Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: An-Nâzi‘ât   Vers:

An-Nâzi‘ât

وَٱلنَّٰزِعَٰتِ غَرۡقٗا
Ndikulumbilira (angelo) amene amazula mwamphamvu (mizimu ya osakhulupirira).[379]
[379] (Ndime 1-5) M’Qur’an nthawi zambiri Allah amalumbilira zolengedwa Zake; zamoyo ndi zopanda moyo, zooneka ndi zosaoneka. Cholinga ndikutilimbikitsa kuti tikhale olingalira luso Lake pa chinthu chilichonse chimene wachilumbilira kuti tizindikire ulemelero Wake ndi mphamvu Zake zoposa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلنَّٰشِطَٰتِ نَشۡطٗا
Ndikulumbiliranso (angelo) amene amachotsa moleza (mizimu ya okhulupirira).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلسَّٰبِحَٰتِ سَبۡحٗا
Ndi omwe amasambira (nayo mizimuyo) mu mlengalenga (ponka nayo ku malo ake oyembekezera).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَٱلسَّٰبِقَٰتِ سَبۡقٗا
Ndi iwo amene akupikisana pokwaniritsa malamulo a Allah.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَٱلۡمُدَبِّرَٰتِ أَمۡرٗا
Ndi iwo (angelo) amene akulongosola malamulo (Ake). (Ndithudi inu anthu mudzauka kwa akufa).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَوۡمَ تَرۡجُفُ ٱلرَّاجِفَةُ
Patsiku lomwe (lipenga loyamba lidzaimbidwa), dziko lapansi ndi mapiri ake zidzagwedezeka (ndipo aliyense adzafa).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
تَتۡبَعُهَا ٱلرَّادِفَةُ
Ndipo kudzatsatira kuyimba kwa lipenga lachiwiri (kumene kudzaukitsa akufa onse).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قُلُوبٞ يَوۡمَئِذٖ وَاجِفَةٌ
Tsiku limenelo mitima idzanjenjemera ndi kuopa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَبۡصَٰرُهَا خَٰشِعَةٞ
Maso a eni mitimayo adzakhala ozyolika (chifukwa chamadandaulo);
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَقُولُونَ أَءِنَّا لَمَرۡدُودُونَ فِي ٱلۡحَافِرَةِ
(Osakhulupirira) akunena: “Kodi nzoona tidzabwezedwa pambuyo pa imfa monga tidalili kale?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَءِذَا كُنَّا عِظَٰمٗا نَّخِرَةٗ
“Pomwe ife titakhala mafupa ofumbwa (tingabwezedwe ndi kuukitsidwa mwa tsopano)?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
قَالُواْ تِلۡكَ إِذٗا كَرَّةٌ خَاسِرَةٞ
Adanena (mokanira ndi mwachipongwe): “Choncho kubwerera kumeneko ngati kudzakhalepodi kudzakhala kotaika (ndi kopanda phindu kwa ife. Pomwe ife sindife oyenera kutaika).”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِنَّمَا هِيَ زَجۡرَةٞ وَٰحِدَةٞ
(Musaganize kubwererako nchinthu chovuta). Ndithundithu Kiyamayo ndi nkuwo umodzi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِذَا هُم بِٱلسَّاهِرَةِ
Mwadzidzidzi (zolengedwa zonse) zidzangoona zili pa dziko latsopano (zili zamoyo).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ مُوسَىٰٓ
Kodi yakufika (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Mûsa?[380]
[380] Kuyambira Ayah iyi mpaka Ayah 26 Allah akumtonthoza mneneri Wake pomuuza nkhani ya Mneneri Musa momwe Farawo adamkanira, ndikuti asaganize kuti vutoli lampeza iye yekha koma kuti aneneri enanso akale lidawaonekeranso. Ndiponso m’ma Ayah amenewa muli chenjezo kwa akafiri kuti aope Allah kuti asawalange monga adamulangira Farawo ndi anthu ake amene adali kutsutsana ndi Allah.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِذۡ نَادَىٰهُ رَبُّهُۥ بِٱلۡوَادِ ٱلۡمُقَدَّسِ طُوًى
Pamene Mbuye wake adamuitana pa chigwa choyera (chotchedwa) Tuwaa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ٱذۡهَبۡ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ إِنَّهُۥ طَغَىٰ
(Adamuuza kuti) pita kwa Farawo ndithu iye wapyola malire, (mkudzitukumula kwake ndikupondereza anthu).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَقُلۡ هَل لَّكَ إِلَىٰٓ أَن تَزَكَّىٰ
Choncho ukamuuze kuti: “Kodi ukufuna kudziyeretsa?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَأَهۡدِيَكَ إِلَىٰ رَبِّكَ فَتَخۡشَىٰ
“Ndikuti ndikuongolere kwa Mbuye wako kuti uzimuopa?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَأَرَىٰهُ ٱلۡأٓيَةَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
(Basi Mûsa) adamuonetsa (Farawo) chozizwitsa chachikulu.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَكَذَّبَ وَعَصَىٰ
Koma (Farawo) adatsutsa (Mûsa pazimene adadza nazo zija) ndi kunyoza.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ثُمَّ أَدۡبَرَ يَسۡعَىٰ
Kenaka adabwerera uku akulimbika kutsutsana naye (Allah),
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَحَشَرَ فَنَادَىٰ
Adawasonkhanitsa (afiti) uku akuitana anthu;
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَقَالَ أَنَا۠ رَبُّكُمُ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Nanena: “Ine ndine mbuye wanu wapamwambamwamba!”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَأَخَذَهُ ٱللَّهُ نَكَالَ ٱلۡأٓخِرَةِ وَٱلۡأُولَىٰٓ
Pamenepo Allah adamulanga chifukwa cha mawu ake omaliza ndi oyamba.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَعِبۡرَةٗ لِّمَن يَخۡشَىٰٓ
Ndithu pa zimenezi pali phunziro (lalikulu) kwa yemwe akuopa Allah.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ءَأَنتُمۡ أَشَدُّ خَلۡقًا أَمِ ٱلسَّمَآءُۚ بَنَىٰهَا
Kodi kulengedwa kwanu, (inu osakhulupirira kuti muuke) nkovuta kapena thambo limene adalimanga (posonkhanitsa mbali zake zosiyanasiyana ndikukhala chinthu chimodzi)?[381]
[381] Tanthauzo lake ndikuti: “Kodi chilengedwe chanu nchovuta kwambiri kuposa chilengedwe cha thambo pamene inu mukuganiza kuti Allah sangathe kukudzutsani pambuyo pa imfa?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
رَفَعَ سَمۡكَهَا فَسَوَّىٰهَا
Adatukula nsinkhu wake ndikulikonza bwino (popanda pena pong’ambika kapena posiyana ndi pena).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَأَغۡطَشَ لَيۡلَهَا وَأَخۡرَجَ ضُحَىٰهَا
Ndipo amauvindikira usiku wake ndi mdima ndipo amatulutsa kuwala wake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلۡأَرۡضَ بَعۡدَ ذَٰلِكَ دَحَىٰهَآ
Ndipo pambuyo pazimenezo, nthaka adaiyala (kuti ikhale yoyenera kuikhala).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَخۡرَجَ مِنۡهَا مَآءَهَا وَمَرۡعَىٰهَا
Adatulutsa m’menemo madzi ake (potulutsa akasupe) ndikumeretsa msipu wake;
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَٱلۡجِبَالَ أَرۡسَىٰهَا
Ndipo mapiri adawakhazikitsa (ndikuwalimbika);
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
مَتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Adachita zonsezi) chifukwa chokusangalatsani inu ndi ziweto zanu.[382]
[382] Mu Ayah iyi Allah akusonyeza kuti Iye ndi Mwini mphamvu zonse zochitira chinthu chilichonse chachikulu kuposa kuwaukitsa akufa; ndiponso akukumbutsa ufulu Wake waukulu womwe adatichitira potipatsa zinthu zonsezo kuti tithandizike nazo.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلطَّآمَّةُ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Choncho likadzafika tsoka lalikulu (tsiku la Qiyâma).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَوۡمَ يَتَذَكَّرُ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا سَعَىٰ
Tsiku limenelo munthu adzakumbukira zimene adachita, (zabwino ndi zoipa).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِمَن يَرَىٰ
Ndipo Moto waukali udzawonetsedwa kwa yense openya.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَأَمَّا مَن طَغَىٰ
Tsono amene adapyola malire (pochita machimo),
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَءَاثَرَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Ndikudzisankhira (yekha) moyo wa pa dziko lapansi,
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِنَّ ٱلۡجَحِيمَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Jahannam ndiwo malo ake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَأَمَّا مَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ وَنَهَى ٱلنَّفۡسَ عَنِ ٱلۡهَوَىٰ
Tsono amene akuopa kuti adzaimilira pamaso pa Mbuye wake, nauletsa mtima wake ku zilakolako zoipa,
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَإِنَّ ٱلۡجَنَّةَ هِيَ ٱلۡمَأۡوَىٰ
Ndithu Munda wamtendere ndiwo adzakhale malo ake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلسَّاعَةِ أَيَّانَ مُرۡسَىٰهَا
Akukufunsa (iwe Mtumiki) (s.a.w) za nthawi (ya tsiku lachimaliziro kuti): “Idzakhala liti?”
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِيمَ أَنتَ مِن ذِكۡرَىٰهَآ
Uli ndi mphamvu yanji iwe yofotokozera za tsikulo? (Iwe ulibe kuzindikira za nthawiyo kotero kuti ungaitchule kwa iwo).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِلَىٰ رَبِّكَ مُنتَهَىٰهَآ
Kwa Mbuye wako ndiko kuli mathero ake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّمَآ أَنتَ مُنذِرُ مَن يَخۡشَىٰهَا
Iwe (ntchito yako) ndikuwachenjeza amene akuiopa; (osati kulengeza zanthawi yake).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
كَأَنَّهُمۡ يَوۡمَ يَرَوۡنَهَا لَمۡ يَلۡبَثُوٓاْ إِلَّا عَشِيَّةً أَوۡ ضُحَىٰهَا
Tsiku limene adzaiona adzakhala ngati sadakhale (pa dziko nthawi yayitali), koma ngati madzulo amodzi kapena masana ake (nthawi ya m’mawa).[383]
[383] Apa tanthauzo lake ndikuti adzaona masiku onse amene adakhala m’dziko ngati lidali ola limodzi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: An-Nâzi‘ât
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen