அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அத்தீன்   வசனம்:

ஸூரா அத்தீன்

وَٱلتِّينِ وَٱلزَّيۡتُونِ
Ndikulumbilira mitengo ya Mkuyu ndi Zitona (pansi pa mitengo imeneyi Ibrahim ndi Nuh (Nowa) adapeza uneneri),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَطُورِ سِينِينَ
Ndi phiri la Sinai (pamene Allah adamulankhulira Mûsa),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَهَٰذَا ٱلۡبَلَدِ ٱلۡأَمِينِ
Ndiponso mzinda uwu (wolemekezeka) wamtendere; (Makka, womwe adapatsiridwa uneneri Muhammad) (s.a.w).
அரபு விரிவுரைகள்:
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِيٓ أَحۡسَنِ تَقۡوِيمٖ
Palibe chikaiko, tamulenga munthu mkalengedwe kabwino, kolingana (ndipo ali ndi mbiri zabwino).[457]
[457] M’gulu la nyama palibe yopambana kuposa munthu mkalengedwe ndi pa nzeru.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ رَدَدۡنَٰهُ أَسۡفَلَ سَٰفِلِينَ
Pambuyo pake tamubwezera pansi kumposa wa pansi.[458]
[458] Munthu ali ndi makhalidwe awiri: Ngati agwiritsa ntchito nzeru zake amaongoka ndipo amaiposa nyama ili yonse. Koma ngati sagwiritsa ntchito nzeru zake amasokera ndi kukhala wapansi kuposa nyama zonse.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ فَلَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونٖ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, adzakhala nawo iwo malipiro osatha.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَمَا يُكَذِّبُكَ بَعۡدُ بِٱلدِّينِ
Tsono nchiyani chakuchititsa kuti ukanire kuuka ndi malipiro pambuyo (poona mphamvu zathu pa chilichonse)?[459]
[459] (Ndime 7-8) Allah akuuza munthu kuti: Pambuyo podziwa kuti Allah ndi Yemwe adapanga zimenezo, ndi chiyani nanga chikumukaikitsa za tsiku la chiweruziro?
அரபு விரிவுரைகள்:
أَلَيۡسَ ٱللَّهُ بِأَحۡكَمِ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Kodi Allah si Muweruzi wa nzeru kuposa aweruzi onse?
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அத்தீன்
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக