Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto * - Teburin Bayani kan wasu Fassarori


Fassarar Ma'anoni Sura: Suratu Al'nas   Aya:

Suratu Al'nas

قُلۡ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلنَّاسِ
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye (Mleri) wa anthu (Yemwe akulinganiza zinthu zawo).[503]
[503] Allah pokhala Mlengi wa anthu ndi amenenso amawalera kuyambira pamene ali m’mimba mpaka kumapeto a moyo wawo pano pa dziko. Kuwaleraku kuli muuzimu, mthupi, mu mpweya, ndi pa chilichonse chofunika pa moyo wawo. Kuonjezera pa zimenezi adawapatsa nzeru ndi kuwasonyeza njira zabwino za dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuzitsata njirazo. Adawasonyezanso njira zoipa za dziko lino lapansi ndi tsiku lachimaliziro. Ndipo adawalamula kuti azipewe njira zoipazo.
Tafsiran larabci:
مَلِكِ ٱلنَّاسِ
Mfumu ya anthu ( Imene iri ndi mphamvu yochita chirichonse pa iwo).
Tafsiran larabci:
إِلَٰهِ ٱلنَّاسِ
Wopembedzedwa wa anthu.
Tafsiran larabci:
مِن شَرِّ ٱلۡوَسۡوَاسِ ٱلۡخَنَّاسِ
Kuzoipa za mnong’onezi (yemwe amathira unong’onezi wake m’mitimaya anthu) yemwenso amabisala (posiya unong’onezi wake ngati mwini mtimawo atankumbukira Allah).[504]
[504] Mnong’onezi wa zoipa amene amabisala ndiye Satana, yemwe ntchito yake ndi kunong’oneza zoipa m’mitima ya anthu pofuna kuwasokeretsa ndi kuwaiwalitsa Allah. Koma akakumana ndi munthu wa chikhulupiliro cha mphamvu kapena yemwe amatamanda kwambiri Mbuye wake Allah, Satanayo amalephera ndipo amathawa; kubwerera m’mbuyo.
Tafsiran larabci:
ٱلَّذِي يُوَسۡوِسُ فِي صُدُورِ ٱلنَّاسِ
Yemwe amanong’oneza mzifuwa za anthu.
Tafsiran larabci:
مِنَ ٱلۡجِنَّةِ وَٱلنَّاسِ
Wochokera m’ziwanda ndi mwa anthu.”[505]
[505] Mchiyankhulo cha Chiarabu aliyense woipitsitsa amatchedwa “shaitan” satana, munthu kapena chiwanda. Satana wa muwanthu ndiwoipitsitsa kwambiri kwa anthu kuposa wa m’ziwanda.
Tafsiran larabci:
 
Fassarar Ma'anoni Sura: Suratu Al'nas
Teburin Jerin Sunayen Surori Lambar shafi
 
Fassarar Ma'anonin Alqura'ni - Fasaara da Yaren Pashto - Teburin Bayani kan wasu Fassarori

Fassarar Maanonin Alurani mai girma zuwa Yaren shishiwa wanda Khalid Ibrahim Bitala kwafi na Shekarar 2020 Miladiyya

Rufewa