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ قَالُوٓاْ ءَامَنَّا وَإِذَا خَلَوۡاْ إِلَىٰ شَيَٰطِينِهِمۡ قَالُوٓاْ إِنَّا مَعَكُمۡ إِنَّمَا نَحۡنُ مُسۡتَهۡزِءُونَ
Ndipo akakumana ndi amene akhulupirira, amanena: “Takhulupirira.” Koma akakhala pa okha ndi asatana awo, amati: “Ndithudi ife tili pamodzi nanu. Timangowachita chipongwe basi.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱللَّهُ يَسۡتَهۡزِئُ بِهِمۡ وَيَمُدُّهُمۡ فِي طُغۡيَٰنِهِمۡ يَعۡمَهُونَ
Allah adzawalipira chipongwe chawocho, ndipo akuwalekelera akungoyumbayumba (kugwira njakata) m’kusokera kwawo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ ٱشۡتَرَوُاْ ٱلضَّلَٰلَةَ بِٱلۡهُدَىٰ فَمَا رَبِحَت تِّجَٰرَتُهُمۡ وَمَا كَانُواْ مُهۡتَدِينَ
Oterewo ndiomwe asinthanitsa chiongoko ndi kusokera, koma malonda awo sadawapindulire chilichonse, tero sadali oongoka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
مَثَلُهُمۡ كَمَثَلِ ٱلَّذِي ٱسۡتَوۡقَدَ نَارٗا فَلَمَّآ أَضَآءَتۡ مَا حَوۡلَهُۥ ذَهَبَ ٱللَّهُ بِنُورِهِمۡ وَتَرَكَهُمۡ فِي ظُلُمَٰتٖ لَّا يُبۡصِرُونَ
Fanizo lawo lili ngati (munthu wa paulendo wafungatiridwa ndi mdima) yemwe wayatsa moto; ndipo pamene udaunika zomwe zidali m’mphepete mwake, Allah nkuwachotsera kuunika kwawoko nawasiya mu mdima osatha kuona.
Tefsiri na arapskom jeziku:
صُمُّۢ بُكۡمٌ عُمۡيٞ فَهُمۡ لَا يَرۡجِعُونَ
(Nakhala ngati) agonthi, abubu, akhungu; ndipo sangabwelerenso (ku chiwongoko).
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَوۡ كَصَيِّبٖ مِّنَ ٱلسَّمَآءِ فِيهِ ظُلُمَٰتٞ وَرَعۡدٞ وَبَرۡقٞ يَجۡعَلُونَ أَصَٰبِعَهُمۡ فِيٓ ءَاذَانِهِم مِّنَ ٱلصَّوَٰعِقِ حَذَرَ ٱلۡمَوۡتِۚ وَٱللَّهُ مُحِيطُۢ بِٱلۡكَٰفِرِينَ
Kapena (fanizo lawonso) lili ngati chimvula chochokera ku mitambo m’kati mwake muukhala mdima, mphenzi ndi kung’anima, naika zala zawo m’makutu mwawo chifukwa chamkokomo ndikuopa imfa (pomwe kutero sikungawathandize chilichonse). Ndipo Allah akudziwa bwinobwino za osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَكَادُ ٱلۡبَرۡقُ يَخۡطَفُ أَبۡصَٰرَهُمۡۖ كُلَّمَآ أَضَآءَ لَهُم مَّشَوۡاْ فِيهِ وَإِذَآ أَظۡلَمَ عَلَيۡهِمۡ قَامُواْۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ لَذَهَبَ بِسَمۡعِهِمۡ وَأَبۡصَٰرِهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Kung’anima kukuyandikira kutsomphola maso awo; nthawi iliyonse kukawaunikira, nkuyenda m’menemo (mkuunikamo). Koma kukawachitira mdima, nkuyima. ndipo Allah akadafuna akadawachotsera kumva kwawo ndi kuona kwawo. Ndithudi, Allah Ngokhoza chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ ٱعۡبُدُواْ رَبَّكُمُ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ وَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ لَعَلَّكُمۡ تَتَّقُونَ
E inu anthu! pembedzani Mbuye wanu Yemwe adakulengani inu ndi omwe adalipo kale, kuti mukhale oopa (Allah).
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِي جَعَلَ لَكُمُ ٱلۡأَرۡضَ فِرَٰشٗا وَٱلسَّمَآءَ بِنَآءٗ وَأَنزَلَ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَخۡرَجَ بِهِۦ مِنَ ٱلثَّمَرَٰتِ رِزۡقٗا لَّكُمۡۖ فَلَا تَجۡعَلُواْ لِلَّهِ أَندَادٗا وَأَنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
(Allah) Yemwe adakupangirani nthaka kukhala ngati mphasa, ndi thambo kukhala ngati denga; ndipo adatsitsa madzi kuchokera ku mitambo natulutsa ndi madziwo zipatso zosiyanasiyana kuti zikhale chakudya chanu. Choncho Allah musampangire anzake uku inu mukudziwa (kuti alibe wothandizana naye).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِن كُنتُمۡ فِي رَيۡبٖ مِّمَّا نَزَّلۡنَا عَلَىٰ عَبۡدِنَا فَأۡتُواْ بِسُورَةٖ مِّن مِّثۡلِهِۦ وَٱدۡعُواْ شُهَدَآءَكُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Ndipo ngati muli m’chikaiko ndi zomwe tamvumbulutsira kapolo wathu (kuti sizinachokere kwa Ife,) tabweretsani sura imodzi yolingana ndi Quraniyi (m’kayankhulidwe ka nzeru ndi kayalidwe ka malamulo ake). Ndipo itanani athandizi anu (kuti akuthandizeni) osakhala Allah; ngati inu mukunena zoona (kuti Qur’an njopekedwa).
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِن لَّمۡ تَفۡعَلُواْ وَلَن تَفۡعَلُواْ فَٱتَّقُواْ ٱلنَّارَ ٱلَّتِي وَقُودُهَا ٱلنَّاسُ وَٱلۡحِجَارَةُۖ أُعِدَّتۡ لِلۡكَٰفِرِينَ
Choncho ngati simutha (kubweretsa sura imodzi yonga ya m’Qurani) ndiye kuti simudzatha. Choncho opani Moto omwe nkhuni zake ndi anthu ndi miyala umene wakonzedwera kwa osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَبَشِّرِ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ أَنَّ لَهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُۖ كُلَّمَا رُزِقُواْ مِنۡهَا مِن ثَمَرَةٖ رِّزۡقٗا قَالُواْ هَٰذَا ٱلَّذِي رُزِقۡنَا مِن قَبۡلُۖ وَأُتُواْ بِهِۦ مُتَشَٰبِهٗاۖ وَلَهُمۡ فِيهَآ أَزۡوَٰجٞ مُّطَهَّرَةٞۖ وَهُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Ndipo auze nkhani yabwino amene akhulupirira nachita ntchito zabwino (molungama) kuti ndithu adzalandira minda ya mtendere momwe mitsinje ikuyenda pansi pake (ndi patsogolo pake). Nthawi iliyonse kumeneko akapatsidwa zipatso ngati chakudya, adzakhala akunena: “Izi ndizomwe tidapatsidwa kale,” (chifukwa chakuti) adzapatsidwa zipatso zofanana (m’maonekedwe ake ndi zimene adapatsidwapo kale. Koma makomedwe ake ngosiyana). Ndiponso akalandira m’menemo akazi oyeretsedwa (kuuve wamtundu uliwonse); ndipo iwo adzakhala m’menemo nthawi yaitali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَسۡتَحۡيِۦٓ أَن يَضۡرِبَ مَثَلٗا مَّا بَعُوضَةٗ فَمَا فَوۡقَهَاۚ فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ فَيَعۡلَمُونَ أَنَّهُ ٱلۡحَقُّ مِن رَّبِّهِمۡۖ وَأَمَّا ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فَيَقُولُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۘ يُضِلُّ بِهِۦ كَثِيرٗا وَيَهۡدِي بِهِۦ كَثِيرٗاۚ وَمَا يُضِلُّ بِهِۦٓ إِلَّا ٱلۡفَٰسِقِينَ
Ndithu Allah sachita manyazi kupereka fanizo la udzudzu ndi choposerapo (pa udzudzuwo). Koma amene akhulupirira akuzindikira kuti (fanizolo) ndiloona ndi lochokera kwa Mbuye wawo. Koma amene sadakhulupirire, akunena: “Kodi Allah akufunanji pa fanizo lotereli?” (Allah) amawalekelera ambiri kusokera ndi fanizo lotere, komanso amawaongola ambiri ndi fanizonso lotere. Komatu sawalekelera kusokera nalo kupatula okhawo opandukira chilamulo (Chake).
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يَنقُضُونَ عَهۡدَ ٱللَّهِ مِنۢ بَعۡدِ مِيثَٰقِهِۦ وَيَقۡطَعُونَ مَآ أَمَرَ ٱللَّهُ بِهِۦٓ أَن يُوصَلَ وَيُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِۚ أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
Omwe akuswa chipangano cha Allah pambuyo pochimanga (kuti adzachikwaniritsa; ndi kutsatira malamulo a Allah), ndiponso amadula (chibale) chomwe Allah adalamula kuti chilumikizidwe, naononga pa dziko (poyambitsa nkhondo ndi ziwawa); iwo ndiamene ali otayika.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كَيۡفَ تَكۡفُرُونَ بِٱللَّهِ وَكُنتُمۡ أَمۡوَٰتٗا فَأَحۡيَٰكُمۡۖ ثُمَّ يُمِيتُكُمۡ ثُمَّ يُحۡيِيكُمۡ ثُمَّ إِلَيۡهِ تُرۡجَعُونَ
Kodi mungamkane chotani Allah chikhalirecho inu mudali akufa ndipo adakupatsani moyo (nakuikani pa dziko lapansi)? Kenako adzakupatsani imfa (ikakwana nthawi yanu yofera). Kenako adzakuukitsani (ndikukutulutsani m’manda). Ndipo kenako mudzabwezedwa kwa Iye (kuti mukaweruzidwe pa zomwe mudali kuchita).
Tefsiri na arapskom jeziku:
هُوَ ٱلَّذِي خَلَقَ لَكُم مَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا ثُمَّ ٱسۡتَوَىٰٓ إِلَى ٱلسَّمَآءِ فَسَوَّىٰهُنَّ سَبۡعَ سَمَٰوَٰتٖۚ وَهُوَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٞ
Iye ndi Yemwe adakulengerani zonse za m’dziko lapansi, kenako adalunjika ku thambo nakonza thambo zisanu ndi ziwiri. Iye Ngodziwa chinthu chilichonse.[2]
[2] Adalunjika ku thambo molingana ndi mmene Allah yo alili osati mofanana ndi zolengedwa Zake.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَالَ رَبُّكَ لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ إِنِّي جَاعِلٞ فِي ٱلۡأَرۡضِ خَلِيفَةٗۖ قَالُوٓاْ أَتَجۡعَلُ فِيهَا مَن يُفۡسِدُ فِيهَا وَيَسۡفِكُ ٱلدِّمَآءَ وَنَحۡنُ نُسَبِّحُ بِحَمۡدِكَ وَنُقَدِّسُ لَكَۖ قَالَ إِنِّيٓ أَعۡلَمُ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Akumbutse (anthu ako nkhani iyi) panthawi yomwe Mbuye wako anati kwa Angelo: “Ine ndikufuna kuika m’dziko lapansi wondiimilira.” (Angelo) adati: “Kodi muika m’menemo amene azidzaonongamo ndi kukhetsa mwazi, pomwe ife tikukulemekezani ndi kukutamandani mokuyeretsani?” (Allah) adati: “Ndithudi, Ine ndikudziwa zimene simukuzidziwa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَعَلَّمَ ءَادَمَ ٱلۡأَسۡمَآءَ كُلَّهَا ثُمَّ عَرَضَهُمۡ عَلَى ٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ فَقَالَ أَنۢبِـُٔونِي بِأَسۡمَآءِ هَٰٓؤُلَآءِ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Ndipo (Allah) adaphunzitsa Adam mayina a (zinthu) zonse; nazibweretsa (zinthuzo) pamaso pa Angelo, naati (kwa Angelo): “Ndiuzeni mayina a zinthu izi ngati mukunena zoona (kuti inu ndinu ozindikira zinthu).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالُواْ سُبۡحَٰنَكَ لَا عِلۡمَ لَنَآ إِلَّا مَا عَلَّمۡتَنَآۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
(Angelo) adati: “Kuyeretsedwa Nkwanu! Ife tilibe kuzindikira kupatula chimene mwatiphunzitsa. Ndithudi, Inu Ngodziwa kwambiri, Anzeru zakuya.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَ يَٰٓـَٔادَمُ أَنۢبِئۡهُم بِأَسۡمَآئِهِمۡۖ فَلَمَّآ أَنۢبَأَهُم بِأَسۡمَآئِهِمۡ قَالَ أَلَمۡ أَقُل لَّكُمۡ إِنِّيٓ أَعۡلَمُ غَيۡبَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَأَعۡلَمُ مَا تُبۡدُونَ وَمَا كُنتُمۡ تَكۡتُمُونَ
(Allah) adanena: “E iwe Adam!: Auze mayina ake (azinthuzo).” Ndipo pamene adawauza mayina ake, (Iye) adati: “Kodi Sindinakuuzeni kuti Ine ndikudziwa zobisika zakumwamba ndi pansi, ndiponso ndikudziwa zimene mukuonetsera poyera ndi zimene mukubisa?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قُلۡنَا لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ ٱسۡجُدُواْ لِأٓدَمَ فَسَجَدُوٓاْ إِلَّآ إِبۡلِيسَ أَبَىٰ وَٱسۡتَكۡبَرَ وَكَانَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo (akumbutse anthu ako nkhani iyi) parnene tidawauza Angelo: “Mgwadireni Adam.” Onse adamugwadira kupatula Iblisi (Satana); anakana nadzitukumula. Tero adali m’modzi mwa osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقُلۡنَا يَٰٓـَٔادَمُ ٱسۡكُنۡ أَنتَ وَزَوۡجُكَ ٱلۡجَنَّةَ وَكُلَا مِنۡهَا رَغَدًا حَيۡثُ شِئۡتُمَا وَلَا تَقۡرَبَا هَٰذِهِ ٱلشَّجَرَةَ فَتَكُونَا مِنَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo tidati: “E iwe Adam! Khala iwe ndi mkazi wako m’mundamo (mu Edeni); idyani m’menemo motakasuka paliponse pamene mwafuna; koma musauyandikire Mtengo uwu kuopera kuti mungakhale mwa odzichitira okha zoipa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَأَزَلَّهُمَا ٱلشَّيۡطَٰنُ عَنۡهَا فَأَخۡرَجَهُمَا مِمَّا كَانَا فِيهِۖ وَقُلۡنَا ٱهۡبِطُواْ بَعۡضُكُمۡ لِبَعۡضٍ عَدُوّٞۖ وَلَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُسۡتَقَرّٞ وَمَتَٰعٌ إِلَىٰ حِينٖ
Koma Satana (Iblisi yemwe uja) adawalakwitsa onse awiriwo (nanyoza lamulo la Allah ndikudya mtengo woletsedwawo), nawatulutsa (mu Mtendere) momwe adaalimo. Ndipo tidawauza: “Tsikani (mukakhale pa dziko lapansi) pakati panu pali chidani. Tsopano pokhala panu ndi pa dziko lapansi, ndipo mukapeza chisangalalo pamenepo kwakanthawi.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَتَلَقَّىٰٓ ءَادَمُ مِن رَّبِّهِۦ كَلِمَٰتٖ فَتَابَ عَلَيۡهِۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo Adam adalandira mawu kuchokera kwa Mbuye wake, (napempha chikhululuko cha Allah kupyolera m’mawuwo), ndipo (Mbuye wake) adavomera kulapa kwake. Ndithudi, Iyeyo Ngolandira kwambiri kulapa, Wachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡنَا ٱهۡبِطُواْ مِنۡهَا جَمِيعٗاۖ فَإِمَّا يَأۡتِيَنَّكُم مِّنِّي هُدٗى فَمَن تَبِعَ هُدَايَ فَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Tidati: “Tsikani m’menemo nonsenu. Ngati chitakufikani chiongoko chochokera kwa Ine, choncho amene adzatsate chiongoko Changacho, pa iwo sipadzakhala mantha. Ndiponso iwo sadzadandaula.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَآ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
“Koma amene sanakhulupirire natsutsa mawu athu, iwowo ndiwo anthu a ku Moto. M’menemo akakhalamo nthawi yaitali.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَتِيَ ٱلَّتِيٓ أَنۡعَمۡتُ عَلَيۡكُمۡ وَأَوۡفُواْ بِعَهۡدِيٓ أُوفِ بِعَهۡدِكُمۡ وَإِيَّٰيَ فَٱرۡهَبُونِ
E inu ana a Israyeli! kumbukirani chisomo Changa chomwe ndidakudalitsani nacho, ndipo kwaniritsani pangano Langa Nanenso ndikwaniritsi pangano lanu. Ndipo Ine Ndekha ndiopeni.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَءَامِنُواْ بِمَآ أَنزَلۡتُ مُصَدِّقٗا لِّمَا مَعَكُمۡ وَلَا تَكُونُوٓاْ أَوَّلَ كَافِرِۭ بِهِۦۖ وَلَا تَشۡتَرُواْ بِـَٔايَٰتِي ثَمَنٗا قَلِيلٗا وَإِيَّٰيَ فَٱتَّقُونِ
Ndipo khulupirirani zimene ndavumbulutsa, zomwe zikuchitira umboni zimene muli nazo, ndipo musakhale oyamba kuzikana; ndipo musagulitse mawu Anga ndi (zinthu za) mtengo wochepa. Ndipo Ine Ndekha ndiopeni.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَلۡبِسُواْ ٱلۡحَقَّ بِٱلۡبَٰطِلِ وَتَكۡتُمُواْ ٱلۡحَقَّ وَأَنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
Ndipo musasakanize choona ndi chonama; ndi kubisa choona uku mukudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَ وَٱرۡكَعُواْ مَعَ ٱلرَّٰكِعِينَ
Ndipo pempherani Swala moyenera ndikupereka chopereka (Zakaat), ndipo weramani pamodzi ndi owerama.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ أَتَأۡمُرُونَ ٱلنَّاسَ بِٱلۡبِرِّ وَتَنسَوۡنَ أَنفُسَكُمۡ وَأَنتُمۡ تَتۡلُونَ ٱلۡكِتَٰبَۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Kodi mukulamula anthu kuchita zabwino ndi kudziiwala inu eni pomwe inu mukuwerenga Buku? Kodi simuzindikira?
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱسۡتَعِينُواْ بِٱلصَّبۡرِ وَٱلصَّلَوٰةِۚ وَإِنَّهَا لَكَبِيرَةٌ إِلَّا عَلَى ٱلۡخَٰشِعِينَ
Ndipo dzithandizeni (pa zinthu zanu) popirira ndi popemphera Swala. Ndithudi, Swala yo ndiyolemera kupatula kwa odzichepetsa (kwa Allah).
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يَظُنُّونَ أَنَّهُم مُّلَٰقُواْ رَبِّهِمۡ وَأَنَّهُمۡ إِلَيۡهِ رَٰجِعُونَ
Omwe akutsimikiza kuti adzakumana ndi Mbuye wawo, ndi kuti adzabwerera kwa Iye.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَتِيَ ٱلَّتِيٓ أَنۡعَمۡتُ عَلَيۡكُمۡ وَأَنِّي فَضَّلۡتُكُمۡ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
E inu ana a Israyeli! Kumbukirani chisomo Changa chomwe ndidakudalitsani nacho. Ndithudi, Ine ndinakuchitirani ubwino kuposa zolengedwa zonse (pa nthawiyo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱتَّقُواْ يَوۡمٗا لَّا تَجۡزِي نَفۡسٌ عَن نَّفۡسٖ شَيۡـٔٗا وَلَا يُقۡبَلُ مِنۡهَا شَفَٰعَةٞ وَلَا يُؤۡخَذُ مِنۡهَا عَدۡلٞ وَلَا هُمۡ يُنصَرُونَ
Choncho opani tsiku lomwe munthu aliyense sadzathandiza mnzake ndi chilichonse, ndipo sikudzavomerezedwa kwa iye (munthuyo) dandaulo lililonse, ndiponso silidzalandiridwa dipo kwa iye; ndipo iwo sadzapulumutsidwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ نَجَّيۡنَٰكُم مِّنۡ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ يَسُومُونَكُمۡ سُوٓءَ ٱلۡعَذَابِ يُذَبِّحُونَ أَبۡنَآءَكُمۡ وَيَسۡتَحۡيُونَ نِسَآءَكُمۡۚ وَفِي ذَٰلِكُم بَلَآءٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَظِيمٞ
Ndipo (kumbukirani) pamene tidakupulumutsani kwa anthu a Farawo, omwe amakuzunzani ndi chilango choipa; adali kuzinga (kupha) ana anu achimuna ndikuwasiya moyo achikazi. Ndipo m’zimenezo mudali mayeso aakulu ochokera kwa Mbuye wanu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ فَرَقۡنَا بِكُمُ ٱلۡبَحۡرَ فَأَنجَيۡنَٰكُمۡ وَأَغۡرَقۡنَآ ءَالَ فِرۡعَوۡنَ وَأَنتُمۡ تَنظُرُونَ
Ndipo (kumbukiraninso) pamene tidailekanitsa nyanja chifukwa cha inu (kuti muoloke pa mchenga wouma), potero tidakupulumutsani ndi kuwamiza anthu a Farawo (pamodzi ndi iye mwini) uku inu mukuona; (chomwe chidali chizizwa choonekera).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ وَٰعَدۡنَا مُوسَىٰٓ أَرۡبَعِينَ لَيۡلَةٗ ثُمَّ ٱتَّخَذۡتُمُ ٱلۡعِجۡلَ مِنۢ بَعۡدِهِۦ وَأَنتُمۡ ظَٰلِمُونَ
(Kumbukiraninso) pamene tidamulonjeza Mûsa masiku makumi anayi (kuti tidzampatsa buku la Taurat patapita masiku makumi anayi pambuyo pa kupulumuka kwanu ndi kuonongeka kwa Farawo); kenako inu mudapembedza thole (mwana wa ng’ombe) pambuyo pake, (iye kulibe, atapita ku chipangano cha Mbuye wake). Ndipo inu muli ochita zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ عَفَوۡنَا عَنكُم مِّنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ لَعَلَّكُمۡ تَشۡكُرُونَ
Kenako tidakukhululukirani pambuyo pa zimenezo, kuti muthokoze (mtendere wa Allah).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ ءَاتَيۡنَا مُوسَى ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡفُرۡقَانَ لَعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Ndipo (kumbukiraninso) pamene Mûsa tidampatsa buku lolekanitsa choonadi ndi chonama kuti inu muongoke (polilingalira ndi kutsatira malamulo ake).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَالَ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِۦ يَٰقَوۡمِ إِنَّكُمۡ ظَلَمۡتُمۡ أَنفُسَكُم بِٱتِّخَاذِكُمُ ٱلۡعِجۡلَ فَتُوبُوٓاْ إِلَىٰ بَارِئِكُمۡ فَٱقۡتُلُوٓاْ أَنفُسَكُمۡ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ عِندَ بَارِئِكُمۡ فَتَابَ عَلَيۡكُمۡۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo (kumbukiraninso) pamene Mûsa adanena kwa anthu ake kuti “E inu anthu anga! Ndithudi, inu mwadzichitira nokha zoipa pompembedza thole (mwana wa ng’ombe). Choncho lapani kwa Mlengi wanu, ndipo iphanani nokha (amene ali abwino aphe oipa). Kutero ndi bwino kwa inu pamaso pa Mlengi wanu.” Choncho (Allah) wavomera kulapa kwanu. Ndithudi, Iye Ngovomera kulapa mochuluka, Wachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قُلۡتُمۡ يَٰمُوسَىٰ لَن نُّؤۡمِنَ لَكَ حَتَّىٰ نَرَى ٱللَّهَ جَهۡرَةٗ فَأَخَذَتۡكُمُ ٱلصَّٰعِقَةُ وَأَنتُمۡ تَنظُرُونَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene Mudati: “E iwe Mûsa!; Sitingakukhulupirire iwe mpaka timuone Allah masomphenya.” Ndipo nkokomo wa moto udakugwirani uku inu mukuona.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ بَعَثۡنَٰكُم مِّنۢ بَعۡدِ مَوۡتِكُمۡ لَعَلَّكُمۡ تَشۡكُرُونَ
Kenako tidakuukitsani ku imfa pambuyo pakufa kwanu, kuti muyamike.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَظَلَّلۡنَا عَلَيۡكُمُ ٱلۡغَمَامَ وَأَنزَلۡنَا عَلَيۡكُمُ ٱلۡمَنَّ وَٱلسَّلۡوَىٰۖ كُلُواْ مِن طَيِّبَٰتِ مَا رَزَقۡنَٰكُمۡۚ وَمَا ظَلَمُونَا وَلَٰكِن كَانُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ يَظۡلِمُونَ
Ndipo tidakuphimbani ndi mthunzi wa mitambo (pamene mudali kuoloka chipululu cha mchenga), ndipo tidakutsitsirani Mana (zakumwa zotsekemera ngati uchi) ndi Salwa (zinziri), ndi kukuuzani: “Idyani zinthu zabwino izi zimene takupatsani.” Komatu sadatichitire Ife choipa koma adali kudzichitira okha zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قُلۡنَا ٱدۡخُلُواْ هَٰذِهِ ٱلۡقَرۡيَةَ فَكُلُواْ مِنۡهَا حَيۡثُ شِئۡتُمۡ رَغَدٗا وَٱدۡخُلُواْ ٱلۡبَابَ سُجَّدٗا وَقُولُواْ حِطَّةٞ نَّغۡفِرۡ لَكُمۡ خَطَٰيَٰكُمۡۚ وَسَنَزِيدُ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene tidati: “Lowani m’mudzi uwu, ndikudya m’menemo motakasuka paliponse pamene mwafuna; ndipo lowerani pachipata chake uku mutawerama (kusonyeza kuthokoza Allah) ndipo nenani: “E Mbuye wathu! Tikhululukireni machimo athu.” “Tikukhululukirani machimo anu ndipo tiwaonjezera (mphoto yaikulu) ochita zabwino.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَبَدَّلَ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ قَوۡلًا غَيۡرَ ٱلَّذِي قِيلَ لَهُمۡ فَأَنزَلۡنَا عَلَى ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ رِجۡزٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ بِمَا كَانُواْ يَفۡسُقُونَ
Koma anthu oipa adasintha (lamulo la Allah, nanena) mawu ena osati amene adawuzidwa. Tero, anthu oipawo tidawatsitsira mliri wochokera kumwamba, chifukwa chakutuluka kwawo m’chilamulo cha Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَإِذِ ٱسۡتَسۡقَىٰ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِۦ فَقُلۡنَا ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡحَجَرَۖ فَٱنفَجَرَتۡ مِنۡهُ ٱثۡنَتَا عَشۡرَةَ عَيۡنٗاۖ قَدۡ عَلِمَ كُلُّ أُنَاسٖ مَّشۡرَبَهُمۡۖ كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ مِن رِّزۡقِ ٱللَّهِ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene Mûsa adapemphera anthu ake madzi kwa Allah (atagwidwa ndi ludzu loopsa m’chipululu), tidati: “Menya mwala ndi ndodo yakoyo.” (Atamenya), anatulukadi m’menemo akasupe khumi ndi awiri. Potero fuko lililonse lidadziwa malo awo omwera. (Izi zidachitika kuti asakangane). Choncho idyani, ndiponso imwani mu zopatsa za Allah (popanda inu kuzivutikira), ndipo musasimbwe pa dziko uku mukuononga.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قُلۡتُمۡ يَٰمُوسَىٰ لَن نَّصۡبِرَ عَلَىٰ طَعَامٖ وَٰحِدٖ فَٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ يُخۡرِجۡ لَنَا مِمَّا تُنۢبِتُ ٱلۡأَرۡضُ مِنۢ بَقۡلِهَا وَقِثَّآئِهَا وَفُومِهَا وَعَدَسِهَا وَبَصَلِهَاۖ قَالَ أَتَسۡتَبۡدِلُونَ ٱلَّذِي هُوَ أَدۡنَىٰ بِٱلَّذِي هُوَ خَيۡرٌۚ ٱهۡبِطُواْ مِصۡرٗا فَإِنَّ لَكُم مَّا سَأَلۡتُمۡۗ وَضُرِبَتۡ عَلَيۡهِمُ ٱلذِّلَّةُ وَٱلۡمَسۡكَنَةُ وَبَآءُو بِغَضَبٖ مِّنَ ٱللَّهِۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ كَانُواْ يَكۡفُرُونَ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ وَيَقۡتُلُونَ ٱلنَّبِيِّـۧنَ بِغَيۡرِ ٱلۡحَقِّۚ ذَٰلِكَ بِمَا عَصَواْ وَّكَانُواْ يَعۡتَدُونَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene mudati: “E iwe Mûsa! Sitingathe kupirira ndi chakudya chamtundu umodzi (chomwe ndi Mana ndi Salwa); choncho tipemphere kwa Mbuye wako kuti atitulutsire (atipatse) ife zimene nthaka imameretsa, monga masamba, nkhaka, adyo, nyemba za mtundu wa chana ndi anyezi.” Iye adati: “Kodi mukufuna kusinthitsa chonyozeka ndi chabwino? Pitani m’midzi, ndipo kumeneko mukapeza zimene mwapemphazi.” Potero adapatsidwa kunyozeka ndi kusauka; nabwerera ndi mkwiyo wa Allah. Zimenezo n’chifukwa chakuti iwo sadali okhulupirira zisonyezo za Allah, ndikuti adali kupha aneneri a Allah popanda chifukwa. Zidali tero chifukwa cha kunyoza kwawo, ndipo adali olumpha malire.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَٱلَّذِينَ هَادُواْ وَٱلنَّصَٰرَىٰ وَٱلصَّٰبِـِٔينَ مَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَعَمِلَ صَٰلِحٗا فَلَهُمۡ أَجۡرُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Ndithu amene akhulupirira (aneneri akale), ndi Ayuda, ndi Akhirisitu ndi Asabayi[3]; aliyense wa iwo amene akhulupirire Allah (tsopano, monga momwe akunenera Mneneri Muhammad (s.a.w) nakhulupiriranso za tsiku lachimaliziro, uku akuchita ntchito zabwino, akalandira mphoto yawo kwa Mbuye wawo. Pa iwo sipadzakhala mantha, ndiponso sadzadandaula.
[3] Amenewa ndi anthu amene adali kunena mau oti Laa ilaaha illa Allah, adali kuwerenga Zabur koma si Ayuda kapena Akhrisitu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ أَخَذۡنَا مِيثَٰقَكُمۡ وَرَفَعۡنَا فَوۡقَكُمُ ٱلطُّورَ خُذُواْ مَآ ءَاتَيۡنَٰكُم بِقُوَّةٖ وَٱذۡكُرُواْ مَا فِيهِ لَعَلَّكُمۡ تَتَّقُونَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi, inu Ayuda) pamene tidalandira chipangano chanu (kuti mudzagwiritsa ntchito zomwe zili m’buku la Taurat), ndipo tidakweza pamwamba panu phiri (la Sinai; tidati kwa inu): “Gwirani mwamphamvu chimene takupatsani, ndipo kumbukirani zili m’menemo (pozigwiritsa ntchito. Ndiponso musazinyozere) kuti mukhale oopa Allah.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ تَوَلَّيۡتُم مِّنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَۖ فَلَوۡلَا فَضۡلُ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ وَرَحۡمَتُهُۥ لَكُنتُم مِّنَ ٱلۡخَٰسِرِينَ
Koma pambuyo pazimenezo mudatembenuka ndikunyoza. Pakadapanda ubwino wa Allah ndi chifundo chake pa inu, mukadakhala mwa otayika (oonongeka pa dziko lapansi).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَقَدۡ عَلِمۡتُمُ ٱلَّذِينَ ٱعۡتَدَوۡاْ مِنكُمۡ فِي ٱلسَّبۡتِ فَقُلۡنَا لَهُمۡ كُونُواْ قِرَدَةً خَٰسِـِٔينَ
Ndithudi mudawadziwa (anthu) amene adapyola malire mwa inu pakuswa kupatulika kwa tsiku la Sabata (m’mene tidawalangira chifukwa chosodza nsomba pa tsiku loletsedwa). Ndipo tidati kwa iwo: “Khalani anyani onyozeka.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَجَعَلۡنَٰهَا نَكَٰلٗا لِّمَا بَيۡنَ يَدَيۡهَا وَمَا خَلۡفَهَا وَمَوۡعِظَةٗ لِّلۡمُتَّقِينَ
Ndipo tidakuchita kukhala anyaniko, chilango chochenjeza amene adalipo pa nthawiyo ndi akudza pambuyo pawo, ndiponso phunziro kwa oopa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَالَ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِۦٓ إِنَّ ٱللَّهَ يَأۡمُرُكُمۡ أَن تَذۡبَحُواْ بَقَرَةٗۖ قَالُوٓاْ أَتَتَّخِذُنَا هُزُوٗاۖ قَالَ أَعُوذُ بِٱللَّهِ أَنۡ أَكُونَ مِنَ ٱلۡجَٰهِلِينَ
(Kumbukiraninso nkhani iyi, inu Ayuda) pamene Mûsa adauza anthu ake: “Ndithudi, Allah akukulamulani kuti muzinge ng’ombe.” Iwo adati: “Kodi ukutichitira zachipongwe?” Iye adati: “(Sichoncho), ndikudzitchinjiriza ndi Allah kukhala mwa anthu aumbuli.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالُواْ ٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ يُبَيِّن لَّنَا مَا هِيَۚ قَالَ إِنَّهُۥ يَقُولُ إِنَّهَا بَقَرَةٞ لَّا فَارِضٞ وَلَا بِكۡرٌ عَوَانُۢ بَيۡنَ ذَٰلِكَۖ فَٱفۡعَلُواْ مَا تُؤۡمَرُونَ
Iwo adati: “Tipemphere kwa Mbuye wako kuti atifotokozere bwino za ng’ombeyo.” Iye adati: “Ndithudi Iye akunena kuti ng’ombeyo simkota kapena mthanthi, koma yapakatikati pa zimenezi. Tero chitani zimene mukulamulidwa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالُواْ ٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ يُبَيِّن لَّنَا مَا لَوۡنُهَاۚ قَالَ إِنَّهُۥ يَقُولُ إِنَّهَا بَقَرَةٞ صَفۡرَآءُ فَاقِعٞ لَّوۡنُهَا تَسُرُّ ٱلنَّٰظِرِينَ
Iwo adatinso: “Tipemphere kwa Mbuye wako kuti atilongosolere maonekedwe ake.” (Mûsa) adati: “Iye akuti ng’ombeyo ikhale yachikasu kwambiri, yowakondweretsa oiwona.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالُواْ ٱدۡعُ لَنَا رَبَّكَ يُبَيِّن لَّنَا مَا هِيَ إِنَّ ٱلۡبَقَرَ تَشَٰبَهَ عَلَيۡنَا وَإِنَّآ إِن شَآءَ ٱللَّهُ لَمُهۡتَدُونَ
Iwo adatinso: “Tipemphere kwa Mbuye wako kuti atilongosolere mmene kakhalidwe kake kalili. Ndithudi, ng’ombe zimene wafotokozazo n’zofanana kwa ife. Ndipo ndithudi, Allah akafuna tikhala oongoka.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَ إِنَّهُۥ يَقُولُ إِنَّهَا بَقَرَةٞ لَّا ذَلُولٞ تُثِيرُ ٱلۡأَرۡضَ وَلَا تَسۡقِي ٱلۡحَرۡثَ مُسَلَّمَةٞ لَّا شِيَةَ فِيهَاۚ قَالُواْ ٱلۡـَٰٔنَ جِئۡتَ بِٱلۡحَقِّۚ فَذَبَحُوهَا وَمَا كَادُواْ يَفۡعَلُونَ
Adati: “Ndithudi Iye akuti, imeneyo ndi n’gombe yosaigwiritsa ntchito yolima m’nthaka, ndiponso yosathilira mbewu; yabwinobwino yopanda banga.” Iwo adati: “Tsopano wabweretsa (mawu a) choonadi.” Choncho adaizinga, koma padatsala pang’ono kuti asachite (lamulolo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَتَلۡتُمۡ نَفۡسٗا فَٱدَّٰرَٰءۡتُمۡ فِيهَاۖ وَٱللَّهُ مُخۡرِجٞ مَّا كُنتُمۡ تَكۡتُمُونَ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene mudapha munthu, kenako mudakangana ndi kukankhirana za munthuyo, (ena ankati uje ndiye wapha, pomwe ena ankati koma uje ndiye wapha). Ndipo Allah atulutsira poyera zimene mudali kubisa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَقُلۡنَا ٱضۡرِبُوهُ بِبَعۡضِهَاۚ كَذَٰلِكَ يُحۡيِ ٱللَّهُ ٱلۡمَوۡتَىٰ وَيُرِيكُمۡ ءَايَٰتِهِۦ لَعَلَّكُمۡ تَعۡقِلُونَ
Choncho tidati: “Mmenyeni (wakufayo) ndi gawo la nyamayo. (Potero auka ndikunena za amene adamupha).” Momwemo Allah adzawaukitsa akufa (m’manda monga adamuukitsira wakufayo pamaso panu), ndipo akukusonyezani zizindikiro Zake kuti mukhale ndi nzeru.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ قَسَتۡ قُلُوبُكُم مِّنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ فَهِيَ كَٱلۡحِجَارَةِ أَوۡ أَشَدُّ قَسۡوَةٗۚ وَإِنَّ مِنَ ٱلۡحِجَارَةِ لَمَا يَتَفَجَّرُ مِنۡهُ ٱلۡأَنۡهَٰرُۚ وَإِنَّ مِنۡهَا لَمَا يَشَّقَّقُ فَيَخۡرُجُ مِنۡهُ ٱلۡمَآءُۚ وَإِنَّ مِنۡهَا لَمَا يَهۡبِطُ مِنۡ خَشۡيَةِ ٱللَّهِۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Koma mitima yanu idauma pa mbuyo pa zimenezo; (nkukhala gwa!) ngati mwala kapena kuposerapo. Ndithudi pali miyala ina yomwe ikutuluka mkati mwake mitsinje; ndipo pali ina imene imang’ambika nkutuluka madzi mkati mwake; ndipo pali ina imene imagudubuzika chifukwa cha kuopa Allah. (Koma inu Ayuda simulalikika ngakhale mpang’ono pomwe). Ndipo Allah sali wonyalanyaza zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ أَفَتَطۡمَعُونَ أَن يُؤۡمِنُواْ لَكُمۡ وَقَدۡ كَانَ فَرِيقٞ مِّنۡهُمۡ يَسۡمَعُونَ كَلَٰمَ ٱللَّهِ ثُمَّ يُحَرِّفُونَهُۥ مِنۢ بَعۡدِ مَا عَقَلُوهُ وَهُمۡ يَعۡلَمُونَ
۞ Kodi (inu Asilamu) mukuyembekezera kuti angakukhulupirireni (Ayudawo) pomwe ena a iwo ankamvera mawu a Allah, kenako nkuwasintha pambuyo powazindikira bwinobwino, uku akudziwa?
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا لَقُواْ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ قَالُوٓاْ ءَامَنَّا وَإِذَا خَلَا بَعۡضُهُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٖ قَالُوٓاْ أَتُحَدِّثُونَهُم بِمَا فَتَحَ ٱللَّهُ عَلَيۡكُمۡ لِيُحَآجُّوكُم بِهِۦ عِندَ رَبِّكُمۡۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Ndipo akakumana ndi amene akhulupirira, amanena: Takhulupirira (kuti uyu, Muhammad (s.a.w) ndi mneneri woona, ndipo watchulidwa m’mabuku athu).” Koma akakhala kwaokha kuseli, amati: “Mukuwauza iwo (Asilamu) zimene Allah anakufotokozerani (m’buku la Taurat) kuti adzakhale ndi mtsutso pa inu kwa Mbuye wanu? Kodi mulibe nzeru?
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَوَلَا يَعۡلَمُونَ أَنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُ مَا يُسِرُّونَ وَمَا يُعۡلِنُونَ
“Kodi sadziwa kuti Allah akudziwa zomwe akubisa ndi zomwe akuonetsera poyera? (Kwa Allah palibe chobisika).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنۡهُمۡ أُمِّيُّونَ لَا يَعۡلَمُونَ ٱلۡكِتَٰبَ إِلَّآ أَمَانِيَّ وَإِنۡ هُمۡ إِلَّا يَظُنُّونَ
Ndipo mwa iwo (Ayudawo) zilipo mbuli zosadziwa kuwerenga buku (la Allah), koma ziyembekezero zabodza basi, ndipo iwo alibe china koma kungoganizira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَوَيۡلٞ لِّلَّذِينَ يَكۡتُبُونَ ٱلۡكِتَٰبَ بِأَيۡدِيهِمۡ ثُمَّ يَقُولُونَ هَٰذَا مِنۡ عِندِ ٱللَّهِ لِيَشۡتَرُواْ بِهِۦ ثَمَنٗا قَلِيلٗاۖ فَوَيۡلٞ لَّهُم مِّمَّا كَتَبَتۡ أَيۡدِيهِمۡ وَوَيۡلٞ لَّهُم مِّمَّا يَكۡسِبُونَ
Chilango cha ukali chili pa amene akulemba buku ndi manja awo, kenako nanena: “Ili lachokera kwa Allah,” (akunena bodzalo) kuti apeze zinthu za mtengo wochepa (za m’dziko lapansi); choncho kuonongeka kuli pa iwo chifukwa cha zomwe manja awo alemba, ndiponso kuonongeka n’kwawo chifukwa cha zomwe akupeza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالُواْ لَن تَمَسَّنَا ٱلنَّارُ إِلَّآ أَيَّامٗا مَّعۡدُودَةٗۚ قُلۡ أَتَّخَذۡتُمۡ عِندَ ٱللَّهِ عَهۡدٗا فَلَن يُخۡلِفَ ٱللَّهُ عَهۡدَهُۥٓۖ أَمۡ تَقُولُونَ عَلَى ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Ndipo akunena: “Sudzatikhudza Moto kupatula masiku owerengeka basi.”Auze: “Kodi mudapangana naye Allah, kuti potero sadzaswa lonjezo Lake, kapena mukungomunenera Allah zimene simukuzidziwa?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
بَلَىٰۚ مَن كَسَبَ سَيِّئَةٗ وَأَحَٰطَتۡ بِهِۦ خَطِيٓـَٔتُهُۥ فَأُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Sichoncho! Koma amene wachita choipa, nam’zungulira machimo akeo, otero ndi anthu a ku Moto. M’menemo adzakhala nthawi yaitali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَنَّةِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Ndipo amene akhulupirira nachita zabwino, iwowo ndiwo anthu a ku Munda wamtendere. M’menemo adzakhala nthawi yaitali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ أَخَذۡنَا مِيثَٰقَ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ لَا تَعۡبُدُونَ إِلَّا ٱللَّهَ وَبِٱلۡوَٰلِدَيۡنِ إِحۡسَانٗا وَذِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَقُولُواْ لِلنَّاسِ حُسۡنٗا وَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَ ثُمَّ تَوَلَّيۡتُمۡ إِلَّا قَلِيلٗا مِّنكُمۡ وَأَنتُم مُّعۡرِضُونَ
Ndipo (akumbutse nkhani iyinso) pamene tidalandira pangano lamphamvu la ana a Israyeli kuti: Musapembedze aliyense koma Allah; ndipo muwachitire zabwino makolo anu ndi achibale anu, ndi amasiye, ndi masikini (osoŵedwa); ndipo nenani kwa anthu mwaubwino; ndipo pempherani Swala moyenera ndi kupereka Zakaat, kenako mudatembenuka monyozera kupatula ochepa mwa inu, ndipo inu ndinu onyozera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ أَخَذۡنَا مِيثَٰقَكُمۡ لَا تَسۡفِكُونَ دِمَآءَكُمۡ وَلَا تُخۡرِجُونَ أَنفُسَكُم مِّن دِيَٰرِكُمۡ ثُمَّ أَقۡرَرۡتُمۡ وَأَنتُمۡ تَشۡهَدُونَ
Ndipo kumbukirani pamene tidalandira pangano lanu kuti simukhetsa mwazi wanu, ndikutinso simudzatulutsana nokha m’nyumba zanu, ndipo inu munavomereza zimenezi, ndipo inu mukuikira umboni zimenezi (koma simudatsate malamulowo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ أَنتُمۡ هَٰٓؤُلَآءِ تَقۡتُلُونَ أَنفُسَكُمۡ وَتُخۡرِجُونَ فَرِيقٗا مِّنكُم مِّن دِيَٰرِهِمۡ تَظَٰهَرُونَ عَلَيۡهِم بِٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡعُدۡوَٰنِ وَإِن يَأۡتُوكُمۡ أُسَٰرَىٰ تُفَٰدُوهُمۡ وَهُوَ مُحَرَّمٌ عَلَيۡكُمۡ إِخۡرَاجُهُمۡۚ أَفَتُؤۡمِنُونَ بِبَعۡضِ ٱلۡكِتَٰبِ وَتَكۡفُرُونَ بِبَعۡضٖۚ فَمَا جَزَآءُ مَن يَفۡعَلُ ذَٰلِكَ مِنكُمۡ إِلَّا خِزۡيٞ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۖ وَيَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ يُرَدُّونَ إِلَىٰٓ أَشَدِّ ٱلۡعَذَابِۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Tsono inu nomwe ndi amene mukuphana ndikuwatulutsa ena a inu m’nyumba zawo; mukuthandiza adani anu powachitira (abale anu masautso) mwauchimo ndi molumpha malire. Koma akakudzerani akaidi ogwidwa ku nkhondo, mukuwaombola, pomwe nkoletsedwa kwa inu kuwatulutsa. Kodi mukukhulupirira mbali ina ya buku, mbali ina nkuikana? Choncho palibe mphoto kwa ochita izi mwa inu koma kuyaluka pamoyo wa pa dziko lapansi; ndipo tsiku la chiweruziro adzalowetsedwa ku chilango chokhwima kwambiri. Ndipo Allah sali wonyalanyaza zimene mukuchita[4].
[4] Ndime iyi ikukamba za Ayuda omwe amapezeka ku Madina nthawi ya Mtumiki (s.a.w). Iwo munthawi ya umbuli adapalana ubwenzi ndi ma Arabu aku Madina. Ena a iwo anali paubwenzi ndi mtundu wa Khazraj, ndipo ena mwa iwo anali paubwenzi ndi mtundu wa Aws. Choncho ikachitika nkhondo pakati pawo, Ayuda ambali iyi adali kupha Ayuda ambali inayi ndikulanda katundu wawo ndikuwagwira ukapolo, zomwe ndizoletsedwa malingana ndi Tora. Kenako nkhondo ikatha adali kuwamasula akapolo aja, pogwiritsa ntchito lamulo la Tora. Nchifukwa chake Allah akuwafunsa mowadzudzula kuti: “Kodi mukukhulupilira mbali ina ya buku, mbali ina nkuikana?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ ٱشۡتَرَوُاْ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا بِٱلۡأٓخِرَةِۖ فَلَا يُخَفَّفُ عَنۡهُمُ ٱلۡعَذَابُ وَلَا هُمۡ يُنصَرُونَ
Iwowo ndi amene asinthanitsa moyo wa dziko lapansi ndi moyo ulinkudza choncho sadzawachepetsera chilango, ndiponso sadzapulumutsidwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَقَدۡ ءَاتَيۡنَا مُوسَى ٱلۡكِتَٰبَ وَقَفَّيۡنَا مِنۢ بَعۡدِهِۦ بِٱلرُّسُلِۖ وَءَاتَيۡنَا عِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ ٱلۡبَيِّنَٰتِ وَأَيَّدۡنَٰهُ بِرُوحِ ٱلۡقُدُسِۗ أَفَكُلَّمَا جَآءَكُمۡ رَسُولُۢ بِمَا لَا تَهۡوَىٰٓ أَنفُسُكُمُ ٱسۡتَكۡبَرۡتُمۡ فَفَرِيقٗا كَذَّبۡتُمۡ وَفَرِيقٗا تَقۡتُلُونَ
Ndithudi Mûsa tidampatsa buku (la Taurat) ndipo tidatsatiza pambuyo pake atumiki (ena). Ndipo Isa (Yesu) mwana wa Mariya tidampatsa zizizwa zoonekera, ndi kumulimbikitsa ndi Mzimu Woyera (Gabrieli). Nthawi iliyonse akakudzerani mtumiki ndi chomwe mitima yanu siikonda, mumadzikweza. Ena mudawatsutsa ndipo ena mudawapha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالُواْ قُلُوبُنَا غُلۡفُۢۚ بَل لَّعَنَهُمُ ٱللَّهُ بِكُفۡرِهِمۡ فَقَلِيلٗا مَّا يُؤۡمِنُونَ
(Iwo) adati: “Mitima yathu yakutidwa, (potero tikulephera kumvetsa ulaliki wako, iwe Muhammad (s.a.w).’’ Iwo ngabodza pa zimene akunenazi. Koma Allah wawatembelera chifukwa cha kusakhulupirira kwawo). Tero n’zochepa zimene akuzikhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَمَّا جَآءَهُمۡ كِتَٰبٞ مِّنۡ عِندِ ٱللَّهِ مُصَدِّقٞ لِّمَا مَعَهُمۡ وَكَانُواْ مِن قَبۡلُ يَسۡتَفۡتِحُونَ عَلَى ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فَلَمَّا جَآءَهُم مَّا عَرَفُواْ كَفَرُواْ بِهِۦۚ فَلَعۡنَةُ ٱللَّهِ عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo pamene buku lidawadzera (m’nyengo ya mtumiki Muhammad {s.a.w}) lochokera kwa Allah, loikira umboni zomwe zili pamodzi ndi iwo (adalikana), pomwe kale (lisadadze bukulo) adali kupempha chithandizo (kupyolera kwa mtumiki wolonjezedwa) chogonjetsera amene sadakhulupirire. Koma pamene chidawadzera chimene adachidziwa, (Qur’an) adachikana. Choncho matembelero a Allah ali pa osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
بِئۡسَمَا ٱشۡتَرَوۡاْ بِهِۦٓ أَنفُسَهُمۡ أَن يَكۡفُرُواْ بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ بَغۡيًا أَن يُنَزِّلَ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦ عَلَىٰ مَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦۖ فَبَآءُو بِغَضَبٍ عَلَىٰ غَضَبٖۚ وَلِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٞ مُّهِينٞ
N’choipa zedi chimene asinthanitsira (chisangalalo cha tsiku lachimaliziro cha) mitima yawo pa kukana kwao zimene Allah adavumbulutsa, chifukwa cha njiru basi kuti Allah watsitsira chifundo chake amene wamfuna mwa akapolo Ake (amene sali Myuda). Potero adabwerera ndi mkwiyo wa Allah kuonjezera pa mkwiyo wakale. Ndipo osakhulupirira adzakhala ndi chilango chosambula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمۡ ءَامِنُواْ بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ قَالُواْ نُؤۡمِنُ بِمَآ أُنزِلَ عَلَيۡنَا وَيَكۡفُرُونَ بِمَا وَرَآءَهُۥ وَهُوَ ٱلۡحَقُّ مُصَدِّقٗا لِّمَا مَعَهُمۡۗ قُلۡ فَلِمَ تَقۡتُلُونَ أَنۢبِيَآءَ ٱللَّهِ مِن قَبۡلُ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndipo akauzidwa (Ayuda): “Khulupirirani zimene Allah wavumbulutsa (kwa mtumiki Muhammad {s.a.w}).” Amanena: “Tikukhulupirira zimene zidavumbulitsidwa kwa ife,” ndipo amazikana zomwe sizili zimenezo ngakhale izo zili zoona, zomwe zikutsimikizira pa zimene ali nazo pamodzi. Nena: “Nanga bwanji mudapha aneneri a Allah kalelo ngati muli okhulupiriradi?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَلَقَدۡ جَآءَكُم مُّوسَىٰ بِٱلۡبَيِّنَٰتِ ثُمَّ ٱتَّخَذۡتُمُ ٱلۡعِجۡلَ مِنۢ بَعۡدِهِۦ وَأَنتُمۡ ظَٰلِمُونَ
Ndipo adakudzerani Mûsa ndi zisonyezo zoonekera, koma pambuyo pake mudapembedza thole (mwana wa ng’ombe), ndipo potero mudali anthu ochita zoipa kwabasi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ أَخَذۡنَا مِيثَٰقَكُمۡ وَرَفَعۡنَا فَوۡقَكُمُ ٱلطُّورَ خُذُواْ مَآ ءَاتَيۡنَٰكُم بِقُوَّةٖ وَٱسۡمَعُواْۖ قَالُواْ سَمِعۡنَا وَعَصَيۡنَا وَأُشۡرِبُواْ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلۡعِجۡلَ بِكُفۡرِهِمۡۚ قُلۡ بِئۡسَمَا يَأۡمُرُكُم بِهِۦٓ إِيمَٰنُكُمۡ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndipo (kumbukirani nkhani iyi, inu ana a Israyeli) pamene tidalandira kwa inu pangano lamphamvu, ndipo tidakukwezerani phiri pamwamba panu (uku tikuti): “Gwiritsani mwamphamvu (malamulo) amene takupatsani, ndipo mverani.” (Iwo) adati: “Tamva (mawu anu), koma tanyozera.” Ndipo adamwetsedwa m’mitima mwawo kukonda kupembedza thole (mwana wang’ombe) chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Nena: “N’choipa zedi chimene chikhulupiliro chanu chikukulamulirani ngati inu mulidi okhulupirira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡ إِن كَانَتۡ لَكُمُ ٱلدَّارُ ٱلۡأٓخِرَةُ عِندَ ٱللَّهِ خَالِصَةٗ مِّن دُونِ ٱلنَّاسِ فَتَمَنَّوُاْ ٱلۡمَوۡتَ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Auze (Ayudawo): “Ngati nyumba yomaliza kwa Allah njanu nokha, osati anthu ena (monga momwe mukunenera), ilakalakeni imfa ngati mukunenadi zoona.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَن يَتَمَنَّوۡهُ أَبَدَۢا بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيهِمۡۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلظَّٰلِمِينَ
Koma sadzailakalaka (imfa) ngakhale pang’ono, chifukwa cha zomwe manja awo adatsogoza (chifukwa cha machimo omwe adadzichitira). Ndipo Allah akudziwa bwino za anthu oipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَتَجِدَنَّهُمۡ أَحۡرَصَ ٱلنَّاسِ عَلَىٰ حَيَوٰةٖ وَمِنَ ٱلَّذِينَ أَشۡرَكُواْۚ يَوَدُّ أَحَدُهُمۡ لَوۡ يُعَمَّرُ أَلۡفَ سَنَةٖ وَمَا هُوَ بِمُزَحۡزِحِهِۦ مِنَ ٱلۡعَذَابِ أَن يُعَمَّرَۗ وَٱللَّهُ بَصِيرُۢ بِمَا يَعۡمَلُونَ
Ndipo muwapeza (Ayuda) kuti ngokondetsetsa kukhala ndi moyo wautali kuposa anthu ena, kuposanso anthu amene akuphatikiza (Allah ndi mafano). Aliyense wa iwo amafuna atapatsidwa moyo wokwana zaka chikwi chimodzi. Pomwe kupatsidwa kwake moyo wautali sikungamuike kutali ndi chilango. Ndipo Allah akuona zonse zimene akuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡ مَن كَانَ عَدُوّٗا لِّـجِبۡرِيلَ فَإِنَّهُۥ نَزَّلَهُۥ عَلَىٰ قَلۡبِكَ بِإِذۡنِ ٱللَّهِ مُصَدِّقٗا لِّمَا بَيۡنَ يَدَيۡهِ وَهُدٗى وَبُشۡرَىٰ لِلۡمُؤۡمِنِينَ
Nena: “Amene akhale mdani wa Gaburieli (chifukwa chobweretsa chivumbulutso kwa Muhammad {s.a.w}, iyeyo ndi mdani wa Allah). Ndithudi, iye waivumbulutsa Qur’an mumtima mwako mwachilolezo cha Allah. Kudzatsimikidzira zomwe zidali patsogolo pake, ndiponso ndi chiongoko ndi nkhani yabwino kwa okhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
مَن كَانَ عَدُوّٗا لِّلَّهِ وَمَلَٰٓئِكَتِهِۦ وَرُسُلِهِۦ وَجِبۡرِيلَ وَمِيكَىٰلَ فَإِنَّ ٱللَّهَ عَدُوّٞ لِّلۡكَٰفِرِينَ
Amene ali mdani wa Allah, angelo Ake, atumiki Ake, Gaburieli ndi Mikayeli, ndithu Allah ndi mdani wa osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَقَدۡ أَنزَلۡنَآ إِلَيۡكَ ءَايَٰتِۭ بَيِّنَٰتٖۖ وَمَا يَكۡفُرُ بِهَآ إِلَّا ٱلۡفَٰسِقُونَ
Ndithu tavumbulutsa kwa iwe zisonyezo zoonekera. Ndipo palibe wozikana koma okhawo opandukira chilamulo cha Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَوَكُلَّمَا عَٰهَدُواْ عَهۡدٗا نَّبَذَهُۥ فَرِيقٞ مِّنۡهُمۚ بَلۡ أَكۡثَرُهُمۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Kodi sizili tero kuti panthawi iliyonse akupangana pangano lamphamvu, ena aiwo akulitaya? Koma ambiri aiwo sakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَمَّا جَآءَهُمۡ رَسُولٞ مِّنۡ عِندِ ٱللَّهِ مُصَدِّقٞ لِّمَا مَعَهُمۡ نَبَذَ فَرِيقٞ مِّنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ كِتَٰبَ ٱللَّهِ وَرَآءَ ظُهُورِهِمۡ كَأَنَّهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo pamene (Ayuda) adawadzera Mtumiki wochokera kwa Allah uku akutsimikidzira chomwe iwo ali nacho, gulu lina mwa omwe adapatsidwa buku adataya buku la Allah kumbuyo kwa misana yawo ngati kuti sakulidziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱتَّبَعُواْ مَا تَتۡلُواْ ٱلشَّيَٰطِينُ عَلَىٰ مُلۡكِ سُلَيۡمَٰنَۖ وَمَا كَفَرَ سُلَيۡمَٰنُ وَلَٰكِنَّ ٱلشَّيَٰطِينَ كَفَرُواْ يُعَلِّمُونَ ٱلنَّاسَ ٱلسِّحۡرَ وَمَآ أُنزِلَ عَلَى ٱلۡمَلَكَيۡنِ بِبَابِلَ هَٰرُوتَ وَمَٰرُوتَۚ وَمَا يُعَلِّمَانِ مِنۡ أَحَدٍ حَتَّىٰ يَقُولَآ إِنَّمَا نَحۡنُ فِتۡنَةٞ فَلَا تَكۡفُرۡۖ فَيَتَعَلَّمُونَ مِنۡهُمَا مَا يُفَرِّقُونَ بِهِۦ بَيۡنَ ٱلۡمَرۡءِ وَزَوۡجِهِۦۚ وَمَا هُم بِضَآرِّينَ بِهِۦ مِنۡ أَحَدٍ إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِۚ وَيَتَعَلَّمُونَ مَا يَضُرُّهُمۡ وَلَا يَنفَعُهُمۡۚ وَلَقَدۡ عَلِمُواْ لَمَنِ ٱشۡتَرَىٰهُ مَا لَهُۥ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ مِنۡ خَلَٰقٖۚ وَلَبِئۡسَ مَا شَرَوۡاْ بِهِۦٓ أَنفُسَهُمۡۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Ndipo adatsatira njira za afiti zomwe asatana adali kuwafotokozera m’nthawi ya ufumu wa Sulaiman. Ndipo Sulaiman sadamkane Allah (sadali mfiti), koma asatana ndi amene adamkana, naphunzitsa anthu ufiti (umene adaudziwa kuyambira kale); natsatiranso (njira za ufiti) zimene zinatsitsidwa kwa Angelo awiri Haruta ndi Maruta (ku midzi ya) ku Babulo. Koma Angelowo sadaphunzitse aliyense pokhapokha atamuuza kuti: “Ife ndife mayeso (ofuna kuona kugonjera kwanu malamulo a Allah); choncho musamkane (Allah).” Komabe ankaphunzira kwa iwo njira zolekanitsira pakati pa munthu ndi mkazi wake, (ndi zina zotero). Ndipo sadavutitse aliyense ndi zimenezo koma mwachilolezo cha Allah. Ndipo akuphunzira zomwe zingawavutitse pomwe sizingawathandize. Ndithudi, akudziwa kuti yemwe wausankha (ufitiwo) sadzakhala ndi gawo lililonse (la zinthu zabwino) tsiku lachimaliziro. Ndithudi, nchoipitsitsa chimene adzisankhira okha akadakhala akudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَوۡ أَنَّهُمۡ ءَامَنُواْ وَٱتَّقَوۡاْ لَمَثُوبَةٞ مِّنۡ عِندِ ٱللَّهِ خَيۡرٞۚ لَّوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Ndipo iwo akadakhulupirira nadzitchinjiriza (ku zoletsedwa), ndithudi, mphoto yochokera kwa Allah ikadakhala yabwino kwa iwo, akadadziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَقُولُواْ رَٰعِنَا وَقُولُواْ ٱنظُرۡنَا وَٱسۡمَعُواْۗ وَلِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابٌ أَلِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Musam’nenere (Mneneri liwu lakuti) “raina” (ndicholinga chomunenera kuti iye ndi mbutuma), koma mnenereni (liwu lakuti) “utiyang’anire,” ndipo mverani malamulo. Kwa osakhulupirira kuli chilango chopweteka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
مَّا يَوَدُّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ وَلَا ٱلۡمُشۡرِكِينَ أَن يُنَزَّلَ عَلَيۡكُم مِّنۡ خَيۡرٖ مِّن رَّبِّكُمۡۚ وَٱللَّهُ يَخۡتَصُّ بِرَحۡمَتِهِۦ مَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ ذُو ٱلۡفَضۡلِ ٱلۡعَظِيمِ
Amene sadakhulupirire mwa anthu a mabuku (Ayuda ndi Akhirisitu) ndi omphatikiza Allah (Arabu), safuna kuti chabwino chilichonse chochokera kwa Mbuye wanu chitsitsidwe kwa inu (Asilamu). Koma Allah amamsankhira chifundo Chake amene wamfuna. Ndipo Allah ndi Mwini ubwino ochuluka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ مَا نَنسَخۡ مِنۡ ءَايَةٍ أَوۡ نُنسِهَا نَأۡتِ بِخَيۡرٖ مِّنۡهَآ أَوۡ مِثۡلِهَآۗ أَلَمۡ تَعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ
Ayah (ndime) iliyonse yomwe tikuifafaniza kapena kuiiwalitsa (mu mtima wako) tikubweretsa yabwino kuposa iyo, kapena yofanana nayo. Kodi sukudziwa kuti Allah Ngokhoza chinthu chilichonse?
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَمۡ تَعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۗ وَمَا لَكُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ مِن وَلِيّٖ وَلَا نَصِيرٍ
Kodi siudziwa kuti ufumu wakumwamba ndi pansi ngwa Allah? Ndipo inu kupatula Iye Allah mulibe mtetezi ngakhale mthandizi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمۡ تُرِيدُونَ أَن تَسۡـَٔلُواْ رَسُولَكُمۡ كَمَا سُئِلَ مُوسَىٰ مِن قَبۡلُۗ وَمَن يَتَبَدَّلِ ٱلۡكُفۡرَ بِٱلۡإِيمَٰنِ فَقَدۡ ضَلَّ سَوَآءَ ٱلسَّبِيلِ
Kodi mukufuna kumfunsa Mtumiki wanu (inu Asilamu) monga momwe Mûsa adafunsidwira kale (mafunso achipongwe)? Ndipo amene angasinthitse chikhulupiliro ndi kusakhulupirira, ndithudi wasokera njira yolingana (yopanda majiga).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَدَّ كَثِيرٞ مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ لَوۡ يَرُدُّونَكُم مِّنۢ بَعۡدِ إِيمَٰنِكُمۡ كُفَّارًا حَسَدٗا مِّنۡ عِندِ أَنفُسِهِم مِّنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُمُ ٱلۡحَقُّۖ فَٱعۡفُواْ وَٱصۡفَحُواْ حَتَّىٰ يَأۡتِيَ ٱللَّهُ بِأَمۡرِهِۦٓۗ إِنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Ambiri mwa amene anapatsidwa mabuku, akufuna kukubwezani (kukutembenuzani) kuti mukhale osakhulupirira pambuyo pa chikhulupiliro chanu, chifukwa chadumbo lomwe lili m’mitima mwawo (lomwe lawapeza) pambuyo powaonekera choonadi poyera. Choncho akhululukireni ndi kuwasiya kufikira Allah adzabweretse lamulo Lake[5]; ndithudi Allah Ngokhoza chilichonse.
[5] Lamulo lake ndilakuwaloleza Asilamu kubwezera pamene aputidwa kapena kuchitidwa mtopola.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَۚ وَمَا تُقَدِّمُواْ لِأَنفُسِكُم مِّنۡ خَيۡرٖ تَجِدُوهُ عِندَ ٱللَّهِۗ إِنَّ ٱللَّهَ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ
Ndipo pempherani Swala moyenera ndiponso perekani Zakaat. Ndipo chilichonse chabwino chimene mukudzitsogozera mukachipeza kwa Allah. Ndithudi, Allah akuona zonse zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالُواْ لَن يَدۡخُلَ ٱلۡجَنَّةَ إِلَّا مَن كَانَ هُودًا أَوۡ نَصَٰرَىٰۗ تِلۡكَ أَمَانِيُّهُمۡۗ قُلۡ هَاتُواْ بُرۡهَٰنَكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Eti akunena: “Palibe amene adzalowe ku Munda wamtendere koma amene ali Myuda Kapena Mkhirisitu.” Zimenezo nzokhumba zawo chabe. Nena: “Bweretsani umboni wanu ngati mukunena zoona.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
بَلَىٰۚ مَنۡ أَسۡلَمَ وَجۡهَهُۥ لِلَّهِ وَهُوَ مُحۡسِنٞ فَلَهُۥٓ أَجۡرُهُۥ عِندَ رَبِّهِۦ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Ayi, koma amene nkhope yake yagonjera kwa Allah uku akuchita zabwino (kwa anthu anzawo) iye ndi amene adzapeza mphoto yake kwa Mbuye wake. Ndipo pa iwo sipadzakhala mantha, ndiponso iwo sadzadandaula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالَتِ ٱلۡيَهُودُ لَيۡسَتِ ٱلنَّصَٰرَىٰ عَلَىٰ شَيۡءٖ وَقَالَتِ ٱلنَّصَٰرَىٰ لَيۡسَتِ ٱلۡيَهُودُ عَلَىٰ شَيۡءٖ وَهُمۡ يَتۡلُونَ ٱلۡكِتَٰبَۗ كَذَٰلِكَ قَالَ ٱلَّذِينَ لَا يَعۡلَمُونَ مِثۡلَ قَوۡلِهِمۡۚ فَٱللَّهُ يَحۡكُمُ بَيۡنَهُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ فِيمَا كَانُواْ فِيهِ يَخۡتَلِفُونَ
Ndipo Ayuda akumanena: “Akhrisitu alibe chilichonse (chotsamira pa chipembedzo chawo);” naonso Akhrisitu akumanena: “Ayuda alibe chilichonse (chotsamira pa chipembedzo chawo),” pomwe onsewa akuwerenga buku (lomwe adawavumbulutsira popanda kutsatira zili m’bukulo). Momwemonso akunena amene sali odziwa (Arabu opembedza mafano) monga zonena zawo (Ayuda). Allah adzaweruza pakati pawo tsiku la chimaliziro pa zomwe adali kusiyana.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَنۡ أَظۡلَمُ مِمَّن مَّنَعَ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ أَن يُذۡكَرَ فِيهَا ٱسۡمُهُۥ وَسَعَىٰ فِي خَرَابِهَآۚ أُوْلَٰٓئِكَ مَا كَانَ لَهُمۡ أَن يَدۡخُلُوهَآ إِلَّا خَآئِفِينَۚ لَهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا خِزۡيٞ وَلَهُمۡ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ عَذَابٌ عَظِيمٞ
Kodi alipo woipitsitsa woposa amene akutsekereza (anthu kulowa) m’misikiti ya Allah kuti lisatchulidwe m’menemo dzina Lake nalimbika kuiononga (misikitiyo)? - Kotero kuti sikunali koyenera kwa iwo kulowa mmenemo koma mwa mantha. Kuyaluka kwa pa dziko lapansi nkwawo ndipo tsiku lachimaliziro iwo adzapeza chilango chachikulu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلِلَّهِ ٱلۡمَشۡرِقُ وَٱلۡمَغۡرِبُۚ فَأَيۡنَمَا تُوَلُّواْ فَثَمَّ وَجۡهُ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ وَٰسِعٌ عَلِيمٞ
Ndipo kuvuma ndi kuzambwe nkwa Allah; ndipo pamalo paliponse pamene mwatembenukira, (pomwe Allah wakulamulirani kuti mutembenukire), pamenepo mupezapo chiyanjo cha Allah. Ndithudi Allah Ngokwanira ponseponse, Wodziwa chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالُواْ ٱتَّخَذَ ٱللَّهُ وَلَدٗاۗ سُبۡحَٰنَهُۥۖ بَل لَّهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ كُلّٞ لَّهُۥ قَٰنِتُونَ
Ndipo (osakhulupirira) akumanena: “Allah wadzipangira mwana.” (Allah) wapatukana ndi zimenezo. Koma (zolengedwa) zonse za kumwamba ndi pansi Nzake. Zonse zikumumvera Iye.
Tefsiri na arapskom jeziku:
بَدِيعُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ وَإِذَا قَضَىٰٓ أَمۡرٗا فَإِنَّمَا يَقُولُ لَهُۥ كُن فَيَكُونُ
(Iye ndi) Mlengi wa thambo ndi nthaka popanda chofanizira. Ndipo akafuna chinthu kuti chichitike amangoti: “Chitika,” ndipo chimachitikadi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ لَا يَعۡلَمُونَ لَوۡلَا يُكَلِّمُنَا ٱللَّهُ أَوۡ تَأۡتِينَآ ءَايَةٞۗ كَذَٰلِكَ قَالَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِم مِّثۡلَ قَوۡلِهِمۡۘ تَشَٰبَهَتۡ قُلُوبُهُمۡۗ قَدۡ بَيَّنَّا ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يُوقِنُونَ
Ndipo aja osadziwa akunena: “Bwanji Allah sakutiyankhula ife? Kapena kutibwerera chizindikiro (chizizwa)?” Mofanana ndi zoyankhula zawozo adanenanso amene adalipo kale. Mitima yawo yalingana. Ndithu Ife tazifotokoza zizindikiro momveka kwa anthu otsimikiza (m’chikhulupiliro).
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَٰكَ بِٱلۡحَقِّ بَشِيرٗا وَنَذِيرٗاۖ وَلَا تُسۡـَٔلُ عَنۡ أَصۡحَٰبِ ٱلۡجَحِيمِ
Ndithudi, Ife takutumiza (iwe Mtumiki {s.a.w}) ndi choonadi kuti ukhale wouza nkhani zabwino ndi wochenjeza. Ndipo siudzafunsidwa za anthu a ku Moto.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَن تَرۡضَىٰ عَنكَ ٱلۡيَهُودُ وَلَا ٱلنَّصَٰرَىٰ حَتَّىٰ تَتَّبِعَ مِلَّتَهُمۡۗ قُلۡ إِنَّ هُدَى ٱللَّهِ هُوَ ٱلۡهُدَىٰۗ وَلَئِنِ ٱتَّبَعۡتَ أَهۡوَآءَهُم بَعۡدَ ٱلَّذِي جَآءَكَ مِنَ ٱلۡعِلۡمِ مَا لَكَ مِنَ ٱللَّهِ مِن وَلِيّٖ وَلَا نَصِيرٍ
Ndipo Ayuda ndi Akhrisitu sangakondwere nawe pokhapokha utatsatira chipembedzo chawo. Nena: “Ndithudi, chiongoko cha Allah ndichomwe chili chiongoko chenicheni.” Ngati utsata zilakolako zawo pambuyo pa zomwe zakudzera, monga kuzindikira (kwenikweni), sudzapeza mtetezi aliyense ngakhale mthandizi kwa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ ءَاتَيۡنَٰهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ يَتۡلُونَهُۥ حَقَّ تِلَاوَتِهِۦٓ أُوْلَٰٓئِكَ يُؤۡمِنُونَ بِهِۦۗ وَمَن يَكۡفُرۡ بِهِۦ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
Anthu omwe tidawapatsa buku naliwerenga kuwerenga koyenera (kopanda kusintha mawu ake ndi matanthauzo ake), iwo ndi amene akulikhulupirira (bukuli la Qur’an). Koma amene angalikane iwowa ndi omwe ali oonongeka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَتِيَ ٱلَّتِيٓ أَنۡعَمۡتُ عَلَيۡكُمۡ وَأَنِّي فَضَّلۡتُكُمۡ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
E inu ana a Israyeli! Kumbukirani chisomo changa chomwe ndidakudalitsani nacho. Ndithudi, ndidakuchitirani zabwino kuposa zolengedwa zonse (panthawi imeneyo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱتَّقُواْ يَوۡمٗا لَّا تَجۡزِي نَفۡسٌ عَن نَّفۡسٖ شَيۡـٔٗا وَلَا يُقۡبَلُ مِنۡهَا عَدۡلٞ وَلَا تَنفَعُهَا شَفَٰعَةٞ وَلَا هُمۡ يُنصَرُونَ
Ndipo opani tsiku lomwe munthu aliyense sadzathandiza munthu mnzake ndi chilichonse, ndipo dipo silidzalandiridwa, ngakhale dandaulo lililonse silidzamthandiza, ndiponso iwo sadzapulumutsidwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَإِذِ ٱبۡتَلَىٰٓ إِبۡرَٰهِـۧمَ رَبُّهُۥ بِكَلِمَٰتٖ فَأَتَمَّهُنَّۖ قَالَ إِنِّي جَاعِلُكَ لِلنَّاسِ إِمَامٗاۖ قَالَ وَمِن ذُرِّيَّتِيۖ قَالَ لَا يَنَالُ عَهۡدِي ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo kumbukirani pamene Ibrahim Mbuye wake (Allah) adamuyesa iye mayeso ndi malamulo ambiri; ndipo iye adakwaniritsa. Adamuuza: “Ndithudi, Ine ndichita iwe kukhala mtsogoleri wa anthu.” (Ibrahim adayankha kuti): “Kodi ndi ana anga omwe?” Adati: “(Inde; koma) lonjezo langa silingawafike ochita zoipa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ جَعَلۡنَا ٱلۡبَيۡتَ مَثَابَةٗ لِّلنَّاسِ وَأَمۡنٗا وَٱتَّخِذُواْ مِن مَّقَامِ إِبۡرَٰهِـۧمَ مُصَلّٗىۖ وَعَهِدۡنَآ إِلَىٰٓ إِبۡرَٰهِـۧمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ أَن طَهِّرَا بَيۡتِيَ لِلطَّآئِفِينَ وَٱلۡعَٰكِفِينَ وَٱلرُّكَّعِ ٱلسُّجُودِ
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene tidapanga nyumba (ya Al-Kaaba) kuti pakhale pamalo pobwererapo anthu (poyendera anthu) ndikukhalanso malo achitetezo. Ndipo pachiteni kukhala popemphelera Swala pamalo pomwe Ibrahim adali kuimilira (pomamga nyumbayo). Ndipo tidalamula Ibrahim ndi Ismail kuti: “Ayeretsereni nyumba Yanga oizungulira (pochita twawaf) ndi amene akuchita m’bindikiro, owerama ndi kulambira (kuswali mmememo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّ ٱجۡعَلۡ هَٰذَا بَلَدًا ءَامِنٗا وَٱرۡزُقۡ أَهۡلَهُۥ مِنَ ٱلثَّمَرَٰتِ مَنۡ ءَامَنَ مِنۡهُم بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ قَالَ وَمَن كَفَرَ فَأُمَتِّعُهُۥ قَلِيلٗا ثُمَّ أَضۡطَرُّهُۥٓ إِلَىٰ عَذَابِ ٱلنَّارِۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
Ndipo (kumbukirani nkhani iyi) pamene Ibrahim adanena: “E Mbuye wanga! Uchiteni mzinda uwu (wa Makka) kukhala wa chitetezo, ndipo zipatseni nzika zake zipatso, amene akukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro mwa iwo. Allah adati: “Nayenso wosakhulupirira ndinkondweretsa pang’ono; kenako ndidzamkankhira ku chilango cha Moto. Taonani kunyansa malo obwerera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ يَرۡفَعُ إِبۡرَٰهِـۧمُ ٱلۡقَوَاعِدَ مِنَ ٱلۡبَيۡتِ وَإِسۡمَٰعِيلُ رَبَّنَا تَقَبَّلۡ مِنَّآۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo (kumbukiraninso) pamene Ibrahim ndi Ismail ankakhazikitsa maziko a nyumba (uku akupempha kwa Allah): “E Mbuye wathu! Tilandireni (ntchito yathuyi), ndithudi, Inu ndinu Akumva; Odziwa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
رَبَّنَا وَٱجۡعَلۡنَا مُسۡلِمَيۡنِ لَكَ وَمِن ذُرِّيَّتِنَآ أُمَّةٗ مُّسۡلِمَةٗ لَّكَ وَأَرِنَا مَنَاسِكَنَا وَتُبۡ عَلَيۡنَآۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
“E Mbuye wathu! Tichiteni Kukhalala Asilamu (ogonjera Inu), pamodzinso ndi ana athu muwachite kukhala fuko la Chisilamu (logonjera Inu). Ndipo tidziwitseni (njira) za mapemphero athu; ndipo landirani kulapa kwathu, ndithudi, Inu Ndinu Wolandira kulapa mochuluka; Wachisoni chosatha.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
رَبَّنَا وَٱبۡعَثۡ فِيهِمۡ رَسُولٗا مِّنۡهُمۡ يَتۡلُواْ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتِكَ وَيُعَلِّمُهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَيُزَكِّيهِمۡۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡحَكِيمُ
“E Mbuye wathu! Atumizireni mtumiki wochokera mwa iwo, kuti awawerengere Ayah (ndime) zanu ndikuwaphunzitsa buku (Lanu) ndi nzeru ndikuti awayeretse. Ndithudi Inu Ndinu Amphamvu zoposa, Anzeru zakuya.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَن يَرۡغَبُ عَن مِّلَّةِ إِبۡرَٰهِـۧمَ إِلَّا مَن سَفِهَ نَفۡسَهُۥۚ وَلَقَدِ ٱصۡطَفَيۡنَٰهُ فِي ٱلدُّنۡيَاۖ وَإِنَّهُۥ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ لَمِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Kodi ndani anganyozere chipembedzo cha Ibrahim posakhala yemwe mtima wake uli wopusa? Ndithudi, tidamsankha (Ibrahim) pa dziko lapansi; ndipo iye tsiku lachimaliziro adzakhala m’modzi wa anthu abwino.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِذۡ قَالَ لَهُۥ رَبُّهُۥٓ أَسۡلِمۡۖ قَالَ أَسۡلَمۡتُ لِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Kumbukiraninso) pamene Mbuye wake adamuuza kuti: “Khala Msilamu (gonjera).” (Iye) adati: “Ndili Msilamu (ndagonjera) kwa Mbuye wa zolengedwa zonse.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَوَصَّىٰ بِهَآ إِبۡرَٰهِـۧمُ بَنِيهِ وَيَعۡقُوبُ يَٰبَنِيَّ إِنَّ ٱللَّهَ ٱصۡطَفَىٰ لَكُمُ ٱلدِّينَ فَلَا تَمُوتُنَّ إِلَّا وَأَنتُم مُّسۡلِمُونَ
Ndipo Ibrahim adalangizanso ana ake za zimenezi, chonchonso Ya’qub (adalangizanso ana ake kuti): “E inu ana anga! Ndithudi, Allah wakusankhirani chipembedzo; choncho musafe pokhapokha muli Asilamu (ogonjera Mulungu).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمۡ كُنتُمۡ شُهَدَآءَ إِذۡ حَضَرَ يَعۡقُوبَ ٱلۡمَوۡتُ إِذۡ قَالَ لِبَنِيهِ مَا تَعۡبُدُونَ مِنۢ بَعۡدِيۖ قَالُواْ نَعۡبُدُ إِلَٰهَكَ وَإِلَٰهَ ءَابَآئِكَ إِبۡرَٰهِـۧمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَ إِلَٰهٗا وَٰحِدٗا وَنَحۡنُ لَهُۥ مُسۡلِمُونَ
Kapena inu (Ayuda ndi Akhrisitu) mudalipo pamene Ya’qub idamdzera imfa, pamene adati kwa ana ake: “Kodi pambuyo panga mudzapembedza yani?” Iwo adayankha nati: “Tidzapembedza Mulungu wako, Mulungu wa makolo ako; Ibrahim, Ismail ndi Ishâq; Mulungu mmodzi basi. Ndipo ife kwa Iye tili Asilamu (ogonjera).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
تِلۡكَ أُمَّةٞ قَدۡ خَلَتۡۖ لَهَا مَا كَسَبَتۡ وَلَكُم مَّا كَسَبۡتُمۡۖ وَلَا تُسۡـَٔلُونَ عَمَّا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Umenewo ndi mbadwo wa anthu umene udamka kale. Udzapeza zimene udachita, ndipo inunso mudzapeza zimene mudachita. Ndipo inu simudzafunsidwa zimene iwo ankachita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالُواْ كُونُواْ هُودًا أَوۡ نَصَٰرَىٰ تَهۡتَدُواْۗ قُلۡ بَلۡ مِلَّةَ إِبۡرَٰهِـۧمَ حَنِيفٗاۖ وَمَا كَانَ مِنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Ndipo (Ayuda ndi Akhrisitu) adati (kwa Asilamu): “Khalani Ayuda kapena Akhrisitu mukhala oongoka.” Nena: “Koma (tikutsata) chipembedzo cha Ibrahim yemwe adaleka zipembedzo zopotoka, ndipo sadali mwa ophatikiza (Allah ndi mafano).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُولُوٓاْ ءَامَنَّا بِٱللَّهِ وَمَآ أُنزِلَ إِلَيۡنَا وَمَآ أُنزِلَ إِلَىٰٓ إِبۡرَٰهِـۧمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَ وَٱلۡأَسۡبَاطِ وَمَآ أُوتِيَ مُوسَىٰ وَعِيسَىٰ وَمَآ أُوتِيَ ٱلنَّبِيُّونَ مِن رَّبِّهِمۡ لَا نُفَرِّقُ بَيۡنَ أَحَدٖ مِّنۡهُمۡ وَنَحۡنُ لَهُۥ مُسۡلِمُونَ
Nenani (inu Asilamu kuwauza Ayuda ndi Akhrisitu); “Takhulupirira Allah ndi zimene zidavumbulutsidwa kwa ife, ndi zimene zidavumbulutsidwa kwa Ibrahim, Ismail, Ishâq, Ya’qub ndi zidzukulu (zake) ndi zimene adapatsidwa Mûsa, Isa (Yesu), ndiponso zimene adapatsidwa aneneri (ena) kuchokera kwa Mbuye wawo. Sitilekanitsa pakati pa mmodzi wa iwo (koma onse tikuwakhulupirira). Ndipo ife kwa Iye tili Asilamu (ogonjera).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِنۡ ءَامَنُواْ بِمِثۡلِ مَآ ءَامَنتُم بِهِۦ فَقَدِ ٱهۡتَدَواْۖ وَّإِن تَوَلَّوۡاْ فَإِنَّمَا هُمۡ فِي شِقَاقٖۖ فَسَيَكۡفِيكَهُمُ ٱللَّهُۚ وَهُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Choncho ngati akhulupirira (Ayuda ndi Akhrisitu) monga mmene mwakhulupirira inu, ndiye kuti awongoka. Koma ngati akutembenuka (posakhulupirira) ndiye kuti iwo ali m’kutsutsana. Choncho Allah akuteteza ku zoipa zawo, ndipo Iye Ngwakumva; Wodziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
صِبۡغَةَ ٱللَّهِ وَمَنۡ أَحۡسَنُ مِنَ ٱللَّهِ صِبۡغَةٗۖ وَنَحۡنُ لَهُۥ عَٰبِدُونَ
(Tsatirani) chiongoko cha Allah (Chisilamu). Kodi ndi ndani amene ali ndi chiongoko chabwino kuposa Allah? Ndipo ife Iye Yekha timupembedza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡ أَتُحَآجُّونَنَا فِي ٱللَّهِ وَهُوَ رَبُّنَا وَرَبُّكُمۡ وَلَنَآ أَعۡمَٰلُنَا وَلَكُمۡ أَعۡمَٰلُكُمۡ وَنَحۡنُ لَهُۥ مُخۡلِصُونَ
Nena (iwe Muhammad {s.a.w} kwa Ayuda ndi Akhrisitu): “Ha! Mukutsutsana nafe za Allah (ponena kuti bwanji wapereka uneneri kumbali ya ife), pomwe Iye ndi Mbuye wathu ndiponso Mbuye wanu? (Pamene mudali olungama adakupatsani uneneri, ndipo pamene mudakhota adakulandani natipatsa ife). Ife tili ndi zochita zathu; inunso muli ndi zochita zanu, ndipo ife tikudzipereka kwathunthu kwa Iye (Allah).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمۡ تَقُولُونَ إِنَّ إِبۡرَٰهِـۧمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَ وَٱلۡأَسۡبَاطَ كَانُواْ هُودًا أَوۡ نَصَٰرَىٰۗ قُلۡ ءَأَنتُمۡ أَعۡلَمُ أَمِ ٱللَّهُۗ وَمَنۡ أَظۡلَمُ مِمَّن كَتَمَ شَهَٰدَةً عِندَهُۥ مِنَ ٱللَّهِۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Kapena (inu Ayuda) mukunena kuti Ibrahim, Ismail Ishâq, Yaqub ndi zidzukulu anali Ayuda kapena Akhrisitu? Nena: “Kodi inu ndi odziwa kwambiri kapena Allah?” Kodi ndani woipitsitsa koposa yemwe wabisa umboni omwe ali nao ochokera kwa Allah! Komatu Allah sali wonyalanyaza pa zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
تِلۡكَ أُمَّةٞ قَدۡ خَلَتۡۖ لَهَا مَا كَسَبَتۡ وَلَكُم مَّا كَسَبۡتُمۡۖ وَلَا تُسۡـَٔلُونَ عَمَّا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Umenewo ndi mbadwo wa anthu umene udamka kale. Udzapeza zimene udachita, ndipo inunso mudzapeza zimene mudachita. Ndipo inu simudzafunsidwa zimene iwo ankachita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ سَيَقُولُ ٱلسُّفَهَآءُ مِنَ ٱلنَّاسِ مَا وَلَّىٰهُمۡ عَن قِبۡلَتِهِمُ ٱلَّتِي كَانُواْ عَلَيۡهَاۚ قُل لِّلَّهِ ٱلۡمَشۡرِقُ وَٱلۡمَغۡرِبُۚ يَهۡدِي مَن يَشَآءُ إِلَىٰ صِرَٰطٖ مُّسۡتَقِيمٖ
۞ Posachedwapa mbutuma za anthu zikhala zikunena: “Nchiyani chimene chawatembenuza ku chibula (mbali yoyang’ana popemphera) chawo chomwe akhala akulunjika nkhope zawo.” Nena: “Kuvuma ndi kuzambwe ndi kwa Allah amamuongolera amene wamfuna kunjira yolunjika.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَكَذَٰلِكَ جَعَلۡنَٰكُمۡ أُمَّةٗ وَسَطٗا لِّتَكُونُواْ شُهَدَآءَ عَلَى ٱلنَّاسِ وَيَكُونَ ٱلرَّسُولُ عَلَيۡكُمۡ شَهِيدٗاۗ وَمَا جَعَلۡنَا ٱلۡقِبۡلَةَ ٱلَّتِي كُنتَ عَلَيۡهَآ إِلَّا لِنَعۡلَمَ مَن يَتَّبِعُ ٱلرَّسُولَ مِمَّن يَنقَلِبُ عَلَىٰ عَقِبَيۡهِۚ وَإِن كَانَتۡ لَكَبِيرَةً إِلَّا عَلَى ٱلَّذِينَ هَدَى ٱللَّهُۗ وَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيُضِيعَ إِيمَٰنَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِٱلنَّاسِ لَرَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Choncho takusankhani (inu Asilamu) kukhala mpingo wabwino (wapakatikati) kuti mukhale mboni pa anthu ndi kuti Mtumiki (s.a.w) akhale mboni pa inu. Ndipo chibula (choyang’ana mbali ya ku Yerusalemu) chomwe udali nacho sitidachichite koma kuti timdziwitse (adziwike kwa anthu) amene akutsata Mtumiki (s.a.w), ndi yemwe akutembenukira m’mbuyo. Ndipo ndithudi, chidali chinthu chovuta kupatula kwa omwe Allah wawaongola. Ndipo nkosayenera kwa Allah kusokoneza Swala zanu, pakuti Allah Ngoleza kwabasi kwa anthu, Ngwachifundo chambiri. [6]
[6] Apa akutanthauza kuti pamene takutsogolerani ku njira yolunjika, takulolani inu ampingo wa Muhammad (s.a.w) kukhala anthu olungama, kulungama kosapyola nako muyeso ndiponso kopanda kuchepetsa chinthu chilichonse chazauzimu, ndi chamoyo wapadziko lino lapansi. Mpingo wa Asilamu ngwapakatikati mzokhulupilira zake zonse. Umalimbikira kugwira ntchito ya zinthu za mdziko ndiponso ya zinthu zauzimu mwakhama, chilichonse mwa zimenezi amachilimbikira mosapyoza muyeso. Limeneli ndilo tanthauzo la “mpingo wapakatikati.’’ Chisilamu sichilekelera munthu mmodzi kuti apondereze anthu ambirimbiri; ndiponso sichilekelera anthu ambiri kusalabadira za munthu mmodzi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَدۡ نَرَىٰ تَقَلُّبَ وَجۡهِكَ فِي ٱلسَّمَآءِۖ فَلَنُوَلِّيَنَّكَ قِبۡلَةٗ تَرۡضَىٰهَاۚ فَوَلِّ وَجۡهَكَ شَطۡرَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۚ وَحَيۡثُ مَا كُنتُمۡ فَوَلُّواْ وُجُوهَكُمۡ شَطۡرَهُۥۗ وَإِنَّ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ لَيَعۡلَمُونَ أَنَّهُ ٱلۡحَقُّ مِن رَّبِّهِمۡۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا يَعۡمَلُونَ
Ndithudi, taona kutembenukatembenuka kwa nkhope yako (kuyang’ana) kumwamba. Choncho tikutembenuzira ku chibula chimene ukuchifunacho. Tero tembenuzira nkhope yako kumbali ya Msikiti Wopatulika (Al-Kaaba). Ndipo paliponse pamene mulipo yang’anitsani nkhope zanu kumene kuli (msikitiwo). Ndithudi amene adapatsidwa buku akudziwitsitsa kuti chimenecho nchoonadi chochokera kwa Mbuye wawo. Ndipo Allah siwonyalanyaza zimene akuchita. (Koma chilichonse chikulembedwa m’kaundula).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَئِنۡ أَتَيۡتَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ بِكُلِّ ءَايَةٖ مَّا تَبِعُواْ قِبۡلَتَكَۚ وَمَآ أَنتَ بِتَابِعٖ قِبۡلَتَهُمۡۚ وَمَا بَعۡضُهُم بِتَابِعٖ قِبۡلَةَ بَعۡضٖۚ وَلَئِنِ ٱتَّبَعۡتَ أَهۡوَآءَهُم مِّنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَكَ مِنَ ٱلۡعِلۡمِ إِنَّكَ إِذٗا لَّمِنَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo awo adapatsidwa buku ngakhale utabwera ndi chisonyezo cha mtundu uliwonse satsata chibula chako, ngakhalenso iwe sutsata chibula chawo. Ndipo ena a iwo sali otsatira chibula cha ena (Akhrisitu satsata chibula cha Ayuda, ndipo Ayuda satsata chibula cha Akhrisitu). Ngati utsatira zofuna zawo, pambuyo pakuti kwakudzera kudziwa ndiye kuti ukhala mwa ochita zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ ءَاتَيۡنَٰهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ يَعۡرِفُونَهُۥ كَمَا يَعۡرِفُونَ أَبۡنَآءَهُمۡۖ وَإِنَّ فَرِيقٗا مِّنۡهُمۡ لَيَكۡتُمُونَ ٱلۡحَقَّ وَهُمۡ يَعۡلَمُونَ
Aja amene tidawapatsa buku akumuzindikira (Mtumiki Muhammad {s.a.w}) monga momwe amawazindikilira ana awo. Koma ena mwa iwo akubisa choonadi uku akudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلۡحَقُّ مِن رَّبِّكَ فَلَا تَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُمۡتَرِينَ
(Kuyang’ana ku Al-Kaaba popemphera Swala ndicho) choonadi chomwe chachokera kwa Mbuye wako, choncho usakhale mmodzi mwa openekera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلِكُلّٖ وِجۡهَةٌ هُوَ مُوَلِّيهَاۖ فَٱسۡتَبِقُواْ ٱلۡخَيۡرَٰتِۚ أَيۡنَ مَا تَكُونُواْ يَأۡتِ بِكُمُ ٱللَّهُ جَمِيعًاۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Ndipo (mpingo) uliwonse udali ndi chibula chimene udali kuchilunjika. Choncho pikisanani pochita zabwino. Paliponse pamene mungakhale Allah adzakubweretsani nonsenu pamodzi (pa tsiku la chimaliziro). Ndithudi, Allah Ngokhoza chinthu chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنۡ حَيۡثُ خَرَجۡتَ فَوَلِّ وَجۡهَكَ شَطۡرَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۖ وَإِنَّهُۥ لَلۡحَقُّ مِن رَّبِّكَۗ وَمَا ٱللَّهُ بِغَٰفِلٍ عَمَّا تَعۡمَلُونَ
Ndipo paliponse pomwe wapita tembenuzira nkhope yako kumbali ya Msikiti Wopatulika (panthawi yopemphera). Chimenecho nchoonadi chochokera kwa Mbuye wako. Ndipo Allah sali wonyalanyaza zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنۡ حَيۡثُ خَرَجۡتَ فَوَلِّ وَجۡهَكَ شَطۡرَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۚ وَحَيۡثُ مَا كُنتُمۡ فَوَلُّواْ وُجُوهَكُمۡ شَطۡرَهُۥ لِئَلَّا يَكُونَ لِلنَّاسِ عَلَيۡكُمۡ حُجَّةٌ إِلَّا ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ مِنۡهُمۡ فَلَا تَخۡشَوۡهُمۡ وَٱخۡشَوۡنِي وَلِأُتِمَّ نِعۡمَتِي عَلَيۡكُمۡ وَلَعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Paliponse pamene wapita (iwe Mtumiki {s.a.w}) tembenuzira nkhope yako kumbali ya Msikiti Wopatulika. Ndipo paliponse pamene (inu Asilamu) muli tembenuzirani nkhope zanu kumbali yake (ya Msikitio) kuti anthu asakhale ndi mtsutso pa inu, kupatula amene adzichitira zoipa mwa iwo. Tero musawaope, koma opani Ine, ndipo ndikwaniritsa chisomo Changa pa inu kuti muongoke.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كَمَآ أَرۡسَلۡنَا فِيكُمۡ رَسُولٗا مِّنكُمۡ يَتۡلُواْ عَلَيۡكُمۡ ءَايَٰتِنَا وَيُزَكِّيكُمۡ وَيُعَلِّمُكُمُ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَيُعَلِّمُكُم مَّا لَمۡ تَكُونُواْ تَعۡلَمُونَ
Monganso tamtumizira Mtumiki (s.a.w) kwa inu wochokera mwa inu kuti akuwerengereni Ayah (ndime) Zathu, ndikukuyeretsani (kuuve wopembedza mafano) ndi kukuphunzitsani buku ndi nzeru, ndikukuphunzitsani zimene simunali kuzidziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَٱذۡكُرُونِيٓ أَذۡكُرۡكُمۡ وَٱشۡكُرُواْ لِي وَلَا تَكۡفُرُونِ
Choncho ndikumbukireni (pondithokoza pa mtendere umene ndakupatsaniwu). Nanenso ndikukumbukirani (pokulipirani mphoto yaikulu). Ndipo ndiyamikeni; musandikane.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱسۡتَعِينُواْ بِٱلصَّبۡرِ وَٱلصَّلَوٰةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلصَّٰبِرِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Dzithandizeni (pa zinthu zanu) popirira, ndi popemphera Swala. Ndithudi, Allah ali pamodzi ndi opirira. [7]
[7] M’ndimeyi Allah akulangiza Asilamu kuti akhale opilira pa masautso amtundu uliwonse amene akukumana nawo. Kupilira ndi chida chakuthwa chopambanitsa munthu ndi kugonjetsera masautso. Munthu wosapilira ndi zopweteka sangapambane pa zofuna zake. Allah akutilangizanso kuti tifunefune chithandizo pochulukitsa Swala chifukwa chakuti imalimbitsa mtima wa munthu pa masautso. Mtumiki (s.a.w) ankati masautso akamukhudza amachita changu kukapemphera Swala. Ndipo ankayankhula kuti: “Allah waupanga mpumulo wanga kukhala mkati mwa Swala.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَقُولُواْ لِمَن يُقۡتَلُ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ أَمۡوَٰتُۢۚ بَلۡ أَحۡيَآءٞ وَلَٰكِن لَّا تَشۡعُرُونَ
Ndipo musanene za amene aphedwa pa njira ya Allah kuti: “Ngakufa.” Iyayi ngamoyo, koma inu simuzindikira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَنَبۡلُوَنَّكُم بِشَيۡءٖ مِّنَ ٱلۡخَوۡفِ وَٱلۡجُوعِ وَنَقۡصٖ مِّنَ ٱلۡأَمۡوَٰلِ وَٱلۡأَنفُسِ وَٱلثَّمَرَٰتِۗ وَبَشِّرِ ٱلصَّٰبِرِينَ
Ndipo ndithu tikuyesani ndi chinachake monga mantha, njala, kuchepa kwa chuma, kutaika kwa miyoyo ndi kuonongeka kwa mbeu. Tero auze nkhani yabwino opirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ إِذَآ أَصَٰبَتۡهُم مُّصِيبَةٞ قَالُوٓاْ إِنَّا لِلَّهِ وَإِنَّآ إِلَيۡهِ رَٰجِعُونَ
Omwe vuto lililonse likawapeza amati: “Ndithudi, ife nga Allah, ndipo ndithu kwa Iye tidzabwerera.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ عَلَيۡهِمۡ صَلَوَٰتٞ مِّن رَّبِّهِمۡ وَرَحۡمَةٞۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُهۡتَدُونَ
Otero ndi amene pa iwo pali madalitso ochokera kwa Mbuye wawo ndi chifundo. Ndiponso iwo ndi amene ali oongoka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ إِنَّ ٱلصَّفَا وَٱلۡمَرۡوَةَ مِن شَعَآئِرِ ٱللَّهِۖ فَمَنۡ حَجَّ ٱلۡبَيۡتَ أَوِ ٱعۡتَمَرَ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِ أَن يَطَّوَّفَ بِهِمَاۚ وَمَن تَطَوَّعَ خَيۡرٗا فَإِنَّ ٱللَّهَ شَاكِرٌ عَلِيمٌ
Ndithudi, Safaa ndi Marwa ndizizindikiro zolemekezera chipembedzo cha Allah. Choncho, amene akukachita mapemphero a Hajj ku nyumbayo, kapena kuchita Umrah, sikulakwa kwa iye kuzungulira pamenepo (pakati pamapiri amenewo). Ndipo amene achite chabwino modzipereka (adzalipidwa). Ndithudi Allah Ngothokoza; Ngodziwa.[8]
[8] Hajj ndi Umrah ndimapemphero amene sangachitike pamalo pena paliponse kupatula mu mzinda wa Makka. Kachitidwe ka mapemphero awiriwa nkofanana. Koma pamakhala kusiyana pang’ono pakati pa Hajj ndi Umrah. Kusiyana kwake kuli motere: Hajj siichitika nthawi iliyonse koma m’miyezi yake yodziwika. Ndipo kutha kwamiyezi ya Hajj ndi masiku khumi am’khumi loyamba a m’mwezi wa Thul Hijjah. Pomwe Umrah ikhoza kuchitika m’mwezi uliwonse umene munthu wafuna.
Pamapiripo Chisilamu chisanadze adaikapo mafano omwe anthu achikunja panthawiyo adali kuwapembedza. Tero pamene Chisilamu chidadza Asilamu ena sadali kuona bwino kukachitira mapemphero pa mapiriwo poganizira za mafano amene adalipo kalelo. Koma adawauza kuti palibe kuipa kulikonse kuchitirapo mapemphero pa malopo chifukwa mafanowo adawachotsapo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَكۡتُمُونَ مَآ أَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡبَيِّنَٰتِ وَٱلۡهُدَىٰ مِنۢ بَعۡدِ مَا بَيَّنَّٰهُ لِلنَّاسِ فِي ٱلۡكِتَٰبِ أُوْلَٰٓئِكَ يَلۡعَنُهُمُ ٱللَّهُ وَيَلۡعَنُهُمُ ٱللَّٰعِنُونَ
Ndithudi, amene akubisa zimene tavumbulutsa zomwe ndi zisonyezo zoonekera poyera, ndi chiongoko pambuyo pozifotokoza mwatsatanetsatane kwa anthu m’Buku, Allah akuwatembelera iwo. Ndiponso akuwatembelera otembelera.[9]
[9] Nkofunika kwa munthu aliyense amene wachidziwa choona kuchita izi:-
a) Kuchivomereza choonacho.
b) Kuchitsata.
c) Kuchifalitsa.
d) Kuchiphunzitsa.
Choncho, masheikh ndi maulama ali ndi mwawi pokhala ndi ntchito yapamwambayi. Achite ntchitoyi modzipereka kwatunthu, mwaulere kapena molandira malipiro ngati alipo. Apitirize kuigwira ntchitoyi pamoyo wawo wonse ngakhale atakumana ndi zovuta pa ntchitoyi. Ntchitoyi njomwe aneneri a Allah adali kugwira. Tero aigwire motsanzira momwe aneneri a Allah adali kuigwilira ntchitoyi pamakhalidwe awo ndi machitidwe awo onse. Kubisa komwe kwanenedwa m’ndimeyi sikubisa mawu a Allah kokha, komanso kubisa maphunziro a zam’dziko ofunika kwa anthu.
Chisilamu chikulimbikitsa kuti ngati munthu akudziwa chilichonse chomwe chili ndi phindu kwa anthu awaphunzitse anzake, asawabisire chifukwa choopa kuti nzeruyo angaitulukire anthu ambiri ndi kuti iye sadzapatsidwa ulemu kapena kuopa kuti ena angampose. Maganizo otere ngosafunika m’Chisilamu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِلَّا ٱلَّذِينَ تَابُواْ وَأَصۡلَحُواْ وَبَيَّنُواْ فَأُوْلَٰٓئِكَ أَتُوبُ عَلَيۡهِمۡ وَأَنَا ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
Kupatula amene alapa ndi kukonza (zolakwika) nachilongosola (choonadicho kwa anthu), iwowo ndi amene ndiwalandira kulapa kwao. Ndipo ine Ngolandira kulapa kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَمَاتُواْ وَهُمۡ كُفَّارٌ أُوْلَٰٓئِكَ عَلَيۡهِمۡ لَعۡنَةُ ٱللَّهِ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ وَٱلنَّاسِ أَجۡمَعِينَ
Ndithudi, arnene sadakhulupirire, namwalira ali osakhulupirira, pa iwo pali matembelero a Allah, angelo ndi anthu onse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
خَٰلِدِينَ فِيهَا لَا يُخَفَّفُ عَنۡهُمُ ٱلۡعَذَابُ وَلَا هُمۡ يُنظَرُونَ
M’menemo (m’chilango cha matembelero) adzakhalamo nthawi yaitali. Ndipo chilango sichidzapeputsidwa kwa iwo, ndipo sadzapatsidwa nthawi (yopumula).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِلَٰهُكُمۡ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞۖ لَّآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلرَّحۡمَٰنُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo mulungu wanu ndi Mulungu mmodzi basi. Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Ngwachifundo chambiri, Ngwachisoni chosatha.[10]
[10] Tanthauzo la ndime iyi ndikuti Mulungu wanu wompembedza ndi mmodzi.
Palibe wompembedza mwachoonadi pa dziko lonse lapansi ndi kumwamba koma Iye Yekha. Iye Ngwachifundo chambiri, Wachisoni kwa zolengedwa Zake; Woyera ndiponso Wotukuka pachikhalidwe Chake chonse. Ndipo ali kutali ndi zimene akumunenerazo. Kodi asatukuke chotani ku zimene akumunenerazo chikhalirecho Iye ndi Yemwe adalenga thambo ndi zonse zam’menemo monga nyenyezi zikuluzikulu zomwe zikuyenda m’menemo mwadongosolo Lake lakuya popanda kuwombana ina ndi inzake. Ndipo m’dziko lapansi adaikamo zolengedwa zambiri zododometsa zomwe zikusonyeza mphamvu Zake zoposa, monga nyama zamoyo ndizomera zosiyanasiyana. Ndipo zikulozera kuti alipo amene adazilenga ndi amene akuziyang’anira yemwe ndi Allah. Dongosolo la zinthuzi likusonyeza kuti Allah ndi mmodzi chifukwa chakuti pakadakhala anzake othandizana naye pakadakhala chisokonezo, wina akadafuna china pomwe wina akufuna china.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ فِي خَلۡقِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَٱخۡتِلَٰفِ ٱلَّيۡلِ وَٱلنَّهَارِ وَٱلۡفُلۡكِ ٱلَّتِي تَجۡرِي فِي ٱلۡبَحۡرِ بِمَا يَنفَعُ ٱلنَّاسَ وَمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلسَّمَآءِ مِن مَّآءٖ فَأَحۡيَا بِهِ ٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ مَوۡتِهَا وَبَثَّ فِيهَا مِن كُلِّ دَآبَّةٖ وَتَصۡرِيفِ ٱلرِّيَٰحِ وَٱلسَّحَابِ ٱلۡمُسَخَّرِ بَيۡنَ ٱلسَّمَآءِ وَٱلۡأَرۡضِ لَأٓيَٰتٖ لِّقَوۡمٖ يَعۡقِلُونَ
Ndithudi, m’kulenga kwa thambo ndi nthaka, ndi kusinthana kwa usiku ndi usana, ndi (kuyenda kwa) zombo zikulu-zikulu zomwe zikuyenda pa nyanja (zitasenza zinthu) zothandiza anthu, ndi madzi amene Allah wawatsitsa kuchokera ku mitambo, naukitsira nawo nthaka pambuyo pokhala youma, nawanditsa m’menemo mtundu uliwonse wa nyama (chifukwa cha madziwo), ndi m’kusinthanasinthana kwa mphepo, ndi mitambo yomwe yalamulidwa kuyenda pakati pa thambo ndi nthaka; ndithudi, (m’mzimenezo) muli zisonyezo kwa anthu anzeru, (kuti Allah alipo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يَتَّخِذُ مِن دُونِ ٱللَّهِ أَندَادٗا يُحِبُّونَهُمۡ كَحُبِّ ٱللَّهِۖ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَشَدُّ حُبّٗا لِّلَّهِۗ وَلَوۡ يَرَى ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ إِذۡ يَرَوۡنَ ٱلۡعَذَابَ أَنَّ ٱلۡقُوَّةَ لِلَّهِ جَمِيعٗا وَأَنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعَذَابِ
Pali ena mwa anthu amene akudzipangira milungu naifanizira ndi Allah. Amaikonda monga momwe akadamkondera Allah. Koma (Asilamu) amene akhulupirira amamkonda Allah koposa. Ndipo akadaona amene adzichitira zoipa pamene azikachiona chilango (akadazindikira kuti) ndithu mphamvu zonse nza Allah, ndipo ndithu Allah Ngolanga mwaukali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِذۡ تَبَرَّأَ ٱلَّذِينَ ٱتُّبِعُواْ مِنَ ٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُواْ وَرَأَوُاْ ٱلۡعَذَابَ وَتَقَطَّعَتۡ بِهِمُ ٱلۡأَسۡبَابُ
(Akumbutse) nthawi imene otsatidwa adzawakana amene adali kuwatsata uku atachiona chilango. Ndipo mgwirizano pakati pawo udzaduka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُواْ لَوۡ أَنَّ لَنَا كَرَّةٗ فَنَتَبَرَّأَ مِنۡهُمۡ كَمَا تَبَرَّءُواْ مِنَّاۗ كَذَٰلِكَ يُرِيهِمُ ٱللَّهُ أَعۡمَٰلَهُمۡ حَسَرَٰتٍ عَلَيۡهِمۡۖ وَمَا هُم بِخَٰرِجِينَ مِنَ ٱلنَّارِ
Ndipo otsatirawo adzati: “Kukadakhala kotheka kwa ife kubwerera (ku moyo wa pa dziko) tikadawakana monga iwo atikanira.” Umo ndi momwe Allah adzikawaonetsera zochita zawo kukhala madandaulo awo. Ndipo iwo sadzatulukanso ku Moto.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ كُلُواْ مِمَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ حَلَٰلٗا طَيِّبٗا وَلَا تَتَّبِعُواْ خُطُوَٰتِ ٱلشَّيۡطَٰنِۚ إِنَّهُۥ لَكُمۡ عَدُوّٞ مُّبِينٌ
E, inu anthu! Idyani zabwino zimene zili m’nthaka zomwe zili zololedwa; ndipo musatsate mapazi a satana. Iye kwa inu ndi mdani woonekeratu.[11]
[11] E inu anthu! Idyani za mdziko lapansi zomwe zili zabwino zimene Allah wakulolezani ndipo musapenekere chilolezo chake. Musadye chinthu chosaloledwa monga kudya chinthu cha wina m’njira ya chinyengo. Musakwatule chuma chamnzanu.
Ndipo chenjerani ndi njira za satana yemwe amakukometserani zoipa. Dziwani kuti iyeyu ndi mdani wanu monga adalili mdani watate wanu Adam. Dziwaninso kuti satanayo salamula kuchita zabwino koma zoipa zokhazokha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّمَا يَأۡمُرُكُم بِٱلسُّوٓءِ وَٱلۡفَحۡشَآءِ وَأَن تَقُولُواْ عَلَى ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Ndithu iye amangokulamulani kuchita zoipa ndi zauve, ndikuti mumnamizire Allah pomunenera zimene simukuzidziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱتَّبِعُواْ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ قَالُواْ بَلۡ نَتَّبِعُ مَآ أَلۡفَيۡنَا عَلَيۡهِ ءَابَآءَنَآۚ أَوَلَوۡ كَانَ ءَابَآؤُهُمۡ لَا يَعۡقِلُونَ شَيۡـٔٗا وَلَا يَهۡتَدُونَ
Ndipo kukanenedwa kwa iwo (kuti): “Tsatirani zimene Allah wavumbulutsa;” akunena: “Koma tikutsatira zimene tidawapeza nazo atate athu.” Kodi ngakhale kuti atate awo sadali kuzindikira chilichonse ndiponso sadali oongoka (awatsatirabe)?[12]
[12] Chikhulupiliro cha munthu kuti chikhale champhamvu ndi chopindula pafunika kuti achidziwe bwinobwino chimene akuchikhulupiliracho. Asangotsatira ndikuchikhulupilira chifukwa choti auje ndi auje adali kuchikhulupilira chimenecho. Zinthu zotere zimawasokeretsa anthu ambiri. Anthu ena amachikhulupilira chinthu chifukwa chakuti makolo awo adali kuchikhulupilira pomwe chinthucho chili chachabe.
Allah adatipatsa dalitso lanzeru kuti tizirigwilitsira ntchito pofuna choonadi cha zinthu, osati kumangotsatira ngati wakhungu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَثَلُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ كَمَثَلِ ٱلَّذِي يَنۡعِقُ بِمَا لَا يَسۡمَعُ إِلَّا دُعَآءٗ وَنِدَآءٗۚ صُمُّۢ بُكۡمٌ عُمۡيٞ فَهُمۡ لَا يَعۡقِلُونَ
Ndipo fanizo la amene sadakhulupirire (omwe akulalikidwa mawu a Allah, ndi makani awo) lili ngati (mbusa) yemwe akukuwira ziweto zake ndi kuzikalipira pomwe izo sizimva tanthauzo la mawu oitanawo, koma kuitana (chabe) ndi kufuula. (Iwo) ndi agonthi, abubu ndi akhungu. Tero iwo sangazindikire.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُلُواْ مِن طَيِّبَٰتِ مَا رَزَقۡنَٰكُمۡ وَٱشۡكُرُواْ لِلَّهِ إِن كُنتُمۡ إِيَّاهُ تَعۡبُدُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Idyani zinthu zabwino zimene takupatsani, ndipo yamikani Allah ngatidi inu mukumpembedza Iye yekha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّمَا حَرَّمَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡمَيۡتَةَ وَٱلدَّمَ وَلَحۡمَ ٱلۡخِنزِيرِ وَمَآ أُهِلَّ بِهِۦ لِغَيۡرِ ٱللَّهِۖ فَمَنِ ٱضۡطُرَّ غَيۡرَ بَاغٖ وَلَا عَادٖ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ
Iye akukuletsani (kudya) nyama yofa yokha, liwende, nyama yankhumba ndi nyama yodulidwa poikuwira mayina a mafano kusiya Allah. Koma amene wasimidwa (nadya) popanda kuchikhumba choletsedwacho ndi mosapyoza muyeso palibe tchimo kwa iye. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.[13]
[13] Apa Allah akutiuza kuti zinthu zinaizi nzoletsedwa kudya koma ngati munthu atavutika kwambiri ndi njala yofuna kufanayo (ndipo kulibe kopeza chakudya chovomerezeka), akumlola kuzidya pamuyeso wothetsa njalayo, osati mokhutitsa.
Chimene chadulidwa pochitchulira dzina lomwe si la Allah monga nyama zomwe zikuzingidwira kukwanitsa maloto a azimu, kapena yomwe yazingidwa chifukwa chotsilika nyumba, kapena kutsilika midzi, ndi zina zomwe zikuzingidwa kuti satana asawavutitse; zonsezi nzoletsedwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَكۡتُمُونَ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلۡكِتَٰبِ وَيَشۡتَرُونَ بِهِۦ ثَمَنٗا قَلِيلًا أُوْلَٰٓئِكَ مَا يَأۡكُلُونَ فِي بُطُونِهِمۡ إِلَّا ٱلنَّارَ وَلَا يُكَلِّمُهُمُ ٱللَّهُ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ وَلَا يُزَكِّيهِمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٌ
Ndithudi, amene akubisa zomwe Allah adavumbulutsa m’buku (la Baibulo) m’malo mwake nasankha zinthu zamtengo wochepa, iwo sadya china mmimba mwawo koma moto basi; ndipo Allah sadzawayankhula tsiku lachimaliziro (mwachifundo koma mokwiya); ndipo sadzawayeretsa. Ndipo iwo adzapeza chilango chopweteka.[14]
[14] Ibunu Abbas adati ndime iyi ikufotokoza za atsogoleri a Chiyuda monga Kaabi bun Ashirafi ndi Maliki bun Swaifi ndi Huyaye bun Akhatwabi. Anthuwa adali kulandira mphatso zambiri zochokera kwa anthu awo owatsatira. Pamene Muhammad (s.a.w) adampatsa uneneri iwo sadakhulupirire chifukwa choopa kuti sapeza mitulo yochokera kwa anthu awo. Tero anabisa kwa anthu za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Apa mpamene Allah adavumbulutsa Ayah (ndime) iyi, yakuti “Ndithudi, amene akubisa zomwe Allah adavumbulutsa m’buku (la Baibulo) m’malo mwake nasankha zinthu za mtengo wochepa iwo sadya china m’mimba mwawo koma moto basi.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ ٱشۡتَرَوُاْ ٱلضَّلَٰلَةَ بِٱلۡهُدَىٰ وَٱلۡعَذَابَ بِٱلۡمَغۡفِرَةِۚ فَمَآ أَصۡبَرَهُمۡ عَلَى ٱلنَّارِ
Iwo ndi amene asinthanitsa kusokera ndi chiongoko, ndiponso chilango ndi chikhululuko. Kodi ndichiyani chikuwachititsa kukhala opirira ndi Moto.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ذَٰلِكَ بِأَنَّ ٱللَّهَ نَزَّلَ ٱلۡكِتَٰبَ بِٱلۡحَقِّۗ وَإِنَّ ٱلَّذِينَ ٱخۡتَلَفُواْ فِي ٱلۡكِتَٰبِ لَفِي شِقَاقِۭ بَعِيدٖ
Zimenezo nchifukwa chakuti Allah adavumbulutsa buku Lake mwa choonadi (ndipo iwo adalikana). Koma amene asemphana pa zabukuli ali mu nkangano wonkera nawo kutali kusiya choonadi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ لَّيۡسَ ٱلۡبِرَّ أَن تُوَلُّواْ وُجُوهَكُمۡ قِبَلَ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ وَلَٰكِنَّ ٱلۡبِرَّ مَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةِ وَٱلۡكِتَٰبِ وَٱلنَّبِيِّـۧنَ وَءَاتَى ٱلۡمَالَ عَلَىٰ حُبِّهِۦ ذَوِي ٱلۡقُرۡبَىٰ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينَ وَٱبۡنَ ٱلسَّبِيلِ وَٱلسَّآئِلِينَ وَفِي ٱلرِّقَابِ وَأَقَامَ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَى ٱلزَّكَوٰةَ وَٱلۡمُوفُونَ بِعَهۡدِهِمۡ إِذَا عَٰهَدُواْۖ وَٱلصَّٰبِرِينَ فِي ٱلۡبَأۡسَآءِ وَٱلضَّرَّآءِ وَحِينَ ٱلۡبَأۡسِۗ أُوْلَٰٓئِكَ ٱلَّذِينَ صَدَقُواْۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُتَّقُونَ
Ubwino suli potembenuzira nkhope zanu mbali yakuvuma ndi kuzambwe (popemphera Swala); koma ubwino weniweni ndi (wa omwe) akukhulupirira Allah, tsiku lachimaliziro, angelo, buku ndi aneneri; napereka chuma - uku eni akuchifunabe - kwa achibale ndi amasiye, ndi masikini ndi a paulendo (omwe alibe choyendera), ndi opempha, ndi kuombolera akapolo; napemphera Swala, napereka chopereka (Zakaat); ndi okwaniritsa malonjezo awo akalonjeza, ndi opirira ndi umphawi ndi matenda ndi panthawi yankhondo. Iwowo ndi amene atsimikiza (Chisilamu chawo). Ndiponso iwowo ndi omwe ali oopa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُتِبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡقِصَاصُ فِي ٱلۡقَتۡلَىۖ ٱلۡحُرُّ بِٱلۡحُرِّ وَٱلۡعَبۡدُ بِٱلۡعَبۡدِ وَٱلۡأُنثَىٰ بِٱلۡأُنثَىٰۚ فَمَنۡ عُفِيَ لَهُۥ مِنۡ أَخِيهِ شَيۡءٞ فَٱتِّبَاعُۢ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَأَدَآءٌ إِلَيۡهِ بِإِحۡسَٰنٖۗ ذَٰلِكَ تَخۡفِيفٞ مِّن رَّبِّكُمۡ وَرَحۡمَةٞۗ فَمَنِ ٱعۡتَدَىٰ بَعۡدَ ذَٰلِكَ فَلَهُۥ عَذَابٌ أَلِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Kwalamulidwa kwa inu Qiswas (kubwezerana) molingana kwa ophedwa; mfulu kwa mfulu, kapolo kwa kapolo, mkazi kwa mkazi. Koma amene wakhululukidwa ndi m’bale wakeyo pa chinthu Chilichonse, atsatire ndi kulonjelera dipolo mwaubwino. (Nayenso wolipa) apereke kwa iye mwa ubwino. Kumeneko ndikufewetsa kumene kwachokera kwa Mbuye wanu, ndiponso chifundo. Ndipo amene alumphe malire pambuyo pa izi, iye adzapeza chilango chopweteka.[15]
[15] Apa akunena kuti, “mfulu kwa mfulu” kuthanthauza kuti aliyense amene wapha nayenso aphedwe. Sikuti aphe munthu wina m’malo mwake.
Chisilamu chisanadze kudali kuponderezana zedi. Mfulu yochokera kufuko la pamwamba, ngati atapha mfulu yafuko la pansi eni a wakuphayo adali kukana kumpereka kuti aphedwe. M’malo mwake amapereka kapolo kuti ndiye aphedwe m’malo mwake. Kapolo wa mfulu wa fuko lapamwamba akapha kapolo wa mfulu wa fuko lapansi sadali kumpereka kuti akaphedwe. Amati: “Kapolo wathuyo ngwapamwamba pomwe wanuyo ngonyozeka. Choncho palibe kufanana pakati pa awiriwa.” Ndipo ngati zitachitika motere kuti kapolo wa onyozeka nkupha kapolo wa odzitukumula, odzitukumulawa amakana kupha kapolo uja m’malo mwake amafuna mfulu yochokera kufuko lonyozekalo. Tero Qur’ani idaletsa machitidwe oterewa. Anthu onse ngofanana, palibe kusiyana pakati pawo. Amene wapha aphedwe yemweyo osati wina, ngakhale atakhala mfulu kapena kapolo. Ili ndilo tanthauzo la Ayah (ndime) imeneyi.
Tsono gawo lina limene likuti: “Koma amene wakhululukidwa ndi m’bale wakeyo...” tanthauzo lake nkuti amene wamphera m’bale wake akamkhululukira wakuphayo amlipiritse dipo la ndalama. Tero apa akumuuza iyeyo kuti ngati atamkhululukira m’bale wakeyo nangomulipiritsa ndalama, alonjelere dipolo mwa ubwino. Nayenso wolipayo apereke mwa ubwino. Asachedwetse mwadala namzunguzazunguza. Tsono gawo lachitatu landime yokhayokhayi likutiuza za chifundo chimene Allah watichitira potilekera ife eni kusankha chiweruzo pankhaniyi.
Munthu yemwe amphera m’bale wake akhoza kuchita izi:
a) Kuliuza boma kuti liphenso yemwe adapha m’bale wakeyo.
b) Kapena kumlipiritsa dipo.
c) Kapena kumkhululukira popanda kulipa chilichonse. Ndipo gawo lomaliza landimeyi akumchenjeza wokhululukayo kuti asangomkhululukira munthuyo pamaso pa anthu kenako nkumuchita chiwembu mobisa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَكُمۡ فِي ٱلۡقِصَاصِ حَيَوٰةٞ يَٰٓأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِ لَعَلَّكُمۡ تَتَّقُونَ
Mu Qiswas (kubwezerana kofanana) muli kusunga moyo kwa inu, E, inu eni nzeru! Kuti mudzitchinjirize (ku mchitidwe ophana).[16]
[16] Muli moyo wabwino m’machitidwe abwino chifukwa chakuti potsata zimenezi aliyense adzakhala wotsata mwambo. Adzaopa kuti ngati apha mnzake nayenso aphedwa. Ngati achitira mnzake choipa nayenso amchitira choipa. Tero popewa zopwetekazo akhala ngati akusunga miyoyo ya anthu ena ndi wake womwe.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كُتِبَ عَلَيۡكُمۡ إِذَا حَضَرَ أَحَدَكُمُ ٱلۡمَوۡتُ إِن تَرَكَ خَيۡرًا ٱلۡوَصِيَّةُ لِلۡوَٰلِدَيۡنِ وَٱلۡأَقۡرَبِينَ بِٱلۡمَعۡرُوفِۖ حَقًّا عَلَى ٱلۡمُتَّقِينَ
Kwalamulidwa kwa inu kuti mmodzi wanu imfa ikamuyandikira, ngati asiya chuma, apereke malangizo (pa zachumacho) kwa makolo ake awiri ndi achibale ake, mwa ubwino. Ichi nchilamulo kwa oopa Allah.[17]
[17] Kale malamulo ogawira chuma cha masiye asanafotokozedwe adampatsa ufulu aliyense kuti alembe wasiya pa zachuma chakecho m’mene mwini angaonere. Wasiyawo ukhale m’njira ya chilungamo yolingana ndi Shariya. Asachite chinyengo cha mtundu uliwonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَمَنۢ بَدَّلَهُۥ بَعۡدَ مَا سَمِعَهُۥ فَإِنَّمَآ إِثۡمُهُۥ عَلَى ٱلَّذِينَ يُبَدِّلُونَهُۥٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo amene asinthe malangizowo pambuyo pakuwamva; uchimo wake uli pa amene akusinthawo. Ndithudi, Allah Ngwakumva; Ngodziwa.[18]
[18] Apa akuwachenjeza amene auzidwa wasiyawo kuti asasinthepo kanthu. Ndipo akunenetsa kuti ngati wasiyawo uwonongedwa ndiye kuti anthu omwe adalandira wasiyawo akhala ndi uchimo chifukwa chosintha wasiyawo. Koma ngati wasiyawo udalembedwa mopanda chilungamo, monga kuti iye adati: “Chuma changa m’dzawapatse ana anga aamuna okha basi,” nkusiya kutchulapo aakazi, apo Allah akuloleza olandira wasiyawo kuti aukonze ndi kuwagawira ana onsewo mwachilungamo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَمَنۡ خَافَ مِن مُّوصٖ جَنَفًا أَوۡ إِثۡمٗا فَأَصۡلَحَ بَيۡنَهُمۡ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo amene waopa kuti wopereka wasiya angapendekere kumbali yokhota kapena ku uchimo, nalinganiza pakati pawo, palibe tchimo kwa iye. Ndithudi, Allah ngokhululuka zedi, Ngwachifundo chambiri.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ كُتِبَ عَلَيۡكُمُ ٱلصِّيَامُ كَمَا كُتِبَ عَلَى ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ لَعَلَّكُمۡ تَتَّقُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Kwalamulidwa kwa inu kusala (m’mwezi wa Ramadan) monga momwe kudalamulidwira kwa anthu akale, inu musadabwere kuti muope Allah (popewa zoletsedwa).
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَيَّامٗا مَّعۡدُودَٰتٖۚ فَمَن كَانَ مِنكُم مَّرِيضًا أَوۡ عَلَىٰ سَفَرٖ فَعِدَّةٞ مِّنۡ أَيَّامٍ أُخَرَۚ وَعَلَى ٱلَّذِينَ يُطِيقُونَهُۥ فِدۡيَةٞ طَعَامُ مِسۡكِينٖۖ فَمَن تَطَوَّعَ خَيۡرٗا فَهُوَ خَيۡرٞ لَّهُۥۚ وَأَن تَصُومُواْ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
(Kusalaku nkwa) masiku owerengeka. Koma amene akhale odwala mwa inu kapena akhale paulendo, (namasula masiku ena), akwaniritse chiwerengerocho m’masiku ena. Ndipo kwa amene sangathe kusala apereke dipo lodyetsa masikini. Ndipo amene achite zabwino mwa chifuniro chake, kutero ndibwino kwa iye. Ndipo kusala (pamene kukulolezedwa kumasula) ndibwino kwa inu, ngati muli odziwadi (kufunika kwa kusala).[19]
[19] Amene sangathe kusala ndi awa:-
a) Okalamba kwambiri omwe abwerera ku umwana, amene sangathe kupilira
ndi njala
b) Odwala amene sangathe kusala ndipo alibe chiyembekezo choti achira. Anthu oterewa akuloledwa kusiya kusala. Ndipo tsiku lililonse aliyense wa iwo apereke chakudya chokwana kudya munthu mmodzi. Chakudya chomwe anthu m’dzikomo amadya. Koma amene ali osauka asachite zimenezi.
Allah amkhululukira pakuti Allah sakakamiza munthu kuchita chimene sangathe kuchichita.
Tsono wodwala yemwe ali ndi chiyembekezo chochira, ndi wapakati amene akuvutika ndi kusala, ndi woyamwitsa amene akuona kuti azunzika akasala, onsewa sapereka dipo lija. Koma adzalipa masiku amene adamasulawo zikawachokera zovutazo monganso zilili ndi wapaulendo. Koma masheikh ena akuti wapakati ndi woyamwitsa nawonso apereke dipo la chakudya. Tero malangizo awanso tikhoza kuwatsata.
Tsono kunena koti: “Ngati mutasala ndi bwino kwa inu...” kukusonyeza kuti kumanga silamulo lomwe Allah watikakamiza kuchita lopanda phindu kwa ife, koma nchinthu chothandiza kwa anthu, makamaka pathupi lathu.
Ndipo kuonjezera apa, Allah, pa tsiku la chimaliziro, adzatipatsa mphoto yabwino. Masiku ano madokotala onse padziko lapansi akuvomereza kuti kusala kuli ndi phindu lalikulu ku thupi la munthu. Ichi ndi chimodzi mwa zizindikiro zosonyeza kuona kwa chipembedzo cha Chisilamu.
Chinenere nkhaniyi papita zaka zambiri, ndipo tsopano omwe sali Asilamu akuvomereza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
شَهۡرُ رَمَضَانَ ٱلَّذِيٓ أُنزِلَ فِيهِ ٱلۡقُرۡءَانُ هُدٗى لِّلنَّاسِ وَبَيِّنَٰتٖ مِّنَ ٱلۡهُدَىٰ وَٱلۡفُرۡقَانِۚ فَمَن شَهِدَ مِنكُمُ ٱلشَّهۡرَ فَلۡيَصُمۡهُۖ وَمَن كَانَ مَرِيضًا أَوۡ عَلَىٰ سَفَرٖ فَعِدَّةٞ مِّنۡ أَيَّامٍ أُخَرَۗ يُرِيدُ ٱللَّهُ بِكُمُ ٱلۡيُسۡرَ وَلَا يُرِيدُ بِكُمُ ٱلۡعُسۡرَ وَلِتُكۡمِلُواْ ٱلۡعِدَّةَ وَلِتُكَبِّرُواْ ٱللَّهَ عَلَىٰ مَا هَدَىٰكُمۡ وَلَعَلَّكُمۡ تَشۡكُرُونَ
(Mwezi mwalamulidwa kusalawu ndi) mwezi wa Ramadan womwe mkati mwake Qur’an idavumbulutsidwa kuti ikhale chiongoko kwa anthu ndi zizindikiro zoonekera poyera za chiongoko. Ndikutinso ikhale cholekanitsa (pakati pa choonadi ndi bodza). Ndipo mwa inu amene akhalepo (pa mudzi) m’mweziwu, asale. Koma amene ali wodwala, kapena ali pa ulendo, akwaniritse chiwerengero m’masiku ena (cha masiku amene sadasale). Allah akukufunirani zopepuka ndipo samakufunirani zovuta, ndiponso (akufuna) kuti mukwaniritse chiwerengerocho ndi kumlemekeza Allah chifukwa chakuti wakutsogolerani, ndikutinso mukhale othokoza.[20]
[20] Allah akufuna kuti tikwaniritse chiwerengero cha masiku makumi atatu (30) kapena makumi awiri ndi mphambu zisanu ndi zinayi (29) chifukwa choti phindu lakumanga silingapezeke mthupi la munthu pokhapokha kumangaku kutakwaniritsidwa m’masiku amenewa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا سَأَلَكَ عِبَادِي عَنِّي فَإِنِّي قَرِيبٌۖ أُجِيبُ دَعۡوَةَ ٱلدَّاعِ إِذَا دَعَانِۖ فَلۡيَسۡتَجِيبُواْ لِي وَلۡيُؤۡمِنُواْ بِي لَعَلَّهُمۡ يَرۡشُدُونَ
Ndipo akapolo anga akakufunsa za ine, (auze kuti) Ine ndili pafupi nawo. Ndimayankha zopempha za wopempha pamene akundipempha. Choncho iwo ayankhe kuitana kwanga ndipo andikhulupirire kuti aongoke. [21]
[21] Sikuti iwe wekha ndiwe uzipempha Allah kuti: “Ndipatseni chakuti; nchiritseni kumatenda akutiakuti,” pomwe iwe suvomera kuitana kwa Allah poleka zimene akukuletsa ndi kutsata zimene akukulamula. Yamba kumuvomera Allah usanayambe kumpempha ndiye kuti pempho lako lidzakhala laphindu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُحِلَّ لَكُمۡ لَيۡلَةَ ٱلصِّيَامِ ٱلرَّفَثُ إِلَىٰ نِسَآئِكُمۡۚ هُنَّ لِبَاسٞ لَّكُمۡ وَأَنتُمۡ لِبَاسٞ لَّهُنَّۗ عَلِمَ ٱللَّهُ أَنَّكُمۡ كُنتُمۡ تَخۡتَانُونَ أَنفُسَكُمۡ فَتَابَ عَلَيۡكُمۡ وَعَفَا عَنكُمۡۖ فَٱلۡـَٰٔنَ بَٰشِرُوهُنَّ وَٱبۡتَغُواْ مَا كَتَبَ ٱللَّهُ لَكُمۡۚ وَكُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ حَتَّىٰ يَتَبَيَّنَ لَكُمُ ٱلۡخَيۡطُ ٱلۡأَبۡيَضُ مِنَ ٱلۡخَيۡطِ ٱلۡأَسۡوَدِ مِنَ ٱلۡفَجۡرِۖ ثُمَّ أَتِمُّواْ ٱلصِّيَامَ إِلَى ٱلَّيۡلِۚ وَلَا تُبَٰشِرُوهُنَّ وَأَنتُمۡ عَٰكِفُونَ فِي ٱلۡمَسَٰجِدِۗ تِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِ فَلَا تَقۡرَبُوهَاۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ ءَايَٰتِهِۦ لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَّقُونَ
Kwaloledwa kwa inu mu usiku wosala kukumana ndi akazi anu. Iwo ali ngati chovala chanu, inunso muli ngati chovala chawo. Allah wadziwa kuti mudali kudzichitira chinyengo nokha. Choncho walandira kulapa kwanu ndipo wakukhululukirani. Tsopano khudzanani nawo ndipo funani chimene Allah wakulamulirani, ndipo idyani ndi kumwa mpaka udziwike bwinobwino kwa inu ulusi woyera kuchokera ku ulusi wakuda kum’bandakucha (kufikira mudziwe kuti kucha kwalowa, usiku watha). Kenako kwaniritsani kusala mpaka dzuwa litalowa. Ndipo musakhudzane nawo (akazi anu) pamene inu mukuchita mbindikiro m’misikiti. Amenewo ndi malire a Allah; choncho musaayandikire. Motere ndimo Allah akulongosolera mwatsatanetsatane zisonyezo zake kwa anthu kuti akhale oopa Allah (potsatira malamulo ake ndi kusiya zoletsedwa). [22]
[22] Pachiyambi pomwe lamulo la kusala lidakhazikitsidwa adawaletsa anthu kukumana ndi akazi awo usiku pambuyo poti iwo agona tulo ngakhale kuti angogona pang’ono pokha. Kukumana ndi mkazi akumane asanagone. Tero lamuloli lidali lovuta kwambiri kwa iwo kulitsata. Ena a iwo adalakwa pang’ono. Choncho kudalengezedwa kuti: “Tsopano pali chilolezo choti akhoza kuchita chilichonse mpaka m’bandakucha. Ndipo kunena koti: “Funani chimene Allah wakulamulani”, ndikulilimbikitsa lamulo kuchilolezocho. Musati kuti poti kale adakuletsani kukumana ndi akazi anu pambuyo pogona tulo ndiye mupitirize kutero - iyayi. Koma tsatirani chilolezocho.
“Itikafu” ndikuchita chitsimikizo munthu chokhala mu msikiti kwamasiku akutiakuti kapena nthawi yakutiyakuti. Ndipo pempheroli limachitika nthawi zambiri m’mwezi wa Ramadan. Akachita chitsimikizocho (niya) saloledwa kutuluka mu msikitimo pokhapokha patakhala chifukwa chachikulu chotulukira, monga kupita kukadzithandiza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَأۡكُلُوٓاْ أَمۡوَٰلَكُم بَيۡنَكُم بِٱلۡبَٰطِلِ وَتُدۡلُواْ بِهَآ إِلَى ٱلۡحُكَّامِ لِتَأۡكُلُواْ فَرِيقٗا مِّنۡ أَمۡوَٰلِ ٱلنَّاسِ بِٱلۡإِثۡمِ وَأَنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
Ndipo musadye chuma chanu pakati panu mwachinyengo pochipereka kwa oweruza (m’njira ya ziphuphu) ndi cholinga choti mudye gawo la chuma cha anthu mwa uchimo uku inu mukudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلۡأَهِلَّةِۖ قُلۡ هِيَ مَوَٰقِيتُ لِلنَّاسِ وَٱلۡحَجِّۗ وَلَيۡسَ ٱلۡبِرُّ بِأَن تَأۡتُواْ ٱلۡبُيُوتَ مِن ظُهُورِهَا وَلَٰكِنَّ ٱلۡبِرَّ مَنِ ٱتَّقَىٰۗ وَأۡتُواْ ٱلۡبُيُوتَ مِنۡ أَبۡوَٰبِهَاۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ لَعَلَّكُمۡ تُفۡلِحُونَ
Akukufunsa za miyezi nena: “Imeneyi ndi miyeso ya nthawi yozindikilira anthu zinthu zawo ndi nthawi ya Hajj.” Ndipo Siubwino kulowera m’nyumba zanu mbali ya kumbuyo kwake, koma ubwino ndiwayemwe akuopa Allah. Ndipo lowerani m’nyumba podzera m’makomo ake. Opani Allah kuti inu mupambane.[23]
[23] M’nthawi ya umbuli anthu ankati akalowa m’mapemphero a Hajj sadali kulowa m’nyumba zawo podzera pakhomo pa nyumba. Ndipo sadalinso kutulukira pakhomo koma amaboola chibowo kuseri kwa nyumba nkumalowerapo ndi kutulukirapo namaganiza kuti kutero ndimapemphero okondweretsa Allah. Tsono apa Allah akuletsa mchitidwe umenewo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَٰتِلُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ٱلَّذِينَ يُقَٰتِلُونَكُمۡ وَلَا تَعۡتَدُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ ٱلۡمُعۡتَدِينَ
Ndipo menyanani nao nkhondo pa njira ya Allah (modziteteza) amene akukuthirani nkhondo. Koma musalumphe malire (powamenya amene sadakuputeni), ndithu Allah sakonda olumpha malire.[24]
[24] lyi ndi imodzi mwa ndime zomwe zikufotokoza bodza la amene akunena kuti chisilamu chidafala ndi lupanga powathira anthu nkhondo mowakakamiza kuti alowe m’Chisilamu.
Limeneli, ndithu ndibodza lamkunkhuniza. Apa pakuonetsa kuti Allah akuwapatsa chilolezo asilamu kuti amenyane ndi amene akuwaputa. Palibe chilolezo kwa iwo chowamenyera anthu osawaputa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱقۡتُلُوهُمۡ حَيۡثُ ثَقِفۡتُمُوهُمۡ وَأَخۡرِجُوهُم مِّنۡ حَيۡثُ أَخۡرَجُوكُمۡۚ وَٱلۡفِتۡنَةُ أَشَدُّ مِنَ ٱلۡقَتۡلِۚ وَلَا تُقَٰتِلُوهُمۡ عِندَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ حَتَّىٰ يُقَٰتِلُوكُمۡ فِيهِۖ فَإِن قَٰتَلُوكُمۡ فَٱقۡتُلُوهُمۡۗ كَذَٰلِكَ جَزَآءُ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo athireni nkhondo (amene akukuthirani nkhondo popanda chifukwa) paliponse pamene mwawapeza; ndipo atulutseni paliponse pamene adakutulutsani; chifukwa kusokoneza anthu pa chipembedzo chawo nkoipitsitsa kuposa kupha. Koma musamenyane nawo pafupi ndi Msikiti Wopatulika pokhapokha atayamba ndiwo kukumenyani pamenepo. Chomwecho ngati atamenyana nanu pamenepo inunso amenyeni. Motero ndi momwe ilili mphoto ya osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِنِ ٱنتَهَوۡاْ فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Koma ngati asiya, ndithudi Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَٰتِلُوهُمۡ حَتَّىٰ لَا تَكُونَ فِتۡنَةٞ وَيَكُونَ ٱلدِّينُ لِلَّهِۖ فَإِنِ ٱنتَهَوۡاْ فَلَا عُدۡوَٰنَ إِلَّا عَلَى ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo menyanani nao kufikira pasakhale masautso (ochokera kwa iwo powasautsa asilamu popanda chifukwa). Ndipo chipembedzo chikhale cha Allah (osati kupembedza anthu). Koma ngati asiya, pasakhale mtopola kupatula kwa okhawo amene ali ochita zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلشَّهۡرُ ٱلۡحَرَامُ بِٱلشَّهۡرِ ٱلۡحَرَامِ وَٱلۡحُرُمَٰتُ قِصَاصٞۚ فَمَنِ ٱعۡتَدَىٰ عَلَيۡكُمۡ فَٱعۡتَدُواْ عَلَيۡهِ بِمِثۡلِ مَا ٱعۡتَدَىٰ عَلَيۡكُمۡۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلۡمُتَّقِينَ
Mwezi wopatulika kwa mwezi wopatulika; ndipo zinthu zopatulika paikidwa kubwezerana. Ndipo amene wakuchitirani mtopola, inunso mchitireni mtopola molingana ndi momwe wakuchitirani mtopola, ndipo opani Allah (musapyoze kuposa momwe wakuchitirani). Ndipo dziwani kuti Allah ali pamodzi ndi oopa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَنفِقُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَلَا تُلۡقُواْ بِأَيۡدِيكُمۡ إِلَى ٱلتَّهۡلُكَةِ وَأَحۡسِنُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo perekani chuma chanu pa njira ya Allah, ndiponso musadziponye ku chionongeko ndi manja anu; chitani zabwino. Ndithudi, Allah amakonda ochita zabwino.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَتِمُّواْ ٱلۡحَجَّ وَٱلۡعُمۡرَةَ لِلَّهِۚ فَإِنۡ أُحۡصِرۡتُمۡ فَمَا ٱسۡتَيۡسَرَ مِنَ ٱلۡهَدۡيِۖ وَلَا تَحۡلِقُواْ رُءُوسَكُمۡ حَتَّىٰ يَبۡلُغَ ٱلۡهَدۡيُ مَحِلَّهُۥۚ فَمَن كَانَ مِنكُم مَّرِيضًا أَوۡ بِهِۦٓ أَذٗى مِّن رَّأۡسِهِۦ فَفِدۡيَةٞ مِّن صِيَامٍ أَوۡ صَدَقَةٍ أَوۡ نُسُكٖۚ فَإِذَآ أَمِنتُمۡ فَمَن تَمَتَّعَ بِٱلۡعُمۡرَةِ إِلَى ٱلۡحَجِّ فَمَا ٱسۡتَيۡسَرَ مِنَ ٱلۡهَدۡيِۚ فَمَن لَّمۡ يَجِدۡ فَصِيَامُ ثَلَٰثَةِ أَيَّامٖ فِي ٱلۡحَجِّ وَسَبۡعَةٍ إِذَا رَجَعۡتُمۡۗ تِلۡكَ عَشَرَةٞ كَامِلَةٞۗ ذَٰلِكَ لِمَن لَّمۡ يَكُنۡ أَهۡلُهُۥ حَاضِرِي ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Ndipo kwaniritsani Hajj ndi Umrah chifukwa chofuna kukondweretsa Allah. (Izi zili mkutsimikiza kulowa m’mapemphero a Hajj). Ndipo ngati mutatsekerezedwa (kukwaniritsa mapempherowo), choncho zingani nyama zimene zili zosavuta kuzipeza (monga mbuzi), ndipo musamete mitu yanu kufikira nsembeyo ifike pamalo pake pozingirapo (pomwe ndi pamalo pamene mwatsekerezedwapo). Ndipo amene mwa inu ali odwala kapena ali ndi zovutitsa ku mutu kwake, (nachita zomwe zidali zoletsedwa monga kumeta) apereke dipo la kusala kapena kupereka sadaka (chopereka chaulere), kapena kuzinga chinyama. Ndipo ngati muli pa mtendere, choncho amene angadzisangalatse pochita Umrah kenako nkuchita Hajj, azinge nyama imene ili yosavuta kupezeka (monga mbuzi). Ndipo Amene sadapeze, asale masiku atatu konko ku hajjiko ndipo asalenso masiku asanu ndi awiri mutabwerera (kwanu). Amenewo ndi masiku khumi okwanira. Lamuloli ndi la yemwe banja lake silili pafupi ndi Msikiti Wopatulika. Ndipo opani Allah, dziwani kuti Allah Ngwaukali polanga.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلۡحَجُّ أَشۡهُرٞ مَّعۡلُومَٰتٞۚ فَمَن فَرَضَ فِيهِنَّ ٱلۡحَجَّ فَلَا رَفَثَ وَلَا فُسُوقَ وَلَا جِدَالَ فِي ٱلۡحَجِّۗ وَمَا تَفۡعَلُواْ مِنۡ خَيۡرٖ يَعۡلَمۡهُ ٱللَّهُۗ وَتَزَوَّدُواْ فَإِنَّ خَيۡرَ ٱلزَّادِ ٱلتَّقۡوَىٰۖ وَٱتَّقُونِ يَٰٓأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِ
(Mapemphero a) Hajj ali ndi miyezi yodziwika, (yomwe ndi: Shawwal, Dhul Qa’da ndi Dhul Hijjah). Amene watsimikiza kuchita Hajj m’miyezi imeneyo, asachite ndi kuyankhula zauve, ndiponso asapandukire malamulo (pochita zoletsedwa uku iye ali m’mapemphero a Hajj), ndiponso asakangane ali m’Hajjimo. Ndipo chabwino chilichonse chimene mungachite, Allah achidziwa. Ndipo dzikonzereni kamba wa paulendo, ndithu kamba wabwino (wadziko lapansi) ndi amene angakupewetseni kupemphapempha, (koma kamba wabwino wa tsiku lachimaliziro ndiko kuopa Allah). Choncho ndiopeni inu eni nzeru.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٌ أَن تَبۡتَغُواْ فَضۡلٗا مِّن رَّبِّكُمۡۚ فَإِذَآ أَفَضۡتُم مِّنۡ عَرَفَٰتٖ فَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ عِندَ ٱلۡمَشۡعَرِ ٱلۡحَرَامِۖ وَٱذۡكُرُوهُ كَمَا هَدَىٰكُمۡ وَإِن كُنتُم مِّن قَبۡلِهِۦ لَمِنَ ٱلضَّآلِّينَ
Sikulakwa kwa inu kufunafuna zabwino kwa Mbuye wanu (pogulitsa zinthu zanu uku muli m’mapemphero a Hajj, kapena kugula). Ndipo mukabwerera kuchokera ku Arafat, tamandani Allah pamalo otchedwa Masha’r Harâm (Muzdalifa). Ndipo mkumbukireni monga momwe adakutsogolerani, chikhalirecho kale mudali mwa osokera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ثُمَّ أَفِيضُواْ مِنۡ حَيۡثُ أَفَاضَ ٱلنَّاسُ وَٱسۡتَغۡفِرُواْ ٱللَّهَۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Kenako yendani limodzi kuchokera pamalo pamene akuchokerapo anthu onse (pomwe ndi pa Arafat), ndipo pemphani chikhululuko kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِذَا قَضَيۡتُم مَّنَٰسِكَكُمۡ فَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ كَذِكۡرِكُمۡ ءَابَآءَكُمۡ أَوۡ أَشَدَّ ذِكۡرٗاۗ فَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يَقُولُ رَبَّنَآ ءَاتِنَا فِي ٱلدُّنۡيَا وَمَا لَهُۥ فِي ٱلۡأٓخِرَةِ مِنۡ خَلَٰقٖ
Ndipo mukamaliza mapemphero anu (tsiku la Idi komwe ndikuponya sangalawe, kuzinga nyama za nsembe, kumeta ndi kuzungulira Ka’aba (Tawaful Ifâda), mtamandeni Allah monga momwe mudali kutamandira makolo anu kapena mtamandeni koposa. Ndipo alipo ena mwa anthu amene akunena (kuti): “E Mbuye wathu! Tipatseni padziko lapansi.” Ndipo iwo alibe gawo lililonse pa tsiku lachimaliziro.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنۡهُم مَّن يَقُولُ رَبَّنَآ ءَاتِنَا فِي ٱلدُّنۡيَا حَسَنَةٗ وَفِي ٱلۡأٓخِرَةِ حَسَنَةٗ وَقِنَا عَذَابَ ٱلنَّارِ
Ndipo alipo ena mwa iwo omwe akunena kuti: “E Mbuye wathu! tipatseni zabwino pa dziko lapansi komanso pa tsiku lachimaliziro mudzatipatsenso zabwino, ndi kutitchinjiriza ku chilango cha Moto.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ نَصِيبٞ مِّمَّا كَسَبُواْۚ وَٱللَّهُ سَرِيعُ ٱلۡحِسَابِ
Iwo ali ndi gawo la zimene adachita; ndipo Allah Ngwachangu pakuwerengera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ فِيٓ أَيَّامٖ مَّعۡدُودَٰتٖۚ فَمَن تَعَجَّلَ فِي يَوۡمَيۡنِ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِ وَمَن تَأَخَّرَ فَلَآ إِثۡمَ عَلَيۡهِۖ لِمَنِ ٱتَّقَىٰۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ إِلَيۡهِ تُحۡشَرُونَ
Ndipo mtamandeni Allah m’masiku owerengeka. Koma amene wachita changu pa masiku awiri okha (nabwerera kwawo) palibe tchimo pa iye. Ndipo amene wachedwerapo palibenso tchimo pa iye kwa amene akuopa Allah. Choncho opani Allah, ndipo dziwani kuti kwa Iye nkumene mudzasonkhanitsidwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يُعۡجِبُكَ قَوۡلُهُۥ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَيُشۡهِدُ ٱللَّهَ عَلَىٰ مَا فِي قَلۡبِهِۦ وَهُوَ أَلَدُّ ٱلۡخِصَامِ
Ndipo mwa anthu alipo amene zoyankhula zake zikukondweretsa (iwe) pano pa dziko la pansi, (koma tsiku lachimaliziro kuipa kwake kudzadziwika). Ndipo iye akutsimikizira Allah kuti akhale mboni pa zomwe zili mu mtima mwake pomwe iye ndi wa makani kwambiri.[25]
[25] Tanthauzo lake nkuti alipo ena mwa anthu omwe angakukometsere zoyankhula zawo ndi kuthwa kwa lirime lawo pomwe iwo chikhalirecho akungoyankhula kuti apeze zinthu za m’dziko.
Ndimeyi ikufotokoza za Al-Akhnas bun Sharik yemwe amati akakumana ndi Mtumiki (s.a.w), amatamanda ndi kusonyeza chikhulupiliro chabodza. Koma akachoka pamaso pa mtumiki (s.a.w) amayenda pa dziko ncholinga choononga.
Umo ndi momwe alili makhalidwe a anthu ena, amangokometsa mawu pomwe zochita zawo nzauve. Tero tichenjere ndi anthu otere.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا تَوَلَّىٰ سَعَىٰ فِي ٱلۡأَرۡضِ لِيُفۡسِدَ فِيهَا وَيُهۡلِكَ ٱلۡحَرۡثَ وَٱلنَّسۡلَۚ وَٱللَّهُ لَا يُحِبُّ ٱلۡفَسَادَ
Koma akachoka (kwa iwe) akuyenda pa dziko (uku ndi uku) ncholinga chofuna kuyipitsapo ndi kuononga zomera ndi miyoyo. Komatu Allah sakonda kuononga.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا قِيلَ لَهُ ٱتَّقِ ٱللَّهَ أَخَذَتۡهُ ٱلۡعِزَّةُ بِٱلۡإِثۡمِۚ فَحَسۡبُهُۥ جَهَنَّمُۖ وَلَبِئۡسَ ٱلۡمِهَادُ
Ndipo akauzidwa kuti: “Opa Allah”, Akugwidwa ndi mwano womupititsa ku machimo, choncho Jahannam ikukwana kwa iye (kuwuchotsa mwano wakewo). Taonani kuipa kwa malo wokakhazikikamo!
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يَشۡرِي نَفۡسَهُ ٱبۡتِغَآءَ مَرۡضَاتِ ٱللَّهِۚ وَٱللَّهُ رَءُوفُۢ بِٱلۡعِبَادِ
Ndipo pali wina mwa anthu amene akugulitsa mzimu wake chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah; ndipo Allah Ngodekha kwa akapolo ake.[26]
[26] Ndimeyi idavumbulutsidwa pankhani yokhudzana ndi wophunzira wina wa Mtumiki (s.a.w) dzina lake Suhaib Al-Rumi. Iyeyu pamene anafuna kusamuka ku Makka kupita ku Madina ma Quraish anamutsekereza, ndipo adamuuza kuti ngati akufuna kusamuka asiye chuma chake chonse, kupanda kutero sangasamuke. Choncho adalolera kusiya chuma chake chonse pofuna kudzipulumutsa yekha kuti asamukire ku Madina. Allah anakondwera nayo nkhaniyi ndipo adavumbulutsa ndimeyi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱدۡخُلُواْ فِي ٱلسِّلۡمِ كَآفَّةٗ وَلَا تَتَّبِعُواْ خُطُوَٰتِ ٱلشَّيۡطَٰنِۚ إِنَّهُۥ لَكُمۡ عَدُوّٞ مُّبِينٞ
E inu amene mwakhulupirira! Lowani m’Chisilamu chonse ndipo musatsatire mapazi a satana. Ndithu iye ndi mdani wanu woonekera poyera.[27]
[27] E inu amene mwakhulupilira! Inu eni mabuku, gonjerani Allah. Ndipo lowani m’Chisilamu kwathunthu posachisokoneza ndi chinachache. Mawuwa adanenedwa pamene Abdullahi bun Salaami adalowa m’Chisilamu yemwe adali mkulu wachiyuda. lye adapempha chilolezo kwa mtumiki (s.a.w) kuti aziliremekezabe tsiku la Sabata (la chiweru) ndi kuti aziwerenga mawu a m’Taurati mu Swala zake zausiku.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِن زَلَلۡتُم مِّنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡكُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ndipo ngati mutaterezuka (kuchimwa) pambuyo pokudzerani zisonyezo (za Allah) zoonekera poyera, dziwani kuti Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya.
Tefsiri na arapskom jeziku:
هَلۡ يَنظُرُونَ إِلَّآ أَن يَأۡتِيَهُمُ ٱللَّهُ فِي ظُلَلٖ مِّنَ ٱلۡغَمَامِ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَقُضِيَ ٱلۡأَمۡرُۚ وَإِلَى ٱللَّهِ تُرۡجَعُ ٱلۡأُمُورُ
Kodi pali china chimene akuyembekeza posakhala kuwadzera Allah m’mithunzi ya mitambo ndi (kuwadzera) angelo; nkuweruzidwa chilamulo (chakuonongeka kwawo)? Komatu zinthu zonse zimabwezedwa kwa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
سَلۡ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ كَمۡ ءَاتَيۡنَٰهُم مِّنۡ ءَايَةِۭ بَيِّنَةٖۗ وَمَن يُبَدِّلۡ نِعۡمَةَ ٱللَّهِ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُ فَإِنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Afunse ana a Israyeli kuti ndizizindikiro zingati zopenyeka zomwe tidawapatsa? Komatu amene angasinthe chisomo cha Allah pambuyo pomudzera, (Allah adzamulanga), ndithudi, Allah ngolanga mwaukali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
زُيِّنَ لِلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱلۡحَيَوٰةُ ٱلدُّنۡيَا وَيَسۡخَرُونَ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْۘ وَٱلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْ فَوۡقَهُمۡ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۗ وَٱللَّهُ يَرۡزُقُ مَن يَشَآءُ بِغَيۡرِ حِسَابٖ
Moyo wa pa dziko lapansi wakometsedwa kwa amene sadakhulupirire, ndipo amawachitira chipongwe amene akhulupirira. Koma amene aopa Allah adzakhala pamwamba pawo tsiku la chiweruziro, ndipo Allah amapatsa amene wamfuna popanda chiwerengero.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كَانَ ٱلنَّاسُ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ فَبَعَثَ ٱللَّهُ ٱلنَّبِيِّـۧنَ مُبَشِّرِينَ وَمُنذِرِينَ وَأَنزَلَ مَعَهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ بِٱلۡحَقِّ لِيَحۡكُمَ بَيۡنَ ٱلنَّاسِ فِيمَا ٱخۡتَلَفُواْ فِيهِۚ وَمَا ٱخۡتَلَفَ فِيهِ إِلَّا ٱلَّذِينَ أُوتُوهُ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ بَغۡيَۢا بَيۡنَهُمۡۖ فَهَدَى ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لِمَا ٱخۡتَلَفُواْ فِيهِ مِنَ ٱلۡحَقِّ بِإِذۡنِهِۦۗ وَٱللَّهُ يَهۡدِي مَن يَشَآءُ إِلَىٰ صِرَٰطٖ مُّسۡتَقِيمٍ
Anthu onse adali a chipembedzo chimodzi (cha Chisilamu panthawi ya Adam kufikira Nuh kenako adayamba kupatukana), ndipo Allah adatumiza aneneri onena nkhani zabwino ndi ochenjeza; ndipo pamodzi nawo adavumbulutsa mabuku achoonadi kuti aweruzire pakati pa anthu pa zimene adasemphana. Ndipo sadasemphane pa zimenezo koma aja amene adapatsidwa mabukuwo pambuyo powadzera zizindikiro zoonekera poyera, chifukwa chakuchitirana dumbo pakati pawo. Koma Allah adawaongolera amene adakhulupirira kuchoonadi cha zomwe adasempaniranazo, mwachifuniro chake. Ndipo Allah amamutsogolera ku njira yolunjika amene wamfuna.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمۡ حَسِبۡتُمۡ أَن تَدۡخُلُواْ ٱلۡجَنَّةَ وَلَمَّا يَأۡتِكُم مَّثَلُ ٱلَّذِينَ خَلَوۡاْ مِن قَبۡلِكُمۖ مَّسَّتۡهُمُ ٱلۡبَأۡسَآءُ وَٱلضَّرَّآءُ وَزُلۡزِلُواْ حَتَّىٰ يَقُولَ ٱلرَّسُولُ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَهُۥ مَتَىٰ نَصۡرُ ٱللَّهِۗ أَلَآ إِنَّ نَصۡرَ ٱللَّهِ قَرِيبٞ
Kodi mukuganiza kuti mukalowa ku Munda wamtendere pomwe sanakudzereni masautso olingana (ndi omwe) adawapeza amene adamuka kale inu musanabadwe? Kusauka ndi matenda zidawakhudza, ndipo adanjenjemeretsedwa koopsa kufikira mtumiki pamodzi ndi amene adakhulupirira naye adati: “Chipulumutso cha Allah chibwera liti?” Dziwani kuti ndithu chipulumutso cha Allah chili pafupi![28]
[28] Apa Allah akufotokoza kuti msilamu aliyense adzapeza mavuto pokwaniritsa Chisilamu chake. Palibe chinthu chopindulitsa chimene chimangopezeka mofewa. Mavuto ndi amene amamkonza munthu kuti akhale olimba. Choncho, munthu asaganize kuti adzapeza chinthu chamtengo wapatali popanda kuchivutikira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَسۡـَٔلُونَكَ مَاذَا يُنفِقُونَۖ قُلۡ مَآ أَنفَقۡتُم مِّنۡ خَيۡرٖ فَلِلۡوَٰلِدَيۡنِ وَٱلۡأَقۡرَبِينَ وَٱلۡيَتَٰمَىٰ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِۗ وَمَا تَفۡعَلُواْ مِنۡ خَيۡرٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ بِهِۦ عَلِيمٞ
Akukufunsa kuti apereke chiyani? Nena: “Chuma chilichonse chimene mungachipereke, (chiperekeni) kwa makolo awiri, achibale, kwa ana amasiye, kwa osauka, ndi kwa apaulendo. Ndipo chabwino chilichonse chimene mungachite, ndithudi, Allah akuchidziwa. ”[29]
[29] Adafunsa izi lisanadze lamulo lakagawidwe ka chuma chamasiye. Pamene lidadza lamulo la kagawidwe ka chuma chamasiye lidaletsa kupereka wasiya (chilawo) kwa anthu owagawira chumacho, chifukwa chakuti aliyense wa iwo Allah adampatsa gawo lakelake. Koma ngati munthu ukufuna kupereka wasiya (chilawo) pachuma chako, pereka wasiyawo iwe usanafe ndipo gawo la wasiyawo lisapyole pa 1/3.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كُتِبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡقِتَالُ وَهُوَ كُرۡهٞ لَّكُمۡۖ وَعَسَىٰٓ أَن تَكۡرَهُواْ شَيۡـٔٗا وَهُوَ خَيۡرٞ لَّكُمۡۖ وَعَسَىٰٓ أَن تُحِبُّواْ شَيۡـٔٗا وَهُوَ شَرّٞ لَّكُمۡۚ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ وَأَنتُمۡ لَا تَعۡلَمُونَ
Kwalamulidwa kwa inu kumenya nkhondo (yotetezera chipembedzo cha Allah ) pomwe iyo (nkhondoyo) njodedwa ndi inu. Komatu mwina mungachide chinthu pomwe icho chili chahwino kwa inu. Mwinanso mungakonde chinthu pomwe icho chili choipa kwa inu. Koma Allah ndiyemwe akudziwa, ndipo inu simudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلشَّهۡرِ ٱلۡحَرَامِ قِتَالٖ فِيهِۖ قُلۡ قِتَالٞ فِيهِ كَبِيرٞۚ وَصَدٌّ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ وَكُفۡرُۢ بِهِۦ وَٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ وَإِخۡرَاجُ أَهۡلِهِۦ مِنۡهُ أَكۡبَرُ عِندَ ٱللَّهِۚ وَٱلۡفِتۡنَةُ أَكۡبَرُ مِنَ ٱلۡقَتۡلِۗ وَلَا يَزَالُونَ يُقَٰتِلُونَكُمۡ حَتَّىٰ يَرُدُّوكُمۡ عَن دِينِكُمۡ إِنِ ٱسۡتَطَٰعُواْۚ وَمَن يَرۡتَدِدۡ مِنكُمۡ عَن دِينِهِۦ فَيَمُتۡ وَهُوَ كَافِرٞ فَأُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Akukufunsa za (lamulo la) kumenya nkhondo m’miyezi yopatulika. nena: “Kumenya nkhondo m’miyeziyo ndi tchimo lalikulu. Komatu kuwatsekereza anthu ku njira ya Allah, ndi kumkana Allah, (ndi kuletsa anthu) ku Msikiti Wopatulikawo, ndi kutulutsa anthu m’menemo nditchimo loposa kwa Allah. Ndipo kutsekereza anthu kuchipembedzo chawo nzoipa kwabasi kuposa kupha. Ndipo sasiya kumenyana nanu kufikira akuchotseni m’chipembedzo chanu ngati angathe. Ndipo mwa inu amene atuluke m’chipembedzo chake, kenako namwalira uku ali osakhulipirira, iwo ndi omwe ntchito zawo zaonongeka pa dziko lapansi mpaka tsiku lachimaliziro. Ndipo iwo ndi anthu a ku Moto. M’menemo adzakhalamo nthawi yaitali.[30]
[30] Otsatira Mneneri (maswahaba) anakumana ndi osakhulupilira padeti ya 30, m’mwezi wa 6 pakalendala ya Chisilamu. Ena amaganiza kuti detilo la pa 30 lidali la m’mwezi wa Rajabu omwe ngoletsedwa kuchitamo nkhondo. Tero Aquraish adamnamizira Muhammad (s.a.w) kuti waswa ulemelero wa miyezi yopatulika. Ndipo adabwera kukamfunsa kuti: “Kodi ndimmene ukuchitira?” Umo ndi momwe Allah adawayankhira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَٱلَّذِينَ هَاجَرُواْ وَجَٰهَدُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ أُوْلَٰٓئِكَ يَرۡجُونَ رَحۡمَتَ ٱللَّهِۚ وَٱللَّهُ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndithudi, amene akhulupirira, ndi amene asamuka namenya nkhondo pa njira ya Allah, iwo ndi amene akuyembekezera chifundo cha Allah. Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلۡخَمۡرِ وَٱلۡمَيۡسِرِۖ قُلۡ فِيهِمَآ إِثۡمٞ كَبِيرٞ وَمَنَٰفِعُ لِلنَّاسِ وَإِثۡمُهُمَآ أَكۡبَرُ مِن نَّفۡعِهِمَاۗ وَيَسۡـَٔلُونَكَ مَاذَا يُنفِقُونَۖ قُلِ ٱلۡعَفۡوَۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ لَكُمُ ٱلۡأٓيَٰتِ لَعَلَّكُمۡ تَتَفَكَّرُونَ
Akukufunsa za mowa ndi njuga. Nena: “M’zimenezo muli (masautso ndi) uchimo waukulu, ndi zina zothandiza kwa anthu. Koma uchimo wake ngwaukulu zedi kuposa zothandiza zake.” Ndipo akukufunsa kuti aperekenji: Auze: “Chimene chapyolerapo (pa zofuna zanu).” Umo ndi momwe Allah akukufotokozerani ma Ayah (malamulo) kuti mulingalire.[31]
[31] Apa akufotokoza kuti masautso ndi mavuto omwe mowa ndi njuga zimadzetsa ngaakulu zedi kuposa ubwino wake. Mowa umamchotsa munthu nzeru pomwe nzeru ndidalitso lalikulu kuposa chilichonse. Ndipo mowa umamuonongera munthu chuma ndi kumdzetsera matenda m’thupi mwake. Nayonso njuga nchimodzimodzi. Imawononga chuma ndi kuyambitsa chidani pakati pa anthu. Zonsezi zimadzetsa chisokonezo ku mtundu wa munthu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۗ وَيَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلۡيَتَٰمَىٰۖ قُلۡ إِصۡلَاحٞ لَّهُمۡ خَيۡرٞۖ وَإِن تُخَالِطُوهُمۡ فَإِخۡوَٰنُكُمۡۚ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ ٱلۡمُفۡسِدَ مِنَ ٱلۡمُصۡلِحِۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ لَأَعۡنَتَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Za m’dziko lapansi ndi (zinthu) za tsiku lachimaliziro. Ndipo akukufunsa za ana amasiye, nena: “Kuwachitira zabwino ndiwo ubwino; ngati mutasakanikirana nawo, (ndibwinonso). Iwo ndi abale anu; ndipo Allah akumdziwa woononga ndi wochita zabwino. Ndipo Allah akadafuna, akadakukhwimitsirani malamulo. Ndithudi, Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَنكِحُواْ ٱلۡمُشۡرِكَٰتِ حَتَّىٰ يُؤۡمِنَّۚ وَلَأَمَةٞ مُّؤۡمِنَةٌ خَيۡرٞ مِّن مُّشۡرِكَةٖ وَلَوۡ أَعۡجَبَتۡكُمۡۗ وَلَا تُنكِحُواْ ٱلۡمُشۡرِكِينَ حَتَّىٰ يُؤۡمِنُواْۚ وَلَعَبۡدٞ مُّؤۡمِنٌ خَيۡرٞ مِّن مُّشۡرِكٖ وَلَوۡ أَعۡجَبَكُمۡۗ أُوْلَٰٓئِكَ يَدۡعُونَ إِلَى ٱلنَّارِۖ وَٱللَّهُ يَدۡعُوٓاْ إِلَى ٱلۡجَنَّةِ وَٱلۡمَغۡفِرَةِ بِإِذۡنِهِۦۖ وَيُبَيِّنُ ءَايَٰتِهِۦ لِلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَتَذَكَّرُونَ
Ndipo musakwatire akazi opembedza mafano mpaka atakhulupirira. Ndithudi, mdzakazi wokhulupirira (Allah) ngwabwino kuposa mfulu ya chikazi yopembedza mafano, ngakhale itakukondweretsani. (Ndipo ana anu aakazi a Chisilamu) musawakwatitse kwa amuna osakhulupirira, mpaka akhulupirire. Ndipo kapolo wokhulupirira (Allah) ngwabwino kuposa mfulu yopembedza mafano, ngakhale ikukukondweretsani. Iwowo akuitanira ku Moto. Koma Allah akuitanira ku Munda wamtendere ndi ku chikhululuko mwa lamulo lake. Ndipo Iye akulongosola mwatsatanetsatane ndime za mawu ake kwa anthu, kuti athe kukumbukira.[32]
[32] Ndime iyi ikuletsa Asilamu kukwatirana ndi anthu osakhulupilira Allah kupatula Akhirisitu ndi Ayuda. Nkosaloledwa mwamuna wa Chisilamu kukwatira mkazi wopembedza mafano. Nkosaloledwa kuti mkazi wa Chisilamu akwatiwe ndi mwamuna wopembedza mafano. Koma mwamuna wa Chisilamu atha kukwatira mkazi wa Chikhrisitu kapena wa Chiyuda pomwe mkazi wa Chisilamu saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wa Chikhrisitu kapena wa Chiyuda.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَيَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلۡمَحِيضِۖ قُلۡ هُوَ أَذٗى فَٱعۡتَزِلُواْ ٱلنِّسَآءَ فِي ٱلۡمَحِيضِ وَلَا تَقۡرَبُوهُنَّ حَتَّىٰ يَطۡهُرۡنَۖ فَإِذَا تَطَهَّرۡنَ فَأۡتُوهُنَّ مِنۡ حَيۡثُ أَمَرَكُمُ ٱللَّهُۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلتَّوَّٰبِينَ وَيُحِبُّ ٱلۡمُتَطَهِّرِينَ
Ndipo (iwo) akukufunsa za kukhala malo amodzi ndi azimayi panthawi imene akusamba, auze (kuti): “Zimenezo ndizovulaza (ndiponso ndiuve). Choncho apatukireni akazi m’nthawi ya matenda akumwezi, ndipo musawayandikire mpaka ayere. Ngati atayera, kumananaoni kupyolera m’njira yomwe Allah wakulamulani. Ndithu Allah amakonda olapa, ndiponso amakonda odziyeretsa. ”
Tefsiri na arapskom jeziku:
نِسَآؤُكُمۡ حَرۡثٞ لَّكُمۡ فَأۡتُواْ حَرۡثَكُمۡ أَنَّىٰ شِئۡتُمۡۖ وَقَدِّمُواْ لِأَنفُسِكُمۡۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُم مُّلَٰقُوهُۗ وَبَشِّرِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Akazi anu ali ngati minda yanu; choncho idzereni minda yanu mmene mungafunire; koma dzitsogozereni zabwino nokha, ndipo opani Allah, ndipo dziwaninso kuti mudzakumana naye. Ndipo auze nkhani yabwino amene akhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَجۡعَلُواْ ٱللَّهَ عُرۡضَةٗ لِّأَيۡمَٰنِكُمۡ أَن تَبَرُّواْ وَتَتَّقُواْ وَتُصۡلِحُواْ بَيۡنَ ٱلنَّاسِۚ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo kulumbilira kwanu dzina la Allah musakuchite kukhala chokuletsani kuchita zinthu zabwino (za m’Chisilamu) ndi kuopa Allah, ndi kuyanjanitsa pakati pa anthu. Ndipo Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[33]
[33] Munthu ngati atalumbira kuti sachita chakutichakuti monga kunena kuti, “ndikulumbira Allah sindidzayankhulana naye uje”, asasiye kukamba naye munthuyo chifukwa chakuti adalumbilira kusayankhulana naye. Koma ayankhulane naye pambuyo popereka dipo kwa masikini pa zomwe adalumbirazo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَّا يُؤَاخِذُكُمُ ٱللَّهُ بِٱللَّغۡوِ فِيٓ أَيۡمَٰنِكُمۡ وَلَٰكِن يُؤَاخِذُكُم بِمَا كَسَبَتۡ قُلُوبُكُمۡۗ وَٱللَّهُ غَفُورٌ حَلِيمٞ
Allah sangakulangeni pa kulumbira kwanu kopanda pake, koma adzakulangani chifukwa cha malumbiro anu amene mitima yanu yatsimikiza mwa mphamvu. Ndipo Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngoleza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لِّلَّذِينَ يُؤۡلُونَ مِن نِّسَآئِهِمۡ تَرَبُّصُ أَرۡبَعَةِ أَشۡهُرٖۖ فَإِن فَآءُو فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Kwa omwe akulumbilira kuti adzipatula kwa akazi awo, (nyengo yawo) ayembekezere miyezi inayi. Koma ngati atabwerera (nakhala pamodzi ndi akazi awo), ndithudi Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi. [34]
[34] Mwamuna akalumbira kuti sakhala naye pamodzi mkazi wake, tero mkaziyo ayembekezere nthawi yamiyezi inayi. Ndipo ngati nthawiyi ipambana asanakhalebe naye pamodzi, apite akamsumire kwa Kadhwi (mkulu wodziwa malamulo a Chisilamu). Ndipo Kadhwiyo akakamize mwamunayo kuti akhale naye pamodzi mkazi wakeyo, apo ayi, awalekanitse ngati izo zitalephereka. Sibwino kuvutitsana pakati pa anthu makamaka pakati pa mwamuna ndi mkazi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِنۡ عَزَمُواْ ٱلطَّلَٰقَ فَإِنَّ ٱللَّهَ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo ngati atatsimikiza kulekana, ndithudi Allah Ngwakumva, Ngodziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلۡمُطَلَّقَٰتُ يَتَرَبَّصۡنَ بِأَنفُسِهِنَّ ثَلَٰثَةَ قُرُوٓءٖۚ وَلَا يَحِلُّ لَهُنَّ أَن يَكۡتُمۡنَ مَا خَلَقَ ٱللَّهُ فِيٓ أَرۡحَامِهِنَّ إِن كُنَّ يُؤۡمِنَّ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ وَبُعُولَتُهُنَّ أَحَقُّ بِرَدِّهِنَّ فِي ذَٰلِكَ إِنۡ أَرَادُوٓاْ إِصۡلَٰحٗاۚ وَلَهُنَّ مِثۡلُ ٱلَّذِي عَلَيۡهِنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ وَلِلرِّجَالِ عَلَيۡهِنَّ دَرَجَةٞۗ وَٱللَّهُ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ndipo akazi osiidwa (asakwatiwe) ayembekezere mpaka kuyeretsedwa kutatu kukwanire. Ndipo nkosafunika kwa iwo kubisa chimene Allah walenga m’mimba zawo, ngati akukhulupiriradi Allah ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo amuna awo ali ndi udindo wowayenereza kuwabwerera m’nthawi imeneyi ngati akufuna kuchita chimvano. Nawonso azimayi ali ndi zofunika kuchitiridwa (ndi amuna awo) monga m’mene ziliri kwa azimayiwo kuchitira amuna awo mwachilamulo cha Shariya. Koma amuna ali ndi udindo okulirapo kuposa iwo. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya. [35]
[35] Mkazi ngati amsudzula ukwati saloledwa kukwatiwa ndi mwamuna wina mpaka Edda yake ithe. Ndipo Edda njosiyanasiyana kwa akazi. Eddayi njotere kusiyana kwake:
1. Mkazi akasiyidwa ali ndi mimba, pamenepo ndiye kuti Edda yake imatha akangobereka. Pompo mwamuna wina akhoza kumkwatira.
2. Ngati wosiidwayo ndi mkazi yemwe sadwala matenda akumwezi
(a) chifukwa chakukalamba
(b) kapena chifukwa chakuti sanakwane zaka zoyambira kudwala kumweziko
(c) kapena chifukwa chakuti chilengedwe chake chili momwemo
(d) kapena zifukwa zina zomwe zimachititsa kuti asadwale matenda akumwezi edda yawo onsewa ndimiyezi itatu. Asakwatiwe mpaka miyezi itatu ithe kuchokera patsiku lomwe adawasudzula.
3. Ngati wosudzulidwayo ndimkazi wodwala matenda akumwezi, Edda yake imatha akamaliza “khului” zitatu. Tsono tanthauzo lakhului maulama amamasulira mosiyanasiyana. Pamazihabi a Imam Shafii tanthauzo lake ndikuyeretsedwa kutatu (twahara zitatu). Choncho kuyeretsedwa kutatuku kukatha kuyambira pomwe adamsudzula, akhoza kukwatiwa. Koma pamazihabi a Kibazi tanthauzo lake ndikudwala kumwezi katatu (hizi zitatu). Kukatha kudwala kumwezi kutatu komwe kwachitika pambuyo pamsudzulo ndiye kuti akhoza kukwatiwa. Edda ngati siinathe mkazi saloledwa kukwatiwa. Ngati atakwatiwa ali mu edda ukwatiwo suvomerezeka. Ndiye kutinso nthawi yonse yomwe mkaziyo akukhala limodzi ndi mwamunayo akuchita naye chiwerewere. Ndipo amene akubadwa mu ukwati wotere ndi ana obadwira mu chiwerewere. Akazi omwe asiidwa ukwati akuwalangiza kuti asabise mimba kuti mwanayo adzadziwike tate wake. Ngati Edda siinathe ndiponso ngati kuchuluka kwa twalaka mwamuna sadamalize, mwamunayo ali ndi ufulu wobwererana ndi mkazi ngati atafuna. Tero padzangofunika kupeza mboni ziwiri zoti zimdziwitse mkaziyo kuti mwamuna wake wabwererana naye. Mkaziyo kapenanso abale ake saloledwa kukaniza zimenezo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلطَّلَٰقُ مَرَّتَانِۖ فَإِمۡسَاكُۢ بِمَعۡرُوفٍ أَوۡ تَسۡرِيحُۢ بِإِحۡسَٰنٖۗ وَلَا يَحِلُّ لَكُمۡ أَن تَأۡخُذُواْ مِمَّآ ءَاتَيۡتُمُوهُنَّ شَيۡـًٔا إِلَّآ أَن يَخَافَآ أَلَّا يُقِيمَا حُدُودَ ٱللَّهِۖ فَإِنۡ خِفۡتُمۡ أَلَّا يُقِيمَا حُدُودَ ٱللَّهِ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِمَا فِيمَا ٱفۡتَدَتۡ بِهِۦۗ تِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِ فَلَا تَعۡتَدُوهَاۚ وَمَن يَتَعَدَّ حُدُودَ ٱللَّهِ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلظَّٰلِمُونَ
Twalaq (mawu achilekaniro cha ukwati omwe akupereka mwayi kwa mwamuna kubwereranso kwa mkazi wake), ndi omwe anenedwa kawiri. Kenako amkhazike (mkaziyo) mwa ubwino (ngati afuna kubwererana naye) kapena alekane mwa ubwino (ngati atafunadi kumleka. Ndipo sangathe kubwererana naye ngati atamunenera kachitatu mawu achilekano pokhapokha atakwatiwa kaye ndi mwamuna wina ndi kusiidwa ndi mwamunayo). Ndipo sizili zololedwa kwa inu kuti mutenge (kulanda) chilichonse chimene mudawapatsa (akazi anu) pokhapokha (onse awiri) ngati akuopa kuti satha kusunga malire a Allah (malamulo a Allah). Ngati muopa kuti sasunga malire a Allah, ndiye kuti pamenepo pakhala popanda tchimo kwa iwo (mwamuna woyamba ndi mkaziyu) kulandira (kapena kupereka) chodziombolera mkazi. Awa ndiwo malire a Allah; choncho musawalumphe. Ndipo amene alumphe malire a Allah (powaswa), iwowo ndiwo anthu ochita zoipa.[36]
[36] Apa akuletsa kumlanda kanthu mkazi kapena kumuuza kuti abweze mahari (chiwongo). Pamalo pamodzi pokha mpomwe pali povomerezeka mkazi kudziombola kwa mwamuna wake ngati mkaziyo njemwe wafuna kuti ukwatiwo uthe, ndiponso ngati palibe choipa chilichonse chomwe mwamunayo akuchita ndipo sangathe kukhala naye mwa mtendere. Pamenepa ndiye kuti mkaziyo abweze chiwongo kuti adzichotsemo muukwati woterowo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِن طَلَّقَهَا فَلَا تَحِلُّ لَهُۥ مِنۢ بَعۡدُ حَتَّىٰ تَنكِحَ زَوۡجًا غَيۡرَهُۥۗ فَإِن طَلَّقَهَا فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِمَآ أَن يَتَرَاجَعَآ إِن ظَنَّآ أَن يُقِيمَا حُدُودَ ٱللَّهِۗ وَتِلۡكَ حُدُودُ ٱللَّهِ يُبَيِّنُهَا لِقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
Tero ngati atamuleka (ndi kunena katatu mawu achilekaniro, choncho mkazi ameneyo) ngosaloledwa kwa iye pambuyo pakutero, kufikira akwatiwe ndi mwamuna wina. (Ngati mwamuna winayo atamusiya), palibe kulakwa kwa awiriwo kubwererana ngati akuona kuti adzasunga malire a Allah. Ndipo awa ndi malire a Allah omwe akuwalongosola kwa anthu odziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا طَلَّقۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ فَبَلَغۡنَ أَجَلَهُنَّ فَأَمۡسِكُوهُنَّ بِمَعۡرُوفٍ أَوۡ سَرِّحُوهُنَّ بِمَعۡرُوفٖۚ وَلَا تُمۡسِكُوهُنَّ ضِرَارٗا لِّتَعۡتَدُواْۚ وَمَن يَفۡعَلۡ ذَٰلِكَ فَقَدۡ ظَلَمَ نَفۡسَهُۥۚ وَلَا تَتَّخِذُوٓاْ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ هُزُوٗاۚ وَٱذۡكُرُواْ نِعۡمَتَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ وَمَآ أَنزَلَ عَلَيۡكُم مِّنَ ٱلۡكِتَٰبِ وَٱلۡحِكۡمَةِ يَعِظُكُم بِهِۦۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٞ
Ndipo pamene musiya akazi powanenera mawu achilekaniro, niiyandikira kukwana nyengo ya edda yawo (chiyembekezero chawo), abwelereni mwa ubwino; kapena lekananaoni mwa ubwino, ndipo musawabwelere mowavutitsa kuti mupyole malire a Allah (poswa malamulo ake). Ndipo amene achite zimenezo ndiye kuti wadzichitira yekha zoipa. Ndipo ndime za mawu a Allah musazichitire chibwana. Ndipo kumbukirani mtendere wa Allah umene uli pa inu; makamaka chisomo chokuvumbulutsirani buku (la Qur’an) ndi kudziwitsidwa nzeru zomwe akukulangizani nazo. Ndipo opani Allah, ndithudi dziwani kuti Allah Ngodziwa chirichonse.[37]
[37] Apa amuna akuwalangiza kuti awabwelere akazi awo mwachangu nthawi ya edda isanathe kuopa kuti ikatha ndiye kuti akwatiwa ndi amuna ena. Komatu akuwalangiza kuti abwererane nawo akaziwo ncholinga chokhala nawo mwaubwino, osati kubwererana nawo ncholinga chowavutitsa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذَا طَلَّقۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ فَبَلَغۡنَ أَجَلَهُنَّ فَلَا تَعۡضُلُوهُنَّ أَن يَنكِحۡنَ أَزۡوَٰجَهُنَّ إِذَا تَرَٰضَوۡاْ بَيۡنَهُم بِٱلۡمَعۡرُوفِۗ ذَٰلِكَ يُوعَظُ بِهِۦ مَن كَانَ مِنكُمۡ يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۗ ذَٰلِكُمۡ أَزۡكَىٰ لَكُمۡ وَأَطۡهَرُۚ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ وَأَنتُمۡ لَا تَعۡلَمُونَ
Ndipo akazi mukawanenera mawu achilekaniro (oyamba ndi achiwiri), iwo nakwaniritsa chiyembekezero chawo, choncho (inu abale amkazi), musawaletse kukwatiwanso ndi amuna awo (kubwererana) ngati pali chimvano pakati pawo mwa ubwino. Zimenezo akulangizidwa nazo mwa inu yemwe akukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Zimenezo nzabwino kwa inu, ndiponso zoyeretsa. Ndipo Allah akudziwa, pomwe inu simudziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَٱلۡوَٰلِدَٰتُ يُرۡضِعۡنَ أَوۡلَٰدَهُنَّ حَوۡلَيۡنِ كَامِلَيۡنِۖ لِمَنۡ أَرَادَ أَن يُتِمَّ ٱلرَّضَاعَةَۚ وَعَلَى ٱلۡمَوۡلُودِ لَهُۥ رِزۡقُهُنَّ وَكِسۡوَتُهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ لَا تُكَلَّفُ نَفۡسٌ إِلَّا وُسۡعَهَاۚ لَا تُضَآرَّ وَٰلِدَةُۢ بِوَلَدِهَا وَلَا مَوۡلُودٞ لَّهُۥ بِوَلَدِهِۦۚ وَعَلَى ٱلۡوَارِثِ مِثۡلُ ذَٰلِكَۗ فَإِنۡ أَرَادَا فِصَالًا عَن تَرَاضٖ مِّنۡهُمَا وَتَشَاوُرٖ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِمَاۗ وَإِنۡ أَرَدتُّمۡ أَن تَسۡتَرۡضِعُوٓاْ أَوۡلَٰدَكُمۡ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِذَا سَلَّمۡتُم مَّآ ءَاتَيۡتُم بِٱلۡمَعۡرُوفِۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ
Ndipo akazi omwe angobereka kumene ayamwitse ana awo zaka ziwiri zathunthu kwa yemwe akufuna kukwaniritsa kuyamwitsa. Ndiudindo wa abambo kuwapezera chakudya chawo ndi chovala chawo (ana awo ndi ) amayiwo, motsatira malamulo a Shariya. Ndipo mzimu wa munthu aliyense sukakamizidwa, koma m’mene ungathere. Ndipo mayi wa mwanayo asazunzidwe chifukwa cha mwana wakeyo. Nayenso bambo wa mwanayo asazunzike chifukwa cha mwana wakeyo. Ndipo lamuloli lilinso chimodzimodzi pa mlowam’malo (ngati bambo atamwalira). Ndipo onse awiri ngati atafuna kumletsa kuyamwa, mogwirizana pakati pa awiriwo, ndi mokambirana palibe kulakwa pa iwo awiriwo. Ndipo ngati mutafuna kuwapezera ana anu akazi ena owayamwitsa (omwe si amayi awo), palibe uchimo mwa inu ngati mwapereka chimene udalonjeza kuwapatsa (oyamwitsawo) mwa ubwino. Ndipo opani Allah; dziwaninso kuti Allah akuona zonse zimene mukuchita.[38]
[38] Mwana amayamwitsidwa ndi mayi wake m’nthawi yazaka ziwiri. Ndipo akhoza kumuyamwitsa mopitilira zaka ziwiri. Ndipo mayiyo akhoza ngati atagwirizana ndi tate wamwanayo kumsiitsa zaka ziwiri zisanakwane ngati ali ndi chitsimikizo choti mwanayo sapeza masautso. Ndipo tate ngati adalekana naye ukwati mayi wa mwanayo pomwe mayiyo akupitiriza kuyamwitsa mwanayo, nkofunika kwa tate wa mwanayo kupereka malipiro kwa mayi wa mwanayo, monga kumpezera chakudya, zovala, ndalama zolipilira pamalo pokhala ndi zina zotere. Mwamuna asanene kwa mkaziyo kuti: “Uyu mwana wako. Tero uwona chochita naye.’’ Pamenepo mpovuta chifukwa mkaziyo sangapeze munthu womthandiza iye ndi mwanayo. Makamaka izi zingachitike ngati mkaziyo sanakwatiwe ndi mwamuna wina. Nayenso mayi wamwanayo asamkhwimitsire mwamunayo malipiro operekedwawo. Koma zonse zikhale zaubwino. Ngati tate wamwanayo palibe, ndiye kuti mlowam’malo wa tateyo ndiye adzakwaniritse zimenezo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ يُتَوَفَّوۡنَ مِنكُمۡ وَيَذَرُونَ أَزۡوَٰجٗا يَتَرَبَّصۡنَ بِأَنفُسِهِنَّ أَرۡبَعَةَ أَشۡهُرٖ وَعَشۡرٗاۖ فَإِذَا بَلَغۡنَ أَجَلَهُنَّ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ فِيمَا فَعَلۡنَ فِيٓ أَنفُسِهِنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٞ
234, Ndipo mwa inu amene amwalira nasiya akazi, choncho (akaziwo) ayembekezere (asakwatiwe) miyezi inayi ndi masiku khumi. Ndipo akakwanitsa nyengo ya chiyembekezero chawo cha edda, sitchimo kwa inu pazimene akaziwo adzichitira okha (monga kudzikongoletsa ndi kudziwonetsa kwa ofunsira ukwati); motsatira malamulo a Shariya. Ndipo Allah Ngodziwa zonse zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ فِيمَا عَرَّضۡتُم بِهِۦ مِنۡ خِطۡبَةِ ٱلنِّسَآءِ أَوۡ أَكۡنَنتُمۡ فِيٓ أَنفُسِكُمۡۚ عَلِمَ ٱللَّهُ أَنَّكُمۡ سَتَذۡكُرُونَهُنَّ وَلَٰكِن لَّا تُوَاعِدُوهُنَّ سِرًّا إِلَّآ أَن تَقُولُواْ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗاۚ وَلَا تَعۡزِمُواْ عُقۡدَةَ ٱلنِّكَاحِ حَتَّىٰ يَبۡلُغَ ٱلۡكِتَٰبُ أَجَلَهُۥۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُ مَا فِيٓ أَنفُسِكُمۡ فَٱحۡذَرُوهُۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ غَفُورٌ حَلِيمٞ
Ndipo sitchimo kwa inu kupereka mawu okuluwika ofunsira ukwati kwa akaziwo (pamene chiyembekezero cha edda yawo chisanathe. Ndiponso palibe uchimo) kapena kubisa mu mtima mwanu, kuwakwatira (chiyembekezo chawo chikadzatha). Allah wadziwa kuti mukhala mukuwakumbukira akaziwo. Koma musawalonjeze mobisa (kuti: “Ikatha edda ndidzakukwatira).” Koma nenani mawu abwino. Ndipo musatsimikize kumanga ukwati mpaka nyengo yolembedwayo ikwanire. Ndipo dziwani kuti Allah akudziwa zomwe zili m’mitima mwanu. Tero muopeni (Allah), dziwaninso kuti Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngoleza.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَّا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن طَلَّقۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ مَا لَمۡ تَمَسُّوهُنَّ أَوۡ تَفۡرِضُواْ لَهُنَّ فَرِيضَةٗۚ وَمَتِّعُوهُنَّ عَلَى ٱلۡمُوسِعِ قَدَرُهُۥ وَعَلَى ٱلۡمُقۡتِرِ قَدَرُهُۥ مَتَٰعَۢا بِٱلۡمَعۡرُوفِۖ حَقًّا عَلَى ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Palibe tchimo pa inu mutawapatsa akazi mawu achilekaniro pomwe simudakhudzane nawo; pomwenso simudawadziwitse gawo la chiwongo chawo; koma asangalatseni (powapatsa chilekaniro). Wopeza bwino apereke malinga ndikupeza bwino kwake; wochepekedwa apereke malingana ndikuchepekedwa kwake. Chilekaniro chosangalatsacho chikhale molingana ndi malamulo a Shariya, ndipo ndilamulo kwa ochita zabwino.[39]
[39] Kuthetsa ukwati nkololedwa m’Chisilamu. Koma ngakhale nkololedwa, Shariya ya Chisilamu imanyansidwa ndimachitidwe othetsa ukwati pokhapokha pakhale zifukwa zovomerezeka ndi Shariya.
Ngati patapezeka zifukwa zochititsa kuti ukwati uthe nkofunika kuti mkwati amchitire mkwatibwi zabwino monga izi:
a) ampatse chiwongo (mahar) chimene chinatsalira ngati sadamalize kupereka.
b) ampatse ndalama zina zapadera zomtulutsira mkaziyo m’nyumba.
c) ampatse chovala, malo okhala, chakudya patsiku lililonse kufikira edda yake itatha ngakhale eddayo itatenga nthawi yaitali.
d) amsiire zinthu zake kuti atenge pamodzi ndi zimene adampatsa. Nkosaloledwa kumlanda chilichonse mwa zimenezi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِن طَلَّقۡتُمُوهُنَّ مِن قَبۡلِ أَن تَمَسُّوهُنَّ وَقَدۡ فَرَضۡتُمۡ لَهُنَّ فَرِيضَةٗ فَنِصۡفُ مَا فَرَضۡتُمۡ إِلَّآ أَن يَعۡفُونَ أَوۡ يَعۡفُوَاْ ٱلَّذِي بِيَدِهِۦ عُقۡدَةُ ٱلنِّكَاحِۚ وَأَن تَعۡفُوٓاْ أَقۡرَبُ لِلتَّقۡوَىٰۚ وَلَا تَنسَوُاْ ٱلۡفَضۡلَ بَيۡنَكُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٌ
Ndipo ngati mwalekana nawo (akaziwo) musanakhudzane nawo mutawadziwitsa gawo la chiwongo chawo, apatseni theka la chimene mudagwirizana kuwapatsa pokhapokha ngati akaziwo atakana okha (theka la chiwongocho), kapena (mwamuna) uja yemwe kumangitsa kwa ukwati kuli m’manja mwake amusiire (chiwongo chonsecho mkaziyo). Ndipo ngati mutasiirana (zimenezo) zingakuyandikitseni kumbali yoopa Allah. Ndipo musaiwale kuchitirana zabwino pakati panu (ngakhale kuti mukulekana). Ndithudi Allah akuona zonse zimene mukuchita.[40]
[40] Ngati udamkwatira mkazi ndipo nkulekana naye usanalowane naye, umpatse theka lachiwongo chomwe chidatchulidwa. Ngati udampatsa chiwongo chonse, ndiye kuti akubwezere theka lake. Koma ndibwino kwa mwamuna kumpatsa mkazi chiwongo chonse ngati anali asanampatse. Ngati anampatsa asaitanitsenso chiwongocho. Ndibwinonso kwa mkazi kubweza chiwongo chonse ngati adampatsa chonse, kapena kukana kuti asampatse ngati anali asanapatsidwe. Aliyense mwa awiriwa asakhale ndi chibaba chofuna kupeza ndalama pakutha pa ukwatiwo. Malamulo tanenawa amagwira ntchito ngati chiwongo chidatchulidwa kuchuluka kwake pomwe ankafunsira ukwati. Koma ngati chiwongocho sanachitchule kuchuluka kwake kotero kuti sadagwirizane za chiwongocho kuti adzapereka mwakutimwakuti, pamenepa ndiye kuti ampatse chinthu cholekanira choti chimsangalatse. Ili ndilo tanthauzo la zomwe zatchulidwa m’ndime ya 236.
Ndithudi apa akutilangiza mwamphamvu kuti tizichitirana zabwino ngakhale panthawi yolekana ukwati. Anthu asaiwale ubwino ndi chikondi zomwe ankachitirana pakati pawo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
حَٰفِظُواْ عَلَى ٱلصَّلَوَٰتِ وَٱلصَّلَوٰةِ ٱلۡوُسۡطَىٰ وَقُومُواْ لِلَّهِ قَٰنِتِينَ
Sungani mokwanira Swala makamaka Swala yapakatikati; ndipo imilirani modzichepetsa kwa Allah.[41]
[41] M’ndime iyi akulimbikitsa kuti Swala zonse anthu azipemphere muunyinji wawo osati munthu payekhapayekha makamaka Swala yapakatikati. Ena mwa maulama adati Swala yapakatikati ndi Swala ya Dhuhr. Imapempheredwa pakatikati pamasana, dzuwa litatentha kwambiri monga momwe zilili m’maiko a Arabu. Pa Swala ya Dhuhr anthu amavutika kwambiri kukapemphera m’misikiti chifukwa chakutentha kwa dzuwa. Choncho apa akuwalimbikitsa kuti azikapemphera m’misikiti ngakhale kuli kotentha. Pomwe ena akuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Fajiri (Subuh) imene imapempheredwa pakatikati panthawi. Simasana ndiponso siusiku. Apa mpanthawi pomwe tulo timakhala tamphamvu. Tero akuwalimbikitsa anthu kusiya tuloto nkupita ku misikiti nkukapemphera Swala ya (jama) yapagulu. Ndipo akutilimbikitsanso kuti tizipemphera mofatsira ndi modzichepetsa. Ndikuti tikamapemphera tizidziwa kuti taimilira pamaso pa Allah. Komanso ma hadith ena atchula zakuti Swala yapakatikati ndi Swala ya Asr.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِنۡ خِفۡتُمۡ فَرِجَالًا أَوۡ رُكۡبَانٗاۖ فَإِذَآ أَمِنتُمۡ فَٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ كَمَا عَلَّمَكُم مَّا لَمۡ تَكُونُواْ تَعۡلَمُونَ
Ndipo ngati muli ndi mantha (kupemphera mwalamulo pamene mukumenyana ndi adani anu), pempherani uku mukuyenda, kapena mutakwera chokwera. Ndipo mukakhala pachitetezo mkumbukireni Allah (pempherani) monga momwe wakuphunzitsirani zomwe simudali kuzidziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ يُتَوَفَّوۡنَ مِنكُمۡ وَيَذَرُونَ أَزۡوَٰجٗا وَصِيَّةٗ لِّأَزۡوَٰجِهِم مَّتَٰعًا إِلَى ٱلۡحَوۡلِ غَيۡرَ إِخۡرَاجٖۚ فَإِنۡ خَرَجۡنَ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ فِي مَا فَعَلۡنَ فِيٓ أَنفُسِهِنَّ مِن مَّعۡرُوفٖۗ وَٱللَّهُ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo mwa inu amene amwalira nasiya akazi awo, alangize (amlowam’malo awo, monga makolo ndi achibale) za akazi awo kuti awapatse zodyera m’nyengo ya chaka chimodzi popanda kutulutsidwa (m’nyumba zomwe ankakhala ndi amuna awo). Koma ngati akaziwo atuluka (okha), palibe kulakwa pa inu pa zimene adzichitira okha zomwe nzogwirizana ndi chilamulo cha Shariya. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa; Ngwanzeru zakuya.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلِلۡمُطَلَّقَٰتِ مَتَٰعُۢ بِٱلۡمَعۡرُوفِۖ حَقًّا عَلَى ٱلۡمُتَّقِينَ
Ndipo akazi osiidwa ukwati, apatsidwe chilekaniro chowasangalatsa m’chilamulo cha Shariya. Ili ndi lamulo kwa amene akuopa Allah.[42]
[42] Pamene mwamuna akumusiya mkazi ukwati pafunika kuti ampatse chinthu china kuwonjezera pa chiwongo. Koma Asilamu ambiri kudera la kuno kum’mawa kwa Afrika m’malo mompatsa chinthu mkazi pomusiya amaitanitsa chinthu kwamkazi kuti awapatse kapena kumlanda katundu kumene.
Machitidwe otere ngoipitsitsa, sali ogwirizana ndi malamulo a Chisilamu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ لَكُمۡ ءَايَٰتِهِۦ لَعَلَّكُمۡ تَعۡقِلُونَ
Umu ndi momwe Allah akukulongosolerani ma Ayah ake (ndime zake) kuti inu mukhale ndi nzeru.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ خَرَجُواْ مِن دِيَٰرِهِمۡ وَهُمۡ أُلُوفٌ حَذَرَ ٱلۡمَوۡتِ فَقَالَ لَهُمُ ٱللَّهُ مُوتُواْ ثُمَّ أَحۡيَٰهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَذُو فَضۡلٍ عَلَى ٱلنَّاسِ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَشۡكُرُونَ
Kodi sudamve (nkhani za) amene adatuluka m’nyumba zawo ali zikwizikwi kuopa imfa? Ndipo Allah adawauza: “Mwalirani,” (ndipo adamwalira chabe popanda chifukwa chilichonse). Kenako Adawaukitsa (kuti adziwe kuti imfa njosathawika). Ndithudi, Allah Ndimwini kuchita zabwino pa anthu, koma anthu ambiri sathokoza.[43]
[43] Ibun Abbas adati anthuwo adali zikwi zinayi. Adatuluka m’nyumba zawo kuthawa mliri wanthomba, nati pakati pawo: “Tipite kudziko lina komwe kulibe mliri wanthomba.” Choncho adayenda mpaka kufika pamalo pena; ndipo Allah adati kwa iwo: “Mwalirani,” ndipo onse anamwaliradi nthawi yomweyo. Ndipo mmodzi wa aneneri adawadutsa iwo ali akufa, nampempha Allah kuti awawukitse kuti azimgwadira. Choncho adawaukitsa. Nkhaniyi tikuphunziramo zoti imfa siithawika.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَٰتِلُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo menyani nkhondo panjira ya Allah, ndipo dziwani kuti Allah Ngwakumva, Ngodziwa chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
مَّن ذَا ٱلَّذِي يُقۡرِضُ ٱللَّهَ قَرۡضًا حَسَنٗا فَيُضَٰعِفَهُۥ لَهُۥٓ أَضۡعَافٗا كَثِيرَةٗۚ وَٱللَّهُ يَقۡبِضُ وَيَبۡصُۜطُ وَإِلَيۡهِ تُرۡجَعُونَ
Kodi ndani angamkongoze Allah ngongole yabwino (yochokera m’chuma chake powapatsa amphawi ndi kupereka pa njira ya Allah) kuti amuonjezere zoonjezera zambiri? Ndipo Allah ndi yemwe amafumbata ndi kutambasula, ndipo kwa Iye nkumene mudzabwezedwa.[44]
[44] Apa anthu akuwalimbikitsa kuti azipereka chuma chawo pa njira zabwino ndipo Allah adzawalipira mphoto yambiri. Asachite umbombo kupereka chuma chawo m’njira zabwino pakuti sadaka siichepetsa chuma koma kuchichulukitsa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلۡمَلَإِ مِنۢ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ مِنۢ بَعۡدِ مُوسَىٰٓ إِذۡ قَالُواْ لِنَبِيّٖ لَّهُمُ ٱبۡعَثۡ لَنَا مَلِكٗا نُّقَٰتِلۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۖ قَالَ هَلۡ عَسَيۡتُمۡ إِن كُتِبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡقِتَالُ أَلَّا تُقَٰتِلُواْۖ قَالُواْ وَمَا لَنَآ أَلَّا نُقَٰتِلَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَقَدۡ أُخۡرِجۡنَا مِن دِيَٰرِنَا وَأَبۡنَآئِنَاۖ فَلَمَّا كُتِبَ عَلَيۡهِمُ ٱلۡقِتَالُ تَوَلَّوۡاْ إِلَّا قَلِيلٗا مِّنۡهُمۡۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi sudamve nkhani ya akuluakulu a ana a Israyeli pambuyo pa Mûsa? Adanena kwa mneneri wawo: “Tidzozere mfumu kuti timenye nkhondo pa njira ya Allah.” Iye (mneneri wawoyo) adati: “Mwinatu simungamenye nkhondoyo ngati kutalamulidwa kwa inu. (Iwo) adati: “Nchotani kuti tisamenye nkhondo pa njira ya Allah pomwe tatulutsidwa m’nyumba zathu pamodzi ndi ana athu?” Koma pamene adalamulidwa kumenya nkhondoyo, adatembenuka, kupatula ochepa mwa iwo. Ndipo Allah akudziwa bwinobwino za anthu ochita zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالَ لَهُمۡ نَبِيُّهُمۡ إِنَّ ٱللَّهَ قَدۡ بَعَثَ لَكُمۡ طَالُوتَ مَلِكٗاۚ قَالُوٓاْ أَنَّىٰ يَكُونُ لَهُ ٱلۡمُلۡكُ عَلَيۡنَا وَنَحۡنُ أَحَقُّ بِٱلۡمُلۡكِ مِنۡهُ وَلَمۡ يُؤۡتَ سَعَةٗ مِّنَ ٱلۡمَالِۚ قَالَ إِنَّ ٱللَّهَ ٱصۡطَفَىٰهُ عَلَيۡكُمۡ وَزَادَهُۥ بَسۡطَةٗ فِي ٱلۡعِلۡمِ وَٱلۡجِسۡمِۖ وَٱللَّهُ يُؤۡتِي مُلۡكَهُۥ مَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٞ
Ndipo mneneri wawoyo adawauza: “Allah wakusankhirani Taluti kukhala mfumu. (Iwo ) adati: “Nchotani kuti iye akhale ndi ufumu pa ife pomwe ife ngoyenera kupeza ufumu kuposa iye, ndipo sadapatsidwe chuma chambiri?” (Iye) adati: “Ndithu Allah wamusankha pa inu, ndipo wamuonjezera kukhala ndi nzeru zopambana ndi kukhala ndi thupi (lamphamvu). Ndipo Allah amampatsa ufumu wake amene wamfuna. Ndipo Allah ndi Mwini zopereka zambiri, Ngodziwa.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَقَالَ لَهُمۡ نَبِيُّهُمۡ إِنَّ ءَايَةَ مُلۡكِهِۦٓ أَن يَأۡتِيَكُمُ ٱلتَّابُوتُ فِيهِ سَكِينَةٞ مِّن رَّبِّكُمۡ وَبَقِيَّةٞ مِّمَّا تَرَكَ ءَالُ مُوسَىٰ وَءَالُ هَٰرُونَ تَحۡمِلُهُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗ لَّكُمۡ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndipo mneneri wawo adawauza (kuti): “Ndithu chizindikiro cha ufumu wake, ndikukudzerani bokosi lomwe mkati mwake muli mpumulo wa miyoyo yanu wochokera kwa Mbuye wanu, ndi zotsalira zomwe adazisiya anthu a Mûsa ndi anthu a Harun, atanyamula angelo. Ndithu m’zimenezo muli chisonyezo kwa inu (chosonyeza kuyenera kwa ufumu wake pa inu) ngati mulidi okhulupirira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَلَمَّا فَصَلَ طَالُوتُ بِٱلۡجُنُودِ قَالَ إِنَّ ٱللَّهَ مُبۡتَلِيكُم بِنَهَرٖ فَمَن شَرِبَ مِنۡهُ فَلَيۡسَ مِنِّي وَمَن لَّمۡ يَطۡعَمۡهُ فَإِنَّهُۥ مِنِّيٓ إِلَّا مَنِ ٱغۡتَرَفَ غُرۡفَةَۢ بِيَدِهِۦۚ فَشَرِبُواْ مِنۡهُ إِلَّا قَلِيلٗا مِّنۡهُمۡۚ فَلَمَّا جَاوَزَهُۥ هُوَ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَهُۥ قَالُواْ لَا طَاقَةَ لَنَا ٱلۡيَوۡمَ بِجَالُوتَ وَجُنُودِهِۦۚ قَالَ ٱلَّذِينَ يَظُنُّونَ أَنَّهُم مُّلَٰقُواْ ٱللَّهِ كَم مِّن فِئَةٖ قَلِيلَةٍ غَلَبَتۡ فِئَةٗ كَثِيرَةَۢ بِإِذۡنِ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ مَعَ ٱلصَّٰبِرِينَ
Choncho, Taluti pamene adapita ndi magulu (ake) a nkhondo, adati: “Allah akuyesani mayeso ndi mtsinje (womwe mukumane nawo panjira komwe mukupitako). Choncho amene akamwe mmenemo sali nane. Koma amene sakamwa adzakhala pamodzi nane kupatula amene watunga ndi dzanja lake (ndikumwa; iyeyo ndiye kuti sadalakwe). Koma (iwo) adamwa m’menemo kupatula ochepa mwa iwo. Choncho pamene adaoloka iye pamodzi ndi aja omwe adakhulupirira limodzi naye, (iwo) adati: “Lero sitingamuthe Jaluti ndi magulu ake a nkhondo.” Omwe adali ndi chitsimikizo chokumana ndi Allah adati: “Kodi ndimagulu angati ochepa amene adagonjetsa magulu ambiri mwa chilolezo cha Allah! Ndipo Allah Ali pamodzi ndi opirira.[45]
[45] Kumvera ndichinthu chachikulu kwabasi kuti zinthu za anthu ziyende bwino. Anthu osamvera zinthu zawo siziyenda bwino. Ndipo apa mfumuyi ikuchoka kupita ku nkhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo lomwe lidali losamvera. Choncho Allah adaiuza mfumu ija kuti iwayese mayeso oti asamwe madzi othetsa ludzu lonse. Amene samvera asawatenge kunka nawo ku bwalo lankhondo poona kuti angayambitse chisokonezo kumeneko.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَمَّا بَرَزُواْ لِجَالُوتَ وَجُنُودِهِۦ قَالُواْ رَبَّنَآ أَفۡرِغۡ عَلَيۡنَا صَبۡرٗا وَثَبِّتۡ أَقۡدَامَنَا وَٱنصُرۡنَا عَلَى ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo pamene adapita kukalimbana ndi Jaluti (mfumu ya adaniwo), pamodzi ndi magulu ake a nkhondo (anthu a Taluti) adati: “E Mbuye wathu! Titsanulireni chipiliro, ndipo limbikitsani mapazi athu: Tithangateni kwa anthu osakhulupirira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَهَزَمُوهُم بِإِذۡنِ ٱللَّهِ وَقَتَلَ دَاوُۥدُ جَالُوتَ وَءَاتَىٰهُ ٱللَّهُ ٱلۡمُلۡكَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَعَلَّمَهُۥ مِمَّا يَشَآءُۗ وَلَوۡلَا دَفۡعُ ٱللَّهِ ٱلنَّاسَ بَعۡضَهُم بِبَعۡضٖ لَّفَسَدَتِ ٱلۡأَرۡضُ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ ذُو فَضۡلٍ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
Choncho, adawagonjetsa mwa chilolezo cha Allah. Ndipo Daud adapha Jaluti; ndipo Allah adampatsa ufumu ndi uneneri, namphunzitsanso zimene adafuna. Allah akadapanda kuwakankha anthu ena kupyolera mwa ena ndiye kuti dziko likadaonongeka. Koma Allah ndi mwini kuchita zabwino pa zolengedwa zonse.[46]
[46] Mneneri Daud adali msirikali m’gulu la nkhondo la mfumu Taluti. Iye adamenya nkhondo ndi cholinga chabwino ndi mwaungwazi zedi mpaka adaipha mfumu ya adaniwo yomwe inkatchedwa Jaluti. Tsono Allah adampatsa ufumu chifukwa chakudzipereka kwakeko.
Tefsiri na arapskom jeziku:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱللَّهِ نَتۡلُوهَا عَلَيۡكَ بِٱلۡحَقِّۚ وَإِنَّكَ لَمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Awa ndi ma Ayah (ndime) a Allah; tikuwawerenga kwa iwe (Mtumiki s.a.w) mwachoonadi. Ndithudi, iwe ndiwe mmodzi mwa atumiki.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ تِلۡكَ ٱلرُّسُلُ فَضَّلۡنَا بَعۡضَهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖۘ مِّنۡهُم مَّن كَلَّمَ ٱللَّهُۖ وَرَفَعَ بَعۡضَهُمۡ دَرَجَٰتٖۚ وَءَاتَيۡنَا عِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ ٱلۡبَيِّنَٰتِ وَأَيَّدۡنَٰهُ بِرُوحِ ٱلۡقُدُسِۗ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا ٱقۡتَتَلَ ٱلَّذِينَ مِنۢ بَعۡدِهِم مِّنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ وَلَٰكِنِ ٱخۡتَلَفُواْ فَمِنۡهُم مَّنۡ ءَامَنَ وَمِنۡهُم مَّن كَفَرَۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا ٱقۡتَتَلُواْ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ يَفۡعَلُ مَا يُرِيدُ
۞ Amenewo ndi aneneri tidawapatsa ulemelero mosiyanitsa pakati pawo, ena kuposa ena. Mwa iwo alipo amene Allah adawalankhula; ndipo ena adawakwezera kwambiri maulemelero awo. Naye Isa (Yesu) mwana wa Mariya tidampatsa zisonyezo zooneka, ndi kumlimbikitsa ndi Mzimu Woyera (rnngelo Gabriel). Allah akadafuna skadamenyana amene adalipo pambuyo pawo, (pa atumikiwo) pambuyo powadzera zizindikiro zooneka, koma adasiyana. Choncho mwa iwo alipo amene adakhulupirira, ndipo ena mwa iwo sadakhulupirire. Ndipo Allah akadafuna, sakadamenyana; koma Allah amachita zimene akufuna.[47]
[47] Ndime iyi ikusonyeza kuti atumiki maulemelero awo ngosiyanasiyana kwa Allah monga momwenso alili anthu ndi angelo ndi zinthu zinanso. Amaposana pakalandiridwe ka ulemelero wawo kwa Allah chifukwa chakusiyana zochita zawo. Zochita za ena nzazikulu zedi kapena zochuluka kwambiri kuposa zochita za anzawo. Ndipo apa Allah watchulapo atatu mwa atumiki akuluakulu omwe ndi:-
(a) Musa amene Allah adayankhula naye ndi kumpatsa zozizwitsa zoonekera.
(b) Ndi mneneri Isa (Yesu) yemwe adampatsa ulemelero waukulu
(c) ndi mneneri Muhammad (s.a.w). Enanso mwa aneneri akuluakulu pali mneneri Ibrahim ndi mneneri Nuh monga momwe ikufotokozera ndime ya chisanu ndi ziwiri (7) yam’surati Ahzab.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَنفِقُواْ مِمَّا رَزَقۡنَٰكُم مِّن قَبۡلِ أَن يَأۡتِيَ يَوۡمٞ لَّا بَيۡعٞ فِيهِ وَلَا خُلَّةٞ وَلَا شَفَٰعَةٞۗ وَٱلۡكَٰفِرُونَ هُمُ ٱلظَّٰلِمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Perekani mwa zimene takupatsani lisanadze tsiku lomwe lilibe kugula (chilichonse chokupulumutsani) ngakhale ubwenzi ngakhalenso dandaulo. Ndipo osakhulupirira ndiwo anthu oipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلۡحَيُّ ٱلۡقَيُّومُۚ لَا تَأۡخُذُهُۥ سِنَةٞ وَلَا نَوۡمٞۚ لَّهُۥ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ مَن ذَا ٱلَّذِي يَشۡفَعُ عِندَهُۥٓ إِلَّا بِإِذۡنِهِۦۚ يَعۡلَمُ مَا بَيۡنَ أَيۡدِيهِمۡ وَمَا خَلۡفَهُمۡۖ وَلَا يُحِيطُونَ بِشَيۡءٖ مِّنۡ عِلۡمِهِۦٓ إِلَّا بِمَا شَآءَۚ وَسِعَ كُرۡسِيُّهُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَۖ وَلَا يَـُٔودُهُۥ حِفۡظُهُمَاۚ وَهُوَ ٱلۡعَلِيُّ ٱلۡعَظِيمُ
Allah palibe wopembedzedwa wina koma Iye, Wamoyo wamuyaya, Woimira ndi Woteteza chilichonse. Kusinza sikumgwira ngakhale tulo. Zonse za kumwamba ndi za pansi nza Iye. Kodi ndani angathe kuombola kwa Iye popanda chilolezo chake? Akudziwa za patsogolo ndi zomwe zili pambuyo pawo ndipo zolengedwazo sizidziwa chilichonse pa zomwe zili m’kudziwa Kwake kupatula chimene wafuna. Mpando wake wachifumu wakwanira kumwamba ndi pansi ndipo sizimamvuta kuzisunga zimenezo. Ndipo Iye (Yekha) Njemwe ali Wapamwambamwamba, Ngwamkulu kwabasi, (Ngolemekezeka kwambiri).[48]
[48] Ndime iyi ikutchedwa Ayat Kursii; ndime yolemekezeka kwambiri. Kwa msilamu aliyense nkofunika kuizindikira bwinobwino ndimeyi kuti azindikire kuti palibe yemwe angamuike patsogolo kapena pambuyo koma lye Allah wapamwambamwamba. Mu hadisi zambiri za Mtumiki akutilimbikitsa kuiwerenga ndimeyi m’malo awa:-
a) tikatha kuchita salamu pa Swala iliyonse ya Faradh
b) tisanagone
c) pamene tikutuluka m’nyumba
d) polowa m’nyumba
e) tikadzazidwa ndi mantha poopa chinthu chomwe tikuchiona ndi chomwe sitikuchiona
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَآ إِكۡرَاهَ فِي ٱلدِّينِۖ قَد تَّبَيَّنَ ٱلرُّشۡدُ مِنَ ٱلۡغَيِّۚ فَمَن يَكۡفُرۡ بِٱلطَّٰغُوتِ وَيُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ فَقَدِ ٱسۡتَمۡسَكَ بِٱلۡعُرۡوَةِ ٱلۡوُثۡقَىٰ لَا ٱنفِصَامَ لَهَاۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
Palibe kukakamiza (munthu kulowa) m’chipembedzo; kulungama kwaonekera poyera kusiyana ndi kusalungama. Choncho amene akumkana satana nakhulupirira Allah, ndiye kuti wagwira chigwiliro cholimba, chomwe sichisweka. Ndipo Allah Ngwakumva; Ngodziwa.[49]
[49] Arabu ena a mu Mzinda wa Madina, Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) asanasamukireko adali kutsata chipembedzo cha Chiyuda. Koma ambiri a iwo adali kupembedza mafano. Pamene chidadza Chisilamu pafupifupi onse omwe ankapembedza mafano adalowa m’ Chisilamu. Koma amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda ndiochepa okha omwe adalowa m’Chisilamu. Ndipo ena ngakhale anali Arabu adatsalirabe m’chipembedzo cha Chiyuda. Choncho, omwe adali asilamu adafuna kukakamiza mwamphamvu amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda kuti alowe m’Chisilamu. Koma Allah adawaletsa kuti palibe kumkakamiza kuti alowe m’Chisilamu yemwe sakufuna. Munthu aliyense adapatsidwa nzeru yomzindikiritsa chabwino ndi choipa. Ngati afuna kusokera nkufuna kwake iye mwini. Ndipo Allah adzamulanga pa tsiku lachimaliziro osati pano padziko lapansi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱللَّهُ وَلِيُّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يُخۡرِجُهُم مِّنَ ٱلظُّلُمَٰتِ إِلَى ٱلنُّورِۖ وَٱلَّذِينَ كَفَرُوٓاْ أَوۡلِيَآؤُهُمُ ٱلطَّٰغُوتُ يُخۡرِجُونَهُم مِّنَ ٱلنُّورِ إِلَى ٱلظُّلُمَٰتِۗ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Allah ndi Mtetezi wa amene akhulupirira, amawatulutsa kumdima ndikuwalowetsa mkuunika, koma amene sadakhulupirire, atetezi awo ndi asatana. Amawatulutsa m’kuunika ndi kuwalowetsa mu mdima; iwo ndi anthu a ku Moto. M’menemo adzakhalamo nthawi yaitali.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِي حَآجَّ إِبۡرَٰهِـۧمَ فِي رَبِّهِۦٓ أَنۡ ءَاتَىٰهُ ٱللَّهُ ٱلۡمُلۡكَ إِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّيَ ٱلَّذِي يُحۡيِۦ وَيُمِيتُ قَالَ أَنَا۠ أُحۡيِۦ وَأُمِيتُۖ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ فَإِنَّ ٱللَّهَ يَأۡتِي بِٱلشَّمۡسِ مِنَ ٱلۡمَشۡرِقِ فَأۡتِ بِهَا مِنَ ٱلۡمَغۡرِبِ فَبُهِتَ ٱلَّذِي كَفَرَۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi sudamve za yemwe adatsutsana ndi Ibrahim pa za Mbuye wake (Allah)? (Ankanyada) pachifukwa chakuti Allah adampatsa ufumu. Ibrahim adati: “Mbuye wanga ndi yemwe amapereka moyo ndi imfa.” Iye adati: “Inenso ndimapereka moyo ndi imfa.” Ibrahim Adati: “Ndithu Allah amatulutsa dzuwa ku vuma, choncho iwe ulitulutse ku zambwe.” Ndipo uja wosakhulupirira adangoti kakasi, (kusowa chonena). Ndipo Allah satsogolera anthu ochita zoipa.[50]
[50] M’nthawi ya mneneri Ibrahim padali mfumu ina yodzikuza yomwe inkadzitcha kuti ndimulungu ndipo anthu ake adali kuipembedza. Pamene mneneri Ibrahim adadza nayamba kuphunzitsa chipembedzo choona ndikuti iyeyo si mulungu, mfumuyo idati kwa mneneri Ibrahim: “Kodi Mulungu wako woonayo amachita chiyani?” Iye adati “Amapereka moyo ndi kuperekanso imfa.” Mfumuyo idachita ngati sidamvetse cholinga cha mawu a mneneri Ibrahim. Idati: “Nanenso ndimachita zimenezo. Taona mmene ndimachitira.” Pompo adalamula kuti abwere nawo anthu awiri omwe adawalamula kuti aphedwe. Iye adalamula kuti mmodzi aphedwe ndipo winayo amsiye. Choncho zidachitika. Tsono adamuuza Ibrahim: “Waona bwanji? Kodi wina sindidampatse moyo ndipo winayo imfa?” Mneneri Ibrahim pomwe anaona kuti mfumuyo ikungodzipusitsa daladala adaiuza chinthu chomwe iyo sikadatha kuchichita. Adati: “Allah amatulutsa dzuwa ku vuma ndipo iwe ulitulutse ku zambwe.” Pamenepo mfumuyo idangoti kakasi, sidachite chilichonse ndiponso sidanene chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَوۡ كَٱلَّذِي مَرَّ عَلَىٰ قَرۡيَةٖ وَهِيَ خَاوِيَةٌ عَلَىٰ عُرُوشِهَا قَالَ أَنَّىٰ يُحۡيِۦ هَٰذِهِ ٱللَّهُ بَعۡدَ مَوۡتِهَاۖ فَأَمَاتَهُ ٱللَّهُ مِاْئَةَ عَامٖ ثُمَّ بَعَثَهُۥۖ قَالَ كَمۡ لَبِثۡتَۖ قَالَ لَبِثۡتُ يَوۡمًا أَوۡ بَعۡضَ يَوۡمٖۖ قَالَ بَل لَّبِثۡتَ مِاْئَةَ عَامٖ فَٱنظُرۡ إِلَىٰ طَعَامِكَ وَشَرَابِكَ لَمۡ يَتَسَنَّهۡۖ وَٱنظُرۡ إِلَىٰ حِمَارِكَ وَلِنَجۡعَلَكَ ءَايَةٗ لِّلنَّاسِۖ وَٱنظُرۡ إِلَى ٱلۡعِظَامِ كَيۡفَ نُنشِزُهَا ثُمَّ نَكۡسُوهَا لَحۡمٗاۚ فَلَمَّا تَبَيَّنَ لَهُۥ قَالَ أَعۡلَمُ أَنَّ ٱللَّهَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٞ
Kapena ngati fanizo la uja amene adadutsa pafupi ndi mudzi umene madenga ndi zipupa zake zidaphwasuka (udaferatu) adati: “Kodi Allah adzaukitsa chotani mudzi uwu pambuyo pakufa kwake?” Ndipo Allah adampatsa imfa kwa nthawi yokwana zaka zana limodzi (100), kenako adamuukitsa namufunsa: “Kodi wakhala nyengo yaitali bwanji?” Adati: “Ndakhala nthawi yatsiku limodzi, kapena theka latsiku.” (Allah) adati: “Korna wakhala zaka zana limodzi, ndipo ona chakudya chako ndi zakumwa zako, sizinaonongeke (sizinavunde). Ndipo yang’ana bulu wako (ali mafupa okhaokha oyoyoka); ndi kuti ukhale chisonyezo kwa anthu, (nchifukwa chake takuukitsa ku imfa). Ndipo yang’ana mafupa (a bulu wako) momwe tingawaukitsire, kenako nkumaaveka minofu.” Choncho pamene zidazindikirika (kwa iye, woukitsidwayo), adati: “Ndikudziwa kuti Allah Ngokhoza chilichonse.”[51]
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّ أَرِنِي كَيۡفَ تُحۡيِ ٱلۡمَوۡتَىٰۖ قَالَ أَوَلَمۡ تُؤۡمِنۖ قَالَ بَلَىٰ وَلَٰكِن لِّيَطۡمَئِنَّ قَلۡبِيۖ قَالَ فَخُذۡ أَرۡبَعَةٗ مِّنَ ٱلطَّيۡرِ فَصُرۡهُنَّ إِلَيۡكَ ثُمَّ ٱجۡعَلۡ عَلَىٰ كُلِّ جَبَلٖ مِّنۡهُنَّ جُزۡءٗا ثُمَّ ٱدۡعُهُنَّ يَأۡتِينَكَ سَعۡيٗاۚ وَٱعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo (kumbukira) pamene Ibrahim adati: “E Mbuye wanga!, Ndionetseni mmene mudzaaukitsire akufa.” (Allah) adati: “Kodi sunakhulupirirebe?” Adati: “Iyayi, (ndikukhulupirira), koma (ndikufuna kuona zimenezo) kuti mtima wanga ukhazikike.” (Allah) adati: “Choncho katenge mbalame zinayi; uzisonkhanitse kwa iwe (mpaka uyizindikire mbalame iliyonse mmene ilili, ndipo kenako uziduledule zonsezo zidutswazidutswa ndikuzisakaniza ndi kuzigawa mzigawo zinayi). Ndipo paphiri lililonse ukaikepo gawo limodzi la zimenezo, ndipo kenako uziitane. Zikudzera zikuthamanga. Ndipo dziwa kuti Allah ndi Mwini mphamvu zoposa, Ngwanzem zakuya.”[52]
[52] Mneneri Ibrahim adalakalaka kuti aone mmene akufa adzaukira kuti chikhulupiliro chake chiwonjezeke mphamvu. Tero Allah adamulamula kuti azinge mbalame zinayi zosiyanasiyana mitundu. Kenako azisakanize ziwalo zake. Ziwalo za mbalame ina zilowe kumbalame ina. Tsono azigawe miyulu inayi. Mulu uliwonse akauike pa phiri lakelake. Kenako aziitane mbalame zija. Ndipo aona kuti chiwalo chilichonse chikuthamangira kumbalame yake, pompo zonsezo zikhalanso mbalame zamoyo monga momwe zidalili poyamba.
Tefsiri na arapskom jeziku:
مَّثَلُ ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ كَمَثَلِ حَبَّةٍ أَنۢبَتَتۡ سَبۡعَ سَنَابِلَ فِي كُلِّ سُنۢبُلَةٖ مِّاْئَةُ حَبَّةٖۗ وَٱللَّهُ يُضَٰعِفُ لِمَن يَشَآءُۚ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٌ
Fanizo la amene akupereka chuma chawo pa njira ya Allah lili ngati fanizo la njere imodzi yomwe yatulutsa ngala zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala iliyonse nkukhalamo njere zana limodzi. Ndipo Allah amamuonjezera amene wamfuna (kuposera pamenepa). Ndipo Allah alinazo zambiri, Ngodziwa.[53]
[53] (Ndime 261-267) zikulimbikitsa kupereka chuma pa njira zabwino ndiponso zikuonetsa ubwino umene woperekayo amalandira kwa Allah. Komatu woperekayo kuti apeze ubwino wa Allah pafunika izi:
(a) apereke chifukwa cha Allah osati ncholinga chodzionetsera kwa anthu,
(b) choperekacho chikhale chabwino. Ngati wapereka zomwe sizabwino ndiye kuti sangapeze mphoto yaikulu,
(c) asawakumbe amene akuwapatsawo.
(d) Asawavutitse. Ndipo ngati atachita zimenezi ndiye kuti sangapeze mphoto koma kungotaya chuma pachabe. Kumbwezera mawu abwino wopempha nkopindulitsa kuposa sadaka yotonzera.
(e) Chimene akuperekacho chikhale chaHalali (chololedwa).Osati chomwe adachipeza m’njira yosavomerezeka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ثُمَّ لَا يُتۡبِعُونَ مَآ أَنفَقُواْ مَنّٗا وَلَآ أَذٗى لَّهُمۡ أَجۡرُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
(Anthu) amene akupereka chuma chawo pa njira ya Allah napanda kutsatiza pa zomwe aperekazo kukumba, ndiponso masautso, iwo ali ndi mphoto kwa Mbuye wawo ndipo pa iwo sipadzakhala mantha; ndiponso sadzadandaula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ قَوۡلٞ مَّعۡرُوفٞ وَمَغۡفِرَةٌ خَيۡرٞ مِّن صَدَقَةٖ يَتۡبَعُهَآ أَذٗىۗ وَٱللَّهُ غَنِيٌّ حَلِيمٞ
Mawu abwino, ndi kukhululukira (amene wakulakwira) nzabwino zedi kuposa sadaka yotsatizidwa ndi masautso. Ndipo Allah ndiyemwe ali Wolemera kwambiri ndiponso Woleza (kwa zolengedwa Zake).
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تُبۡطِلُواْ صَدَقَٰتِكُم بِٱلۡمَنِّ وَٱلۡأَذَىٰ كَٱلَّذِي يُنفِقُ مَالَهُۥ رِئَآءَ ٱلنَّاسِ وَلَا يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۖ فَمَثَلُهُۥ كَمَثَلِ صَفۡوَانٍ عَلَيۡهِ تُرَابٞ فَأَصَابَهُۥ وَابِلٞ فَتَرَكَهُۥ صَلۡدٗاۖ لَّا يَقۡدِرُونَ عَلَىٰ شَيۡءٖ مِّمَّا كَسَبُواْۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Musaononge sadaka zanu pokumba ndiponso popereka masautso, monga yemwe akupereka chuma chake modzionetsera kwa anthu, ndipo sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro. Choncho fanizo lake lili ngati thanthwe lomwe pamwamba pake pali dothi. Kenako nkulifikira chimvula (nkuchotsa dothi lonse lija), nkulisiya lopanda kanthu. Tero sadzatha kupeza chilichonse pazimene adachita. Ndipo Allah satsogolera anthu osakhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَثَلُ ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُمُ ٱبۡتِغَآءَ مَرۡضَاتِ ٱللَّهِ وَتَثۡبِيتٗا مِّنۡ أَنفُسِهِمۡ كَمَثَلِ جَنَّةِۭ بِرَبۡوَةٍ أَصَابَهَا وَابِلٞ فَـَٔاتَتۡ أُكُلَهَا ضِعۡفَيۡنِ فَإِن لَّمۡ يُصِبۡهَا وَابِلٞ فَطَلّٞۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٌ
Ndipo fanizo la anthu amene akupereka chuma chawo chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah ndi kulimbikitsa mitima yawo (pa chipembedzo cha Allah) lili ngati fanizo la munda umene uli pachitunda, chiufikira chimvula tero nubweretsa zinthu zake dzochuluka moonjeza kawiri (kuposera pachikhalidwe chake). Ndipo ngati chimvula sichidaudzere, ndiye kuti yamawawa (nkuukwanira mundawo). Ndipo Allah akuona zonse zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَيَوَدُّ أَحَدُكُمۡ أَن تَكُونَ لَهُۥ جَنَّةٞ مِّن نَّخِيلٖ وَأَعۡنَابٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ لَهُۥ فِيهَا مِن كُلِّ ٱلثَّمَرَٰتِ وَأَصَابَهُ ٱلۡكِبَرُ وَلَهُۥ ذُرِّيَّةٞ ضُعَفَآءُ فَأَصَابَهَآ إِعۡصَارٞ فِيهِ نَارٞ فَٱحۡتَرَقَتۡۗ كَذَٰلِكَ يُبَيِّنُ ٱللَّهُ لَكُمُ ٱلۡأٓيَٰتِ لَعَلَّكُمۡ تَتَفَكَّرُونَ
Kodi mmodzi wa inu angakonde kukhala ndi munda wa mitengo ya kanjedza ndi mphesa womwe pansi pake mitsinje ikuyenda, iye mmenemo napeza dzinthu dzamitundumitundu, numpeza ukalamba uku ali ndi ana ofooka; ndipo kamvuluvulu wa moto naugwera (mundawo), nupseleratu (angazikonde zimenezi)? Umo ndimomwe Allah akukulongosolerani ma Ayah (ndime za mawu Ake) kuti muganizire.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَنفِقُواْ مِن طَيِّبَٰتِ مَا كَسَبۡتُمۡ وَمِمَّآ أَخۡرَجۡنَا لَكُم مِّنَ ٱلۡأَرۡضِۖ وَلَا تَيَمَّمُواْ ٱلۡخَبِيثَ مِنۡهُ تُنفِقُونَ وَلَسۡتُم بِـَٔاخِذِيهِ إِلَّآ أَن تُغۡمِضُواْ فِيهِۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ غَنِيٌّ حَمِيدٌ
E inu amene mwakhulupirira! Perekani zabwino zochokera m’zimene mwapeza ndi zimene takutulutsirani m’nthaka, ndipo musalinge kupereka choipa chomwe inu simukadachilandira (ngati akanakupatsani) pokhapokha mochitsinzinira. (Nanga Allah ndiye alandire choipacho)? Ndipo dziwani kuti Allah Ngolemera (ndiponso) Ngotamandidwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلشَّيۡطَٰنُ يَعِدُكُمُ ٱلۡفَقۡرَ وَيَأۡمُرُكُم بِٱلۡفَحۡشَآءِۖ وَٱللَّهُ يَعِدُكُم مَّغۡفِرَةٗ مِّنۡهُ وَفَضۡلٗاۗ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٞ
Satana amakuopsezani ndi umphawi ndi kukulamulirani kuchita zoipa (monga umbombo), pomwe Allah akukulonjezani chikhululuko kuchokera kwa Iye ndi ubwino (waukulu ngati mupereka); ndipo Allah ali nazo zambiri, Ngodziwa.[54]
[54] (Ndime 268-271) apa Allah akuwalimbikitsa mtima amene akupereka kuti panthawi iliyonse pamene akupereka Allah adzawaonjezera. Ndipo akuwachenjeza kuti asamamvetsere udyerekezi wa satana umene amauthira m’mitima yawo powauza kuti: “Ngati mupereka, musauka.” Koma Allah akuwauza kuti: “Perekani simusauka. M’malomwake mupeza bwino pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro.”
M’ndime zomwezi Allah wafotokoza za (lonjezo) “naziri” kuti naziri iliyonse imene tikumlonjeza Allah akuidziwa.
Mawu oti “Naziri” nga Chiarabu. M’chichewa akuthandauza kuti, “ndikapeza chakuti ndidzachita chakutichakuti,” “kapena kuti, akachira m’bale wanga ndidzapereka chakutichakuti kwa Allah.”
Mawu anaziriwa siabwino pa malamulo a Chisilamu, ngakhale kuti anthu ambiri amakonda kuchita naziri poganizira kuti akatero Allah awayankha mwachangu namaganiziranso kuti naziri nchinthu chabwino m’Chisilamu pomwe chili chosafunika m’Chisilamu.
Kusafunika kwa naziri m’Chisilamu kuli kotere: Umati: “Allah akandichitira chakutichakuti inenso ndichita chakutichakuti.” Mawu oterewa sali mawu abwino ndiponso akusonyeza kupanda mwambo ndiponso akusonyeza umbombo.
Chifukwa chakuti munthu ofuna kupereka kanthu sanganene kuti: “Muyambe mwandichitira chakuti ndipo ndikupatsani.” Koma ngakhale zili choncho akwaniritsebe malonjezowo. Koma ngati malonjezowo ali pa chinthu choletsedwa asawakwaniritse, ndipo m’malo mwake apereke dipo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يُؤۡتِي ٱلۡحِكۡمَةَ مَن يَشَآءُۚ وَمَن يُؤۡتَ ٱلۡحِكۡمَةَ فَقَدۡ أُوتِيَ خَيۡرٗا كَثِيرٗاۗ وَمَا يَذَّكَّرُ إِلَّآ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Amapatsa nzeru (zothandiza) amene wamfuna; ndipo amene wapatsidwa nzeru, ndithudi, wapatsidwa zabwino zambiri. Ndipo (zoterezi) sakumbukira koma eni nzeru okha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَآ أَنفَقۡتُم مِّن نَّفَقَةٍ أَوۡ نَذَرۡتُم مِّن نَّذۡرٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُهُۥۗ وَمَا لِلظَّٰلِمِينَ مِنۡ أَنصَارٍ
Ndipo chilichonse chomwe mungapereke kapena naziri (lonjezo) iliyonse yomwe mwalonjeza Allah, ndithudi, Allah akudziwa zonsezi. Ndipo anthu ochita zoipa sadzakhala ndi athandizi.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِن تُبۡدُواْ ٱلصَّدَقَٰتِ فَنِعِمَّا هِيَۖ وَإِن تُخۡفُوهَا وَتُؤۡتُوهَا ٱلۡفُقَرَآءَ فَهُوَ خَيۡرٞ لَّكُمۡۚ وَيُكَفِّرُ عَنكُم مِّن سَيِّـَٔاتِكُمۡۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٞ
Ngati mupereka sadaka moonetsera, ndibwino; ngati mungaipereke mobisa, ndikuipereka kwa osauka, umenewo ndiubwino woposa kwa inu. Ndipo akufafanizirani zoipa zanu (ngati mutero). Ndipo Allah akudziwa zonse zimene mukuchita.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ لَّيۡسَ عَلَيۡكَ هُدَىٰهُمۡ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ يَهۡدِي مَن يَشَآءُۗ وَمَا تُنفِقُواْ مِنۡ خَيۡرٖ فَلِأَنفُسِكُمۡۚ وَمَا تُنفِقُونَ إِلَّا ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ ٱللَّهِۚ وَمَا تُنفِقُواْ مِنۡ خَيۡرٖ يُوَفَّ إِلَيۡكُمۡ وَأَنتُمۡ لَا تُظۡلَمُونَ
Siudindo wako kuwaongola, koma Allah amamuongola amene wamfuna, (udindo wako nkulalikira kokha). Ndipo chuma chilichonse chimene mungachipereke, (phindu lake) lili pa inu eni, ndipo musapereke pokhapokha pofunafuna chikondi cha Allah. Ndipo chuma chilichonse chimene mungachipereke adzakubwezerani mokwanira (mphoto yake), ndipo simudzaponderezedwa.[55]
[55] Apa akumuuza Mtumiki (s.a.w) pamodzi ndi aliyense wolamula kuchita zabwino ndikuletsa kuchita zoipa kuti udindo wawo nkufikitsa uthengawo. Pa iwo palibe vuto ngati anthuwo savomereza, iwo adzapezabe mphoto yolamulira zabwino ndikuletsa zoipa ngakhale kuti sanawatsatire.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لِلۡفُقَرَآءِ ٱلَّذِينَ أُحۡصِرُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ لَا يَسۡتَطِيعُونَ ضَرۡبٗا فِي ٱلۡأَرۡضِ يَحۡسَبُهُمُ ٱلۡجَاهِلُ أَغۡنِيَآءَ مِنَ ٱلتَّعَفُّفِ تَعۡرِفُهُم بِسِيمَٰهُمۡ لَا يَسۡـَٔلُونَ ٱلنَّاسَ إِلۡحَافٗاۗ وَمَا تُنفِقُواْ مِنۡ خَيۡرٖ فَإِنَّ ٱللَّهَ بِهِۦ عَلِيمٌ
(Sadakazo ziperekedwe) kwa amphawi amene atsekerezedwa pa njira ya Allah, amene sangathe kuyenda pa dziko (kukachita ntchito yopezera zofunika pamoyo wawo). Amene sadziwa za chikhalidwe chawo, amawaganizira kuti ngolemera chifukwa chakudziletsa kwawo (kupemphapempha). Ungawazindikire (kuti ngosowedwa) ndi zizindikiro zawo. Sapempha anthu mwaliuma. Ndipo chabwino chilichonse chimene mukupereka, ndithudi, Allah ali Wodziwa za icho.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يُنفِقُونَ أَمۡوَٰلَهُم بِٱلَّيۡلِ وَٱلنَّهَارِ سِرّٗا وَعَلَانِيَةٗ فَلَهُمۡ أَجۡرُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Amene akupereka chuma chawo usiku ndi usana, mobisa ndi moonekera, ali ndi malipiro awo kwa Mbuye wawo; ndipo pa iwo sipadzakhala mantha, ndiponso sadzadandaula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱلَّذِينَ يَأۡكُلُونَ ٱلرِّبَوٰاْ لَا يَقُومُونَ إِلَّا كَمَا يَقُومُ ٱلَّذِي يَتَخَبَّطُهُ ٱلشَّيۡطَٰنُ مِنَ ٱلۡمَسِّۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ قَالُوٓاْ إِنَّمَا ٱلۡبَيۡعُ مِثۡلُ ٱلرِّبَوٰاْۗ وَأَحَلَّ ٱللَّهُ ٱلۡبَيۡعَ وَحَرَّمَ ٱلرِّبَوٰاْۚ فَمَن جَآءَهُۥ مَوۡعِظَةٞ مِّن رَّبِّهِۦ فَٱنتَهَىٰ فَلَهُۥ مَا سَلَفَ وَأَمۡرُهُۥٓ إِلَى ٱللَّهِۖ وَمَنۡ عَادَ فَأُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Amene akudya riba (chuma cha katapira) sadzauka (m’manda) koma monga momwe amaimira munthu okhudzidwa ndi ziwanda, mwamisala. (Ndipo) izi nchifukwa chakuti amanena: “Malonda ngolingana ndi katapira,” pomwe Allah waloleza malonda ndipo waletsa katapira. Ndipo amene wamufika ulaliki wochokera kwa Mbuye wake (woletsa katapira) nasiya, choncho chomwe chidapita nchake. Ndipo chiweruzo chake chili kwa Allah (akaona chochita naye). Koma amene abwerera (kuchita malonda a katapira), amenewo ndiwo anthu a ku Moto, mmenemo adzakhalamo nthawi yaitali.[56]
[56] Ndime iyi yikuletsa kukongoza m’njira yakatapira. Allah akumuopseza mwamphamvu munthu wodya riba. Akumuuza kuti adziwe kuti ali pankhondo yolimbana ndi Allah. Allah akukalipa zedi kwa anthu ochita malonda akatapira. Tero pewani kuchita malonda akatapira.. Kodi inu muli ndi nyonga zomenyerana ndi Allah?
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَمۡحَقُ ٱللَّهُ ٱلرِّبَوٰاْ وَيُرۡبِي ٱلصَّدَقَٰتِۗ وَٱللَّهُ لَا يُحِبُّ كُلَّ كَفَّارٍ أَثِيمٍ
Allah amachotsa madalitso pa (chuma cha) katapira ndipo amaika madalitso pa chaulere. Ndipo Allah sakonda aliyense wosakhulupirira, wamachimo ambiri.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَوُاْ ٱلزَّكَوٰةَ لَهُمۡ أَجۡرُهُمۡ عِندَ رَبِّهِمۡ وَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Ndithudi, amene akhulupirira, nachita zabwino, napemphera Swala moyenera ndi kupereka chopereka (Zakaat), iwo akapeza malipiro awo kwa Mbuye wawo. Ndipo pa iwo sipadzakhala mantha ndiponso sadzadandaula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَذَرُواْ مَا بَقِيَ مِنَ ٱلرِّبَوٰٓاْ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah, ndipo siyani zimene zatsalira m’katapira, ngati inu mulidi okhulupirira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَإِن لَّمۡ تَفۡعَلُواْ فَأۡذَنُواْ بِحَرۡبٖ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦۖ وَإِن تُبۡتُمۡ فَلَكُمۡ رُءُوسُ أَمۡوَٰلِكُمۡ لَا تَظۡلِمُونَ وَلَا تُظۡلَمُونَ
Ngati simuchita (zimenezo), dziwani kuti mukulimbana ndi Allah ndi Mtumiki Wake. Ndipo ngati mulapa, maziko a chuma chanu ndi anu. Musapondereze, ndiponso musaponderezedwe.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِن كَانَ ذُو عُسۡرَةٖ فَنَظِرَةٌ إِلَىٰ مَيۡسَرَةٖۚ وَأَن تَصَدَّقُواْ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
Ndipo ngati wokongola ali ndi mavuto, choncho (wokongoza) amdikire mpaka apeze bwino. Koma ngati inu (okongoza mungakhululuke pakusiya kuitanitsa ngongole) muisintha kuti ikhale sadaka, ndibwino kwa inu ngati mukudziwa (zimenezo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱتَّقُواْ يَوۡمٗا تُرۡجَعُونَ فِيهِ إِلَى ٱللَّهِۖ ثُمَّ تُوَفَّىٰ كُلُّ نَفۡسٖ مَّا كَسَبَتۡ وَهُمۡ لَا يُظۡلَمُونَ
Ndipo liopeni tsiku lomwe inu mudzabwezedwa kwa Allah. Ndipo kenako munthu aliyense adzalipidwa mokwanira pa zonse zimene adachita (ndi manja ake), ndipo iwo sadzaponderezedwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا تَدَايَنتُم بِدَيۡنٍ إِلَىٰٓ أَجَلٖ مُّسَمّٗى فَٱكۡتُبُوهُۚ وَلۡيَكۡتُب بَّيۡنَكُمۡ كَاتِبُۢ بِٱلۡعَدۡلِۚ وَلَا يَأۡبَ كَاتِبٌ أَن يَكۡتُبَ كَمَا عَلَّمَهُ ٱللَّهُۚ فَلۡيَكۡتُبۡ وَلۡيُمۡلِلِ ٱلَّذِي عَلَيۡهِ ٱلۡحَقُّ وَلۡيَتَّقِ ٱللَّهَ رَبَّهُۥ وَلَا يَبۡخَسۡ مِنۡهُ شَيۡـٔٗاۚ فَإِن كَانَ ٱلَّذِي عَلَيۡهِ ٱلۡحَقُّ سَفِيهًا أَوۡ ضَعِيفًا أَوۡ لَا يَسۡتَطِيعُ أَن يُمِلَّ هُوَ فَلۡيُمۡلِلۡ وَلِيُّهُۥ بِٱلۡعَدۡلِۚ وَٱسۡتَشۡهِدُواْ شَهِيدَيۡنِ مِن رِّجَالِكُمۡۖ فَإِن لَّمۡ يَكُونَا رَجُلَيۡنِ فَرَجُلٞ وَٱمۡرَأَتَانِ مِمَّن تَرۡضَوۡنَ مِنَ ٱلشُّهَدَآءِ أَن تَضِلَّ إِحۡدَىٰهُمَا فَتُذَكِّرَ إِحۡدَىٰهُمَا ٱلۡأُخۡرَىٰۚ وَلَا يَأۡبَ ٱلشُّهَدَآءُ إِذَا مَا دُعُواْۚ وَلَا تَسۡـَٔمُوٓاْ أَن تَكۡتُبُوهُ صَغِيرًا أَوۡ كَبِيرًا إِلَىٰٓ أَجَلِهِۦۚ ذَٰلِكُمۡ أَقۡسَطُ عِندَ ٱللَّهِ وَأَقۡوَمُ لِلشَّهَٰدَةِ وَأَدۡنَىٰٓ أَلَّا تَرۡتَابُوٓاْ إِلَّآ أَن تَكُونَ تِجَٰرَةً حَاضِرَةٗ تُدِيرُونَهَا بَيۡنَكُمۡ فَلَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٌ أَلَّا تَكۡتُبُوهَاۗ وَأَشۡهِدُوٓاْ إِذَا تَبَايَعۡتُمۡۚ وَلَا يُضَآرَّ كَاتِبٞ وَلَا شَهِيدٞۚ وَإِن تَفۡعَلُواْ فَإِنَّهُۥ فُسُوقُۢ بِكُمۡۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَۖ وَيُعَلِّمُكُمُ ٱللَّهُۗ وَٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Mukamakongozana ngongole kwa nyengo yodziwika ilembeni. Ndipo mlembi pakati panu alembe mwachilungamo; ndipo mlembi asakane kulemba monga momwe Allah wamphunzitsira; choncho alembe. Ndipo alakatule (mawu olembedwawo ndi wokongolayo) yemwe ngongole ili pa iye. Nayenso aope Allah, Mbuye wake, ndipo asapungule chilichonse m’menemo (m’ngongole). Ndipo ngati wokongola ndiozelezeka kapena wofooka, kapena iye mwini sangathe kulembetsa (momveka), choncho amulembetsere myang’aniri (wakili) wake (yemwe akuyang’anira zinthu zake) mwachilungamo. Ndipo funiraponi mboni ziwiri zochokera mwa anthu anu aamuna (asilamu). Koma ngati amuna awiri palibe, choncho apezeke mwamuna mmodzi ndi akazi awiri (kuti aikire umboniwo), amene mumavomereza kukhala mboni kuti ngati mmodzi mwa iwo (akazi awiriwo) angaiwale mmodzi wawo akumbutse winayo. Ndipo mboni zisakane zikaitanidwa. Ndiponso musanyozere kulemba (ngongoleyo) yaing’ono kapena yaikulu mpaka nyengo yake. Zimenezo (kulembako) ndibwino kwa Allah, ndipo ncholungama zedi kumbali yaumboni, ndiponso nchothandiza kuti musakhale ndi chipeneko. Koma akakhala malonda omwe ali pompo omwe mukupatsana pakati panu (tsintho) sikulakwa kwa inu kusawalemba. Koma funani mboni pamene mukugulitsana. Komatu asavutitsidwe mlembi ndiponso mboni. Ngati mutachita zimenezo (zoletsedwazo) kumeneko ndiko kutuluka (m’chilamulo cha Mulungu wanu), ndipo opani Allah, Allah akukuphunzitsani. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.[57]
[57] Apa akuwalimbikitsa anthu kuti azilemba akamakongozana zinthu kuti pasakhale mkangano ndikukanirana kuti sanakongozane. Ngakhale ngongoleyo ikhale yochepa pafunika ndithu kulemba. Ndipo polembetsa ngongoleyo wokongolayo ndiye adzinena mawu olembedwawo poopa kuti akayankhula wokongoza akhoza kuonjeza mawu ndipo wokongola nkuchita manyazi kumbweza pakuti mkono wopempha ngwapansi pomwe wopereka ngwapamwamba. Ndipo pamene wolemba akuuzidwa kuti asawakanire kuwalembera osadziwa kulemba, akutanthauza kuti anthu azithandizana pakati pawo. Ndipo olemba akuwalangizanso kuti alembe zokhazo zomwe akuuzidwa ndipo afunirepo mboni zotsimikiza kuti alembadi. Ndipo mbonizo zisainire pamenepo. Oikira umboni afunika kukhala amuna awiri a Chisilamu. Ngati palibe amuna awiriwo, mmalo mwa mwamuna mmodzi zilowe mboni ziwiri zachikazi chifukwa chikumbumtima cha akazi nchochepa poyerekeza ndi cha amuna.Ndipo anthu akuwauzanso kuti akawapempha kuti aikire umboni pa chinthu asakane. Kuikira umboni ndi ntchito yabwino yotsimikizira choona ndi kukana chonama. Koma pa malonda ogulitsana dzanja ndi dzanja sipafunika kulemba koma pamangofunika mboni basi. Ndipo pomwe kwanenedwa kuti: “Asavutitsidwe olembawo ndi oikira umboniwo,’’ akusonyeza kuti ngati ntchito yolembayo ndi kuikira umboniwo nzotenga nthawi yaitali kotero kuti olembawo ndi mbonizo iwachedwetsera ntchito zawo zomwe amapezera zowathandiza pa moyo wawo, ayenera kuwalipira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَإِن كُنتُمۡ عَلَىٰ سَفَرٖ وَلَمۡ تَجِدُواْ كَاتِبٗا فَرِهَٰنٞ مَّقۡبُوضَةٞۖ فَإِنۡ أَمِنَ بَعۡضُكُم بَعۡضٗا فَلۡيُؤَدِّ ٱلَّذِي ٱؤۡتُمِنَ أَمَٰنَتَهُۥ وَلۡيَتَّقِ ٱللَّهَ رَبَّهُۥۗ وَلَا تَكۡتُمُواْ ٱلشَّهَٰدَةَۚ وَمَن يَكۡتُمۡهَا فَإِنَّهُۥٓ ءَاثِمٞ قَلۡبُهُۥۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ عَلِيمٞ
Ndipo ngati muli pa ulendo, ndipo simudapeze mlembi, choncho (wokongoza) apatsidwe chikole (pinyolo) m’manja mwake. Ngati wina wasungitsa mmodzi wa inu chinthu (pomudalira wokhulupirika) choncho amene wayesedwa wokhulupirikayo abweze chinthucho kwa mwini wake, ndipo aope Allah, Mbuye wake. Ndipo musabise umboni (ngakhale uli wokuipirani). Ndipo amene abise ndiye kuti mu mtima mwake mwalowa uchimo; ndipo Allah akudziwa zonse zimene mukuchita.[58]
[58] Apa akunena kuti ngati anthu ali pamalo pomwe palibe wodziwa kulemba ndipo akukongozana, wokongozedwayo apereke chikole kwa wokongoza kuti achisunge wokongozayo. Ndipo adzabwezera akadzabweza ngongoleyo. Ngati atalephera kubweza ngongoleyo chikolecho chigulitsidwe ndi muweruzi nkumpatsa wokongozayo ndalama zolingana nzomwe adamkongoza. Zotsalira pa chinthu chogulitsidwacho azipereke kwa mwini chikolecho. Uwu ndiwo ubwino wachikole pa malamulo a Chisilamu. Akalephera kubweza ngongoleyo chinthucho chimagulitsidwa ndi boma ndikumpatsa mwini ngongoleyo choyenerana naye pomwe chotsaliracho amachipereka kwa mwini wake. Kwa amene wagwirizira chikolecho saloledwa kuchita nacho chilichonse. Ngati akuchita nacho ntchito nkumachidyelera ndiye kuti akuchita machitidwe akatapira omwe ali oletsedwa. Koma chinthucho angochisunga.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لِّلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۗ وَإِن تُبۡدُواْ مَا فِيٓ أَنفُسِكُمۡ أَوۡ تُخۡفُوهُ يُحَاسِبۡكُم بِهِ ٱللَّهُۖ فَيَغۡفِرُ لِمَن يَشَآءُ وَيُعَذِّبُ مَن يَشَآءُۗ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ
Zonse zakumwamba ndi zapansi nza Allah. Kaya muonetsera poyera zomwe zili m’mitima mwanu kapena kuzibisa, Allah adzakuchitirani nazo chiwerengero. Kenako adzakhululukira amene wamfuna (atalapa). Ndipo adzamlanga amene wamfuna (akapanda kulapa). Ndipo Allah Ngokhoza chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
ءَامَنَ ٱلرَّسُولُ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡهِ مِن رَّبِّهِۦ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَۚ كُلٌّ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَمَلَٰٓئِكَتِهِۦ وَكُتُبِهِۦ وَرُسُلِهِۦ لَا نُفَرِّقُ بَيۡنَ أَحَدٖ مِّن رُّسُلِهِۦۚ وَقَالُواْ سَمِعۡنَا وَأَطَعۡنَاۖ غُفۡرَانَكَ رَبَّنَا وَإِلَيۡكَ ٱلۡمَصِيرُ
Mtumiki wakhulupirira zimene zavumbulutsidwa kwa iye kuchokera kwa Mbuye wake. Naonso asilamu (akhulupirira). Onse akhulupirira Allah, angelo Ake, mabuku Ake ndi atumiki Ake. (Iwo pamodzi ndi Mtumiki wawoyo akunena kuti): “Sitingalekanitse aliyense pakati pa atumiki Ake, (onse tikuwakhulupirira).” Ndipo akunena: “Tamva ndiponso tamvera, (choncho tikukupemphani) chikhululuko chanu. E Mbuye wathu! Ndipo kwa Inu nkobwerera.”[59]
[59] (Ndime 285-286) ndime ziwirizi zili ndi ubwino ndi madalitso ambiri monga momwe ilili ndime ya Ayatu Kursii yanambala 255 m’sura yomweyi.
Akutilangiza kuziwerenga ndimezi m’malo monse momwe Ayatu Kursii imawerengedwa. Qur’an yonse ikuphunzitsa asilamu kuti asasiyanitse pakati pa aneneri. Koma awavomereze onse ndi kuwakhulupilira amene adadza patsogolo pa Mtumiki Muhammad (s.a.w). Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndiye womaliza mwa aneneriwo. Ndipo amadziwika ndi dzina lakuti “Khatamu nNabiyyina’’ “womaliza mwa Aneneri.” Ndipo amene sakhulupilira kuti Muhammad (s.a.w) ngomaliza mwa aneneri nakhulupilira munthu wamba yemwe akungodzinamiza kuti iye ndi mneneri, monga momwe chikhulupiliro cha Akadiyani chilili ndiye kuti iyeyo watuluka m’Chisilamu ndipo ndi munthu wakunja.
Asilamu sakana mneneri aliyense mwa Aneneri omwe adalipo Mtumiki Muhammad (s.a.w) asanadze. Koma iwo amakhulupilira kuti malamulo akayendetsedwe ka zipembedzo zawo kadafafanizidwa chifukwa chakudza kwa mtumiki Muhammad (s.a.w). Nyengo ino ndinyengo yotsatira mtumiki Muhammad (s.a.w) pazochitachita. Koma pazinthu zokhudza chikhulupiliro, Aneneri onse adadza ndi lamulo limodzi monga momwe Allah akufotokozera m’ndime ya 13, Sûrat Shura.
Ndipo m’ndime zimenezi za 285 ndi 286 zikuphunzitsanso miyambo ya Chisilamu ndi mapemphero (maduwa) momwe tingampemphere Allah. Ndimezi zikufotokoza za chisomo cha Allah chomwe chili pa ife anthu Ake kuti Allah sakakamiza koma chimene angathe kuchichita akapolo Ake. Ndiponso sawalanga ngati atachita zinthu molakwitsa kapena moiwala.
Ndime ziwirizi zikusonyeza makhalidwe a Asilamu ndi zinthu zawo zimene amazikhulupilira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَا يُكَلِّفُ ٱللَّهُ نَفۡسًا إِلَّا وُسۡعَهَاۚ لَهَا مَا كَسَبَتۡ وَعَلَيۡهَا مَا ٱكۡتَسَبَتۡۗ رَبَّنَا لَا تُؤَاخِذۡنَآ إِن نَّسِينَآ أَوۡ أَخۡطَأۡنَاۚ رَبَّنَا وَلَا تَحۡمِلۡ عَلَيۡنَآ إِصۡرٗا كَمَا حَمَلۡتَهُۥ عَلَى ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِنَاۚ رَبَّنَا وَلَا تُحَمِّلۡنَا مَا لَا طَاقَةَ لَنَا بِهِۦۖ وَٱعۡفُ عَنَّا وَٱغۡفِرۡ لَنَا وَٱرۡحَمۡنَآۚ أَنتَ مَوۡلَىٰنَا فَٱنصُرۡنَا عَلَى ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Allah sakakamiza mzimu uliwonse koma chimene chili cholingana ndi kukhoza kwake. (Ndipo phindu la) zimene mzimuwo udapeza ndilake ndiponso kuluza kwa zomwe udapeza nkwake. (Asilamuwo amanena) “E Mbuye wathu! Musatilange tikaiwala kapena tikalakwitsa, E Mbuye wathu! Musatisenzetse mtolo (wamalamulo) monga munawasenzetsera amene adalipo patsogolo pathu. E Mbuye wathu! Musatisenzetse chimene sitingachithe. Tifafanizireni machimo athu, tikhululukireni zolakwa zathu, ndiponso tichitireni chifundo. Inu Ndinu Mtetezi wathu. Choncho tithangateni ku anthu osakhulupirira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: Sura el-Bekara
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje