وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی الطارق   ئایه‌تی:

سورەتی الطارق

وَٱلسَّمَآءِ وَٱلطَّارِقِ
Ndikulumbilira ku mwamba ndi Nyenyezi imene imadza usiku,
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلطَّارِقُ
Chitakudziwitse nchiyani za Nyenyezi yodza usikuyo?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلنَّجۡمُ ٱلثَّاقِبُ
Imeneyo ndi nyenyezi yowala kwambiri (mu mdima).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِن كُلُّ نَفۡسٖ لَّمَّا عَلَيۡهَا حَافِظٞ
Ndithudi palibe mzimu uliwonse koma uli ndi msungi wake (amene akuuyang’anira ndikulemba zonse zochita zake).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ مِمَّ خُلِقَ
Aganizire munthu, kodi adalengedwa kuchokera kuchiyani?
تەفسیرە عەرەبیەکان:
خُلِقَ مِن مَّآءٖ دَافِقٖ
Adalengedwa kuchokera ku madzi ofwamphuka.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَخۡرُجُ مِنۢ بَيۡنِ ٱلصُّلۡبِ وَٱلتَّرَآئِبِ
Amatuluka kuchokera pakati pa mafupa a msana (wa mwamuna) ndi chifuwa (cha mkazi).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّهُۥ عَلَىٰ رَجۡعِهِۦ لَقَادِرٞ
Ndithu Iye ndiwakutha, kumbwezeranso (ku moyo pa mbuyo pa imfa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
يَوۡمَ تُبۡلَى ٱلسَّرَآئِرُ
Tsiku limene zobisika zonse zidzaonekera poyera.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَمَا لَهُۥ مِن قُوَّةٖ وَلَا نَاصِرٖ
Munthu sadzakhala ndi mphamvu (tsiku limenelo zodzitetezera iye mwini) ndiponso sadzakhala ndi mtetezi.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلسَّمَآءِ ذَاتِ ٱلرَّجۡعِ
Ndikulumbiliranso mitambo yobweretsabweretsa mvula.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلۡأَرۡضِ ذَاتِ ٱلصَّدۡعِ
Ndi nthaka imene imang’ambika (potulutsa m’mera),
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلٞ فَصۡلٞ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndi mawu olekanitsa (Haqq ndi Bâtwil - choona ndi chonama).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا هُوَ بِٱلۡهَزۡلِ
Imeneyi sinkhambakamwa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّهُمۡ يَكِيدُونَ كَيۡدٗا
Ndithudi iwo akukonza chiwembu.[416]
[416] (Ndime15-16) Tanthauzo lake ndikuti akafiri (osakhulupilira) akuchita ndale kuti azimitse dangalira la Qur’an ndikuyesetsa kuti awabweze amene adakhulupilira ndiponso ndikufuna kumupha Mneneri (s.a.w). Naye Allah akuwachitira ndale powaonongera ziwembu zawo zomwe amazikonza.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأَكِيدُ كَيۡدٗا
Nanenso ndikuwakonzera chiwembu (champhamvu kwambiri chimene sangathe kuchipewa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَمَهِّلِ ٱلۡكَٰفِرِينَ أَمۡهِلۡهُمۡ رُوَيۡدَۢا
Basi, apatse nthawi osakhulupirira apatse nthawi pang’ono, (aona posachedwa).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی الطارق
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن