அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அஷ்ஷுஅரா   வசனம்:

ஸூரா அஷ்ஷுஅரா

طسٓمٓ
Tâ-Sîn-Mîm.
அரபு விரிவுரைகள்:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Izi ndi Ayah (ndime) za buku (la Qur’an) lofotokoza chilichonse (chofunika m’chipembedzo).
அரபு விரிவுரைகள்:
لَعَلَّكَ بَٰخِعٞ نَّفۡسَكَ أَلَّا يَكُونُواْ مُؤۡمِنِينَ
Mwina iwe (Mtumiki Muhammad {s.a.w}) udziononga wekha (ndi madandaulo) chifukwa chakuti (iwo) sadakhale okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِن نَّشَأۡ نُنَزِّلۡ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ ءَايَةٗ فَظَلَّتۡ أَعۡنَٰقُهُمۡ لَهَا خَٰضِعِينَ
Tikadafuna, tikadawatsitsira chizizwa kuchokera kumwamba; kotero kuti makosi awo akadadzichepetsa ndi chizizwacho, (sakadatha kucheukira kwina koma sitifuna kukakamiza anthu kuti akhale Asilamu).[295]
[295] Mtumiki Muhammad (s.a.w) adali kuwawidwa mtima kwambiri poona kuti anthu sakuvomereza uthenga wachoonadi umene iye adadza nawo, ndipo adali kuwamvera chisoni kwambiri. Choncho Allah adamtonthoza pomuuza kuti: “Usadziphe wekha chifukwa chokhala ndi maganizo owamvera chisoni.” Allah akadafuna kuwaongola mowakakamiza akadatha kutero; koma sadafune.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَا يَأۡتِيهِم مِّن ذِكۡرٖ مِّنَ ٱلرَّحۡمَٰنِ مُحۡدَثٍ إِلَّا كَانُواْ عَنۡهُ مُعۡرِضِينَ
Ndipo palibe pamene chikuwadzera chivumbulutso chatsopano chochokera kwa (Allah) Wachifundo chambiri koma amazipatula ku icho (chivumbulutso).
அரபு விரிவுரைகள்:
فَقَدۡ كَذَّبُواْ فَسَيَأۡتِيهِمۡ أَنۢبَٰٓؤُاْ مَا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndithu atsutsa; choncho posachedwapa ziwadzera nkhani zomwe adali kuzichitira chipongwe.
அரபு விரிவுரைகள்:
أَوَلَمۡ يَرَوۡاْ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَمۡ أَنۢبَتۡنَا فِيهَا مِن كُلِّ زَوۡجٖ كَرِيمٍ
Kodi sadaone nthaka? Ndimmera ungati taumeretsa m’menemo kuchokera mu mtundu ulionse, wokongola?
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezo muli zizindikiro (zosonyeza mphamvu za Allah). Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِذۡ نَادَىٰ رَبُّكَ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱئۡتِ ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo (akumbutse) pamene Mbuye wako adaitana (m’neneri) Mûsa; adamuuza: “Pita kwa anthu ochita zoipa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَوۡمَ فِرۡعَوۡنَۚ أَلَا يَتَّقُونَ
Anthu a Farawo; (auze): “Kodi sawopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبِّ إِنِّيٓ أَخَافُ أَن يُكَذِّبُونِ
(Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ine ndikuopa kuti anganditsutse.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَيَضِيقُ صَدۡرِي وَلَا يَنطَلِقُ لِسَانِي فَأَرۡسِلۡ إِلَىٰ هَٰرُونَ
Ndipo chingabanike chifuwa changa (ndi maganizo, chifukwa chakunditsutsa kwawo); ndiponso lirime langa siliyankhula momveka bwino. Choncho tumizaninso uthengawu kwa Harun (kuti tikhale awiri ndipo azikandithangata pantchito yangayi).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَهُمۡ عَلَيَّ ذَنۢبٞ فَأَخَافُ أَن يَقۡتُلُونِ
Ndipo iwowo ndili nawo mlandu ndipo ndikuopa kuti angandiphe (pobwezera chimene ndidawalakwira powaphera munthu wawo).
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ كَلَّاۖ فَٱذۡهَبَا بِـَٔايَٰتِنَآۖ إِنَّا مَعَكُم مُّسۡتَمِعُونَ
(Allah) adati: “Iyayi! Pitani pamodzi ndi zozizwa Zathu; ndithu Ife tikakhala nanu limodzi (pokuthangatani) uku tikumvetsera (zimene azikanena).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأۡتِيَا فِرۡعَوۡنَ فَقُولَآ إِنَّا رَسُولُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Choncho mpitireni Farawo, ndipo kamuuzeni kuti: “Ife ndi atumiki a Mbuye wa zolengedwa zonse.”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَنۡ أَرۡسِلۡ مَعَنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“(Tatumidwa) kuti uwapereke kwa ife ana a Israyeli (kuti tinke nawo ku Sham).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ أَلَمۡ نُرَبِّكَ فِينَا وَلِيدٗا وَلَبِثۡتَ فِينَا مِنۡ عُمُرِكَ سِنِينَ
(Farawo) adati (kwa Mûsa): “Kodi sitidakulere kwathu uli mwana, ndi kukhala nafe pa moyo wako zaka zambiri?”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَفَعَلۡتَ فَعۡلَتَكَ ٱلَّتِي فَعَلۡتَ وَأَنتَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
“Ndipo udachita chochita chako chimene udachichita, ndipo iwe ndiwe mmodzi wa osathokoza!”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ فَعَلۡتُهَآ إِذٗا وَأَنَا۠ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
(Mûsa) adati: “Ndidachita zimenezo pomwe ine ndidali mmodzi wa osazindikira zinthu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَفَرَرۡتُ مِنكُمۡ لَمَّا خِفۡتُكُمۡ فَوَهَبَ لِي رَبِّي حُكۡمٗا وَجَعَلَنِي مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
“Choncho ndidakuthawani pomwe ndidakuopani; tsono Mbuye wanga wandipatsa nzeru zoweruzira (zinthu), ndi kundisankha kukhala mmodzi wa atumiki.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتِلۡكَ نِعۡمَةٞ تَمُنُّهَا عَلَيَّ أَنۡ عَبَّدتَّ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“Ndipo kodi umenewu ndimtendere wonditonzera pomwe mudawaika muukapolo ana a Israyeli!”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ وَمَا رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Farawo adati: “Kodi ndani Mbuye wa zolengedwayo?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُم مُّوقِنِينَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wa thambo ndi nthaka ndi zapakati pake, ngati muli ndi chitsimikizo. (Amachita chilichonse m’menemo mmene wafunira; kupereka moyo ndi imfa).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ لِمَنۡ حَوۡلَهُۥٓ أَلَا تَسۡتَمِعُونَ
(Farawo) adauza omwe adali m’mphepete mwake (mwachipongwe): “Kodi simukumva (mawu achibwanawa)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبُّكُمۡ وَرَبُّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Mûsa adapitiriza kunena) adati: “Allah ndi Mbuye wanu komanso Mbuye wamakolo anu oyamba.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ إِنَّ رَسُولَكُمُ ٱلَّذِيٓ أُرۡسِلَ إِلَيۡكُمۡ لَمَجۡنُونٞ
(Farawo) adati (kwa anthu ake pofuna kuwakwiitsa): “Ndithu Mtumiki wanu amene watumidwa kwa inu, ngwamisala.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wakuvuma ndi kuzambwe, ndi zomwe ziri pakati pake ngati mumazindikira (zinthu, muzindikira izi).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ لَئِنِ ٱتَّخَذۡتَ إِلَٰهًا غَيۡرِي لَأَجۡعَلَنَّكَ مِنَ ٱلۡمَسۡجُونِينَ
(Farawo) adati: “Ngati udzipangira mulungu wina kusiya ine, ndikuchita kukhala mmodzi wa omangidwa kundende.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ أَوَلَوۡ جِئۡتُكَ بِشَيۡءٖ مُّبِينٖ
(Mûsa) adati: “Kodi ngakhale nditakubweretsera chinthu choonekera poyera (chosonyeza kuti zimene ndikunenazi ndizoona ndatumidwa ndi Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ فَأۡتِ بِهِۦٓ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Farawo) adati: “Chibweretse, ngati uli mwa onena zoona.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَلۡقَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ ثُعۡبَانٞ مُّبِينٞ
Ndipo (Mûsa) adaponya (pansi) ndodo yake, mwadzidzidzi idasanduka njoka yopenyeka.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَنَزَعَ يَدَهُۥ فَإِذَا هِيَ بَيۡضَآءُ لِلنَّٰظِرِينَ
Ndipo adatulutsa dzanja lake; pompo lidali loyera (kwambiri) kwa (onse) openya.
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ لِلۡمَلَإِ حَوۡلَهُۥٓ إِنَّ هَٰذَا لَسَٰحِرٌ عَلِيمٞ
(Farawo) adauza akuluakulu omwe adali m’mphepete mwake: “Ndithu uyu ndi wamatsenga wodziwa kwambiri.”
அரபு விரிவுரைகள்:
يُرِيدُ أَن يُخۡرِجَكُم مِّنۡ أَرۡضِكُم بِسِحۡرِهِۦ فَمَاذَا تَأۡمُرُونَ
“Akufuna kukutulutsani m’dziko lanu ndi matsenga ake; kodi nanga mukuti chiyani?”[296]
[296] Farawo adasimidwa, adatha nzeru zedi ndi mawu amene adali kutuluka m’kamwa mwa Musa kotero kuti adangoti kakasi, kusowa chonena, nayamba kuwafunsa nzeru ndi malangizo anthu ake pomwe iye ankadzitcha kuti ndi mulungu wodziwa zonse, wamphamvu zoposa.
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُوٓاْ أَرۡجِهۡ وَأَخَاهُ وَٱبۡعَثۡ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
(Anthu) adati (kwa Farawo): “Mpatse nthawi ndi m’bale wakeyo, ndipo tumiza (amithenga) m’mizinda yonse osonkhanitsa anthu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
يَأۡتُوكَ بِكُلِّ سَحَّارٍ عَلِيمٖ
“Ndipo akubweretsera amatsenga onse odziwa kwabasi (kotero kuti adzampambana Mûsa).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَجُمِعَ ٱلسَّحَرَةُ لِمِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Choncho amatsenga adasonkhanitsidwa mu nthawi ya tsiku lodziwika.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقِيلَ لِلنَّاسِ هَلۡ أَنتُم مُّجۡتَمِعُونَ
Ndipo anthu adauzidwa: “Kodi inu musonkhana? (Choncho, sonkhanani).”
அரபு விரிவுரைகள்:
لَعَلَّنَا نَتَّبِعُ ٱلسَّحَرَةَ إِن كَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
“Mwina tingawatsatire amatsenga ngati iwo ndiamene apambane.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَلَمَّا جَآءَ ٱلسَّحَرَةُ قَالُواْ لِفِرۡعَوۡنَ أَئِنَّ لَنَا لَأَجۡرًا إِن كُنَّا نَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo pamene amatsenga adadza, adati kwa Farawo: “Kodi tidzakhala ndi mphoto ngati ife ndife tipambane?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ نَعَمۡ وَإِنَّكُمۡ إِذٗا لَّمِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
(Farawo) adati: “Inde, (ndipo kuonjezera apo) ndithu inu mudzakhala mwa amene amakhala pafupi (ndi ine, monga nduna zanga).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ لَهُم مُّوسَىٰٓ أَلۡقُواْ مَآ أَنتُم مُّلۡقُونَ
Mûsa adati kwa iwo: “Ponyani zimene mufuna kuponya (zosonyeza kuya kwa matsenga anu).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَلۡقَوۡاْ حِبَالَهُمۡ وَعِصِيَّهُمۡ وَقَالُواْ بِعِزَّةِ فِرۡعَوۡنَ إِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Choncho adaponya zingwe zawo ndi ndodo zawo, ndipo adati: “Kupyolera mu mphamvu za Farawo, ndithu ife ndife opambana.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَلۡقَىٰ مُوسَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ تَلۡقَفُ مَا يَأۡفِكُونَ
Kenako Mûsa adaponya ndodo yake; mwadzidzidzi iyo idameza zabodza zomwe iwo adakonza.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأُلۡقِيَ ٱلسَّحَرَةُ سَٰجِدِينَ
Pamenepo amatsenga adadzigwetsa pansi molambira.
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Tamkhulupirira Mbuye wa zolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa ndi Harun.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ ءَامَنتُمۡ لَهُۥ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّهُۥ لَكَبِيرُكُمُ ٱلَّذِي عَلَّمَكُمُ ٱلسِّحۡرَ فَلَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَۚ لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ وَلَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Farawo) adati: “Ha! Mwamkhulupirira chotani ndisanakulolezeni? Ndithu iyeyu ndimkulu wanu amene adakuphunzitsani matsenga. Choncho posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni) ndithu ndidula manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa (podula mkono wakumanja ndi mwendo wakumanzere; kapena kudula mkono wakumanzere ndi mwendo wakumanja), ndipo kenako ndikupachikani nonsenu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ لَا ضَيۡرَۖ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Amatsenga) adati: “Palibe vuto, ndithu ife (tonse) tibwerera kwa Mbuye wathu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّا نَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لَنَا رَبُّنَا خَطَٰيَٰنَآ أَن كُنَّآ أَوَّلَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndithu ife tikuyembekezera kuti Mbuye wathu atikhululukire zolakwa zathu; pokhala oyamba mwa okhulupirira.”
அரபு விரிவுரைகள்:
۞ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنۡ أَسۡرِ بِعِبَادِيٓ إِنَّكُم مُّتَّبَعُونَ
Ndipo tidamvumbulutsira Mûsa (kuti): “Pita ndi anthu anga m’nthawi yausiku (musamuke m’dziko la Iguputo); ndithu inu mutsatidwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَرۡسَلَ فِرۡعَوۡنُ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
Choncho Farawo adatuma (owatuma) kuti asonkhanitse anthu m’mizinda (kuti aletse ana a Israyeli kutuluka).
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَشِرۡذِمَةٞ قَلِيلُونَ
(Adawauza otumidwa aja kuti auze anthu kuti): “Ndithu awa (ana a Israyeli) ndikagulu kochepa.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّهُمۡ لَنَا لَغَآئِظُونَ
Ndipo ndithu iwo akutikwiitsa.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّا لَجَمِيعٌ حَٰذِرُونَ
Koma ndithu ife tonse (ndife ochuluka komabe ngakhale zili choncho) tikuwaopa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَخۡرَجۡنَٰهُم مِّن جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Choncho tidawatulutsa m’minda ndi mwa akasupe.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَكُنُوزٖ وَمَقَامٖ كَرِيمٖ
Ndi m’nkhokwe za chuma ndi m’malo okongola.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَٰلِكَۖ وَأَوۡرَثۡنَٰهَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Momwemo ndi mmene tidawachitira ndipo tidawalowetsera chokolo zinthu zawo zonse kwa ana a Israyeli.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَتۡبَعُوهُم مُّشۡرِقِينَ
Choncho (anthu a Farawo ndi iye mwini) adawatsatira (ana a Israyeli) dzuwa litatuluka.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَلَمَّا تَرَٰٓءَا ٱلۡجَمۡعَانِ قَالَ أَصۡحَٰبُ مُوسَىٰٓ إِنَّا لَمُدۡرَكُونَ
Ndipo pamene magulu awiri adaonana (anthu a Farawo ndi anthu a Mûsa), anthu a Mûsa adati: “Ndithu ife tigwidwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ كَلَّآۖ إِنَّ مَعِيَ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
(Mûsa) adati: “Iyayi! Ndithu Mbuye wanga ali nane pamodzi. Andiongolera (kuti ife tonse tipulumuke).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡبَحۡرَۖ فَٱنفَلَقَ فَكَانَ كُلُّ فِرۡقٖ كَٱلطَّوۡدِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidam’vumbulutsira mawu Mûsa (akuti): “Menya nyanja ndi ndodo yako.” Ndipo idagawikana, mbali iliyonse idali ngati phiri lalikulu.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَزۡلَفۡنَا ثَمَّ ٱلۡأٓخَرِينَ
Ndipo tidawayandikitsa pamenepo anthu enawo, (Farawo ndi anthu ake nalowa pa njira yomweyo pambuyo pa Mûsa ndi anthu ake).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَنجَيۡنَا مُوسَىٰ وَمَن مَّعَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidapulumutsa Mûsa ndi onse amene adali nawo (mpaka adaoloka nyanjayo, madzi ali chiimire mbali iyi ndi iyi).
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo, (Farawo ndi anthu ake).
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro. Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa (amalanga ndi chilango choopsa omwe amunyoza); Wachisoni (kwa omkhulupirira ndi kumumvera).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ إِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo awerengere (osakhulupirira) nkhani ya (M’neneri) Ibrahim.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَا تَعۡبُدُونَ
Pamene adafunsa bambo wake ndi anthu ake (kuti); “Kodi mukupembedza chiyani?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ نَعۡبُدُ أَصۡنَامٗا فَنَظَلُّ لَهَا عَٰكِفِينَ
Adati: “Tikupembedza mafano; ndipo tipitiriza kuwapembedza.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ هَلۡ يَسۡمَعُونَكُمۡ إِذۡ تَدۡعُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi amakumvani mukawaitana?”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَوۡ يَنفَعُونَكُمۡ أَوۡ يَضُرُّونَ
“Kapena amakuthandizani (mukawapembedza) kapena amapereka masautso kwa inu (mukasiya kuwapembedza)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ بَلۡ وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا كَذَٰلِكَ يَفۡعَلُونَ
(Iwo) adati: “Koma tidapeza makolo athu akuchita zimenezi.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ أَفَرَءَيۡتُم مَّا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi mukuwaona awa amene mwakhala mukuwapembedza,”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُمُ ٱلۡأَقۡدَمُونَ
“Inu ndi makolo anu amene adatsogola?”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَإِنَّهُمۡ عَدُوّٞ لِّيٓ إِلَّا رَبَّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndithu iwo ndiadani anga, kupatula Mbuye wa zolengedwa zonse;”
அரபு விரிவுரைகள்:
ٱلَّذِي خَلَقَنِي فَهُوَ يَهۡدِينِ
“Yemwe adandilenga, ndiponso Yemwe akundiongolera (kunjira yolungama);”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱلَّذِي هُوَ يُطۡعِمُنِي وَيَسۡقِينِ
“Ndiyemwe akundidyetsa ndi kundimwetsa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِذَا مَرِضۡتُ فَهُوَ يَشۡفِينِ
“Ndipo ndikadwala ndiyemwe amandichiritsa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱلَّذِي يُمِيتُنِي ثُمَّ يُحۡيِينِ
“Ndi Amene adzandipatsa imfa, ndipo (tsiku la Qiyâma) adzandidzutsa;”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱلَّذِيٓ أَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لِي خَطِيٓـَٔتِي يَوۡمَ ٱلدِّينِ
“Ndi Yemwe ndikuyembekezera kuti adzandikhululukira zolakwa zanga tsiku la malipiro.”
அரபு விரிவுரைகள்:
رَبِّ هَبۡ لِي حُكۡمٗا وَأَلۡحِقۡنِي بِٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni nzeru zoweruzira (zinthu), ndikundilumikiza ndi anthu abwino;”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱجۡعَل لِّي لِسَانَ صِدۡقٖ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
“Ndipatseni kutchulidwa kwabwino kwa anthu ena odza pambuyo;”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱجۡعَلۡنِي مِن وَرَثَةِ جَنَّةِ ٱلنَّعِيمِ
“Ndichiteni kukhala mmodzi mwa olandira Munda wamtendere;”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱغۡفِرۡ لِأَبِيٓ إِنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
“Ndipo khululukirani bambo wanga; ndithu iye adali mmodzi wa osokera;”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَا تُخۡزِنِي يَوۡمَ يُبۡعَثُونَ
“Ndipo musadzandiyalutse pa tsiku loukitsidwa anthu (ku imfa);”
அரபு விரிவுரைகள்:
يَوۡمَ لَا يَنفَعُ مَالٞ وَلَا بَنُونَ
“Tsiku lomwe chuma ndi ana sizidzathandiza (aliyense).”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا مَنۡ أَتَى ٱللَّهَ بِقَلۡبٖ سَلِيمٖ
“Kupatula yemwe adzadza kwa Allah ndi mtima woyera (iye ndiamene adzathandizidwa patsikulo).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأُزۡلِفَتِ ٱلۡجَنَّةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Ndipo Munda wamtendere udzayandikitsidwa kwa oopa (Allah),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِلۡغَاوِينَ
Ndipo Jahannam idzaonetsedwa kwa opotoka;
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقِيلَ لَهُمۡ أَيۡنَ مَا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
Ndipo kudzanenedwa kwa iwo: “Ali kuti amene mudali kuwapembedza aja,
அரபு விரிவுரைகள்:
مِن دُونِ ٱللَّهِ هَلۡ يَنصُرُونَكُمۡ أَوۡ يَنتَصِرُونَ
M’malo mwa Allah? Kodi angathe kukuthandizani kapena kudzithandiza okha?”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَكُبۡكِبُواْ فِيهَا هُمۡ وَٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo iwo ndi opotoka ena adzaponyedwa ndi nkhope zawo m’menemo (mu Jahannam).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَجُنُودُ إِبۡلِيسَ أَجۡمَعُونَ
Ndi magulu onse ankhondo a Iblis (omwe adali kukometsa kwa anthu zoipa ndi machimo).
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ وَهُمۡ فِيهَا يَخۡتَصِمُونَ
Adzanena (movomereza kulakwa kwawo) uku naonso ali m’menemo, akukangana (ndi anzawo omwe adawasokeretsa):
அரபு விரிவுரைகள்:
تَٱللَّهِ إِن كُنَّا لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٍ
“Ndikulumbira Allah, ndithu tidali m’kusokera kowonekera.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ نُسَوِّيكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Pamene timakufananitsani ndi Mbuye wa zolengedwa.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَضَلَّنَآ إِلَّا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
Ndipo sadatisokeretse, koma oipa okha basi.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَمَا لَنَا مِن شَٰفِعِينَ
Choncho ife tilibe aomboli (otiombola),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَا صَدِيقٍ حَمِيمٖ
Ngakhalenso bwenzi wapamtima (woti angatipulumutse kumasautsowa).
அரபு விரிவுரைகள்:
فَلَوۡ أَنَّ لَنَا كَرَّةٗ فَنَكُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Tikadapeza mwayi wobwerera (ku moyo wa padziko), tikadakhala mwa okhulupirira.”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi, muli malingaliro akulu, koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, ndiye Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ نُوحٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Nuh adatsutsa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ نُوحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene adawauza Nuh m’bale wawo kuti: “Kodi simukuopa (Allah ngakhale nditakuuzani zoopsa zimene zikukudikirani)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine kwa inu ndine Mtumiki wokhulupirika;”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
۞ قَالُوٓاْ أَنُؤۡمِنُ لَكَ وَٱتَّبَعَكَ ٱلۡأَرۡذَلُونَ
(Iwo) adati: “Nchotani kuti tikukhulupirire iwe chikhalirecho anthu wamba ndi amene akukutsatira?”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ وَمَا عِلۡمِي بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
(Nuh) adati: “Sindikudziwa zimene adali kuchita (zomwe zachititsa kuti Allah awaongolere kunjira yoongoka).”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنۡ حِسَابُهُمۡ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّيۖ لَوۡ تَشۡعُرُونَ
“Chiwerengero chawo sichili kwina koma kwa Mbuye wanga, mukadakhala mukuzindikira.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَنَا۠ بِطَارِدِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndipo sindine wopirikitsa okhulupirira (ku chipembedzo cha Allah kuti inu olemekezeka muchikhulupirire).”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنۡ أَنَا۠ إِلَّا نَذِيرٞ مُّبِينٞ
“Ine sikanthu , koma ndine mchenjezi woonekera.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰنُوحُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمَرۡجُومِينَ
(Iwo) adati: “Ngati susiya, iwe Nuh, (zonena zakozi) ndithu ukhala mmodzi mwa ogendedwa (miyala mpaka ufe).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبِّ إِنَّ قَوۡمِي كَذَّبُونِ
(Nuh) adati (kwa Allah): “Mbuye wanga! Ndithu anthu anga anditsutsa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱفۡتَحۡ بَيۡنِي وَبَيۡنَهُمۡ فَتۡحٗا وَنَجِّنِي وَمَن مَّعِيَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Choncho weruzani pakati panga ndi pakati pa iwo (chiweruzo chabwino), ndipo ndipulumutseni pamodzi ndi amene alinane mwa okhulupirira.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَمَن مَّعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
Choncho, tidampulumutsa pamodzi ndi omwe adali naye m’chombo chodzadza (ndi chilichonse chamoyo chomwe chidalipo m’dziko, chachimuna ndi chachikazi chidaikidwa m’menemo).
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا بَعۡدُ ٱلۡبَاقِينَ
Pambuyo pake tidawamiza otsalawo.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; Ngwachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَّبَتۡ عَادٌ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Naonso Âdi adatsutsa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ هُودٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo (Mneneri) Hûd adawafunsa kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu;”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho, muopeni Allah ndipo mverani ine.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo pazimenezi sindikukupemphani malipiro; ndithu malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَتَبۡنُونَ بِكُلِّ رِيعٍ ءَايَةٗ تَعۡبَثُونَ
“Kodi mukudzimangira nyumba pamalo paliponse pachitunda pokongola, moseweretsa?”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَتَّخِذُونَ مَصَانِعَ لَعَلَّكُمۡ تَخۡلُدُونَ
“Ndipo mukudzimangira (nyumba zonga) linga ngati kuti mukuona kuti mudzakhala muyaya?”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِذَا بَطَشۡتُم بَطَشۡتُمۡ جَبَّارِينَ
“Ndipo mukamamenya nkhondo mumamenya modzitukumula.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِيٓ أَمَدَّكُم بِمَا تَعۡلَمُونَ
“Ndipo muopeni Yemwe adakupatsani zimene mukuzidziwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَمَدَّكُم بِأَنۡعَٰمٖ وَبَنِينَ
“Adakupatsani ziweto ndi ana.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَجَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
“Ndi minda ndi akasupe.”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ سَوَآءٌ عَلَيۡنَآ أَوَعَظۡتَ أَمۡ لَمۡ تَكُن مِّنَ ٱلۡوَٰعِظِينَ
Iwo adati: “Kwa ife nchimodzimodzi, utichenjeze kapena iwe usakhale mmodzi mwa ochenjeza.”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا خُلُقُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndithu kutero (anthu ena kudzitcha atumiki a Allah), sikanthu koma ndi machitidwe a anthu akale.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
“Ndipo ife sitidzalangidwa (monga momwe ukunenera).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَكَذَّبُوهُ فَأَهۡلَكۡنَٰهُمۡۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho adamtsutsa, ndipo tidawaononga. Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako ndiye Wamphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
A Samudu (naonso) adatsutsa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ صَٰلِحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Swalih adawauza kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndimtumiki wokhulupirika kwa inu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo mverani ine.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi. Palibe kumene kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wa zolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَتُتۡرَكُونَ فِي مَا هَٰهُنَآ ءَامِنِينَ
“Kodi (mukuganizira kuti) mudzasiidwa mwamtendere pa izi zili pano (popanda imfa kukudzerani?)”
அரபு விரிவுரைகள்:
فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
“M’minda ndi mu akasupe?”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَزُرُوعٖ وَنَخۡلٖ طَلۡعُهَا هَضِيمٞ
“Ndi (m’minda) yammera ndi mitengo yakanjedza yamikoko yakupsa yofewa?”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَنۡحِتُونَ مِنَ ٱلۡجِبَالِ بُيُوتٗا فَٰرِهِينَ
“Ndipo mukugoba nyumba m’mapiri mwaluso.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَا تُطِيعُوٓاْ أَمۡرَ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
“Ndipo musamvere za awo opyola malire.”
அரபு விரிவுரைகள்:
ٱلَّذِينَ يُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا يُصۡلِحُونَ
“Amene akuononga pa dziko, ndipo sakonza.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
مَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا فَأۡتِ بِـَٔايَةٍ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Iwe suli kanthu, koma munthu ngati ife; tabwera ndi chozizwitsa, ngati ndiwedi mmodzi wa onena zoona!”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ هَٰذِهِۦ نَاقَةٞ لَّهَا شِرۡبٞ وَلَكُمۡ شِرۡبُ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Iye adati: “(Ndakubweretserani) ngamira iyi yaikazi; (koma) ili ndi gawo lake lakumwa, ndipo inu muli ndi gawo lanu lakutunga (madzi) patsiku lodziwika. (Tsiku lina lotunga rnadzi anthu).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابُ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndipo musaikhudze ndi choipa chilichonse kuopera kuti chingakupezeni chilango cha tsiku lalikulu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَعَقَرُوهَا فَأَصۡبَحُواْ نَٰدِمِينَ
Koma iwo adaipha; ndipo adali odzinena (pamene chidadza chilango cha Allah).
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَخَذَهُمُ ٱلۡعَذَابُۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho chilango (cha Allah) chidawaononga, ndithu pa zimenezi pali phunziro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; wachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ لُوطٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Luti adatsutsa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ لُوطٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Luti adanena kwa iwo (kuti): “Kodi simuopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; palibe komwe kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wazolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَتَأۡتُونَ ٱلذُّكۡرَانَ مِنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi mukugonana ndi amuna (anzanu) muzolengedwa (za Allah),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَذَرُونَ مَا خَلَقَ لَكُمۡ رَبُّكُم مِّنۡ أَزۡوَٰجِكُمۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٌ عَادُونَ
“Ndikusiya amene Mbuye wanu adakulengerani kuti akhale akazi anu? Ndithu inu ndinu anthu olumpha malire.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰلُوطُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُخۡرَجِينَ
Iwo adati: “Ngati susiya (izi), E iwe Luti! ndithu ukhala mmodzi wa opirikitsidwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ إِنِّي لِعَمَلِكُم مِّنَ ٱلۡقَالِينَ
Iye adati: “Ndithu ine ndine m’modzi wakuzida izi zochita zanu (choncho Sindisiya kuzidzudzula).”
அரபு விரிவுரைகள்:
رَبِّ نَجِّنِي وَأَهۡلِي مِمَّا يَعۡمَلُونَ
“E Mbuye wanga! Ndipulumutseni ine ndi banja langa ku (matsoka a) zimene akuchita.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَنَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidampulumutsa iye ndi onse a pa banja lake,
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yaikazi idali mwa otsalira m’mbuyo.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Titatero tidawaononga enawo.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji, mvula ya ochenjezedwa!
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pazimenezi pali malingaliro. Koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَّبَ أَصۡحَٰبُ لۡـَٔيۡكَةِ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a m’dziko lamitengo yambiri (Madiana) adatsutsa atumiki.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ شُعَيۡبٌ أَلَا تَتَّقُونَ
(Akumbutse) pamene (Mneneri) Shuaib adati kwa iwo: “Kodi simuopa (Allah)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; kulibe malipiro anga koma kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
۞ أَوۡفُواْ ٱلۡكَيۡلَ وَلَا تَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُخۡسِرِينَ
“Kwaniritsani mulingo (pamalonda pamene mukupima), ndipo musakhale mwaopungula (mulingo).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَزِنُواْ بِٱلۡقِسۡطَاسِ ٱلۡمُسۡتَقِيمِ
“Ndipo yesani ndi sikelo yolungama (yolondola).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَا تَبۡخَسُواْ ٱلنَّاسَ أَشۡيَآءَهُمۡ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo musawachepetsere anthu zinthu zawo, ndiponso musayende padziko uku mukuononga.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ وَٱلۡجِبِلَّةَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndipo muopeni amene adalenga inu ndiponso zolengedwa zoyamba (zimene zidanka kale).”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا وَإِن نَّظُنُّكَ لَمِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
“Ndipo iwe suli kanthu koma munthu ngati ife, ndipo ndithu tikukutsimikizira kuti ndiwe mmodzi wa abodza.”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَأَسۡقِطۡ عَلَيۡنَا كِسَفٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Choncho tigwetsere zidutswa za thambo (kuti zitiononge) ngati uli mmodzi wa onena zoona.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبِّيٓ أَعۡلَمُ بِمَا تَعۡمَلُونَ
(Shuaib) adati: “Mbuye wanga Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita. (Akadzaona kuti inu ngoyenera kulangidwa ndizidutswa za thambo, adzakulangani).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَكَذَّبُوهُ فَأَخَذَهُمۡ عَذَابُ يَوۡمِ ٱلظُّلَّةِۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٍ
Koma adamutsutsa. Ndipo chidawagwera chilango chatsiku la mthunzi; ndithu chimenecho chidali chilango cha tsiku lalikulu.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّهُۥ لَتَنزِيلُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo, ndithu iyi (Qur’an) ndiyo chivumbulutso cha Mbuye wazolengedwa zonse.
அரபு விரிவுரைகள்:
نَزَلَ بِهِ ٱلرُّوحُ ٱلۡأَمِينُ
Mzimu Wokhulupirika (Jiburil) udaivumbulutsa.
அரபு விரிவுரைகள்:
عَلَىٰ قَلۡبِكَ لِتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُنذِرِينَ
Pa mtima wako kuti ukhale mmodzi wa achenjezi,
அரபு விரிவுரைகள்:
بِلِسَانٍ عَرَبِيّٖ مُّبِينٖ
M’chiyankhulo cha Chiarabu chomveka bwino.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنَّهُۥ لَفِي زُبُرِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo ndithu izi (zomwe zili m’Qur’an) zilipo m’mabuku akale.
அரபு விரிவுரைகள்:
أَوَلَمۡ يَكُن لَّهُمۡ ءَايَةً أَن يَعۡلَمَهُۥ عُلَمَٰٓؤُاْ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Kodi sipadapezeke chisonyezo kwa iwo kuti akuidziwa (Qur’an) odziwa mwa ana a Israyeli (kotero kuti ena alowa m’Chisilamu)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَوۡ نَزَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ بَعۡضِ ٱلۡأَعۡجَمِينَ
Ndipo tikadaivumbulutsa kwa wina amene sali Muarabu,
அரபு விரிவுரைகள்:
فَقَرَأَهُۥ عَلَيۡهِم مَّا كَانُواْ بِهِۦ مُؤۡمِنِينَ
Kotero kuti nkuwawerengera momveka bwino, sakadaikhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
كَذَٰلِكَ سَلَكۡنَٰهُ فِي قُلُوبِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Momwemo ndimo tidalowetsera kuitsutsa (Qur’an) m’mitima ya oipa.
அரபு விரிவுரைகள்:
لَا يُؤۡمِنُونَ بِهِۦ حَتَّىٰ يَرَوُاْ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَلِيمَ
Sangaikhulupirire kufikira ataona chilango chowawa.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَيَأۡتِيَهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Choncho chidzawadzera mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَيَقُولُواْ هَلۡ نَحۡنُ مُنظَرُونَ
Tero adzayamba kunena: “Kodi ife tipatsidwa nthawi (yoti tilape)?”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi akuchifulumizitsa chilango Chathu?
அரபு விரிவுரைகள்:
أَفَرَءَيۡتَ إِن مَّتَّعۡنَٰهُمۡ سِنِينَ
Kodi ukuona bwanji, ngati titawasangalatsa zaka (zankhaninkhani).
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ جَآءَهُم مَّا كَانُواْ يُوعَدُونَ
Kenako nkuwadzera (chilango) chomwe adalonjezedwa,
அரபு விரிவுரைகள்:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يُمَتَّعُونَ
Sizidawathandize zomwe adali kusangalatsidwa nazozo.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآ أَهۡلَكۡنَا مِن قَرۡيَةٍ إِلَّا لَهَا مُنذِرُونَ
Ndipo sitidauononge mudzi uliwonse koma udali ndi achenjezi.
அரபு விரிவுரைகள்:
ذِكۡرَىٰ وَمَا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Kuti akhale) chikumbutso. Ndipo sitidali osalungama (powaononga popanda kuwachenjeza).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَا تَنَزَّلَتۡ بِهِ ٱلشَّيَٰطِينُ
Ndipo asatana sadaivumbulutse (iyi Qur’an monga osakhulupirira akunenera monyoza).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَا يَنۢبَغِي لَهُمۡ وَمَا يَسۡتَطِيعُونَ
Ndipo sikoyenera kwa iwo (kuivumbulutsa Qur’an) ndiponso sangathe.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّهُمۡ عَنِ ٱلسَّمۡعِ لَمَعۡزُولُونَ
Ndithu iwo ngotsekerezedwa kumvetsera (zimene angelo amalankhula kumwamba).
அரபு விரிவுரைகள்:
فَلَا تَدۡعُ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَ فَتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُعَذَّبِينَ
Choncho usapembedze mulungu wina pamodzi ndi Allah, kuti ungakhale mwa olangidwa.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَنذِرۡ عَشِيرَتَكَ ٱلۡأَقۡرَبِينَ
Ndipo achenjeze abale ako a pafupi.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱخۡفِضۡ جَنَاحَكَ لِمَنِ ٱتَّبَعَكَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndipo fungatira ndi phiko lako amene akutsata mwa okhulupirira. (Ukhale wachifundo kwa iwo).
அரபு விரிவுரைகள்:
فَإِنۡ عَصَوۡكَ فَقُلۡ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّمَّا تَعۡمَلُونَ
Ngati atakunyoza, nena: “Ine ndili kutali ndi zimene mukuchitazo.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱلۡعَزِيزِ ٱلرَّحِيمِ
Ndipo tsamira kwa (Mbuye wako) Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
ٱلَّذِي يَرَىٰكَ حِينَ تَقُومُ
Yemwe akukuona pamene ukuimilira (pamapemphero).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَتَقَلُّبَكَ فِي ٱلسَّٰجِدِينَ
Ndikutembenukatembenuka kwako (pogwetsa mphumi yako pansi ndi kudzuka ndi kuimilira) pamodzi ndi ogwetsa mphumi pansi (polambira Allah).
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndithu Iye Ngwakumva; Ngodziwa chilichonse.
அரபு விரிவுரைகள்:
هَلۡ أُنَبِّئُكُمۡ عَلَىٰ مَن تَنَزَّلُ ٱلشَّيَٰطِينُ
Kodi ndikuuzeni amene asatana amawatsikira?
அரபு விரிவுரைகள்:
تَنَزَّلُ عَلَىٰ كُلِّ أَفَّاكٍ أَثِيمٖ
Amamtsikira yense wabodza lamkunkhuniza; wamachimo.
அரபு விரிவுரைகள்:
يُلۡقُونَ ٱلسَّمۡعَ وَأَكۡثَرُهُمۡ كَٰذِبُونَ
Amawaponyera (asatana anzawo a mu anthu) zimene azimva. Koma ambiri a iwo ngabodza.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱلشُّعَرَآءُ يَتَّبِعُهُمُ ٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo alakatuli (olakatula zopanda phindu) amatsatidwa ndi (anthu) opotoka.
அரபு விரிவுரைகள்:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّهُمۡ فِي كُلِّ وَادٖ يَهِيمُونَ
Kodi suona kuti iwo akungoyumbayumba m’chigwa chilichonse (chamawu)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَنَّهُمۡ يَقُولُونَ مَا لَا يَفۡعَلُونَ
Ndithunso iwo akunena zomwe sachita.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَذَكَرُواْ ٱللَّهَ كَثِيرٗا وَٱنتَصَرُواْ مِنۢ بَعۡدِ مَا ظُلِمُواْۗ وَسَيَعۡلَمُ ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ أَيَّ مُنقَلَبٖ يَنقَلِبُونَ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, ndikumamtchula Allah mowirikiza, ndikuzipulumutsa okha pambuyo pochitiridwa zoipa. Ndipo posachedwa amene adzichitira okha zoipa adziwa kotembenukira komwe adzatembenukire.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அஷ்ஷுஅரா
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக