Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura At-Taariq   Versículo:

Sura At-Taariq

وَٱلسَّمَآءِ وَٱلطَّارِقِ
Ndikulumbilira ku mwamba ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
Las Exégesis Árabes:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلطَّارِقُ
Chitakudziwitse nchiyani za Nyenyezi yodza usikuyo?
Las Exégesis Árabes:
ٱلنَّجۡمُ ٱلثَّاقِبُ
Imeneyo ndi nyenyezi yowala kwambiri (mu mdima).
Las Exégesis Árabes:
إِن كُلُّ نَفۡسٖ لَّمَّا عَلَيۡهَا حَافِظٞ
Ndithudi palibe mzimu uliwonse koma uli ndi msungi wake (amene akuuyang’anira ndikulemba zonse zochita zake).
Las Exégesis Árabes:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ مِمَّ خُلِقَ
Aganizire munthu, kodi adalengedwa kuchokera kuchiyani?
Las Exégesis Árabes:
خُلِقَ مِن مَّآءٖ دَافِقٖ
Adalengedwa kuchokera ku madzi ofwamphuka.
Las Exégesis Árabes:
يَخۡرُجُ مِنۢ بَيۡنِ ٱلصُّلۡبِ وَٱلتَّرَآئِبِ
Amatuluka kuchokera pakati pa mafupa a msana (wa mwamuna) ndi chifuwa (cha mkazi).
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهُۥ عَلَىٰ رَجۡعِهِۦ لَقَادِرٞ
Ndithu Iye ndiwakutha, kumbwezeranso (ku moyo pa mbuyo pa imfa).
Las Exégesis Árabes:
يَوۡمَ تُبۡلَى ٱلسَّرَآئِرُ
Tsiku limene zobisika zonse zidzaonekera poyera.
Las Exégesis Árabes:
فَمَا لَهُۥ مِن قُوَّةٖ وَلَا نَاصِرٖ
Munthu sadzakhala ndi mphamvu (tsiku limenelo zodzitetezera iye mwini) ndiponso sadzakhala ndi mtetezi.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلرَّجۡعِ
Ndikulumbiliranso mitambo yobweretsabweretsa mvula.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلۡأَرۡضِ ذَاتِ ٱلصَّدۡعِ
Ndi nthaka imene imang’ambika (potulutsa m’mera),
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلٞ فَصۡلٞ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndi mawu olekanitsa (Haqq ndi Bâtwil - choona ndi chonama).
Las Exégesis Árabes:
وَمَا هُوَ بِٱلۡهَزۡلِ
Imeneyi sinkhambakamwa.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهُمۡ يَكِيدُونَ كَيۡدٗا
Ndithudi iwo akukonza chiwembu.[416]
[416] (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupilira) akuchita ndale kuti azimitse dangalira la Qur’an ndikuyesetsa kuti awabweze amene adakhulupilira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Naye Allah akuwachitira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amazikonza.
Las Exégesis Árabes:
وَأَكِيدُ كَيۡدٗا
Nanenso ndikuwakonzera chiwembu (champhamvu kwambiri chimene sangathe kuchipewa).
Las Exégesis Árabes:
فَمَهِّلِ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَمۡهِلۡهُمۡ رُوَيۡدَۢا
Basi, apatse nthawi osakhulupirira apatse nthawi pang’ono, (aona posachedwa).
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura At-Taariq
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar