ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: سوره عاديات   آیه:

سوره عاديات

وَٱلۡعَٰدِيَٰتِ ضَبۡحٗا
Ndikulumbilira akavalo othamanga ali ndi phuma,
تفسیرهای عربی:
فَٱلۡمُورِيَٰتِ قَدۡحٗا
Ndi otulutsa moto ku zikhotwa (pomenyetsa miyendo m’miyala),
تفسیرهای عربی:
فَٱلۡمُغِيرَٰتِ صُبۡحٗا
Ndi othira nkhondo adani mmawa (dzuwa lisadatuluke),
تفسیرهای عربی:
فَأَثَرۡنَ بِهِۦ نَقۡعٗا
Ndi kuulutsa fumbi lambiri (kwa adani) nthawi imeneyo,
تفسیرهای عربی:
فَوَسَطۡنَ بِهِۦ جَمۡعًا
Ndikulowelera mkatikati mwa adani.
تفسیرهای عربی:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لِرَبِّهِۦ لَكَنُودٞ
Ndithu munthu ali wokanira Mbuye wake, (sathokoza Allah pa zimene amdalitsa nazo).[472]
[472] Tanthauzo la “kukanira Mbuye wake” ndi kuukanira mtendere Wake. Ndipo kukanira mtendere ndiko kusagwiritsira ntchito mtenderewo mnjira zabwino, monga m’mapemphero ndi zina zotero.
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّهُۥ عَلَىٰ ذَٰلِكَ لَشَهِيدٞ
Ndithudi iye pa zimenezi ndi mboni (yodzichitira yekha kupyolera mzochitachita zake).
تفسیرهای عربی:
وَإِنَّهُۥ لِحُبِّ ٱلۡخَيۡرِ لَشَدِيدٌ
Ndipo ndithu iye ndiwokonda chuma kwambiri (ndiponso ngwamsulizo).[473]
[473] Kapena kuti ali wofunitsitsa chuma kwambiri; kumeneko ndikumangoti mtima dyokodyoko pachuma. Ukachipeza ndikumachichitira umbombo ndipo ndikumaganiza kuti chumacho nchopambana china chilichonse.
تفسیرهای عربی:
۞ أَفَلَا يَعۡلَمُ إِذَا بُعۡثِرَ مَا فِي ٱلۡقُبُورِ
Kodi sakudziwa zikadzatulutsidwa za m’manda,
تفسیرهای عربی:
وَحُصِّلَ مَا فِي ٱلصُّدُورِ
Ndikudzasonkhanitsidwa ndi kuonekera poyera zomwe zidali m’mitima?
تفسیرهای عربی:
إِنَّ رَبَّهُم بِهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّخَبِيرُۢ
Ndithu tsiku limenelo Mbuye wawo adzawadziwa kwambiri (ndikuwalongosolera zonse zochita zawo).[474]
[474] “Kuwadziwa kwambiri,” kukutanthauza kuti Iye ngodziwa zazikuluzikulu ndi zazing’onozing’ono zoonekera poyera ndi zobisika. Tsiku limenelo adzawalipira chilichonse chimene adachita.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: سوره عاديات
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن