Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Kafirun   Ajeti:

Suretu El Kafirun

قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡكَٰفِرُونَ
Nena (iwe Mtumiki) (s.a.w): E inu anthu osakhulupirira![493]
[493] (Ndime 1-6) Osakhulupilira a mu mzinda wa Makka pamene adaona kuti atopa, sangathe kuzimitsa dangalira la Usilamu ndipo adamuona Mneneri (s.a.w) tsiku lililonse akuonjezera khama pa ntchito yake, chipembedzo nacho chikunkerankera mtsogolo, adapempha Muhammad (s.a.w) kuti pakhale chimvano pakati pa iwo ndi iye choti amupembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w) chaka chimodzi pamodzi naye, nayenso pa chaka chinacho asakanikirane nawo popembedza milungu yawo chaka chimodzinso. Kumeneku ndiko kuti chaka, apembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w), nayenso apembedze milungu yawo chaka chinacho. Apa ndipo pamene idavumbulutsidwa Surayi. Cholinga chake ndi ichi: Inu muli ndi milungu yanu, inenso ndili ndi Mulungu wanga. Sizingatheke kusakanikirana pakati pa milungu yanu yonama ndi Mulungu wanga woona, ngakhalenso ndi mapemphero anu onama ndi mapemphero anga owona. Inu muli ndi chipembedzo ndichikhulupiliro chanu, inenso ndili ndi chipembedzo ndi chikhulupiliro changa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
لَآ أَعۡبُدُ مَا تَعۡبُدُونَ
Sindipembedza chimene inu mukuchipembedza (kusiya Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Inunso simumpembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَآ أَنَا۠ عَابِدٞ مَّا عَبَدتُّمۡ
Ndiponso ine sindidzapembedza chimene inu mwakhala mukuchipembedza (chifukwa inu ndinu ophatikiza Allah ndi zinthu zina).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Ndipo inu simudzampembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
لَكُمۡ دِينُكُمۡ وَلِيَ دِينِ
Inu muli ndi chipembedzo chanu (chimene mukuchikhulupirira), inenso ndili ndi chipembedzo changa (chimene Allah wandisankhira).
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Kafirun
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll