Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu At-Tin   Versículo:

Suratu At-Tin

وَٱلتِّينِ وَٱلزَّيۡتُونِ
Ndikulumbilira mitengo ya Mkuyu ndi Zitona (pansi pa mitengo imeneyi Ibrahim ndi Nuh (Nowa) adapeza uneneri),
Os Tafssir em língua árabe:
وَطُورِ سِينِينَ
Ndi phiri la Sinai (pamene Allah adamulankhulira Mûsa),
Os Tafssir em língua árabe:
وَهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ ٱلۡأَمِينِ
Ndiponso mzinda uwu (wolemekezeka) wamtendere; (Makka, womwe adapatsiridwa uneneri Muhammad) (s.a.w).
Os Tafssir em língua árabe:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِيٓ أَحۡسَنِ تَقۡوِيمٖ
Palibe chikaiko, tamulenga munthu mkalengedwe kabwino, kolingana (ndipo ali ndi mbiri zabwino).[457]
[457] M’gulu la nyama palibe yopambana kuposa munthu mkalengedwe ndi pa nzeru.
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ رَدَدۡنَٰهُ أَسۡفَلَ سَٰفِلِينَ
Pambuyo pake tamubwezera pansi kumposa wa pansi.[458]
[458] Munthu ali ndi makhalidwe awiri: Ngati agwiritsa ntchito nzeru zake amaongoka ndipo amaiposa nyama ili yonse. Koma ngati sagwiritsa ntchito nzeru zake amasokera ndi kukhala wapansi kuposa nyama zonse.
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ فَلَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونٖ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, adzakhala nawo iwo malipiro osatha.
Os Tafssir em língua árabe:
فَمَا يُكَذِّبُكَ بَعۡدُ بِٱلدِّينِ
Tsono nchiyani chakuchititsa kuti ukanire kuuka ndi malipiro pambuyo (poona mphamvu zathu pa chilichonse)?[459]
[459] (Ndime 7-8) Allah akuuza munthu kuti: Pambuyo podziwa kuti Allah ndi Yemwe adapanga zimenezo, ndi chiyani nanga chikumukaikitsa za tsiku la chiweruziro?
Os Tafssir em língua árabe:
أَلَيۡسَ ٱللَّهُ بِأَحۡكَمِ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Kodi Allah si Muweruzi wa nzeru kuposa aweruzi onse?
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu At-Tin
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar