Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Al-Ma'ārij   Ayah:

Surah Al-Ma'ārij

سَأَلَ سَآئِلُۢ بِعَذَابٖ وَاقِعٖ
Wopempha adapempha kuti chiwadzere msanga chilango chopezekacho, (m’kupempha kwa chipongwe ndi kotsutsa).
Tafsir berbahasa Arab:
لِّلۡكَٰفِرِينَ لَيۡسَ لَهُۥ دَافِعٞ
Kwa okanira palibe angachitsekereze.
Tafsir berbahasa Arab:
مِّنَ ٱللَّهِ ذِي ٱلۡمَعَارِجِ
Chochokera kwa Allah Mwini makwelero.
Tafsir berbahasa Arab:
تَعۡرُجُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَٱلرُّوحُ إِلَيۡهِ فِي يَوۡمٖ كَانَ مِقۡدَارُهُۥ خَمۡسِينَ أَلۡفَ سَنَةٖ
Angelo ndi Jiburil amakwera kwa Iye (Allah) m’tsiku lomwe kutalika kwake kuli ngati zaka zikwi makumi asanu (50 000).
Tafsir berbahasa Arab:
فَٱصۡبِرۡ صَبۡرٗا جَمِيلًا
Choncho, pirira (iwe Mtumiki (s.a.w) kupirira kwabwino,
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّهُمۡ يَرَوۡنَهُۥ بَعِيدٗا
Ndithu iwo akuliona (tsiku la Qiyâma) kuti lili kutali (silingachitike).
Tafsir berbahasa Arab:
وَنَرَىٰهُ قَرِيبٗا
Koma Ife tikuliona kuti lilipafupi (ndilochitika).
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَ تَكُونُ ٱلسَّمَآءُ كَٱلۡمُهۡلِ
Tsiku limene thambo lidzakhala ngati mtovu wosungunuka.
Tafsir berbahasa Arab:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya (wongouluka wokha).
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا يَسۡـَٔلُ حَمِيمٌ حَمِيمٗا
Ndipo m’bale sadzafunsa za m’bale wake.
Tafsir berbahasa Arab:
يُبَصَّرُونَهُمۡۚ يَوَدُّ ٱلۡمُجۡرِمُ لَوۡ يَفۡتَدِي مِنۡ عَذَابِ يَوۡمِئِذِۭ بِبَنِيهِ
Ngakhale adzawalole kuti aonane ndi kudziwana pakati pawo (sadzafunsana). Wochimwa adzalakalaka kuti akadaziwombola ku chilango cha tsiku limenelo ndi ana ake.
Tafsir berbahasa Arab:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَأَخِيهِ
Ndi mkazi wake, ndi m’bale wake.
Tafsir berbahasa Arab:
وَفَصِيلَتِهِ ٱلَّتِي تُـٔۡوِيهِ
Ndi akumtundu wake amene amamsunga.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا ثُمَّ يُنجِيهِ
Ndi (kulipira) zonse za m’dziko, kuti zimpulumutse.
Tafsir berbahasa Arab:
كَلَّآۖ إِنَّهَا لَظَىٰ
Iyayi, (siya iwe wamachimo zimene ukulakalakazo)! Ndithu umenewu ndi Moto wa malawi.
Tafsir berbahasa Arab:
نَزَّاعَةٗ لِّلشَّوَىٰ
Wosupula mwamphamvu khungu.
Tafsir berbahasa Arab:
تَدۡعُواْ مَنۡ أَدۡبَرَ وَتَوَلَّىٰ
Udzaitana (potchula dzina la aliyense) amene adachitembenuzira msana choona ndi kunyoza.
Tafsir berbahasa Arab:
وَجَمَعَ فَأَوۡعَىٰٓ
Adasonkhanitsa (chuma) ndi kusunga (m’nkhokwe zake popanda kuperekera chopereka cha Allah).
Tafsir berbahasa Arab:
۞ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ خُلِقَ هَلُوعًا
Ndithu munthu walengedwa kukhala wosapirira.
Tafsir berbahasa Arab:
إِذَا مَسَّهُ ٱلشَّرُّ جَزُوعٗا
Mavuto akamkhudza amada nkhawa.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِذَا مَسَّهُ ٱلۡخَيۡرُ مَنُوعًا
Koma zabwino zikamkhudza amamana (ena ndi kuiwala mavuto amene adali nawo).
Tafsir berbahasa Arab:
إِلَّا ٱلۡمُصَلِّينَ
Kupatula opemphera Swala, (iwo alibe mbiri zoipazi).
Tafsir berbahasa Arab:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ دَآئِمُونَ
Iwo amene sadukiza mapemphero awo a swala; (sakuwaleka ngakhale zivute chotani).
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ فِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ مَّعۡلُومٞ
Ndi amene mchuma chawo muli gawo lodziwika (Zakaat),
Tafsir berbahasa Arab:
لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
La wopempha ndi wosapempha.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ يُصَدِّقُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndi amene akuvomereza za tsiku la malipiro (ndi kumalikonzekera.)
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ هُم مِّنۡ عَذَابِ رَبِّهِم مُّشۡفِقُونَ
Ndi iwo amene akuopa chilango chochokera kwa Mbuye wawo.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ عَذَابَ رَبِّهِمۡ غَيۡرُ مَأۡمُونٖ
Ndithu chilango cha Mbuye wawo nchosapulumuka nacho (munthu woipa).
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِفُرُوجِهِمۡ حَٰفِظُونَ
Ndiponso iwo amene akusunga umaliseche wawo (posachita chiwerewere),
Tafsir berbahasa Arab:
إِلَّا عَلَىٰٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ أَوۡ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ فَإِنَّهُمۡ غَيۡرُ مَلُومِينَ
Kupatula kwa akazi awo ndi amene manja awo akumanja apeza; ndithu pazimenezo iwo sangadzudzulidwe.
Tafsir berbahasa Arab:
فَمَنِ ٱبۡتَغَىٰ وَرَآءَ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡعَادُونَ
Koma amene angafune (zina) kusiya zimenezi iwowo ndiwo olumpha malire.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِأَمَٰنَٰتِهِمۡ وَعَهۡدِهِمۡ رَٰعُونَ
Ndi iwo amene amasunga mwaubwino zimene amasungitsidwa ndi zimene alonjeza.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ هُم بِشَهَٰدَٰتِهِمۡ قَآئِمُونَ
Ndi iwo amene amaima molungama popereka umboni wawo.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ يُحَافِظُونَ
Ndiponso iwo amene amasunga (mwaubwino) mapemphero awo a swala.
Tafsir berbahasa Arab:
أُوْلَٰٓئِكَ فِي جَنَّٰتٖ مُّكۡرَمُونَ
Amene ali ndi mbiri zimenezi adzakhala m’Minda (yamtendere) ali olemekezedwa.
Tafsir berbahasa Arab:
فَمَالِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ قِبَلَكَ مُهۡطِعِينَ
Kodi kuli chiyani kwa amene akana (chikhulupiliro) akuthamangira kwa iwe (maso ali pamtunda)?
Tafsir berbahasa Arab:
عَنِ ٱلۡيَمِينِ وَعَنِ ٱلشِّمَالِ عِزِينَ
Atakuzungulira ena chakumanja ena chakumanzere.
Tafsir berbahasa Arab:
أَيَطۡمَعُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُدۡخَلَ جَنَّةَ نَعِيمٖ
Kodi akulakalaka aliyense mwa iwo kuti akalowetsedwe ku Munda wamtendere?
Tafsir berbahasa Arab:
كَلَّآۖ إِنَّا خَلَقۡنَٰهُم مِّمَّا يَعۡلَمُونَ
Asiye (kukhumba kwawo kokalowa ku Munda wamtendere)! Ndithu Ife tidawalenga kuchokera m’zimene akudziwa (madzi opanda pake).
Tafsir berbahasa Arab:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِرَبِّ ٱلۡمَشَٰرِقِ وَٱلۡمَغَٰرِبِ إِنَّا لَقَٰدِرُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kuvuma ndi kuzambwe konse ndithu Ndife Wokhoza.
Tafsir berbahasa Arab:
عَلَىٰٓ أَن نُّبَدِّلَ خَيۡرٗا مِّنۡهُمۡ وَمَا نَحۡنُ بِمَسۡبُوقِينَ
Kuwasintha ndi kudzetsa abwino kuposa iwo; Ife palibe (chilichonse) chotipambana.
Tafsir berbahasa Arab:
فَذَرۡهُمۡ يَخُوضُواْ وَيَلۡعَبُواْ حَتَّىٰ يُلَٰقُواْ يَوۡمَهُمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Asiye azingolankhula zopanda pake ndi kumangosewera mpaka adzakumane ndi tsiku lawo limene akulonjezedwa.
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَ يَخۡرُجُونَ مِنَ ٱلۡأَجۡدَاثِ سِرَاعٗا كَأَنَّهُمۡ إِلَىٰ نُصُبٖ يُوفِضُونَ
Tsiku limene adzatuluke m’manda uku akuthamanga (kudza kwa woitana) ngati kuti akuthamangira kumafano awo (amene adali kuwapembedza).
Tafsir berbahasa Arab:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۚ ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلَّذِي كَانُواْ يُوعَدُونَ
Maso awo ali zyoli, (osatha kuwakweza); kuyaluka kutawaphimba! Limenelo ndilo tsiku lomwe adali kulonjezedwa (pomwe adali padziko lapansi.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Al-Ma'ārij
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup