Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: Al-‘Alaq   Versetto:

Al-‘Alaq

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
Esegesi in lingua araba:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِنۡ عَلَقٍ
Adalenga munthu kuchokera ku magazi owundana.[461]
[461] Madzi ambewu ya munthu, pambuyo pokhazikika mchiberekero kwa masiku makumi anayi, amatembenuka ndikukhala magazi. Ili ndilo tanthauzo la Ayah imeneyi.
Esegesi in lingua araba:
ٱقۡرَأۡ وَرَبُّكَ ٱلۡأَكۡرَمُ
Werenga! Ndipo Mbuye wako ndi Wopereka kwambiri.[462]
[462] Ayah 3 ndi 5 Mtumiki (s.a.w) akuyankhidwa pa kunena kwake kwa kuti: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Choncho Allah akumuuza kuti Iye ndi Mfulu weniweni, ndi Yemwe adawaphunzitsa anthu kulemba ndi cholembera ndi zonse zomwe sadali kuzidziwa. Kwa ufulu Wake wochuluka ndi mphamvu Zake pa chilichonse, sichovuta kwa Iye (Allah) kumphunzitsa Mtumiki Wake kuwerenga molakatula.
Esegesi in lingua araba:
ٱلَّذِي عَلَّمَ بِٱلۡقَلَمِ
Yemwe waphunzitsa (munthu kulemba) ndi cholembera.
Esegesi in lingua araba:
عَلَّمَ ٱلۡإِنسَٰنَ مَا لَمۡ يَعۡلَمۡ
Waphunzitsa munthu zinthu (zambiri) zomwe (iye) sadali kuzidziwa.
Esegesi in lingua araba:
كَلَّآ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَيَطۡغَىٰٓ
Zoona ndithu koma munthu akupyola malire (podzikweza).
Esegesi in lingua araba:
أَن رَّءَاهُ ٱسۡتَغۡنَىٰٓ
Chifukwa chodziona kuti walemera.
Esegesi in lingua araba:
إِنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلرُّجۡعَىٰٓ
Palibe chikaiko, (iwe Mneneri (s.a.w) kobwerera (onse) nkwa Mbuye wako basi; (adzawaukitsa).[463]
[463] Tanthauzo lake nkuti musanyengedwe ndi chumacho chifukwa chakuti, popanda chikaiko, mubwerera kwa Mbuye wanu ndipo chumacho sichidzakuthandizani chilichonse pa maso Pake.
Esegesi in lingua araba:
أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يَنۡهَىٰ
Kodi wamuona yemwe akuletsa,
Esegesi in lingua araba:
عَبۡدًا إِذَا صَلَّىٰٓ
Kapolo (wa Allah) akamapemphera?
Esegesi in lingua araba:
أَرَءَيۡتَ إِن كَانَ عَلَى ٱلۡهُدَىٰٓ
Tandiuza ngati ali pachiongoko?
Esegesi in lingua araba:
أَوۡ أَمَرَ بِٱلتَّقۡوَىٰٓ
Kapena kuti akulamulira zoopa Allah?
Esegesi in lingua araba:
أَرَءَيۡتَ إِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰٓ
Tandiuza (za woletsayo) ngati akutsutsa (zimene wadza nazo Mneneri) ndikunyoza (chikhulupiliro ndi ntchito yabwino)?
Esegesi in lingua araba:
أَلَمۡ يَعۡلَم بِأَنَّ ٱللَّهَ يَرَىٰ
Kodi sakudziwa kuti Allah akuona (machitidwe ake. Ndipo adzamlipira)?
Esegesi in lingua araba:
كَلَّا لَئِن لَّمۡ يَنتَهِ لَنَسۡفَعَۢا بِٱلنَّاصِيَةِ
Ayi ndithu ngati sasiya timukoka tsitsi lapatsumba (tiligwira mwamphamvu tsumba lake ndikukamponya ku Moto).
Esegesi in lingua araba:
نَاصِيَةٖ كَٰذِبَةٍ خَاطِئَةٖ
Tsumba labodza (ndiponso) lamachimo.
Esegesi in lingua araba:
فَلۡيَدۡعُ نَادِيَهُۥ
Basi aliitane gulu lakelo, (la amene amakhala nawo pabwalo kuti amthandize pano pa dziko kapena tsiku lachimaliziro),
Esegesi in lingua araba:
سَنَدۡعُ ٱلزَّبَانِيَةَ
Nafe tiitana azabaniya (angelo a ku Moto).
Esegesi in lingua araba:
كَلَّا لَا تُطِعۡهُ وَٱسۡجُدۡۤ وَٱقۡتَرِب۩
Ayi ndithu usamumvere (pa zimene akukuletsazo); koma gwetsa nkhope yako pansi, ndipo dziyandikitse kwa Mbuye wako.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: Al-‘Alaq
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi