Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Al-Fīl   Ayah:

Surah Al-Fīl

أَلَمۡ تَرَ كَيۡفَ فَعَلَ رَبُّكَ بِأَصۡحَٰبِ ٱلۡفِيلِ
Kodi sudaone momwe Mbuye wako adawachitira eni njovu?[485]
[485] Sura imeneyi ikufotokoza mbiri imene idachitika pafupi ndi mzinda wa Makka mchaka cha 570 A.C. Dziko la Yemen lidali kulamulidwa ndi anthu a mtundu wa Ahabashi (ochokera ku Ethiopia). Iwowo pa nthawi imemeyo adali Akhristu. Bwana Mkubwa (Gavanala) waku Yemen pa nthawiyo adali Abraha. Abrahayu adafuna kuwaletsa Arabu kuti asamapite ku Makka kukayendera Kaaba. Pa chifukwa ichi adamanga tchalichi lalikulu kwambiri ndiponso lokongola lomwe lidali mu mzinda wa Sana‘a. Adawakakamiza Arabu kuyendera tchalichilo m’malo mopita ku Al-Kaaba. Pamene Arabu adamva zimenezi zidawanyansa. Ndipo adadza munthu wina wochokera ku fuko la Kinaana ndikukalowa m’tchalichimo ndikuchitiramo chimbudzi. Adatenga chimbudzicho ndikupakapaka m’zipupa za tchalichi lija chifukwa chonyansidwa ndi nyumbayo kuti siidali yoyenera kulowa m’malo mwa Kaaba. Pamene adaona izi, Abraha adakwiya kwambiri ndipo adalumbira kuti sachitira mwina koma kukagumula Kaaba. Adasonkhanitsa gulu la nkhondo lalikulu momwe mudalinso njovu zakuti zikamthandize kugumula Al-Kaaba. Choncho adauyatsa ulendo kupita ku mzinda wa Makka. Abraha pamene adafika ku Makka, adatumiza munthu kwa Arabu kuti awafotokozere kuti iye sadadze kudzawathira nkhondo, koma adadzera kudzagumula Al-Kaaba. Choncho adawapempha kuti amupatse danga kuti atero. Abdul Mutwalib adalamula anthu ake onse kuti achoke mu mzindawo apite ku mapiri. Iye adakalowa Mnyumba ya Kaaba ndipo adapempha Allah kuti ayipulumutse nyumba Yake yopatulika. Kenaka nayenso adawatsatira anzake ku mapiri kuja ndipo adangokhala phee, kuti amuone bwino yemwe adali kulimbana ndi Allah pomugumulira nyumba Yake. Abraha pamene adadziwa kuti Arabu atuluka mu mzindamo adakonzeka kulowa m’Makka ndi kugumula Al-Kaaba. Koma Allah Wamphamvu zonse adamutumizira gulu Lake la nkhondo monga momwe mukuwerengera pa Ayah yachitatu. Ankhondo a Abraha ena adafera pompo koma ena pamodzi ndi iye mwini, adathawa ndikukafera kwawo ku Yemen. pa chifukwa chimenechi Arabu ankachitcha chaka chimenechi kuti “chaka cha njovu.” Choncho mwana aliyense wobadwa m’chakachi ankatchedwa mwana wobadwa m’chaka cha njovu. Ndipo Mneneri Muhammad (s.a.w) adabadwa m’chaka chimenechi ndipo ankadziwikanso monga mwana wobadwa m’chaka cha njovu.
Tafsir berbahasa Arab:
أَلَمۡ يَجۡعَلۡ كَيۡدَهُمۡ فِي تَضۡلِيلٖ
Kodi sadachichite chiwembu chawo kukhala chosokera (chopanda phindu?)
Tafsir berbahasa Arab:
وَأَرۡسَلَ عَلَيۡهِمۡ طَيۡرًا أَبَابِيلَ
Ndipo adawatumizira magulumagulu a mbalame otsatizana. (ndipo adawazungulira mbali zonse).
Tafsir berbahasa Arab:
تَرۡمِيهِم بِحِجَارَةٖ مِّن سِجِّيلٖ
Zimawagenda ndi miyala ya moto.
Tafsir berbahasa Arab:
فَجَعَلَهُمۡ كَعَصۡفٖ مَّأۡكُولِۭ
Choncho adawachita ngati m’mera wodyedwa (ndi nyama ndi kulavulidwa).
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Al-Fīl
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup