ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی سوره: سوره دخان   آیه:

سوره دخان

حمٓ
Hâ-Mîm.
تفسیرهای عربی:
وَٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Ndikulumbilira buku lofotokoza momveka.
تفسیرهای عربی:
إِنَّآ أَنزَلۡنَٰهُ فِي لَيۡلَةٖ مُّبَٰرَكَةٍۚ إِنَّا كُنَّا مُنذِرِينَ
Ndithu tidaivumbulutsa (Qur’an) mu usiku wodala. Ife ndithu Ndiachenjezi.
تفسیرهای عربی:
فِيهَا يُفۡرَقُ كُلُّ أَمۡرٍ حَكِيمٍ
Mu (usiku) umenewu chinthu chilichonse chanzeru chimaweruzidwa ndi kulongosoledwa.
تفسیرهای عربی:
أَمۡرٗا مِّنۡ عِندِنَآۚ إِنَّا كُنَّا مُرۡسِلِينَ
Mwa chilamulo chochokera kwa Ife. Ndithu Ife ndife otumiza atumiki (kuti achenjeze anthu).
تفسیرهای عربی:
رَحۡمَةٗ مِّن رَّبِّكَۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
(Chifukwa cha) chifundo chochokera kwa Mbuye wako. Ndithu Iye Ngwakumva zonse, Wodziwa kwabasi.
تفسیرهای عربی:
رَبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُم مُّوقِنِينَ
Mbuye wa thambo ndi nthaka ndi zapakati pake, ngati muli otsimikiza.
تفسیرهای عربی:
لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُۖ رَبُّكُمۡ وَرَبُّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Palibe wopembedzedwa moona koma Iye basi. Amapereka moyo ndikupereka imfa, Mbuye wanu ndi Mbuye wa makolo anu oyamba.
تفسیرهای عربی:
بَلۡ هُمۡ فِي شَكّٖ يَلۡعَبُونَ
Koma iwo (okanira) ali mchikaiko akungosewera, (potsatira zilakolako zawo zoipa).
تفسیرهای عربی:
فَٱرۡتَقِبۡ يَوۡمَ تَأۡتِي ٱلسَّمَآءُ بِدُخَانٖ مُّبِينٖ
Basi, yembekezera tsiku limene thambo lidzadze ndi utsi woonekera (konsekonse).
تفسیرهای عربی:
يَغۡشَى ٱلنَّاسَۖ هَٰذَا عَذَابٌ أَلِيمٞ
Udzawaphimba anthu onse (ndipo adzakhala akunena:) “Ichi ndi chilango chowawa.
تفسیرهای عربی:
رَّبَّنَا ٱكۡشِفۡ عَنَّا ٱلۡعَذَابَ إِنَّا مُؤۡمِنُونَ
E Mbuye wathu! Tichotsereni chilangochi, ndithu ife tikhulupirira.”
تفسیرهای عربی:
أَنَّىٰ لَهُمُ ٱلذِّكۡرَىٰ وَقَدۡ جَآءَهُمۡ رَسُولٞ مُّبِينٞ
(Kodi lero) kukumbukira kuwapindulira chiyani iwo? Chikhalirecho mtumiki wolongosola chilichonse adawadzera.
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ تَوَلَّوۡاْ عَنۡهُ وَقَالُواْ مُعَلَّمٞ مَّجۡنُونٌ
Koma sadamlabadire uku akumnena kuti: “Waphunzitsidwa (ndi anthu), ndiponso wopenga.”
تفسیرهای عربی:
إِنَّا كَاشِفُواْ ٱلۡعَذَابِ قَلِيلًاۚ إِنَّكُمۡ عَآئِدُونَ
Ndithu Ife tichotsa chilangocho pang’ono (koma) inu mubwerezanso (machimo anu).
تفسیرهای عربی:
يَوۡمَ نَبۡطِشُ ٱلۡبَطۡشَةَ ٱلۡكُبۡرَىٰٓ إِنَّا مُنتَقِمُونَ
(Kumbuka, iwe Mtumiki), tsiku limene tidzawalanga chilango chachikulu; ndithu Ife ndife olanga.
تفسیرهای عربی:
۞ وَلَقَدۡ فَتَنَّا قَبۡلَهُمۡ قَوۡمَ فِرۡعَوۡنَ وَجَآءَهُمۡ رَسُولٞ كَرِيمٌ
Ndipo ndithu iwo asadadze, tidawayesa anthu a Farawo. Ndiponso adawadzera mtumiki wolemekezeka,
تفسیرهای عربی:
أَنۡ أَدُّوٓاْ إِلَيَّ عِبَادَ ٱللَّهِۖ إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
Kuti: “Ndipatseni akapolo a Allah. Ndithu ine kwa inu ndi Mtumiki wokhulupirika.”
تفسیرهای عربی:
وَأَن لَّا تَعۡلُواْ عَلَى ٱللَّهِۖ إِنِّيٓ ءَاتِيكُم بِسُلۡطَٰنٖ مُّبِينٖ
“Ndipo musadzikweze kwa Allah. Ndithu ine ndikubweretserani chisonyezo choonekera.”
تفسیرهای عربی:
وَإِنِّي عُذۡتُ بِرَبِّي وَرَبِّكُمۡ أَن تَرۡجُمُونِ
“Ndipo Ine ndadzitchinjiriza ndi Mbuye Wanga ndiponso Mbuye wanu (ku chiwembu chofuna kundipha) pondigenda (ndi miyala).”
تفسیرهای عربی:
وَإِن لَّمۡ تُؤۡمِنُواْ لِي فَٱعۡتَزِلُونِ
“Ndipo ngati simundikhulupirira, ndipatukeni (musandivutitse).”
تفسیرهای عربی:
فَدَعَا رَبَّهُۥٓ أَنَّ هَٰٓؤُلَآءِ قَوۡمٞ مُّجۡرِمُونَ
“(Koma adamchitira mtopola). Ndipo iye adaitana Mbuye wake kuti: “Awa ndithu ndi anthu oipa.”
تفسیرهای عربی:
فَأَسۡرِ بِعِبَادِي لَيۡلًا إِنَّكُم مُّتَّبَعُونَ
(Allah adamuuza kuti): “Pita ndi akapolo Anga usiku; ndithu inu mulondoledwa.”
تفسیرهای عربی:
وَٱتۡرُكِ ٱلۡبَحۡرَ رَهۡوًاۖ إِنَّهُمۡ جُندٞ مُّغۡرَقُونَ
“Ndipo isiye nyanja ili momwemo, zii. ndithu iwo ndikhamu (lankhondo) limene limizidwa.”
تفسیرهای عربی:
كَمۡ تَرَكُواْ مِن جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Kodi ndi minda ingati ndi akasupe zomwe adazisiya atamizidwa!
تفسیرهای عربی:
وَزُرُوعٖ وَمَقَامٖ كَرِيمٖ
Ndiponso mmera ndi malo abwino!
تفسیرهای عربی:
وَنَعۡمَةٖ كَانُواْ فِيهَا فَٰكِهِينَ
Ndi mtendere (waukulu) umene adali kusangalala nawo mmenemo.
تفسیرهای عربی:
كَذَٰلِكَۖ وَأَوۡرَثۡنَٰهَا قَوۡمًا ءَاخَرِينَ
Umo ndi mmene zidalili. Ndipo tidawapatsa anthu ena zimenezo.
تفسیرهای عربی:
فَمَا بَكَتۡ عَلَيۡهِمُ ٱلسَّمَآءُ وَٱلۡأَرۡضُ وَمَا كَانُواْ مُنظَرِينَ
Thambo ndi nthaka sizidawalilire ndipo sadapatsidwe mpata (wobwereranso pa dziko).
تفسیرهای عربی:
وَلَقَدۡ نَجَّيۡنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ مِنَ ٱلۡعَذَابِ ٱلۡمُهِينِ
Ndipo ndithu tidapulumutsa ana a Israyeli ku chilango choyalutsa.
تفسیرهای عربی:
مِن فِرۡعَوۡنَۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَالِيٗا مِّنَ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
Chochokera kwa Farawo; ndithu iye adali wodzikweza ndiponso mmodzi wa opyola malire.
تفسیرهای عربی:
وَلَقَدِ ٱخۡتَرۡنَٰهُمۡ عَلَىٰ عِلۡمٍ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo ndithu tidawasankha (Ayuda nthawi imeneyo) pa mitundu ina m’kudziwa Kwathu,
تفسیرهای عربی:
وَءَاتَيۡنَٰهُم مِّنَ ٱلۡأٓيَٰتِ مَا فِيهِ بَلَٰٓؤٞاْ مُّبِينٌ
Ndipo tidawapatsa zisonyezo (kupyolera m’dzanja la Mûsa) momwe mudali mayeso oonekera poyera kwa iwo.
تفسیرهای عربی:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَيَقُولُونَ
Ndithu awa (Aquraish) akunena (kuti):
تفسیرهای عربی:
إِنۡ هِيَ إِلَّا مَوۡتَتُنَا ٱلۡأُولَىٰ وَمَا نَحۡنُ بِمُنشَرِينَ
“Palibe china choposera pa imfa yathu yoyambayi, ndipo ife sitidzaukitsidwa.”
تفسیرهای عربی:
فَأۡتُواْ بِـَٔابَآئِنَآ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
“Choncho tibweretsereni makolo athu (amene adafa), ngati mukunena zoona (kuti kuli kuuka).”
تفسیرهای عربی:
أَهُمۡ خَيۡرٌ أَمۡ قَوۡمُ تُبَّعٖ وَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ أَهۡلَكۡنَٰهُمۡۚ إِنَّهُمۡ كَانُواْ مُجۡرِمِينَ
Kodi iwo ndi abwino (ndi kupambana pa nyonga), kapena anthu a Tubba (mafumu a kudziko la Yemen) ndi amene adalipo kale iwo asadadze? Tidawaononga. Ndithu iwo adali oipa.
تفسیرهای عربی:
وَمَا خَلَقۡنَا ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ وَمَا بَيۡنَهُمَا لَٰعِبِينَ
Ndipo sitidalenge thambo ndi nthaka ndi zimene zili pakati paizo, mwachibwana.
تفسیرهای عربی:
مَا خَلَقۡنَٰهُمَآ إِلَّا بِٱلۡحَقِّ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Sitidalenge ziwirizi koma mwachoonadi; koma anthu ambiri sakudziwa.
تفسیرهای عربی:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ مِيقَٰتُهُمۡ أَجۡمَعِينَ
Ndithu tsiku lachiweruziro ndiyo nthawi yawo onse (imene alonjezedwa).
تفسیرهای عربی:
يَوۡمَ لَا يُغۡنِي مَوۡلًى عَن مَّوۡلٗى شَيۡـٔٗا وَلَا هُمۡ يُنصَرُونَ
Tsiku limene m’bale sadzathandiza m’bale wake pa chilichonse (ku chilango cha Allah), ngakhale iwo sadzapulumutsidwa.
تفسیرهای عربی:
إِلَّا مَن رَّحِمَ ٱللَّهُۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Kupatula amene Allah adzawachitira chifundo. Ndithu Iye Ngwamphamvu zoposa, Ngwachisoni chosatha.
تفسیرهای عربی:
إِنَّ شَجَرَتَ ٱلزَّقُّومِ
Ndithu mtengo wa Zakkumi.
تفسیرهای عربی:
طَعَامُ ٱلۡأَثِيمِ
Ndi chakudya cha ochimwa.
تفسیرهای عربی:
كَٱلۡمُهۡلِ يَغۡلِي فِي ٱلۡبُطُونِ
(Kutentha kwake) ngati mtovu wosungunulidwa, (wotentha kwambiri;) udzakhala ukuwira mmimba.
تفسیرهای عربی:
كَغَلۡيِ ٱلۡحَمِيمِ
Monga kuwira kwa madzi otentha kwambiri.
تفسیرهای عربی:
خُذُوهُ فَٱعۡتِلُوهُ إِلَىٰ سَوَآءِ ٱلۡجَحِيمِ
(Kudzanenedwa): “Mgwireni; mkokereni (ndi kumponya) pakatikati pa Jahena!”
تفسیرهای عربی:
ثُمَّ صُبُّواْ فَوۡقَ رَأۡسِهِۦ مِنۡ عَذَابِ ٱلۡحَمِيمِ
“Kenako mthireni pamwamba pamutu wake chilango chamadzi otentha!”
تفسیرهای عربی:
ذُقۡ إِنَّكَ أَنتَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡكَرِيمُ
(Adzauzidwa mwachipongwe): “Lawa! Ndithu iwe ndiwe wamphamvu zambiri, wolemekezeka, (monga momwe udali kudzitamira muja).”
تفسیرهای عربی:
إِنَّ هَٰذَا مَا كُنتُم بِهِۦ تَمۡتَرُونَ
“Ndithu izi ndi zimene mudali kuzikaikira zija!”
تفسیرهای عربی:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي مَقَامٍ أَمِينٖ
Ndithu oopa Allah adzakhala pa malo a chitetezo.
تفسیرهای عربی:
فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Mminda ndi mu akasupe.
تفسیرهای عربی:
يَلۡبَسُونَ مِن سُندُسٖ وَإِسۡتَبۡرَقٖ مُّتَقَٰبِلِينَ
Adzavala (nsalu) za silika wopyapyala ndi silika wokhuthala uku atayang’anizana (nkhope).
تفسیرهای عربی:
كَذَٰلِكَ وَزَوَّجۡنَٰهُم بِحُورٍ عِينٖ
Umo ndi mmene zidzakhalire; ndipo tidzawakwatitsa ndi akazi okongola amaso aakulu.
تفسیرهای عربی:
يَدۡعُونَ فِيهَا بِكُلِّ فَٰكِهَةٍ ءَامِنِينَ
Mmenemo adzakhala akuitanitsa mtundu uliwonse wa zipatso, mwamtendere;
تفسیرهای عربی:
لَا يَذُوقُونَ فِيهَا ٱلۡمَوۡتَ إِلَّا ٱلۡمَوۡتَةَ ٱلۡأُولَىٰۖ وَوَقَىٰهُمۡ عَذَابَ ٱلۡجَحِيمِ
Sadzalawa imfa mmenemo, kupatula imfa yoyamba ija; ndipo adzawateteza kuchilango cha Jahena,
تفسیرهای عربی:
فَضۡلٗا مِّن رَّبِّكَۚ ذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Chifundo chochokera kwa Mbuye wako! Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu!
تفسیرهای عربی:
فَإِنَّمَا يَسَّرۡنَٰهُ بِلِسَانِكَ لَعَلَّهُمۡ يَتَذَكَّرُونَ
Ndithu taifewetsa (Qur’an) mchiyankhulo chako (cha Chiarabu) kuti akumbukire.
تفسیرهای عربی:
فَٱرۡتَقِبۡ إِنَّهُم مُّرۡتَقِبُونَ
Choncho yembekeza; iwonso akuyembekezera, (kodi ndani chimtsikire chilango pakati panu).
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی سوره: سوره دخان
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن