Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: AL-‘ÂDIYÂT   Verset:

AL-‘ÂDIYÂT

وَٱلۡعَٰدِيَٰتِ ضَبۡحٗا
Ndikulumbilira akavalo othamanga ali ndi phuma,
Les exégèses en arabe:
فَٱلۡمُورِيَٰتِ قَدۡحٗا
Ndi otulutsa moto ku zikhotwa (pomenyetsa miyendo m’miyala),
Les exégèses en arabe:
فَٱلۡمُغِيرَٰتِ صُبۡحٗا
Ndi othira nkhondo adani mmawa (dzuwa lisadatuluke),
Les exégèses en arabe:
فَأَثَرۡنَ بِهِۦ نَقۡعٗا
Ndi kuulutsa fumbi lambiri (kwa adani) nthawi imeneyo,
Les exégèses en arabe:
فَوَسَطۡنَ بِهِۦ جَمۡعًا
Ndikulowelera mkatikati mwa adani.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لِرَبِّهِۦ لَكَنُودٞ
Ndithu munthu ali wokanira Mbuye wake, (sathokoza Allah pa zimene amdalitsa nazo).[472]
[472] Tanthauzo la “kukanira Mbuye wake” ndi kuukanira mtendere Wake. Ndipo kukanira mtendere ndiko kusagwiritsira ntchito mtenderewo mnjira zabwino, monga m’mapemphero ndi zina zotero.
Les exégèses en arabe:
وَإِنَّهُۥ عَلَىٰ ذَٰلِكَ لَشَهِيدٞ
Ndithudi iye pa zimenezi ndi mboni (yodzichitira yekha kupyolera mzochitachita zake).
Les exégèses en arabe:
وَإِنَّهُۥ لِحُبِّ ٱلۡخَيۡرِ لَشَدِيدٌ
Ndipo ndithu iye ndiwokonda chuma kwambiri (ndiponso ngwamsulizo).[473]
[473] Kapena kuti ali wofunitsitsa chuma kwambiri; kumeneko ndikumangoti mtima dyokodyoko pachuma. Ukachipeza ndikumachichitira umbombo ndipo ndikumaganiza kuti chumacho nchopambana china chilichonse.
Les exégèses en arabe:
۞ أَفَلَا يَعۡلَمُ إِذَا بُعۡثِرَ مَا فِي ٱلۡقُبُورِ
Kodi sakudziwa zikadzatulutsidwa za m’manda,
Les exégèses en arabe:
وَحُصِّلَ مَا فِي ٱلصُّدُورِ
Ndikudzasonkhanitsidwa ndi kuonekera poyera zomwe zidali m’mitima?
Les exégèses en arabe:
إِنَّ رَبَّهُم بِهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّخَبِيرُۢ
Ndithu tsiku limenelo Mbuye wawo adzawadziwa kwambiri (ndikuwalongosolera zonse zochita zawo).[474]
[474] “Kuwadziwa kwambiri,” kukutanthauza kuti Iye ngodziwa zazikuluzikulu ndi zazing’onozing’ono zoonekera poyera ndi zobisika. Tsiku limenelo adzawalipira chilichonse chimene adachita.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: AL-‘ÂDIYÂT
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture