وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی اللیل   ئایه‌تی:

سورەتی اللیل

وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَغۡشَىٰ
Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ
Ndi usana pamene kukuyera.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰٓ
Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ سَعۡيَكُمۡ لَشَتَّىٰ
Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446]
[446] Tanthauzo lake ndikuti mwa anthu alipo ena amene amachita zabwino ndipo ena amachita zoipa. Ena amagwira ntchito zothandiza pambuyo pa imfa pamodzi ndi kutumikira Allah. Ndipo pali ena omwe amangokhala otanganidwa ndi zadziko lapansi. Ena amachita zinthu zopindula pomwe ena satero.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَمَّا مَنۡ أَعۡطَىٰ وَٱتَّقَىٰ
Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447]
[447] Tanthauzo lake apa ndikupereka chuma ndi kudzipereka pa zauzimu. Ndiye kuti munthu agwiritsire ntchito chuma chake m’njira ya Allah ndiponso kwa anthu anzake. Ayeneranso kudzipereka iye mwini pa moyo wauzimu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَصَدَّقَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448]
[448] Tanthauzo la “Kuvomereza zinthu zabwino” ndiko kugwirizana nazo zimene Allah walamula, chifukwa chakuti Iye amalamula zinthu zabwino zokhazokha ndikuletsa zoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡيُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449]
[449] Tanthauzo la Ayah imeneyi ndikuti: Timufewetsera njira yochitira zinthu zabwino mpaka kufikira kuti akapanda kuchita chinthu chabwino sapeza mtendere mu mtima mwake.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana;
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَكَذَّبَ بِٱلۡحُسۡنَىٰ
Ndi kumatsutsa zinthu zabwino,
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلۡعُسۡرَىٰ
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku mavuto (a muyaya).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا يُغۡنِي عَنۡهُ مَالُهُۥٓ إِذَا تَرَدَّىٰٓ
Ndipo chuma chake sichidzamthandiza (chilichonse) akadzagwera ku Moto.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِنَّ عَلَيۡنَا لَلۡهُدَىٰ
Ndithu Ife ndi amene timawalongosolera anthu njira yabwino ndi njira yoipa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَإِنَّ لَنَا لَلۡأٓخِرَةَ وَٱلۡأُولَىٰ
Ndipo ndithu moyo womaliza ndi moyo woyamba uli m’manja mwathu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
فَأَنذَرۡتُكُمۡ نَارٗا تَلَظَّىٰ
Basi, ndikukuchenjezani za Moto woyaka mwa mphamvu.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
لَا يَصۡلَىٰهَآ إِلَّا ٱلۡأَشۡقَى
Sakaulowa koma (kafiri) woipitsitsa kwambiri.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِي كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ
Yemwe amatsutsa (choona) ndi kunyoza (zisonyezo za Allah).
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَسَيُجَنَّبُهَا ٱلۡأَتۡقَى
Koma yemwe akuopa Allah kwambiri akatalikitsidwa ndi Moto.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
ٱلَّذِي يُؤۡتِي مَالَهُۥ يَتَزَكَّىٰ
Amene akupereka chuma chake ndi cholinga chodziyeretsa.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَمَا لِأَحَدٍ عِندَهُۥ مِن نِّعۡمَةٖ تُجۡزَىٰٓ
Ndipo palibe aliyense kwa iye, amene adamchitira za chifundo zomwe zikulipidwa.[450]
[450] (Ndime 19-20)Tanthauzo la ma Ayah awiriwa nkuti munthu uyu sakupereka chuma chake chifukwa chobwezera chifundo cha anthu, kapena kuti adzamubwezerenso iye chifundo, koma akupereka chifukwa chofuna chikondi cha Mbuye wake basi.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
إِلَّا ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Koma (akuchita zimenezi) kufuna chikondi cha Mbuye wake Wapamwambamwamba.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
وَلَسَوۡفَ يَرۡضَىٰ
Ndipo posachedwa adzasangalala.[451]
[451] Tanthauzo lake apa ndikuti Allah adzamukondweretsa ndi malipiro Ake abwino kufikira munthuyo adzakondwera. Ma Ayah, kuyambira 17 mpaka 21, adatsika chifukwa cha Sayyidina Abu Bakr (r.a) yemwe adali kupereka chuma chake powagula akapolo omwe adali kuzunzidwa ndi mabwana awo chifukwa cholowa Chisilamu, pambuyo pake amawapatsa ufulu. Ndipo m’modzi wa iwowa ndi Sayyidina Bilal (r.a) amene adali Muazzini wa Mneneri Muhammad (s.a.w). Chomwechonso Ayah zimenezi zikumkhudza aliyense amene akugwiritsa ntchito chuma chake mnjira yopulumutsira chipembedzo.
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان سوره‌تی: سورەتی اللیل
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن