அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அல்பலக்   வசனம்:

ஸூரா அல்பலக்

قُلۡ أَعُوذُ بِرَبِّ ٱلۡفَلَقِ
Nena: “Ndikudzitchinjiriza ndi Mbuye wam’bandakucha.[499]
[499] Surayi ndi yotsatirayi, zidavumbulutsidwa nthawi imodzi. Koma pali kutsutsana; ena akuti zidavumbulutsidwa ku Makka pomwe ena akuti zidavumbulutsidwa ku Madina. Sura ziwirizi zikutiphunzitsa m’mene tingadziikire mchitetezo cha Allah, ndiponso tikuphunzitsidwa kuti Iye (Allah) ndi mwini mphamvu zonse. Atha kumuteteza munthu kuchinthu chilichonse chifukwa chakuti Iye (Allah) ndi Mlengi wa chinthu chilichonse. Choncho, yemwe asiya chitetezo Chake ndikumafuna chitetezo cha ufiti, azimu, manda, ndi zina zotero ndiye kuti akuziika iye mwini kumachitidwe a “SHIRIK” (kupembedza mafano).
அரபு விரிவுரைகள்:
مِن شَرِّ مَا خَلَقَ
Kuchokera ku zoipa zimene Iye adazilenga.[500]
[500] “Zomwe adalenga” zikutanthauza chilichonse cholengedwa, chamoyo ndi chopanda moyo; chooneka ndi chosaoneka.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمِن شَرِّ غَاسِقٍ إِذَا وَقَبَ
Ndi ku zoipa za usiku pamene mdima ukulowa mwa mphamvu.[501]
[501] Palibe chikaiko, usiku wa mdima uli ndi zoopsa zambiri zomwe sizipezeka masana ndi usiku wowala. Mu usiku wa mdima, mumayenda zinthu zoopsa zambiri, monga zirombo zolusa, akuba, achiwembu ndi zina zambiri. Kukacha zonsezi zimabisala koma kukada zimatuluka.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمِن شَرِّ ٱلنَّفَّٰثَٰتِ فِي ٱلۡعُقَدِ
Ndi ku zoipa za afiti omwe amauzira mu mfundo.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمِن شَرِّ حَاسِدٍ إِذَا حَسَدَ
Ndiponso ku zoipa za wansanje pamene akuchita nsanje.”[502]
[502] “Wanjiru” kapena “Wansanje” uyu ndi munthu amene amanyansidwa akamuona mnzake atadalitsidwa ndi dalitso la mtundu uliwonse. Ndipo amakhumba kuti dalitsolo limuchokere ngakhale kuti lisamufikire iye. Njiru ndi tchimo lalikulu ndiponso ndi nthenda yoipa kwambiri. Mwina munthu wanjiru amabisa njiru yake mu mtima mpaka kufa nayo. Apo amapuma iye pamodzi ndi anthu aja amene ankawachitira njiru. Mwina amalephera kuibisa mu mtima ndipo amaionetsera poyera kotero kuti amachita zotheka kuti amuchotsere mnzake uja dalitso lomwe wapatsidwa ndi Allah. Akalephera izi, amangoganiza za kumupha; njiru iyi ndi yoipa kwambiri.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அல்பலக்
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக