क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद * - अनुवादों की सूची


अर्थों का अनुवाद सूरा: सूरा अल्-आ़दियात   आयत:

सूरा अल्-आ़दियात

وَٱلۡعَٰدِيَٰتِ ضَبۡحٗا
Ndikulumbilira akavalo othamanga ali ndi phuma,
अरबी तफ़सीरें:
فَٱلۡمُورِيَٰتِ قَدۡحٗا
Ndi otulutsa moto ku zikhotwa (pomenyetsa miyendo m’miyala),
अरबी तफ़सीरें:
فَٱلۡمُغِيرَٰتِ صُبۡحٗا
Ndi othira nkhondo adani mmawa (dzuwa lisadatuluke),
अरबी तफ़सीरें:
فَأَثَرۡنَ بِهِۦ نَقۡعٗا
Ndi kuulutsa fumbi lambiri (kwa adani) nthawi imeneyo,
अरबी तफ़सीरें:
فَوَسَطۡنَ بِهِۦ جَمۡعًا
Ndikulowelera mkatikati mwa adani.
अरबी तफ़सीरें:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لِرَبِّهِۦ لَكَنُودٞ
Ndithu munthu ali wokanira Mbuye wake, (sathokoza Allah pa zimene amdalitsa nazo).[472]
[472] Tanthauzo la “kukanira Mbuye wake” ndi kuukanira mtendere Wake. Ndipo kukanira mtendere ndiko kusagwiritsira ntchito mtenderewo mnjira zabwino, monga m’mapemphero ndi zina zotero.
अरबी तफ़सीरें:
وَإِنَّهُۥ عَلَىٰ ذَٰلِكَ لَشَهِيدٞ
Ndithudi iye pa zimenezi ndi mboni (yodzichitira yekha kupyolera mzochitachita zake).
अरबी तफ़सीरें:
وَإِنَّهُۥ لِحُبِّ ٱلۡخَيۡرِ لَشَدِيدٌ
Ndipo ndithu iye ndiwokonda chuma kwambiri (ndiponso ngwamsulizo).[473]
[473] Kapena kuti ali wofunitsitsa chuma kwambiri; kumeneko ndikumangoti mtima dyokodyoko pachuma. Ukachipeza ndikumachichitira umbombo ndipo ndikumaganiza kuti chumacho nchopambana china chilichonse.
अरबी तफ़सीरें:
۞ أَفَلَا يَعۡلَمُ إِذَا بُعۡثِرَ مَا فِي ٱلۡقُبُورِ
Kodi sakudziwa zikadzatulutsidwa za m’manda,
अरबी तफ़सीरें:
وَحُصِّلَ مَا فِي ٱلصُّدُورِ
Ndikudzasonkhanitsidwa ndi kuonekera poyera zomwe zidali m’mitima?
अरबी तफ़सीरें:
إِنَّ رَبَّهُم بِهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّخَبِيرُۢ
Ndithu tsiku limenelo Mbuye wawo adzawadziwa kwambiri (ndikuwalongosolera zonse zochita zawo).[474]
[474] “Kuwadziwa kwambiri,” kukutanthauza kuti Iye ngodziwa zazikuluzikulu ndi zazing’onozing’ono zoonekera poyera ndi zobisika. Tsiku limenelo adzawalipira chilichonse chimene adachita.
अरबी तफ़सीरें:
 
अर्थों का अनुवाद सूरा: सूरा अल्-आ़दियात
सूरों की सूची पृष्ठ संख्या
 
क़ुरआन के अर्थों का अनुवाद - चेवा अनुवाद - अनुवादों की सूची

पवित्र क़ुरआन के अर्थों का चेवा अनुवाद। अनुवाद ख़ालिद अबराहीम बेताला ने किया है। प्रति वर्ष 2020 ईसवी।

बंद करें