د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: عبس   آیت:

عبس

عَبَسَ وَتَوَلَّىٰٓ
Adachita tsinya (Mneneri) ndi kuyang’ana kumbali.[384]
[384] Tsiku lina Mneneri (s.a.w) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza. Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum. Sadadziwe kuti Mneneri (s.a.w) ali wotanganidwa. Adamukuwira: “E Iwe Mneneri wa Allah! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Allah.” Ndipo ankangomubwerezera-bwerezera mawu amenewa. Mneneri (s.a.w) pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, adamchitira tsinya wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; sadamumvere. Basi pamenepa Allah akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
عربي تفسیرونه:
أَن جَآءَهُ ٱلۡأَعۡمَىٰ
Chifukwa chakuti adamdzera wakhungu (kudzamfunsa zokhudzana ndi chipembedzo chake pamene iye adali kuyankhula ndi atsogoleri Achiquraishi).
عربي تفسیرونه:
وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّهُۥ يَزَّكَّىٰٓ
Nanga chingakudziwitse nchiyani kuti mwina iye angadziyeretse (pomvera ulaliki wako watsopano)?
عربي تفسیرونه:
أَوۡ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ ٱلذِّكۡرَىٰٓ
Kapena akumbukira, ndipo kukumbukirako kumthandiza?
عربي تفسیرونه:
أَمَّا مَنِ ٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma amene wadzikwaniritsa (ndi chuma chake ndi mphamvu zake),
عربي تفسیرونه:
فَأَنتَ لَهُۥ تَصَدَّىٰ
Ameneyo ndi yemwe ukumchitira chidwi.
عربي تفسیرونه:
وَمَا عَلَيۡكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ
Palibe chilichonse pa iwe ngati sadziyeretsa.
عربي تفسیرونه:
وَأَمَّا مَن جَآءَكَ يَسۡعَىٰ
Koma amene wakudzera uku akuthamanga (kufuna maphunziro ndi chiongoko),
عربي تفسیرونه:
وَهُوَ يَخۡشَىٰ
Ndipo iye akuopa (Allah mu mtima mwake).
عربي تفسیرونه:
فَأَنتَ عَنۡهُ تَلَهَّىٰ
Za iye, iwe sukusamala, (ukuyikira chidwi kwa wina).
عربي تفسیرونه:
كَلَّآ إِنَّهَا تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithudi iyi (Qur’an) ndi chikumbutso (chenjezo).[385]
[385] (Ndime 11-16) Apa Allah akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur’an ndi ulaliki chabe, amene afuna kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake. Ndiponso adamufotokozera kuti Qur’an idachokera m’mabuku olemekezeka; idachokera ku “Lauhil-Mahfudh” mabuku omwe ali m’manja mwa Angelo olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
عربي تفسیرونه:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Basi, amene wafuna alangizika (ndi Qur’an, ndipo amene sakufuna msiye).
عربي تفسیرونه:
فِي صُحُفٖ مُّكَرَّمَةٖ
(Malangizowa akuchokera) mmakalata olemekezeka (kwa Allah);
عربي تفسیرونه:
مَّرۡفُوعَةٖ مُّطَهَّرَةِۭ
Apamwamba ndiponso oyeretsedwa (kumbiri iliyonse yopunguka);
عربي تفسیرونه:
بِأَيۡدِي سَفَرَةٖ
Omwe ali m’manja mwa Alembi (Angelo).
عربي تفسیرونه:
كِرَامِۭ بَرَرَةٖ
Olemekezeka, omvera.
عربي تفسیرونه:
قُتِلَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَآ أَكۡفَرَهُۥ
Waonongeka (watembeleredwa) munthu. Nkotani kusayamika kwake kotereku.
عربي تفسیرونه:
مِنۡ أَيِّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥ
Kuchokera mchinthu chanji chimene iye adamulenga.
عربي تفسیرونه:
مِن نُّطۡفَةٍ خَلَقَهُۥ فَقَدَّرَهُۥ
Kuchokera ku dontho lamadzi (onyozeka) adamulenga, namkonzeratu mkalengedwe kosiyanasiyana.
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ ٱلسَّبِيلَ يَسَّرَهُۥ
Kenako adamfewetsera njira (yotulukira m’mimba mwa mai ake).
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ أَمَاتَهُۥ فَأَقۡبَرَهُۥ
Ndipo amamchititsa kuti amwalire namukumbula m’manda,
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ إِذَا شَآءَ أَنشَرَهُۥ
Kenako akadzafuna adzamuukitsa (pambuyo pa imfa).
عربي تفسیرونه:
كَلَّا لَمَّا يَقۡضِ مَآ أَمَرَهُۥ
Ayi ndithu (munthu) sanakwaniritsebe zimene adamulamula Mbuye wake (Allah chingakhale wakhala nthawi yaitali pa dziko lapansi).
عربي تفسیرونه:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ إِلَىٰ طَعَامِهِۦٓ
Alingalire munthu (mmene chilili) chakudya chake;[386]
[386] Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang’ane chakudya chimene akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Allah.
عربي تفسیرونه:
أَنَّا صَبَبۡنَا ٱلۡمَآءَ صَبّٗا
Ndithu Ife timagwetsa mvula yambiri (kuchokera ku mitambo).
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ شَقَقۡنَا ٱلۡأَرۡضَ شَقّٗا
Kenako timaing’amba nthaka kuti mmera utuluke;
عربي تفسیرونه:
فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا حَبّٗا
Ndipo timameretsa m’menemo njere (ya chakudya cha anthu ndi zina zimene amasunga mnkhokwe),
عربي تفسیرونه:
وَعِنَبٗا وَقَضۡبٗا
Ndi mphesa ndi msipu.
عربي تفسیرونه:
وَزَيۡتُونٗا وَنَخۡلٗا
Ndi mzitona (wabwino) ndi (zipatso za) kanjedza,
عربي تفسیرونه:
وَحَدَآئِقَ غُلۡبٗا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo,
عربي تفسیرونه:
وَفَٰكِهَةٗ وَأَبّٗا
Ndi zipatso (zodyedwa ndi anthu) ndi msipu (wodyedwa ndi nyama);
عربي تفسیرونه:
مَّتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Tazimeretsa zimenezo kuti) zikondweretse inu ndi ziweto zanu.
عربي تفسیرونه:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلصَّآخَّةُ
Choncho likadzafika lipenga logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa makosi).
عربي تفسیرونه:
يَوۡمَ يَفِرُّ ٱلۡمَرۡءُ مِنۡ أَخِيهِ
Patsikuli munthu adzathawa m’bale wake,
عربي تفسیرونه:
وَأُمِّهِۦ وَأَبِيهِ
Mayi wake ndi bambo wake,
عربي تفسیرونه:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَبَنِيهِ
Mkazi wake ndi ana ake.
عربي تفسیرونه:
لِكُلِّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ يَوۡمَئِذٖ شَأۡنٞ يُغۡنِيهِ
Munthu aliyense mwa iwo, tsiku limenelo adzakhala ndi zakezake zotangwanika nazo. (Sadzalabadira za anzake).
عربي تفسیرونه:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ مُّسۡفِرَةٞ
Tsiku limenelo nkhope zina zidzakhala zowala;[387]
[387] (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri: amene adakhulupilira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma Ayah 40 ndi 42.
عربي تفسیرونه:
ضَاحِكَةٞ مُّسۡتَبۡشِرَةٞ
Zosekelera ndi zachimwemwe (chifukwa cha nkhani yabwino ya ku Munda wamtendere.)
عربي تفسیرونه:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ عَلَيۡهَا غَبَرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zokutidwa ndi fumbi.
عربي تفسیرونه:
تَرۡهَقُهَا قَتَرَةٌ
Mdima udzazikuta.
عربي تفسیرونه:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَفَرَةُ ٱلۡفَجَرَةُ
Iwo ndi anthu osakhulupirira oipa (olakwira Allah).
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: عبس
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول