Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: AN-NABA’   Verset:

AN-NABA’

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ
۞ Kodi akufunsana zachiyani?
Les exégèses en arabe:
عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلۡعَظِيمِ
Za nkhani yayikulu ija.
Les exégèses en arabe:
ٱلَّذِي هُمۡ فِيهِ مُخۡتَلِفُونَ
Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]
[372] Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupilira Allah) adali kufunsana wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Qiyâma ndi uneneri wa Mtumiki Muhammad. Amafunsana kuti, “Kodi nzoona tidzauka m’manda, nanga nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?” Adali kufunsananso kuti, “Kodi zakuti Allah ndi Mmodzi ndi zoona?”
Les exégèses en arabe:
كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]
[373] Kuyankhula koti: “Kallaa” kwanenedwa kwambiri m’Qur’an. Tanthauzo lake nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]
[374] Allah, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi sadadziwebe mpaka pano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Allah, ndikuti Allah ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lachimaliziro; pamene munthu aliyense adzalipidwa pa zimene adachita? Basi tsiku lachimaliziro likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
Les exégèses en arabe:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ مِهَٰدٗا
Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]
[375] Kuyambira Ayah iyi, kudzafika Ayah 16, Allah akusonyeza anthu Ake madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka madalitso amenewa m’dziko sangawasiye anthu Ake m’kusokera popanda kuwatumizira munthu wowaongolera ku njira yabwino, ndikuwadziwitsa zamtendere wapadziko ndi tsiku lachimaliziro. Ndikuti Allah amene adapanga zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake. Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
Les exégèses en arabe:
وَٱلۡجِبَالَ أَوۡتَادٗا
Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?
Les exégèses en arabe:
وَخَلَقۡنَٰكُمۡ أَزۡوَٰجٗا
Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).
Les exégèses en arabe:
وَجَعَلۡنَا نَوۡمَكُمۡ سُبَاتٗا
Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).
Les exégèses en arabe:
وَجَعَلۡنَا ٱلَّيۡلَ لِبَاسٗا
Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).
Les exégèses en arabe:
وَجَعَلۡنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشٗا
Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;
Les exégèses en arabe:
وَبَنَيۡنَا فَوۡقَكُمۡ سَبۡعٗا شِدَادٗا
Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;
Les exégèses en arabe:
وَجَعَلۡنَا سِرَاجٗا وَهَّاجٗا
Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);
Les exégèses en arabe:
وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡمُعۡصِرَٰتِ مَآءٗ ثَجَّاجٗا
Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;
Les exégèses en arabe:
لِّنُخۡرِجَ بِهِۦ حَبّٗا وَنَبَاتٗا
Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).
Les exégèses en arabe:
وَجَنَّٰتٍ أَلۡفَافًا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ كَانَ مِيقَٰتٗا
Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.
Les exégèses en arabe:
يَوۡمَ يُنفَخُ فِي ٱلصُّورِ فَتَأۡتُونَ أَفۡوَاجٗا
Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.
Les exégèses en arabe:
وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ أَبۡوَٰبٗا
Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.
Les exégèses en arabe:
وَسُيِّرَتِ ٱلۡجِبَالُ فَكَانَتۡ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]
[376] Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati akhazikika monga m’mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje louluka ndi mphepo.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتۡ مِرۡصَادٗا
Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).
Les exégèses en arabe:
لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابٗا
Mbuto ya opyola malire.[377]
[377] Jahannam ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lachimaliziro. Apa Allah akutidziwitsa kuti Jahannam ndi malo amene akudikira akafiri kuti m’menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo powasonyeza zizindikiro zoti iwo ndi aneneri a Allah. Ndiponso kumulakwira Allah pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa Allah, kukana utumiki wa Mahammad (s.a.w) ndi kukana uthenga wa Qur’an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
Les exégèses en arabe:
لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحۡقَابٗا
Adzakhala m’menemo muyaya.
Les exégèses en arabe:
لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرۡدٗا وَلَا شَرَابًا
Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);
Les exégèses en arabe:
إِلَّا حَمِيمٗا وَغَسَّاقٗا
Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);
Les exégèses en arabe:
جَزَآءٗ وِفَاقًا
Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.
Les exégèses en arabe:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ لَا يَرۡجُونَ حِسَابٗا
Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);
Les exégèses en arabe:
وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابٗا
Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.
Les exégèses en arabe:
وَكُلَّ شَيۡءٍ أَحۡصَيۡنَٰهُ كِتَٰبٗا
Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.
Les exégèses en arabe:
فَذُوقُواْ فَلَن نَّزِيدَكُمۡ إِلَّا عَذَابًا
Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ مَفَازًا
Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.
Les exégèses en arabe:
حَدَآئِقَ وَأَعۡنَٰبٗا
Minda ndi zipatso za mphesa.
Les exégèses en arabe:
وَكَوَاعِبَ أَتۡرَابٗا
Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.
Les exégèses en arabe:
وَكَأۡسٗا دِهَاقٗا
Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.
Les exégèses en arabe:
لَّا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا كِذَّٰبٗا
Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.
Les exégèses en arabe:
جَزَآءٗ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابٗا
Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]
[378] Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri: Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Allah kumene anthu Ake abwino adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m’mene afotokozera mu Ayah iyi ndi msura zina. Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa (osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa zake. Koma mowa wa patsiku la Qiyâma udzakhala wopanda zoipa.
Les exégèses en arabe:
رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلرَّحۡمَٰنِۖ لَا يَمۡلِكُونَ مِنۡهُ خِطَابٗا
Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);
Les exégèses en arabe:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ صَفّٗاۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنۡ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحۡمَٰنُ وَقَالَ صَوَابٗا
Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.
Les exégèses en arabe:
ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلۡحَقُّۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا
Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).
Les exégèses en arabe:
إِنَّآ أَنذَرۡنَٰكُمۡ عَذَابٗا قَرِيبٗا يَوۡمَ يَنظُرُ ٱلۡمَرۡءُ مَا قَدَّمَتۡ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلۡكَافِرُ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ تُرَٰبَۢا
Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: AN-NABA’
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture