Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Qiyaama   Versículo:

Sura Al-Qiyaama

لَآ أُقۡسِمُ بِيَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ
Ndikulumbilira tsiku lachimaliziro.
Las Exégesis Árabes:
وَلَآ أُقۡسِمُ بِٱلنَّفۡسِ ٱللَّوَّامَةِ
Ndikulumbiliranso mzimu wodzidzudzula (pa cholakwa chimene wachita. Ndithu mudzaukitsidwa; mafupa anu omwazikana atasonkhanitsidwa.)
Las Exégesis Árabes:
أَيَحۡسَبُ ٱلۡإِنسَٰنُ أَلَّن نَّجۡمَعَ عِظَامَهُۥ
Kodi munthu akuganiza kuti Ife (Amene tidamlenga kuchokera popanda chilichonse) sitidzatha kusonkhanitsa mafupa ake (ofumbwa)?
Las Exégesis Árabes:
بَلَىٰ قَٰدِرِينَ عَلَىٰٓ أَن نُّسَوِّيَ بَنَانَهُۥ
Iyayi, Ife tikhoza (kutisonkhanitsa) ndi kutilongosola bwino timizere takunsonga kwa zala zake. (Mafupa ake ndiye osanena)!
Las Exégesis Árabes:
بَلۡ يُرِيدُ ٱلۡإِنسَٰنُ لِيَفۡجُرَ أَمَامَهُۥ
Koma munthu akufuna kuti apitirize kuchimwa (mmasiku akudza) mtsogolo mwake.
Las Exégesis Árabes:
يَسۡـَٔلُ أَيَّانَ يَوۡمُ ٱلۡقِيَٰمَةِ
Akufunsa (mwa chipongwe): “Kodi lidzakhala liti tsiku la chimaliziro?”
Las Exégesis Árabes:
فَإِذَا بَرِقَ ٱلۡبَصَرُ
Pamene maso adzangoti tong’oo (ndi mantha),
Las Exégesis Árabes:
وَخَسَفَ ٱلۡقَمَرُ
Ndi kuchoka kuwala kwa mwezi,
Las Exégesis Árabes:
وَجُمِعَ ٱلشَّمۡسُ وَٱلۡقَمَرُ
Ndipo dzuwa ndi mwezi ndikusonkhanitsidwa.
Las Exégesis Árabes:
يَقُولُ ٱلۡإِنسَٰنُ يَوۡمَئِذٍ أَيۡنَ ٱلۡمَفَرُّ
Munthu adzanena tsiku limenelo: “Nkuti kothawira (chilangochi?)”
Las Exégesis Árabes:
كَلَّا لَا وَزَرَ
(Adzauzidwa): “Iyayi, (iwe munthu) palibe pothawira (pako)!”
Las Exégesis Árabes:
إِلَىٰ رَبِّكَ يَوۡمَئِذٍ ٱلۡمُسۡتَقَرُّ
Tsiku limenelo kobwerera (anthu) ndi kwa Mbuye wako basi.
Las Exégesis Árabes:
يُنَبَّؤُاْ ٱلۡإِنسَٰنُ يَوۡمَئِذِۭ بِمَا قَدَّمَ وَأَخَّرَ
Tsiku limenelo munthu adzauzidwa zochita zake zimene adazitsogoza ndi zimene adazichedwetsa.
Las Exégesis Árabes:
بَلِ ٱلۡإِنسَٰنُ عَلَىٰ نَفۡسِهِۦ بَصِيرَةٞ
Koma munthu adzadzichitira umboni yekha pa mzimu wake.
Las Exégesis Árabes:
وَلَوۡ أَلۡقَىٰ مَعَاذِيرَهُۥ
Ngakhale atapereka madandaulo ake (otani kuti apulumuke nawo sadzapulumuka).
Las Exégesis Árabes:
لَا تُحَرِّكۡ بِهِۦ لِسَانَكَ لِتَعۡجَلَ بِهِۦٓ
Usaigwedezere (Qur’an) lirime lako (pamene ikuvumbulutsidwa) kuti uifulumilire (kuiwerenga ndi kuisunga mu mtima).
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ عَلَيۡنَا جَمۡعَهُۥ وَقُرۡءَانَهُۥ
Ndithu ndiudindo wathu kuisonkhanitsa (mu mtima mwako) ndi kukhazikitsa kawerengedwe kake (palirime lako).
Las Exégesis Árabes:
فَإِذَا قَرَأۡنَٰهُ فَٱتَّبِعۡ قُرۡءَانَهُۥ
Choncho pamene tikukuwerengera iwe tsatira kuwerenga kwakeko (uku uli chete).
Las Exégesis Árabes:
ثُمَّ إِنَّ عَلَيۡنَا بَيَانَهُۥ
Kenako, ndithu ndiudindo Wathu kulongosola (zimene siukumvetsa),
Las Exégesis Árabes:
كَلَّا بَلۡ تُحِبُّونَ ٱلۡعَاجِلَةَ
Iyayi koma mukukonda moyo wa pa dziko.
Las Exégesis Árabes:
وَتَذَرُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Ndipo mukusiya moyo wa tsiku lachimaliziro.
Las Exégesis Árabes:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ نَّاضِرَةٌ
Nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zowala,
Las Exégesis Árabes:
إِلَىٰ رَبِّهَا نَاظِرَةٞ
Zili kumuyang’ana Mbuye wawo.
Las Exégesis Árabes:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذِۭ بَاسِرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zoziya (zokhwinyata).
Las Exégesis Árabes:
تَظُنُّ أَن يُفۡعَلَ بِهَا فَاقِرَةٞ
Zikuyembekezeka kuti zilandira tsoka lodula msana.
Las Exégesis Árabes:
كَلَّآ إِذَا بَلَغَتِ ٱلتَّرَاقِيَ
Sichoncho! Pamene mzimu udzafika pa nthitimtima, (pomwe pakumana mafupa am’mapewa).
Las Exégesis Árabes:
وَقِيلَ مَنۡۜ رَاقٖ
Ndipo ndikunenedwa ndani angamchiritse!
Las Exégesis Árabes:
وَظَنَّ أَنَّهُ ٱلۡفِرَاقُ
Ndipo (iye mwini wake), nkutsimikiza kuti ndithu uku ndikusiyana (ndi dziko lapansi),
Las Exégesis Árabes:
وَٱلۡتَفَّتِ ٱلسَّاقُ بِٱلسَّاقِ
Ndipo miyendo idzasanjikizana; (iyi ndi nthawi yochoka mzimu).
Las Exégesis Árabes:
إِلَىٰ رَبِّكَ يَوۡمَئِذٍ ٱلۡمَسَاقُ
Tsiku limenelo koperekedwa (anthu onse) nkwa Mbuye wako.
Las Exégesis Árabes:
فَلَا صَدَّقَ وَلَا صَلَّىٰ
Ndipo sadakhulupirire komanso sadapemphere Swala (zisanu),
Las Exégesis Árabes:
وَلَٰكِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
Koma (m’malo mwake) adatsutsa ndi kunyoza.
Las Exégesis Árabes:
ثُمَّ ذَهَبَ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ يَتَمَطَّىٰٓ
Kenaka adapita kubanja lake (uku akuyenda) monyada.
Las Exégesis Árabes:
أَوۡلَىٰ لَكَ فَأَوۡلَىٰ
Kuonongeka nkwako (iwe wotsutsa)! Kuonongeka zedi!
Las Exégesis Árabes:
ثُمَّ أَوۡلَىٰ لَكَ فَأَوۡلَىٰٓ
Ndiponso kuonongeka nkwako! kuonongeka zedi!
Las Exégesis Árabes:
أَيَحۡسَبُ ٱلۡإِنسَٰنُ أَن يُتۡرَكَ سُدًى
Kodi munthu akuganiza kuti angosiidwa chabe? (Sadzaweruzidwa)?
Las Exégesis Árabes:
أَلَمۡ يَكُ نُطۡفَةٗ مِّن مَّنِيّٖ يُمۡنَىٰ
Kodi sadali dontho la umuna umene udafwamphukira (m’chiberekero)?
Las Exégesis Árabes:
ثُمَّ كَانَ عَلَقَةٗ فَخَلَقَ فَسَوَّىٰ
Kenako adakhala nthinthi (ntchintchi) ya magazi, ndipo adamlenga ndi kumlinganiza (monga munthu).
Las Exégesis Árabes:
فَجَعَلَ مِنۡهُ ٱلزَّوۡجَيۡنِ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ
Ndipo adalenga kuchokera mmenemo mitundu iwiri: mwamuna ndi mkazi.
Las Exégesis Árabes:
أَلَيۡسَ ذَٰلِكَ بِقَٰدِرٍ عَلَىٰٓ أَن يُحۡـِۧيَ ٱلۡمَوۡتَىٰ
Kodi (Iye amene adayambitsa chilengedwe choyambachi) sangathe kuwapatsa moyo akufa?
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Qiyaama
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar