அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா நூஹ்   வசனம்:

ஸூரா நூஹ்

إِنَّآ أَرۡسَلۡنَا نُوحًا إِلَىٰ قَوۡمِهِۦٓ أَنۡ أَنذِرۡ قَوۡمَكَ مِن قَبۡلِ أَن يَأۡتِيَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndithu Ife tidamtuma Nuh kwa anthu ake, (ndikumuuza kuti): “Chenjeza anthu ako chisadawafike chilango chowawa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ يَٰقَوۡمِ إِنِّي لَكُمۡ نَذِيرٞ مُّبِينٌ
Adanena (Nuh): “E inu anthu anga! Ndithu ine ndimchenjezi kwa inu woonekera poyera (wolongosola za uthenga wa Mbuye wanu m’chiyankhulo chimene mukuchidziwa).”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَنِ ٱعۡبُدُواْ ٱللَّهَ وَٱتَّقُوهُ وَأَطِيعُونِ
“Mpembedzeni Allah ndipo rnuopeni ndikutinso mundimvere (pazimene ndikukulangizani).”
அரபு விரிவுரைகள்:
يَغۡفِرۡ لَكُم مِّن ذُنُوبِكُمۡ وَيُؤَخِّرۡكُمۡ إِلَىٰٓ أَجَلٖ مُّسَمًّىۚ إِنَّ أَجَلَ ٱللَّهِ إِذَا جَآءَ لَا يُؤَخَّرُۚ لَوۡ كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
“(Ngati mutero) adzakukhululukirani machimo anu ndi kukutalikitsirani moyo wanu kufikira m’nthawi imene yaikidwa (kuti ndiwo malire a kutalika kwa moyo). Ndithu nthawi ya Allah ikabwera siyichedwetsedwa (ngakhale pang’ono) mukadakhala mukudziwa.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ رَبِّ إِنِّي دَعَوۡتُ قَوۡمِي لَيۡلٗا وَنَهَارٗا
Adanena (Nuh): “E Mbuye wanga! Ndithu ine ndaitanira anthu anga (ku chikhulupiliro) usiku ndi usana (popanda kufooka).”
அரபு விரிவுரைகள்:
فَلَمۡ يَزِدۡهُمۡ دُعَآءِيٓ إِلَّا فِرَارٗا
“Kuitana kwanga sikudaonjezere (chilichonse) koma kuthawa basi (kuchikhulupiliro Chanu).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِنِّي كُلَّمَا دَعَوۡتُهُمۡ لِتَغۡفِرَ لَهُمۡ جَعَلُوٓاْ أَصَٰبِعَهُمۡ فِيٓ ءَاذَانِهِمۡ وَٱسۡتَغۡشَوۡاْ ثِيَابَهُمۡ وَأَصَرُّواْ وَٱسۡتَكۡبَرُواْ ٱسۡتِكۡبَارٗا
Ndipo ine nthawi iliyonse ndikawaitanira (ku chikhulupiliro Chanu) kuti mwakhululukire, akuika zala zawo m’makutu mwawo (kuti asamve uthenga Wanu), ndipo akudziphimba ndi nsalu zawo (kuti asaone nkhope yanga), ndipo akupitiriza kukana kwawo ndi kudzikweza kwakukulu.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ إِنِّي دَعَوۡتُهُمۡ جِهَارٗا
Kenaka ine ndawaitanira (kwa Inu) ndi mawu ofuula,
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ إِنِّيٓ أَعۡلَنتُ لَهُمۡ وَأَسۡرَرۡتُ لَهُمۡ إِسۡرَارٗا
Kenakanso (ine ndawaitanira) molengeza poyera ndiponso mwachinsinsi mobisa.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَقُلۡتُ ٱسۡتَغۡفِرُواْ رَبَّكُمۡ إِنَّهُۥ كَانَ غَفَّارٗا
Choncho ndidati (kwa anthu anga): Pemphani kwa Mbuye wanu chikhululuko (pa kukana kwanu ndi kutonza kwanu), ndithu Iye ali Wokhululuka kwambiri.
அரபு விரிவுரைகள்:
يُرۡسِلِ ٱلسَّمَآءَ عَلَيۡكُم مِّدۡرَارٗا
Akutumizirani mvula yotsika mochuluka,
அரபு விரிவுரைகள்:
وَيُمۡدِدۡكُم بِأَمۡوَٰلٖ وَبَنِينَ وَيَجۡعَل لَّكُمۡ جَنَّٰتٖ وَيَجۡعَل لَّكُمۡ أَنۡهَٰرٗا
Ndikukupatsani chuma ndi ana, (zomwe ndi zokongoletsa za dziko lapansi), ndi kukupangirani minda (yokongola) ndi kukupangirani mitsinje (yothilira mbewu zanu ndi kumwetsa ziweto zanu).
அரபு விரிவுரைகள்:
مَّا لَكُمۡ لَا تَرۡجُونَ لِلَّهِ وَقَارٗا
Kodi chifukwa ninji simupereka ulemu kwa Allah (woyenera Umulungu Wake kuti akakuchitireni chifundo ndi kukupulumutsani ku chilango)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقَدۡ خَلَقَكُمۡ أَطۡوَارًا
Pomwe Iye adakulengani mnjira zosiyanasiyana; (madzi a umunthu, kenako magazi, kenako magazi ochindikala, kenako mafupa ndipo kenako mnofu),
அரபு விரிவுரைகள்:
أَلَمۡ تَرَوۡاْ كَيۡفَ خَلَقَ ٱللَّهُ سَبۡعَ سَمَٰوَٰتٖ طِبَاقٗا
Kodi simudaone momwe Allah adalengera thambo zisanu ndi ziwiri mosanjikizana?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَجَعَلَ ٱلۡقَمَرَ فِيهِنَّ نُورٗا وَجَعَلَ ٱلشَّمۡسَ سِرَاجٗا
Ndi kuyika mwezi mthambomo kukhala kuunika, ndiponso kuyika dzuwa kukhala nyali.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱللَّهُ أَنۢبَتَكُم مِّنَ ٱلۡأَرۡضِ نَبَاتٗا
Ndipo Allah adakulengani kuchokera m’nthaka monga mmera.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ يُعِيدُكُمۡ فِيهَا وَيُخۡرِجُكُمۡ إِخۡرَاجٗا
Kenako adzakubwezerani momwemo ndikudzakutulutsaninso (popanda cholepheretsa).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَٱللَّهُ جَعَلَ لَكُمُ ٱلۡأَرۡضَ بِسَاطٗا
Ndipo Allah wakupangirani nthaka kukhala ngati choyala,
அரபு விரிவுரைகள்:
لِّتَسۡلُكُواْ مِنۡهَا سُبُلٗا فِجَاجٗا
Kuti muziyendayenda m’menemo m’njira zazikulu.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قَالَ نُوحٞ رَّبِّ إِنَّهُمۡ عَصَوۡنِي وَٱتَّبَعُواْ مَن لَّمۡ يَزِدۡهُ مَالُهُۥ وَوَلَدُهُۥٓ إِلَّا خَسَارٗا
Adanena Nuh: “Mbuye wanga! Ndithu anthu anga andinyoza (pa zimene ndawalamula kuti akhulupirire Inu ndi kupempha chikhululuko chanu), ndipo (ofooka mwa iwo) amtsatira yemwe chuma chake ndi ana ake sizidzamuonjezera (chilichonse chabwino) koma kutaika (ndi kuonongeka pa tsiku lachimaliziro).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَكَرُواْ مَكۡرٗا كُبَّارٗا
Ndipo (eni chuma ndi ana) awatchera (otsatira awo) ndale zazikulu (ndi zopyola muyeso kuti asakhulupirire).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقَالُواْ لَا تَذَرُنَّ ءَالِهَتَكُمۡ وَلَا تَذَرُنَّ وَدّٗا وَلَا سُوَاعٗا وَلَا يَغُوثَ وَيَعُوقَ وَنَسۡرٗا
Ndipo adanena (kwa owatsatira awo): “Musasiye kupembedza milungu yanu; musamusiye Wadda, Suwaa’, Yaghutha, Ya’uqa ndi Nasra” (maina a mafano awo).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقَدۡ أَضَلُّواْ كَثِيرٗاۖ وَلَا تَزِدِ ٱلظَّٰلِمِينَ إِلَّا ضَلَٰلٗا
Ndipo ndithu iwo asokeretsa (anthu) ambiri; ndipo musawaonjezere ochita zoipa (china chake) koma kusokera basi.”
அரபு விரிவுரைகள்:
مِّمَّا خَطِيٓـَٰٔتِهِمۡ أُغۡرِقُواْ فَأُدۡخِلُواْ نَارٗا فَلَمۡ يَجِدُواْ لَهُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ أَنصَارٗا
Chifukwa cha zochimwa zawo adamizidwa ndi kulowetsedwa ku Moto (waukulu woyaka); sadapeze owapulumutsa ndi kuwateteza m’malo mwa Allah.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَقَالَ نُوحٞ رَّبِّ لَا تَذَرۡ عَلَى ٱلۡأَرۡضِ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ دَيَّارًا
Ndipo adanena Nuh (atataya mtima za anthu ake): “Mbuye wanga! Musasiye aliyense mwa osakhulupirira kukhala pa dziko.”
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّكَ إِن تَذَرۡهُمۡ يُضِلُّواْ عِبَادَكَ وَلَا يَلِدُوٓاْ إِلَّا فَاجِرٗا كَفَّارٗا
“Ndithu Inu Mbuye wanga ngati muwasiya (popanda kuwaononga ndi kuwathetsa) asokeretsa akapolo anu (kunjira yolungama). Ndipo sangabereke (ana abwino) koma oipa; osakhulupirira (okhala kutali ndi choonadi, ndiponso onyoza Inu).”
அரபு விரிவுரைகள்:
رَّبِّ ٱغۡفِرۡ لِي وَلِوَٰلِدَيَّ وَلِمَن دَخَلَ بَيۡتِيَ مُؤۡمِنٗا وَلِلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِۖ وَلَا تَزِدِ ٱلظَّٰلِمِينَ إِلَّا تَبَارَۢا
“Mbuye wanga! Ndikhululukireni ndi makolo anga, ndi aliyense walowa m’nyumba yanga ali okhulupirira ndi okhulupirira amuna ndi okhulupirira akazi. Ndipo musawaonjezere anthu achinyengo chinachake koma kuwaononga basi.”
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா நூஹ்
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக