クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 章: 慈善章   節:

慈善章

أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يُكَذِّبُ بِٱلدِّينِ
Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
[487] Sura imeneyi ikufotokoza m’mene alili makhalidwe a anthu ambiri, ngakhale amene amadzitcha kuti ndi Asilamu. Aliyense amene ali ndi makhalidwe otere ndiye kuti sakhulupilira za tsiku la chiweruziro. Akadakhala kuti akukhulupilira za tsikuli, sibwenzi akusiya kuwachitira za chifundo osauka ndi amasiye. Sapereka chithandizo ngakhale kulimbikitsa ena ngati iye alibe.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَذَٰلِكَ ٱلَّذِي يَدُعُّ ٱلۡيَتِيمَ
Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَوَيۡلٞ لِّلۡمُصَلِّينَ
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
アラビア語 クルアーン注釈:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَن صَلَاتِهِمۡ سَاهُونَ
Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]
[488] Kuchitira mphwayi mapemphero (Swala), kumeneku ndiko kupemphera modukizadukiza. Tsiku lina nkupempherapo, tsiku lina ayi. Kapenanso kupemphera modzionetsera kwa anthu (riyaa).
アラビア語 クルアーン注釈:
ٱلَّذِينَ هُمۡ يُرَآءُونَ
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
[489] Riyaa ndiko kuchita ntchito yabwino ndicholinga choonetsa anthu, kuti akuone kuti ndiwe wabwino, mwina kuti ukhale wokondedwa ndi anthu. Kapenanso kuti upeze za m’matumba mwawo. Amenewa ndi machitidwe a “Shiriki” (kum’phatikiza Allah ndi zolengedwa Zake pa mapemphero) ndiponso ndi njira yobera anthu.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَيَمۡنَعُونَ ٱلۡمَاعُونَ
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 章: 慈善章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる