വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ പരിഭാഷ * - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക


പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: സൂറത്തുത്തക്വീർ   ആയത്ത്:

സൂറത്തുത്തക്വീർ

إِذَا ٱلشَّمۡسُ كُوِّرَتۡ
Pamene dzuwa lidzakulungidwe (ndikuchotsedwa kuwala kwake),[388]
[388] Surah zambiri zimene zidavumbulutsidwa ku Makka zimanena zododometsa za tsiku lachimaliziro.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلنُّجُومُ ٱنكَدَرَتۡ
Ndi pamene nyenyezi zidzathothoke (ndi kuchoka dangalira lake),
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡجِبَالُ سُيِّرَتۡ
Ndi pamene mapiri adzayendetsedwe (kuchoka mmalo mwake),[389]
[389] Tsiku limenelo mapiri adzakhala osalimba ngati thonje limene likungouluka ndi mphepo.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡعِشَارُ عُطِّلَتۡ
Ndi pamene ngamira zabere lamiyezi khumi zidzasiidwe (zopanda oziyang’anira),[390]
[390] Ngamira za bere ndi chuma cha mtengo wapatali kwa Aarabu. Akuuzidwa apa kuti tsiku limenelo adzazisiya osazilabadira konse.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡوُحُوشُ حُشِرَتۡ
Ndi pamene nyama za mtchire zidzasonkhanitsidwe pamodzi (kuchokera mmalo osiyanasiyana chifukwa chakuopsa kwakukulu kwa tsikulo),[391]
[391] Mwa zina zododometsa pa tsiku limenelo ndi nyama za mtchire kusonkhanitsidwa pamodzi popanda kumenyana kapena kudyana.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡبِحَارُ سُجِّرَتۡ
Ndi pamene nyanja zidzayatsidwe moto,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلنُّفُوسُ زُوِّجَتۡ
Ndi pamene mizimu idzalumikizidwe (ndi matupi ake),
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡمَوۡءُۥدَةُ سُئِلَتۡ
Ndi pamene mwana wamkazi yemwe adaikidwa m’manda wamoyo adzafunsidwe,[392]
[392] (Ndime 8-9) Ma Ayah awiriwa akufotokoza momwe Aarabu adalili Usilamu usadabwere. Munthu ankati akapatsidwa mphatso ya mwana wa mkazi adali kukhumudwa ndi kudandaula kwambiri. Ankanena kuti asungwana ngopanda phindu ndipo kuti kudali kuononga zinthu pakumulera, kumudyetsa, ndi kumuveka. Ndipo akadzakhala wachiwerewere adzakhala manyazi aakulu kwa makolo ake. Pamene chidadza chisilamu chidathetsa mkhalidwewu. Ndipo apa Allah akutisonyeza kuti patsiku limenelo, la chiweruziro, mwana uja adaikidwa wa moyo, adzafunsidwa kuti adaphedwa ndi tchimo lanji. Iye adzayankha kuti sadachite tchimo lililonse koma adaphedwa mopanda chilungamo.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
بِأَيِّ ذَنۢبٖ قُتِلَتۡ
Ndi tchimo lanji adaphedwera?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلصُّحُفُ نُشِرَتۡ
Ndi pamene makalata (momwe mudalembedwa zochita za aliyense) adzatambasulidwe ndi kugawidwa (kuti awerengedwe),[393]
[393] Awa ndi makalata achiwerengero momwe mwalembedwa zabwino za munthu ndi zoipa zake. Tsiku limenelo munthu aliyense adzapatsidwa yake kalata kuti aone iye mwini zoipa ndi zabwino zake.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلسَّمَآءُ كُشِطَتۡ
Ndi pamene thambo lidzayalulidwe (kuchoka mmalo mwake),
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡجَحِيمُ سُعِّرَتۡ
Ndi pamene Jahena idzasonkhezeredwe mwamphamvu,[394]
[394] (Ndime12-13) Tsiku limenelo Jannah idzayandikitsidwa kwa ochita zabwino ndiponso Moto udzayandikitsidwa kwa ochita zoipa kuti aone kumalo kwake.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَإِذَا ٱلۡجَنَّةُ أُزۡلِفَتۡ
Ndi pamene Jannah idzayandikitsidwe,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
عَلِمَتۡ نَفۡسٞ مَّآ أَحۡضَرَتۡ
(Zikadzachitika zimenezi) mzimu uliwonse udzadziwa zimene wabweretsa (zabwino ndi zoipa).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِٱلۡخُنَّسِ
Ndikulumbilira nyenyezi zimene zimabwerera masana ndi kutulukanso usiku.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
ٱلۡجَوَارِ ٱلۡكُنَّسِ
Zomwe zimayenda kenako nkubisika,
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا عَسۡعَسَ
Ndi usiku pamene ukulowa.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَا تَنَفَّسَ
Ndi m’mawa kukamacha;
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلُ رَسُولٖ كَرِيمٖ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi liwu la mthenga wa Allah (Jibril) wolemekezeka,[395]
[395] (Ndime 19-20) Mthenga wolemekezeka womveredwa uko kumwamba ndi Jibril (Gabriele) yemwe ndi wamkulu wa angelo onse. Iye ndiyemwe adali kubweretsa Qur’an mwa lamulo la Allah kwa Mneneri Wake Muhammad (s.a.w). Ndipo ulemelero wa Qur’an ndi ulemelero wa Mneneri (s.a.w) chifukwa choti munthu wolemekezeka amamutumizira mthenga wolemekezekanso. Ndipo uthenga wabwino umapatsidwa kwa Mneneri wabwino woposa onse.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
ذِي قُوَّةٍ عِندَ ذِي ٱلۡعَرۡشِ مَكِينٖ
Mwini mphamvu ndi mwini ulemelero kwa Mwini Arsh (Mpando wa chifumu),
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
مُّطَاعٖ ثَمَّ أَمِينٖ
Womveredwa kumeneko ndiponso wokhulupirika (pachivumbulutso).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَا صَاحِبُكُم بِمَجۡنُونٖ
Ndipo m’bale wanuyu siwamisala ayi.[396]
[396] (Ndime 22-25) Anthu okanira pamene adasowa chonena kwa mneneri (s.a.w) adali kunena nkhani zabodza kuti Mtumiki (s.a.w) wapenga ndikuti zomwe akuyankhula sadapatsidwe ndi Jibril.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَلَقَدۡ رَءَاهُ بِٱلۡأُفُقِ ٱلۡمُبِينِ
Ndithu ndikulumbira kuti (iye Mtumiki) (s.a.w) adamuona (Jibril) mchizimezime (chakum’mawa) chooneka bwino.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَا هُوَ عَلَى ٱلۡغَيۡبِ بِضَنِينٖ
Ndipo sali iye (Mtumiki) waumbombo ndi chivumbulutso (koma amafikitsa zonse ndi kuziphunzitsa kwa anthu).
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَا هُوَ بِقَوۡلِ شَيۡطَٰنٖ رَّجِيمٖ
(Chivumbulutso chomwe chavumbulutsidwachi kwa iye) si mawu a satana wothamangitsidwa (mchifundo cha Allah);
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
فَأَيۡنَ تَذۡهَبُونَ
Nanga mukupita kuti?
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
إِنۡ هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
(Qur’ani) iyi sichina koma ndi chikumbutso cha zolengedwa zonse.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَسۡتَقِيمَ
Kwa yemwe mwa inu akufuna kuyenda mu njira yoongoka.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَا تَشَآءُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُ رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo simungafune chinthu mwa inu nokha pokhapokha atafuna Allah Mbuye wa zolengedwa zonse.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
 
പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: സൂറത്തുത്തക്വീർ
സൂറത്തുകളുടെ സൂചിക പേജ് നമ്പർ
 
വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ പരിഭാഷ - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക

പരിശുദ്ധ ഖുർആൻ ആശയ വിവർത്തനം ചെവ്വ ഭാഷയിൽ, പരിഭാഷ: ഖാലിദ് ഇബ്റാഹീം പെറ്റാല, 2020 പതിപ്പ്

അടക്കുക