Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Ghâshiyah   Vers:

Al-Ghâshiyah

هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡغَٰشِيَةِ
Kodi yakudzera, (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Qiyâma (imene idzaphimba anthu ndi zoopsa zake)?
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ خَٰشِعَةٌ
Nkhope zina tsiku limenelo, zidzakhala zonyozeka,[425]
[425] Tanthauzo la nkhope apa ndi eni nkhopezo. Amene akunenedwa pamenepa ndi anthu oipa. Allah watchula nkhope chifukwa ndi chiwalo cholemekezeka pa chilengedwe cha munthu ndipo ndi pamene pali chithunzi chake.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
عَامِلَةٞ نَّاصِبَةٞ
Zogwira ntchito yotopetsa kwambiri.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
تَصۡلَىٰ نَارًا حَامِيَةٗ
Zikalowa ku Moto wotentha kwambiri.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
تُسۡقَىٰ مِنۡ عَيۡنٍ ءَانِيَةٖ
Zikamwetsedwa mu kasupe wotentha kwabasi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَّيۡسَ لَهُمۡ طَعَامٌ إِلَّا مِن ضَرِيعٖ
Sadzakhala ndichakudya koma minga.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَّا يُسۡمِنُ وَلَا يُغۡنِي مِن جُوعٖ
Yosanenepetsa (thupi) ndiponso yosathetsa njala.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ نَّاعِمَةٞ
Nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zosangalala.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لِّسَعۡيِهَا رَاضِيَةٞ
Zidzakondwera ndi malipiro a zochita zake (za pa dziko lapansi).[426]
[426] Tanthauzo la “kukondweretsedwa ndi zochita zawo’’ ndikuti anthu abwino adzakondwera ndi ntchito zawo zabwino zomwe adazichita pa dziko lapansi akadzakhala ndi malipiro abwino pa tsiku lachimaliziro.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’minda ya pamwamba (Jannah).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَّا تَسۡمَعُ فِيهَا لَٰغِيَةٗ
Sizikamva m’menemo mawu oipa, (otukwana ndi kulaula).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِيهَا عَيۡنٞ جَارِيَةٞ
Mmenemo muli kasupe woyenda (mokongola).[427]
[427] (Ndime 12-16) Zosangalatsa zenizeni za tsiku lachimaliziro monga momwe adatiuzira Mneneri (s.a.w) kuti ku Jannah kuli zinthu zimene diso silidapenyepo ngakhale khutu silidamvepo ndipo sizidapitepo m’maganizo a munthu. Choncho zokondweretsa izi zimene Allah watiuza apa akungofanizira ndi zinthu zomwe tikuzidziwa.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِيهَا سُرُرٞ مَّرۡفُوعَةٞ
Mmenemo muli makama a pamwamba,
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَأَكۡوَابٞ مَّوۡضُوعَةٞ
Ndi zikho zoikidwa bwino (pamaso pawo),
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَنَمَارِقُ مَصۡفُوفَةٞ
Ndi misamiro yoikidwa bwino m’mizeremizere
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَزَرَابِيُّ مَبۡثُوثَةٌ
Ndi mphasa (zamtengo wapatali, carpet) zoyalidwa ponseponse.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
أَفَلَا يَنظُرُونَ إِلَى ٱلۡإِبِلِ كَيۡفَ خُلِقَتۡ
Kodi (akunyozera kulingalira zisonyezo za Allah), sakulingalira kungamira idalengedwa motani?[428]
[428] (Ndime 17-20) Allah akuwauza kuti ayang’ane chilengedwe cha ngamira, thambo, mapiri ndi nthaka. Pambuyo pake alingalire, aone kuti amene adalenga zimenezo ngotha kuchita chilichonse monga kuukitsa anthu m’manda. Cholinga cha Allah potchula zinthu zimenezi, ngakhale kuti malangizowa nga munthu aliyense, koma adali kuwauza akafiri a pa Makka amene zinthu zimenezi maso awo ankaziona nthawi ndi nthawi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِلَى ٱلسَّمَآءِ كَيۡفَ رُفِعَتۡ
Ndi thambo (limene akuliona nthawi zonse) m’mene lidatukulidwira (kutali popanda mzati)?
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِلَى ٱلۡجِبَالِ كَيۡفَ نُصِبَتۡ
Ndi mapiri momwe adakhazikitsidwira (molimba)?
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَإِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَيۡفَ سُطِحَتۡ
Ndi nthaka momwe idayalidwira.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَذَكِّرۡ إِنَّمَآ أَنتَ مُذَكِّرٞ
Basi, kumbutsa (anthu) ndithu iwe, ndiwe mkumbutsi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
لَّسۡتَ عَلَيۡهِم بِمُصَيۡطِرٍ
Sindiwe wokakamiza anthu (kuti akhulupirire).[429]
[429] Ayah iyi ikukwana kuwatsutsa adani a Chisilamu amene akunena kuti, “chipembedzo cha Chisilamu chidafala ndi lupanga.” Kutanthauza kuti ankawakakamiza anthu kuti achivomere chipembedzochi. Sichodabwitsa kuona adani a Chisilamu akuchinyoza chipembedzochi, koma chodabwitsa nchakuti mawu onamawa nkumatulukanso mkamwa mwa anthu omwe amadzitcha kuti ndi Asilamu. Nzoona alipo ena mwa anthu odziwa za chipembedzo (ma Ulama) amene adanena kuti chipembedzo cha Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga. Koma simonga momwe akutanthauzilira adani amene sadziwa za Chisilamu nkumangotsatira mabodza a akuluakulu awo. Cholinga cha ma Ulama ponena kuti “Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga” kumeneko ndi kudziteteza kwa adani omwe adafuna kuchithetsa, osati kuwakakamiza anthu kulowa mchipembedzo. Kukakamiza anthu kulowa mChisilamu nkosaloledwa. Amene akudziwa mbiri ya Chisilamu, akudziwa kuti Asilamu sadalamulidwe kuchita Jihâd mpaka pamene akafiri adali kuwazunza. Pali nkhani zambiri za Maswahaba (otsatira Mneneri) (s.a.w) ku Madina pamene adafuna kuwakakamiza ana awo kulowa m’Chisilamu, koma Mneneri adawakaniza kutero. Basi, munthu amene akunena zoterezo mwina akutero pa chifukwa chosadziwa za chipembedzo cha Chisilamu, mwinanso nkukhala misala basi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِلَّا مَن تَوَلَّىٰ وَكَفَرَ
Koma amene anyoza ndi kukanira (ulaliki wako),
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فَيُعَذِّبُهُ ٱللَّهُ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَكۡبَرَ
Allah amulanga chilango chachikulu zedi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّ إِلَيۡنَآ إِيَابَهُمۡ
Ndithu kobwerera kwawo ndi kwa Ife basi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ثُمَّ إِنَّ عَلَيۡنَا حِسَابَهُم
Ndipo ndithu kuwerengedwa kwawo kuli kwa Ife.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Ghâshiyah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen