Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Falaq   Versículo:

Suratu Al-Falaq

قُلۡ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلۡفَلَقِ
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye wam’bandakucha.[499]
[499] Surayi ndi yotsatirayi, zidavumbulutsidwa nthawi imodzi. Koma pali kutsutsana; ena akuti zidavumbulutsidwa ku Makka pomwe ena akuti zidavumbulutsidwa ku Madina. Sura ziwirizi zikutiphunzitsa m’mene tingadziikire mchitetezo cha Allah, ndiponso tikuphunzitsidwa kuti Iye (Allah) ndi mwini mphamvu zonse. Atha kumuteteza munthu kuchinthu chilichonse chifukwa chakuti Iye (Allah) ndi Mlengi wa chinthu chilichonse. Choncho, yemwe asiya chitetezo Chake ndikumafuna chitetezo cha ufiti, azimu, manda, ndi zina zotero ndiye kuti akuziika iye mwini kumachitidwe a “SHIRIK” (kupembedza mafano).
Os Tafssir em língua árabe:
مِن شَرِّ مَا خَلَقَ
Kuchokera ku zoipa zimene Iye adazilenga.[500]
[500] “Zomwe adalenga” zikutanthauza chilichonse cholengedwa, chamoyo ndi chopanda moyo; chooneka ndi chosaoneka.
Os Tafssir em língua árabe:
وَمِن شَرِّ غَاسِقٍ إِذَا وَقَبَ
Ndi ku zoipa za usiku pamene mdima ukulowa mwa mphamvu.[501]
[501] Palibe chikaiko, usiku wa mdima uli ndi zoopsa zambiri zomwe sizipezeka masana ndi usiku wowala. Mu usiku wa mdima, mumayenda zinthu zoopsa zambiri, monga zirombo zolusa, akuba, achiwembu ndi zina zambiri. Kukacha zonsezi zimabisala koma kukada zimatuluka.
Os Tafssir em língua árabe:
وَمِن شَرِّ ٱلنَّفَّٰثَٰتِ فِي ٱلۡعُقَدِ
Ndi ku zoipa za afiti omwe amauzira mu mfundo.
Os Tafssir em língua árabe:
وَمِن شَرِّ حَاسِدٍ إِذَا حَسَدَ
Ndiponso ku zoipa za wansanje pamene akuchita nsanje.”[502]
[502] “Wanjiru” kapena “Wansanje” uyu ndi munthu amene amanyansidwa akamuona mnzake atadalitsidwa ndi dalitso la mtundu uliwonse. Ndipo amakhumba kuti dalitsolo limuchokere ngakhale kuti lisamufikire iye. Njiru ndi tchimo lalikulu ndiponso ndi nthenda yoipa kwambiri. Mwina munthu wanjiru amabisa njiru yake mu mtima mpaka kufa nayo. Apo amapuma iye pamodzi ndi anthu aja amene ankawachitira njiru. Mwina amalephera kuibisa mu mtima ndipo amaionetsera poyera kotero kuti amachita zotheka kuti amuchotsere mnzake uja dalitso lomwe wapatsidwa ndi Allah. Akalephera izi, amangoganiza za kumupha; njiru iyi ndi yoipa kwambiri.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Falaq
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar