Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Surah: Al-Mursalāt   Ayah:

Al-Mursalāt

وَٱلۡمُرۡسَلَٰتِ عُرۡفٗا
Ndikulumbilira mphepo yomwe ikuomba motsatizana.
Arabic explanations of the Qur’an:
فَٱلۡعَٰصِفَٰتِ عَصۡفٗا
Ndi mphepo yamkuntho ikamakuntha.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَٱلنَّٰشِرَٰتِ نَشۡرٗا
Ndi mphepo yobalalitsa mitambo ndi mvula.
Arabic explanations of the Qur’an:
فَٱلۡفَٰرِقَٰتِ فَرۡقٗا
Ndi ma Ayah osiyanitsa pakati pachoona ndi chonama;
Arabic explanations of the Qur’an:
فَٱلۡمُلۡقِيَٰتِ ذِكۡرًا
Ndi angelo opereka chivumbulutso kwa aneneri.
Arabic explanations of the Qur’an:
عُذۡرًا أَوۡ نُذۡرًا
Kuti chichotse madandaulo kapena chikhale chenjezo;
Arabic explanations of the Qur’an:
إِنَّمَا تُوعَدُونَ لَوَٰقِعٞ
Ndithu zimene mukulonjezedwa (kuti chimaliziro chidzakhalapo) zidzachitikadi (popanda chipeneko),
Arabic explanations of the Qur’an:
فَإِذَا ٱلنُّجُومُ طُمِسَتۡ
Pamene nyenyezi zidzafafanizidwa (kuwala kwake ndi kuchotsedwa m’malo mwake).
Arabic explanations of the Qur’an:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ فُرِجَتۡ
Ndiponso pamene thambo lidzang‘ambidwa.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ نُسِفَتۡ
Ndi pamenenso mapiri adzachotsedwa m’malo mwake ndi kuperedwa (kukhala fumbi).
Arabic explanations of the Qur’an:
وَإِذَا ٱلرُّسُلُ أُقِّتَتۡ
Ndi pamene atumiki adzasonkhanitsidwa pa nthawi yake, (kuti apereke umboni ku mibadwo yawo).
Arabic explanations of the Qur’an:
لِأَيِّ يَوۡمٍ أُجِّلَتۡ
Kodi nditsiku lanji azichedwetsera (zinthu zikuluzikulu kuti zidzachitike)?
Arabic explanations of the Qur’an:
لِيَوۡمِ ٱلۡفَصۡلِ
Nditsiku loweruza (pakati pa zolengedwa).
Arabic explanations of the Qur’an:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِ
Nchiyani chingakudziwitse za tsiku la chiweruzirolo?
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabic explanations of the Qur’an:
أَلَمۡ نُهۡلِكِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Kodi sitidawaononge (anthu) akale (chifukwa cha machimo awo, monga anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu)?
Arabic explanations of the Qur’an:
ثُمَّ نُتۡبِعُهُمُ ٱلۡأٓخِرِينَ
Kenako titsatiza ena (okana Allah m’kuonongekako monga tidawachitira oyamba),
Arabic explanations of the Qur’an:
كَذَٰلِكَ نَفۡعَلُ بِٱلۡمُجۡرِمِينَ
Chomwecho tiwachitiranso ochimwa.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabic explanations of the Qur’an:
أَلَمۡ نَخۡلُقكُّم مِّن مَّآءٖ مَّهِينٖ
Kodi sitidakulengeni kuchokera ku madzi onyozeka, (madzi ambewu ya munthu)?
Arabic explanations of the Qur’an:
فَجَعَلۡنَٰهُ فِي قَرَارٖ مَّكِينٍ
Kenako tidawaika pamalo okhazikika (kuti chilengedwe chake chikwanire pamenepo),
Arabic explanations of the Qur’an:
إِلَىٰ قَدَرٖ مَّعۡلُومٖ
Mpaka nyengo yodziwika (imene tidaipima kuti mwana abadwe).
Arabic explanations of the Qur’an:
فَقَدَرۡنَا فَنِعۡمَ ٱلۡقَٰدِرُونَ
Tidaipima nyengoyo; taonani kupima bwino Ife opima!
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabic explanations of the Qur’an:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ كِفَاتًا
Kodi sitidaichite nthaka kukhala yofungatira,
Arabic explanations of the Qur’an:
أَحۡيَآءٗ وَأَمۡوَٰتٗا
Amoyo ndi akufa?
Arabic explanations of the Qur’an:
وَجَعَلۡنَا فِيهَا رَوَٰسِيَ شَٰمِخَٰتٖ وَأَسۡقَيۡنَٰكُم مَّآءٗ فُرَاتٗا
Ndipo tidaika m’menemo mapiri ataliatali (olimbitsa nthaka), ndipo takumwetsani madzi okoma.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo Lathu lakuuka ku imfa).
Arabic explanations of the Qur’an:
ٱنطَلِقُوٓاْ إِلَىٰ مَا كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
(Kudzanenedwa kwa okana tsiku la chimaliziro:) Pitani kuzimene mudali kuzitsutsa zija.
Arabic explanations of the Qur’an:
ٱنطَلِقُوٓاْ إِلَىٰ ظِلّٖ ذِي ثَلَٰثِ شُعَبٖ
Pitani kumthunzi (wautsi wa ku Moto) wa nthambi zitatu,
Arabic explanations of the Qur’an:
لَّا ظَلِيلٖ وَلَا يُغۡنِي مِنَ ٱللَّهَبِ
Simthunzi (wamtendere) ndiponso siwotchinjiriza ku malawi a Moto.”
Arabic explanations of the Qur’an:
إِنَّهَا تَرۡمِي بِشَرَرٖ كَٱلۡقَصۡرِ
Ndithu motowo umaponya mphalikira (mbaliwali) zazikulu ngati nyumba,
Arabic explanations of the Qur’an:
كَأَنَّهُۥ جِمَٰلَتٞ صُفۡرٞ
Zonga ngati ngamira zachikasu.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (zimenezi).
Arabic explanations of the Qur’an:
هَٰذَا يَوۡمُ لَا يَنطِقُونَ
Ili ndi tsiku lomwe sadzayankhula.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَلَا يُؤۡذَنُ لَهُمۡ فَيَعۡتَذِرُونَ
Ndipo sadzapatsidwa chilolezo (choyankhulira) kuti apereke madandaulo awo.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (za tsiku limenelo).
Arabic explanations of the Qur’an:
هَٰذَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِۖ جَمَعۡنَٰكُمۡ وَٱلۡأَوَّلِينَ
(Adzauzidwa kuti): Ili ndi tsiku loweruza (pakati pa abwino ndi oipa takusonkhanitsani inu (otsutsa Muhammad {s.a.w}), ndi akale (otsutsa aneneri akale).
Arabic explanations of the Qur’an:
فَإِن كَانَ لَكُمۡ كَيۡدٞ فَكِيدُونِ
Ngati muli ndi ndale (yodzipulumutsira ku chilango Changa) ndichiteni ndaleyo!
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (lonjezo la Allah).
Arabic explanations of the Qur’an:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي ظِلَٰلٖ وَعُيُونٖ
Ndithu oopa (Allah tsiku limenelo) adzakhala mu mthunzi ndi mitsinje,
Arabic explanations of the Qur’an:
وَفَوَٰكِهَ مِمَّا يَشۡتَهُونَ
Ndipo adzakhala ndi zipatso zomwe azidzazifuna.
Arabic explanations of the Qur’an:
كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ هَنِيٓـَٔۢا بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
(Kudzanenedwa kwa iwo): “Idyani, imwani mokondwa chifukwa cha zabwino zomwe mudali kuchita (mu moyo wa dziko lapansi).
Arabic explanations of the Qur’an:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umo ndi mmene Ife timawalipirira ochita zabwino.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (mtendere wa Allah)
Arabic explanations of the Qur’an:
كُلُواْ وَتَمَتَّعُواْ قَلِيلًا إِنَّكُم مُّجۡرِمُونَ
Idyani, sangalalani pang’ono m’kanthawi kochepa; ndithu inu ndinu ochimwa (chifukwa chakumphatikiza Allah ndi zolengedwa).
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (mtendere wa Allah).
Arabic explanations of the Qur’an:
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱرۡكَعُواْ لَا يَرۡكَعُونَ
Ndipo kukanenedwa kwa iwo: “Weramani, (pembedzani Allah).” sawerengera.
Arabic explanations of the Qur’an:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Kuonongeka kwakukulu tsiku limenelo kuli pa otsutsa (malamulo a Allah).
Arabic explanations of the Qur’an:
فَبِأَيِّ حَدِيثِۭ بَعۡدَهُۥ يُؤۡمِنُونَ
Kodi ndi nkhani iti imene adzaikhulupirira pambuyo pa Iyi (Qur’an)?
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Surah: Al-Mursalāt
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close