Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Yūsuf   Ayah:

Yūsuf

الٓرۚ تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Alif-Lâm-Ra. Izi ndi Ayah (ndime) za m’buku lomwe likuonetsera poyera (chilichonse chofunika).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّآ أَنزَلۡنَٰهُ قُرۡءَٰنًا عَرَبِيّٗا لَّعَلَّكُمۡ تَعۡقِلُونَ
Ndithu Ife taivumbulutsa Qur’an ya Charabu kuti inu muzindikire.
Ang mga Tafsir na Arabe:
نَحۡنُ نَقُصُّ عَلَيۡكَ أَحۡسَنَ ٱلۡقَصَصِ بِمَآ أَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡكَ هَٰذَا ٱلۡقُرۡءَانَ وَإِن كُنتَ مِن قَبۡلِهِۦ لَمِنَ ٱلۡغَٰفِلِينَ
Ife tikukusimbira nkhani zabwino zedi pokuzindikiritsa Qur’an iyi; ndithu udali mmodzi mwa osadziwa zinthu, isanakufike.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِذۡ قَالَ يُوسُفُ لِأَبِيهِ يَٰٓأَبَتِ إِنِّي رَأَيۡتُ أَحَدَ عَشَرَ كَوۡكَبٗا وَٱلشَّمۡسَ وَٱلۡقَمَرَ رَأَيۡتُهُمۡ لِي سَٰجِدِينَ
Akumbutse za Yûsuf pamene adauza bambo wake: “E inu bambo wanga! Ndithu ine ndaona kutulo nyenyezi khumi ndi imodzi, dzuwa ndi mwezi, zonsezo ndaziona zikundigwadira.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ يَٰبُنَيَّ لَا تَقۡصُصۡ رُءۡيَاكَ عَلَىٰٓ إِخۡوَتِكَ فَيَكِيدُواْ لَكَ كَيۡدًاۖ إِنَّ ٱلشَّيۡطَٰنَ لِلۡإِنسَٰنِ عَدُوّٞ مُّبِينٞ
(Bambo wake) adati: “E iwe mwana wanga! Usawasimbire abale ako maloto ako (kuopa kuti) angakuchitire chiwembu; ndithu satana kwa munthu, ndi mdani woonekera.”[228]
[228] Sibwino munthu kufotokozera anthu chisomo chako chonse ngati palibe zofunikira kutero. Dziwani kuti mwini madalitso ngochitiridwa dumbo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَكَذَٰلِكَ يَجۡتَبِيكَ رَبُّكَ وَيُعَلِّمُكَ مِن تَأۡوِيلِ ٱلۡأَحَادِيثِ وَيُتِمُّ نِعۡمَتَهُۥ عَلَيۡكَ وَعَلَىٰٓ ءَالِ يَعۡقُوبَ كَمَآ أَتَمَّهَا عَلَىٰٓ أَبَوَيۡكَ مِن قَبۡلُ إِبۡرَٰهِيمَ وَإِسۡحَٰقَۚ إِنَّ رَبَّكَ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
“Ndipo momwemo Mbuye wako akusankha komanso akuphunzitsa kumasulira nkhani (za maloto) ndi kukwaniritsa mtendere Wake pa iwe, ndi pa mbumba ya Ya’qub monga momwe adakwaniritsira kwa makolo ako kale, Ibrahim ndi Ishaq. Ndithu Mbuye wako Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ لَّقَدۡ كَانَ فِي يُوسُفَ وَإِخۡوَتِهِۦٓ ءَايَٰتٞ لِّلسَّآئِلِينَ
Ndithu mwa Yûsuf ndi abale ake, muli malingaliro ambiri kwa ofunsa (zinthu kuti adziwe).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِذۡ قَالُواْ لَيُوسُفُ وَأَخُوهُ أَحَبُّ إِلَىٰٓ أَبِينَا مِنَّا وَنَحۡنُ عُصۡبَةٌ إِنَّ أَبَانَا لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٍ
Kumbuka pamene (abale a Yûsuf) adati: “Ndithu Yûsuf ndi m’bale wake (Binyamini) ngokondeka zedi kwa bambo wathu kuposa ife pomwe ife ndife gulu lamphamvu. Ndithu bambo wathu ali mkusokera koonekera (sadziwa yemwe ali ndi chithandizo chokwanira).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱقۡتُلُواْ يُوسُفَ أَوِ ٱطۡرَحُوهُ أَرۡضٗا يَخۡلُ لَكُمۡ وَجۡهُ أَبِيكُمۡ وَتَكُونُواْ مِنۢ بَعۡدِهِۦ قَوۡمٗا صَٰلِحِينَ
“Mupheni Yûsuf kapena mukamponye ku dziko (lakutali), kuti nkhope ya bambo wanu ikutembenukireni (pakuti nthawi imeneyo Yûsuf sadzakhalapo, yemwe akumkonda kwambiriyo); ndipo pambuyo pake (mutalapa tchimoli) mdzakhala abwino, (kwa Allah).”[229]
[229] Dyera loipa kwambiri ndiko kunena koti: “Tandisiyani ndichite machimo, kenako ndidzalapa.” Dziwani kuti machimo omwe Allah angawakhululuke ngomwe munthu wawachita mosazindikira kapena kuti popanda kuwafunafuna, osati owachita mwadaladala ncholinga choti adzalapa pambuyo pake monga momwe abale ake a Yusuf ankaganizira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ قَآئِلٞ مِّنۡهُمۡ لَا تَقۡتُلُواْ يُوسُفَ وَأَلۡقُوهُ فِي غَيَٰبَتِ ٱلۡجُبِّ يَلۡتَقِطۡهُ بَعۡضُ ٱلسَّيَّارَةِ إِن كُنتُمۡ فَٰعِلِينَ
Adanena wonena mwa iwo: “Musamuphe Yûsuf, koma mponyeni m’chitsime chakuya; adzamtola ena a paulendo ngati inu mwalingadi kutelo.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا مَا لَكَ لَا تَأۡمَ۬نَّا عَلَىٰ يُوسُفَ وَإِنَّا لَهُۥ لَنَٰصِحُونَ
(Pambuyo pogwirizana paganizo lomuponya m’chitsime chakuya adapita kwa bambo wawo) anati: “E bambo wathu! Kodi bwanji simutikhulupirira pa Yûsuf, pomwe ife timamfunira zabwino?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَرۡسِلۡهُ مَعَنَا غَدٗا يَرۡتَعۡ وَيَلۡعَبۡ وَإِنَّا لَهُۥ لَحَٰفِظُونَ
Mperekeni mawa pamodzi ndi ife (kubusa) kuti akadye mokondwa ndi kusewera; ndithudi, ife tikamsamala.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ إِنِّي لَيَحۡزُنُنِيٓ أَن تَذۡهَبُواْ بِهِۦ وَأَخَافُ أَن يَأۡكُلَهُ ٱلذِّئۡبُ وَأَنتُمۡ عَنۡهُ غَٰفِلُونَ
(Bambo wawo) adati: “Ndithu zikundidandaulitsa zakuti mupite naye; ndikuopa kuti angajiwe ndi mimbulu pomwe inu simukulabadira za iye.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ لَئِنۡ أَكَلَهُ ٱلذِّئۡبُ وَنَحۡنُ عُصۡبَةٌ إِنَّآ إِذٗا لَّخَٰسِرُونَ
(Iwo) adati: “Ngati mimbulu itamudya pomwe ife ndife gulu lanyonga kwambiri, ndiye kuti tidzakhala otaika.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا ذَهَبُواْ بِهِۦ وَأَجۡمَعُوٓاْ أَن يَجۡعَلُوهُ فِي غَيَٰبَتِ ٱلۡجُبِّۚ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡهِ لَتُنَبِّئَنَّهُم بِأَمۡرِهِمۡ هَٰذَا وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Ndipo pamene adanka naye ndi kugwirizana pakati pawo kuti amuike mchitsime chakuya, (adamuikadi). Ndipo tidamzindikiritsa iye (Yûsuf): “Ndithu udzawauza chinthu chawochi (chimene akuchitirachi) pomwe iwo sakudziwa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءُوٓ أَبَاهُمۡ عِشَآءٗ يَبۡكُونَ
Ndipo adadza kwa bambo awo madzulo akulira,
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ يَٰٓأَبَانَآ إِنَّا ذَهَبۡنَا نَسۡتَبِقُ وَتَرَكۡنَا يُوسُفَ عِندَ مَتَٰعِنَا فَأَكَلَهُ ٱلذِّئۡبُۖ وَمَآ أَنتَ بِمُؤۡمِنٖ لَّنَا وَلَوۡ كُنَّا صَٰدِقِينَ
Akunena: “E bambo wathu! Tidapita kokapikisana (kuthamanga), ndipo tidamsiya Yûsuf pomwe padali ziwiya zathu; choncho mimbulu yamudya koma inu simutikhulupirira (pa zimene tikukuuzanizi) ngakhale kuti tikunena zoona.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءُو عَلَىٰ قَمِيصِهِۦ بِدَمٖ كَذِبٖۚ قَالَ بَلۡ سَوَّلَتۡ لَكُمۡ أَنفُسُكُمۡ أَمۡرٗاۖ فَصَبۡرٞ جَمِيلٞۖ وَٱللَّهُ ٱلۡمُسۡتَعَانُ عَلَىٰ مَا تَصِفُونَ
Ndiponso adabwera ndi mkanjo wake (wa Yûsuf) uli ndi magazi abodza. (Bambo wawo pamene adauona mkanjowo uli wosang’ambika) adati: “Koma mitima yanu yakukometserani chinthu (chomwe mwamchitira mnzanu mwa chifuniro chanu; ndipo chimene ine ndingachite ndi) kupirira kwabwino; ndipo Allah ndi Wopemphedwa chithandizo pa zimene mukunenazi.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءَتۡ سَيَّارَةٞ فَأَرۡسَلُواْ وَارِدَهُمۡ فَأَدۡلَىٰ دَلۡوَهُۥۖ قَالَ يَٰبُشۡرَىٰ هَٰذَا غُلَٰمٞۚ وَأَسَرُّوهُ بِضَٰعَةٗۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِمَا يَعۡمَلُونَ
Ndipo aulendo adadza (pafupi ndi chitsimecho) ndipo adatuma wotunga madzi wawo, choncho iye adaponya ndowa yake (m’chitsime, ndipo akukoka ndowa ija adaona mwana) nati: “Eee, chisangalalo changa! Aka kamwana kakamuna!” Pomwepo iwo (amene adalipo pa chitsimepo) adam’bisa (kwa a paulendo anzawo) monga katundu wamalonda (yemwe adamgula). Koma Allah ankadziwa zimene adali kuchita (ndipo adanka naye ku Iguputo).[230]
[230] 19-20. Apa tikuona kuti kugulitsana anthu kudayambika kalekale zedi kuyambira zaka 4,000 zapitazo mu nthawi ya umbuli. Koma adani achipembedzo cha Chisilamu akuchinamizira Chisilamu kuti ndicho chidadza ndi ukapolo wogulitsa anthu. Chikhalirecho Chisilamu ndicho chidadza kuzalimbikitsa zopereka ufulu kwa kapolo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَشَرَوۡهُ بِثَمَنِۭ بَخۡسٖ دَرَٰهِمَ مَعۡدُودَةٖ وَكَانُواْ فِيهِ مِنَ ٱلزَّٰهِدِينَ
Ndipo adamgulitsa pa mtengo wochepa ndi ndalama zapang’ono, zowerengeka (poopa kuti angawadzere eni mwanayo). Ndipo sadalabadire za iye.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ ٱلَّذِي ٱشۡتَرَىٰهُ مِن مِّصۡرَ لِٱمۡرَأَتِهِۦٓ أَكۡرِمِي مَثۡوَىٰهُ عَسَىٰٓ أَن يَنفَعَنَآ أَوۡ نَتَّخِذَهُۥ وَلَدٗاۚ وَكَذَٰلِكَ مَكَّنَّا لِيُوسُفَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلِنُعَلِّمَهُۥ مِن تَأۡوِيلِ ٱلۡأَحَادِيثِۚ وَٱللَّهُ غَالِبٌ عَلَىٰٓ أَمۡرِهِۦ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo uja (amene) adamgula ku Iguputo, adati kwa mkazi wake: “Mkonzere pokhala pabwino (kapolo uyu), mwina angatithandize kapena tingamsandutse kukhala mwana (wathu).” Motero tidamkhazika Yûsuf m’dziko (la Iguputo mwachisangalalo), ndi kuti timphunzitse kumasulira nkhani (maloto). Ndipo Allah Ngopambana pa zinthu Zake (zimene wafuna kuti zichitike); koma anthu ambiri sadziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا بَلَغَ أَشُدَّهُۥٓ ءَاتَيۡنَٰهُ حُكۡمٗا وَعِلۡمٗاۚ وَكَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo pamene (Yûsuf) adafika pa nsinkhu wozindikira zinthu, tidampatsa kuweruza ndi nzeru. Umo ndi momwe timawalipirira ochita zabwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَرَٰوَدَتۡهُ ٱلَّتِي هُوَ فِي بَيۡتِهَا عَن نَّفۡسِهِۦ وَغَلَّقَتِ ٱلۡأَبۡوَٰبَ وَقَالَتۡ هَيۡتَ لَكَۚ قَالَ مَعَاذَ ٱللَّهِۖ إِنَّهُۥ رَبِّيٓ أَحۡسَنَ مَثۡوَايَۖ إِنَّهُۥ لَا يُفۡلِحُ ٱلظَّٰلِمُونَ
Ndipo mkazi uja yemwe m’nyumba mwake mudali iye adamlakalaka (Yûsuf) popanda iye kufuna. Ndipo (mkaziyo) adatseka zitseko nati: “Bwera kuno.” (Yûsuf) adati: “Ndikudzitchinjiriza ndi Allah (kuchita tchimolo). Ndithu iye (mwamuna wako) ndi bwana wanga. Wandikonzera bwino pokhala panga (m’nyumba mwakemu, ndipo sindichita chinyengo chotere). Ndithu achinyengo siziwayendera bwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَقَدۡ هَمَّتۡ بِهِۦۖ وَهَمَّ بِهَا لَوۡلَآ أَن رَّءَا بُرۡهَٰنَ رَبِّهِۦۚ كَذَٰلِكَ لِنَصۡرِفَ عَنۡهُ ٱلسُّوٓءَ وَٱلۡفَحۡشَآءَۚ إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Ndipo (mkaziyo) adaikira mtima pa iye (kuti achite naye kanthu), ndipo naye (Yûsuf) adaikira mtima pa iye (kuti ammenye). Pakadapanda kuona chisonyezo cha Mbuye wake (chakumzindikiritsa kuti asatero, akadammenya. Koma adamthawa). Tidachita izi kuti timchotsere chinthu choipa ndi chauve; ndithudi, iye adali mwa akapolo athu oyeretsedwa.[231]
[231] Musamchitire choipa amene wakuchitirani chabwino, ngakhalenso amene wakuchitrani choipa kumene. Makamaka amene sadakuchitireni choipa (ndiye chisimu). Koma alipo anthu ena oipitsitsa zedi amene amachitira zoipa yemwe akuwachitira zabwino. Anthu otero ngoipitsitsa kuposa nyama zamtchire, ndipo oterewa Allah adzawakhaulitsa koopsa. Ndipo machitidwe okhala mwamuna ndi mkazi kuseri kwaokha ngoletsedwa m’shariya ya Chisilamu chifukwa mwamuna kukhala ndi mkazi amene sali mnyazi wake kumalakwitsa. Musati awa ndi alamu ndikhoza kukhala nawo pawokha. Kukhala ndi mlamu wako kuseri, ndi ngozi imeneyo!
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱسۡتَبَقَا ٱلۡبَابَ وَقَدَّتۡ قَمِيصَهُۥ مِن دُبُرٖ وَأَلۡفَيَا سَيِّدَهَا لَدَا ٱلۡبَابِۚ قَالَتۡ مَا جَزَآءُ مَنۡ أَرَادَ بِأَهۡلِكَ سُوٓءًا إِلَّآ أَن يُسۡجَنَ أَوۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo (onse awiri) adathamangitsana kukhomo (uku Yûsuf akuthawa) ndipo (mkaziyo) adang’amba mkanjo wake chakumbuyo. Ndipo awiriwa adampeza bwana wake (wa mkaziyo yemwe ndimwamuna wake) pakhomo; mkaziyo adati (kwa mwamuna wake mwaugogodi): “Palibe mphoto kwa yemwe akufuna kuchita choipa ndi mkazi wako koma kumponya kundende, kapena kupatsidwa chilango chowawa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ هِيَ رَٰوَدَتۡنِي عَن نَّفۡسِيۚ وَشَهِدَ شَاهِدٞ مِّنۡ أَهۡلِهَآ إِن كَانَ قَمِيصُهُۥ قُدَّ مِن قُبُلٖ فَصَدَقَتۡ وَهُوَ مِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
(Yûsuf) adati (podziteteza): “(Mkazi) uyu ndi yemwe wandifuna popanda ine kumufuna.” Ndipo mboni yochokera ku banja la mkaziyo idaikira umboni; (idati): “Ngati mkanjo wake wang’ambidwa cha kutsogolo, ndiye kuti (mkazi uyu) akunena zoona, ndipo iye (Yûsuf) ndi mmodzi mwa onena zabodza.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِن كَانَ قَمِيصُهُۥ قُدَّ مِن دُبُرٖ فَكَذَبَتۡ وَهُوَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Koma ngati mkanjo wake wang’ambidwa chakumbuyo ndiye kuti (mkazi uyu) wanena bodza ndipo iye (Yûsuf) ndi mmodzi mwa onena zoona.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا رَءَا قَمِيصَهُۥ قُدَّ مِن دُبُرٖ قَالَ إِنَّهُۥ مِن كَيۡدِكُنَّۖ إِنَّ كَيۡدَكُنَّ عَظِيمٞ
Choncho (mwamuna uja) pamene adaona mkanjo wake (wa Yûsuf) utang’ambidwa chakumbuyo, (adadziwa kuti Yûsuf ndi amene amafuna kugwiliridwa), adati: “Ndithudi, izi ndi ndale zanu akazi. Ndithu ndale zanu ndi zazikulu (iwe mkazi wanga ndi amene udatsimikiza kuchita choipa ndi mnyamatayu).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
يُوسُفُ أَعۡرِضۡ عَنۡ هَٰذَاۚ وَٱسۡتَغۡفِرِي لِذَنۢبِكِۖ إِنَّكِ كُنتِ مِنَ ٱلۡخَاطِـِٔينَ
“Yûsuf! Zisiye izi (usauze aliyense). Ndipo (iwe mkazi) pempha chikhululuko ku tchimo lako. Ndithu iwe ndiwe mmodzi mwa olakwa!”
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَقَالَ نِسۡوَةٞ فِي ٱلۡمَدِينَةِ ٱمۡرَأَتُ ٱلۡعَزِيزِ تُرَٰوِدُ فَتَىٰهَا عَن نَّفۡسِهِۦۖ قَدۡ شَغَفَهَا حُبًّاۖ إِنَّا لَنَرَىٰهَا فِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٖ
Ndipo akazi a mu mzindamo (ataimva nkhaniyi) anati: “Mkazi wa nduna akulakalaka m’nyamata wake popanda kulakalakidwa ndi iye; ndithu chikondi chamufooketsa zedi; ndithudi, ife tikumuona (mkaziyu kuti) ali m’kusokera koonekera.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا سَمِعَتۡ بِمَكۡرِهِنَّ أَرۡسَلَتۡ إِلَيۡهِنَّ وَأَعۡتَدَتۡ لَهُنَّ مُتَّكَـٔٗا وَءَاتَتۡ كُلَّ وَٰحِدَةٖ مِّنۡهُنَّ سِكِّينٗا وَقَالَتِ ٱخۡرُجۡ عَلَيۡهِنَّۖ فَلَمَّا رَأَيۡنَهُۥٓ أَكۡبَرۡنَهُۥ وَقَطَّعۡنَ أَيۡدِيَهُنَّ وَقُلۡنَ حَٰشَ لِلَّهِ مَا هَٰذَا بَشَرًا إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا مَلَكٞ كَرِيمٞ
Ndipo (mkazi wa nduna) pamene adamva kunyogodola kwawo, adawaitana (kuti adzaone kukongola kwa Yûsuf kuti adziwe kuti yemwe wathedwa nzeru polakalaka Yûsuf ngosayenera kudzudzulidwa). Ndipo adawakonzera phwando ndikupatsa aliyense wa iwo mpeni; kenaka adamuuza (Yûsuf): “Tuluka ndi kubwera pamaso pa iwo.” Choncho pamene (akazi aja) adamuona, adaona kuti nchinthu chachikulu zedi ndipo adadzicheka manja awo (ndi mipeni ija. Sadazindikire kuti akudzicheka chifukwa cha chidwi ndi kukongola kwa Yûsuf), ndipo adati: “Hasha Lillah! (tikudzitchinjiriza kwa Allah) uyu simunthu, uyu sichina koma ndi mngelo wolemekezeka.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَتۡ فَذَٰلِكُنَّ ٱلَّذِي لُمۡتُنَّنِي فِيهِۖ وَلَقَدۡ رَٰوَدتُّهُۥ عَن نَّفۡسِهِۦ فَٱسۡتَعۡصَمَۖ وَلَئِن لَّمۡ يَفۡعَلۡ مَآ ءَامُرُهُۥ لَيُسۡجَنَنَّ وَلَيَكُونٗا مِّنَ ٱلصَّٰغِرِينَ
(Mkazi wa nduna) adati: “Uyu ndi amene mumandidzudzula naye. Ndithudi ndidamulakalaka pomwe iye samandifuna ndipo anadziteteza. Ndipo ngati sachita chimene ndikumulamula, ndithu amangidwa ndipo ndithu akhala m’gulu la onyozeka!”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ رَبِّ ٱلسِّجۡنُ أَحَبُّ إِلَيَّ مِمَّا يَدۡعُونَنِيٓ إِلَيۡهِۖ وَإِلَّا تَصۡرِفۡ عَنِّي كَيۡدَهُنَّ أَصۡبُ إِلَيۡهِنَّ وَأَكُن مِّنَ ٱلۡجَٰهِلِينَ
(Yûsuf) adati: “E Mbuye wanga! Ndende ndi yabwino kwa ine kuposa izi akundiitanira. Ngati simundichotsera ndale zawo ndiye kuti ndiwacheukira ndikukhala mmodzi mwa mbuli.”[232]
[232] Akazi aja atamuona Yûsuf tsiku limenelo nawonso anadzazidwa ndi chikondi chachikulu nayamba kumtumizira mithenga ndi makalata. Ndipo Yûsuf adaganiza kuti ndibwino angopita kundende poopa kuti akaziwo angamulakwitse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَٱسۡتَجَابَ لَهُۥ رَبُّهُۥ فَصَرَفَ عَنۡهُ كَيۡدَهُنَّۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo Mbuye wake adamuyankha (pempho lake) ndikumchotsera ndale zawo. Ndithudi, Iye Ngwakumva, Ngodziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ بَدَا لَهُم مِّنۢ بَعۡدِ مَا رَأَوُاْ ٱلۡأٓيَٰتِ لَيَسۡجُنُنَّهُۥ حَتَّىٰ حِينٖ
Kenako kudaoneka kwa iwo, (nduna ndi anthu ake) pambuyo poona zizindikiro (zonse zakuyeretsedwa kwa Yûsuf) kuti akamponye kundende kwa nthawi yochepa (pofuna kumusungira ulemu mkazi wa nduna).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَدَخَلَ مَعَهُ ٱلسِّجۡنَ فَتَيَانِۖ قَالَ أَحَدُهُمَآ إِنِّيٓ أَرَىٰنِيٓ أَعۡصِرُ خَمۡرٗاۖ وَقَالَ ٱلۡأٓخَرُ إِنِّيٓ أَرَىٰنِيٓ أَحۡمِلُ فَوۡقَ رَأۡسِي خُبۡزٗا تَأۡكُلُ ٱلطَّيۡرُ مِنۡهُۖ نَبِّئۡنَا بِتَأۡوِيلِهِۦٓۖ إِنَّا نَرَىٰكَ مِنَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo anyamata awiri adalowa m’ndende pamodzi ndi iye. Mmodzi mwa iwo adati (kumuuza Yûsuf): “Ndithu ine ndalota ndikufulula mowa.” Ndipo wina adati: “Ndithu ine ndalota ndikusenza mikate pamutu panga yomwe idali kudyedwa ndi mbalame. Tiuze tanthauzo lake. Ndithu ife tikukuona iwe kuti ndiwe mmodzi wa anthu abwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ لَا يَأۡتِيكُمَا طَعَامٞ تُرۡزَقَانِهِۦٓ إِلَّا نَبَّأۡتُكُمَا بِتَأۡوِيلِهِۦ قَبۡلَ أَن يَأۡتِيَكُمَاۚ ذَٰلِكُمَا مِمَّا عَلَّمَنِي رَبِّيٓۚ إِنِّي تَرَكۡتُ مِلَّةَ قَوۡمٖ لَّا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَهُم بِٱلۡأٓخِرَةِ هُمۡ كَٰفِرُونَ
(Yûsuf) adati: “(Kupyolera mu uneneri umene ndapatsidwa ndingathe kukumasulirani maloto anuwa ndi zinthu zina zobisika kwa inu), sichikudzerani chakudya cha mtundu uliwonse choti mungapatsidwe koma ndikhala nditakumasulirani tanthauzo lake chisanakufikeni; (ngati mukufunadi ndikuchitirani zimenezi). Izi ndi zina mwa zomwe Mbuye wanga wandiphunzitsa. Ndithudi, ine ndasiya njira za anthu osakhulupirira Allah ndiponso omwe akukana za tsiku la chimaliziro.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱتَّبَعۡتُ مِلَّةَ ءَابَآءِيٓ إِبۡرَٰهِيمَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَۚ مَا كَانَ لَنَآ أَن نُّشۡرِكَ بِٱللَّهِ مِن شَيۡءٖۚ ذَٰلِكَ مِن فَضۡلِ ٱللَّهِ عَلَيۡنَا وَعَلَى ٱلنَّاسِ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَشۡكُرُونَ
“Ndipo ine ndatsata chipembedzo cha makolo anga Ibrahim, Ishâq ndi Ya’qub; ndipo sikudali koyenera kwa ife kumphatikiza Allah ndi chilichonse. (Ndipo kuzindikira) zimenezi ndi ubwino wa Allah umene uli pa ife ndi anthu ena, koma anthu ambiri sathokoza.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰصَٰحِبَيِ ٱلسِّجۡنِ ءَأَرۡبَابٞ مُّتَفَرِّقُونَ خَيۡرٌ أَمِ ٱللَّهُ ٱلۡوَٰحِدُ ٱلۡقَهَّارُ
“E inu anzanga awiri a m’ndende! Kodi milungu yambiri yosiyana ndiyo yabwino (kupembedzedwa), kapena Allah Mmodzi Mwini mphamvu (pachilichonse)?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَا تَعۡبُدُونَ مِن دُونِهِۦٓ إِلَّآ أَسۡمَآءٗ سَمَّيۡتُمُوهَآ أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُم مَّآ أَنزَلَ ٱللَّهُ بِهَا مِن سُلۡطَٰنٍۚ إِنِ ٱلۡحُكۡمُ إِلَّا لِلَّهِ أَمَرَ أَلَّا تَعۡبُدُوٓاْ إِلَّآ إِيَّاهُۚ ذَٰلِكَ ٱلدِّينُ ٱلۡقَيِّمُ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
“Simupembedza china kusiya Iye (Allah) koma ndi maina basi amene inu nokha mudawatcha ndi makolo anu, Allah sadatsitse umboni uliwonse pa zimenezo. Palibe lamulo lina koma ndi la Allah basi. Walamula kuti musampembedze aliyense koma Iye basi. Chimenecho ndicho chipembedzo choongoka, koma anthu ambiri sadziwa (monga inu mulili popembedza mafano).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰصَٰحِبَيِ ٱلسِّجۡنِ أَمَّآ أَحَدُكُمَا فَيَسۡقِي رَبَّهُۥ خَمۡرٗاۖ وَأَمَّا ٱلۡأٓخَرُ فَيُصۡلَبُ فَتَأۡكُلُ ٱلطَّيۡرُ مِن رَّأۡسِهِۦۚ قُضِيَ ٱلۡأَمۡرُ ٱلَّذِي فِيهِ تَسۡتَفۡتِيَانِ
“E inu anzanga awiri a m’ndende! Tsono mmodzi wa inu (abwerera ku ntchito yake) azikamwetsa mowa bwana wake (monga zidalili poyamba); koma winayo aphedwa mopachikidwa, ndipo mbalame zidzadya mmutu wake. Chiweruzo chaweruzidwa kale (kwa Farawo) pa chinthu chomwe mudali kufunsa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ لِلَّذِي ظَنَّ أَنَّهُۥ نَاجٖ مِّنۡهُمَا ٱذۡكُرۡنِي عِندَ رَبِّكَ فَأَنسَىٰهُ ٱلشَّيۡطَٰنُ ذِكۡرَ رَبِّهِۦ فَلَبِثَ فِي ٱلسِّجۡنِ بِضۡعَ سِنِينَ
Ndipo (Yûsuf) adauza yemwe adamdziwa kuti apulumuka mwa awiriwo: “Ukandikumbuke ponditchula pamaso pa bwana wako (Farawo; ukamuuze kuti ndamangidwa popanda tchimo).” Koma satana adamuiwalitsa kumkumbutsa bwana wake. Tero (mneneri Yûsuf) adakhala m’ndende zaka zingapo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ ٱلۡمَلِكُ إِنِّيٓ أَرَىٰ سَبۡعَ بَقَرَٰتٖ سِمَانٖ يَأۡكُلُهُنَّ سَبۡعٌ عِجَافٞ وَسَبۡعَ سُنۢبُلَٰتٍ خُضۡرٖ وَأُخَرَ يَابِسَٰتٖۖ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمَلَأُ أَفۡتُونِي فِي رُءۡيَٰيَ إِن كُنتُمۡ لِلرُّءۡيَا تَعۡبُرُونَ
Ndipo (tsiku lina) mfumu (Farawo adalota) nati (kwa nduna zake): “Ndithudi, ine ndalota ng’ombe zisanu ndi ziwiri zonenepa zikudyedwa ndi ng’ombe zisanu ndi ziwiri zowonda ndiponso ndalota ngala zisanu ndi ziwiri zaziwisi ndi zina (zisanu ndi ziwiri) zouma. E inu akuluakulu! Ndimasulireni maloto angawa, ngati inu mumatha kumasulira maloto.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُوٓاْ أَضۡغَٰثُ أَحۡلَٰمٖۖ وَمَا نَحۡنُ بِتَأۡوِيلِ ٱلۡأَحۡلَٰمِ بِعَٰلِمِينَ
(Iwo) adati: “Amenewa ndi maloto osakanikirana (simaloto omveka)! Ndipo ife sitili odziwa kumasulira maloto amtundu umenewu.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ ٱلَّذِي نَجَا مِنۡهُمَا وَٱدَّكَرَ بَعۡدَ أُمَّةٍ أَنَا۠ أُنَبِّئُكُم بِتَأۡوِيلِهِۦ فَأَرۡسِلُونِ
Pamenepo amene adapulumuka mwa awiri aja adanena atakumbukira (pempho la Yûsuf) patapita nyengo (yaitali), adati: “Ine ndikuuzani tanthauzo lake. Choncho nditumeni (kuti ndikakufunireni tanthauzo lake).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
يُوسُفُ أَيُّهَا ٱلصِّدِّيقُ أَفۡتِنَا فِي سَبۡعِ بَقَرَٰتٖ سِمَانٖ يَأۡكُلُهُنَّ سَبۡعٌ عِجَافٞ وَسَبۡعِ سُنۢبُلَٰتٍ خُضۡرٖ وَأُخَرَ يَابِسَٰتٖ لَّعَلِّيٓ أَرۡجِعُ إِلَى ٱلنَّاسِ لَعَلَّهُمۡ يَعۡلَمُونَ
(Adanka kundende ndikumpempha Yûsuf chikhululuko chifukwa cha kuiwala kwake. Ndipo adati): “Yûsuf! E iwe woona! Tiuze za ng’ombe zisanu ndi ziwiri zonenepa zikudyedwa ndi zisanu ndi ziwiri zoonda, ndi ngala zisanu ndi ziwiri zaziwisi ndi zina zouma; kuti ine ndibwelere kwa anthu kuti akadziwe.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ تَزۡرَعُونَ سَبۡعَ سِنِينَ دَأَبٗا فَمَا حَصَدتُّمۡ فَذَرُوهُ فِي سُنۢبُلِهِۦٓ إِلَّا قَلِيلٗا مِّمَّا تَأۡكُلُونَ
(Yûsuf) adati: “Mudzalima zaka zisanu ndi ziwiri mondondozana ndi mwakhama ndipo zimene mwakolola zisiyeni m’ngala zake, kupatula zochepa zimene muzidzadya (kuti zam’ngalazo mudzadye mzaka zanjala).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ يَأۡتِي مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ سَبۡعٞ شِدَادٞ يَأۡكُلۡنَ مَا قَدَّمۡتُمۡ لَهُنَّ إِلَّا قَلِيلٗا مِّمَّا تُحۡصِنُونَ
“Kenako pambuyo pake zidzadza zaka zisanu ndi ziwiri za masautso zomwe zidzadya zimene mudasunga m’mbuyo, kupatula zochepa zimene muzidzazisunga (mobisa kuti zidzakhale mbewu.)”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ يَأۡتِي مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ عَامٞ فِيهِ يُغَاثُ ٱلنَّاسُ وَفِيهِ يَعۡصِرُونَ
“Kenako pambuyo pa izi chidzadza chaka chomwe anthu m’menemo adzapulumutsidwa (ndi Allah), ndipo m’menemo adzafinya (zakumwa).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ ٱلۡمَلِكُ ٱئۡتُونِي بِهِۦۖ فَلَمَّا جَآءَهُ ٱلرَّسُولُ قَالَ ٱرۡجِعۡ إِلَىٰ رَبِّكَ فَسۡـَٔلۡهُ مَا بَالُ ٱلنِّسۡوَةِ ٱلَّٰتِي قَطَّعۡنَ أَيۡدِيَهُنَّۚ إِنَّ رَبِّي بِكَيۡدِهِنَّ عَلِيمٞ
Ndipo mfumu idati: “M’bweretseni iye kwa ine.” Koma pamene mthenga (wa Mfumu) adamfika (Yûsuf, iye) adati: “Bwerera kwa bwana wako ndipo ukamfunse nkhani ya akazi omwe ankadzicheka manja awo. Ndithu Mbuye wanga akudziwa bwino ndale zawo. (Koma ndikufuna Mfumu kuti idziwe za kuyera kwanga kuti andiyeretsere maganizo ndipo asandiope).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ مَا خَطۡبُكُنَّ إِذۡ رَٰوَدتُّنَّ يُوسُفَ عَن نَّفۡسِهِۦۚ قُلۡنَ حَٰشَ لِلَّهِ مَا عَلِمۡنَا عَلَيۡهِ مِن سُوٓءٖۚ قَالَتِ ٱمۡرَأَتُ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡـَٰٔنَ حَصۡحَصَ ٱلۡحَقُّ أَنَا۠ رَٰوَدتُّهُۥ عَن نَّفۡسِهِۦ وَإِنَّهُۥ لَمِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Mfumu idasonkhanitsa akazi aja ndipo) idati: “Kodi nkhani yanu njotani pamene mudamulakalaka Yûsuf pomwe iye sakufuna?” Adati: “Hasha Lillah! (Tikudzitchinjiriza kwa Allah)! Ife sitidadziwe choipa chilichonse kwa iye. (Tidayesayesa kuti achite nafe choipa koma sadalole).” (Nayenso) mkazi wa nduna adati: “Tsopano choonadi chatsimikizika; ine ndine amene ndidamulakalaka pomwe iye sakufuna. Ndithu iye ndi mmodzi mwa owona.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ذَٰلِكَ لِيَعۡلَمَ أَنِّي لَمۡ أَخُنۡهُ بِٱلۡغَيۡبِ وَأَنَّ ٱللَّهَ لَا يَهۡدِي كَيۡدَ ٱلۡخَآئِنِينَ
(Yûsuf adati): “Zimenezo (zofuna kuti afunsidwe chonchi) n’chifukwa chakuti (nduna) idziwe kuti ine sindidaichitire zoipa iyo kulibe, ndi kuti Allah saongolera ndale za anthu achinyengo (kuti zipambane).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَمَآ أُبَرِّئُ نَفۡسِيٓۚ إِنَّ ٱلنَّفۡسَ لَأَمَّارَةُۢ بِٱلسُّوٓءِ إِلَّا مَا رَحِمَ رَبِّيٓۚ إِنَّ رَبِّي غَفُورٞ رَّحِيمٞ
۞ “Ndipo ine sindikuyeretsa mtima wanga. Ndithu mtima uliwonse umalamulira kwambiri ku zoipa kupatula umene Mbuye wanga wauchitira chifundo. Ndithudi, Mbuye wanga Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ ٱلۡمَلِكُ ٱئۡتُونِي بِهِۦٓ أَسۡتَخۡلِصۡهُ لِنَفۡسِيۖ فَلَمَّا كَلَّمَهُۥ قَالَ إِنَّكَ ٱلۡيَوۡمَ لَدَيۡنَا مَكِينٌ أَمِينٞ
Choncho Mfumu idati: “Mubwere naye kwa ine kuti ine mwini ndimsankhe.” Ndipo pamene adayankhula naye, (Mfumu) idati: “Ndithu iwe lero kwa ife wakhala wolemekezeka, wokhulupirika.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ ٱجۡعَلۡنِي عَلَىٰ خَزَآئِنِ ٱلۡأَرۡضِۖ إِنِّي حَفِيظٌ عَلِيمٞ
(Yûsuf) adati: “Ndiikeni kukhala muyang’aniri wa nkhokwe za dzinthu zam’dziko lonse. Ndithudi, ine ndine msungi wodziwa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَكَذَٰلِكَ مَكَّنَّا لِيُوسُفَ فِي ٱلۡأَرۡضِ يَتَبَوَّأُ مِنۡهَا حَيۡثُ يَشَآءُۚ نُصِيبُ بِرَحۡمَتِنَا مَن نَّشَآءُۖ وَلَا نُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndipo motero tidampatsa ulemelero Yûsuf m’dziko (la Iguputo); amakhala m’menemo paliponse pamene wafuna. Timam’bweretsera chifundo Chathu amene tamfuna, ndipo sitisokoneza malipiro a ochita zabwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَأَجۡرُ ٱلۡأٓخِرَةِ خَيۡرٞ لِّلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَكَانُواْ يَتَّقُونَ
Ndithudi malipiro a tsiku la chimaliziro ngabwino zedi kwa amene akhulupirira ndipo adali kumuopa (Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءَ إِخۡوَةُ يُوسُفَ فَدَخَلُواْ عَلَيۡهِ فَعَرَفَهُمۡ وَهُمۡ لَهُۥ مُنكِرُونَ
Ndipo adadza abale (ake) a Yûsuf (kukafuna chakudya kumeneko pamene ku Kenani kudagwa chilala chadzaoneni) ndikulowa kwa iye, ndipo (iye) adawazindikira pomwe iwo sankamzindikira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا جَهَّزَهُم بِجَهَازِهِمۡ قَالَ ٱئۡتُونِي بِأَخٖ لَّكُم مِّنۡ أَبِيكُمۡۚ أَلَا تَرَوۡنَ أَنِّيٓ أُوفِي ٱلۡكَيۡلَ وَأَنَا۠ خَيۡرُ ٱلۡمُنزِلِينَ
Ndipo pamene adawakonzera chakudya chawo, adati: “(Ngatimudzabwereranso kachiwiri) mudzabwere ndi m‘bale wanu wa kumbali ya bambo anu, kodi simuona kuti ine ndikukwaniritsa muyeso, ndipo ndine wabwino kwambiri polandira (alendo)?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِن لَّمۡ تَأۡتُونِي بِهِۦ فَلَا كَيۡلَ لَكُمۡ عِندِي وَلَا تَقۡرَبُونِ
“Koma ngati simudzandibweretsera iye, simudzakhala ndi mulingo (wachakudya) kwa ine, ndipo musadzandiyandikire.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ سَنُرَٰوِدُ عَنۡهُ أَبَاهُ وَإِنَّا لَفَٰعِلُونَ
(Iwo) adati: “Tikayesetsa kuwanyengelera bambo wake za iye (kufikira akatipatse). Ndithu ife tikachita zimenezi.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ لِفِتۡيَٰنِهِ ٱجۡعَلُواْ بِضَٰعَتَهُمۡ فِي رِحَالِهِمۡ لَعَلَّهُمۡ يَعۡرِفُونَهَآ إِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمۡ لَعَلَّهُمۡ يَرۡجِعُونَ
Ndipo (Yûsuf) adati kwa anyamata ake a ntchito: “Ikani chuma chawo m’mitolo yawo kuti akachizindikire akabwerera ku mawanja awo. (Tachita izi kuti) mwina angabwelerenso (kuno).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا رَجَعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيهِمۡ قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا مُنِعَ مِنَّا ٱلۡكَيۡلُ فَأَرۡسِلۡ مَعَنَآ أَخَانَا نَكۡتَلۡ وَإِنَّا لَهُۥ لَحَٰفِظُونَ
Ndipo pamene adabwerera kwa bambo wawo, adati: “E bambo wathu! Tikamanidwa muyeso wa chakudya (pa ulendo wachiwiri pokhapokha titsagane ndi m’bale wathuyu). Choncho mtumizeni m’bale wathu pamodzi ndi ife kuti akatipimire (mlingo wokwana); ndithu ife tikamsunga.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ هَلۡ ءَامَنُكُمۡ عَلَيۡهِ إِلَّا كَمَآ أَمِنتُكُمۡ عَلَىٰٓ أَخِيهِ مِن قَبۡلُ فَٱللَّهُ خَيۡرٌ حَٰفِظٗاۖ وَهُوَ أَرۡحَمُ ٱلرَّٰحِمِينَ
(Ya’qub) adati: “Kodi ndingakukhulupirireni pa iye kuposa momwe ndidakukhulupirirani pa m’bale wake kale (yemwe mudamsokeretsa)? Koma Allah ndi Yemwe ali Wabwino posunga, Ndipo Iye Ngwachifundo zedi kuposa achifundo onse.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا فَتَحُواْ مَتَٰعَهُمۡ وَجَدُواْ بِضَٰعَتَهُمۡ رُدَّتۡ إِلَيۡهِمۡۖ قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا مَا نَبۡغِيۖ هَٰذِهِۦ بِضَٰعَتُنَا رُدَّتۡ إِلَيۡنَاۖ وَنَمِيرُ أَهۡلَنَا وَنَحۡفَظُ أَخَانَا وَنَزۡدَادُ كَيۡلَ بَعِيرٖۖ ذَٰلِكَ كَيۡلٞ يَسِيرٞ
Ndipo pamene adatsekula katundu wawo, adapeza chuma chawo chabwezedwa kwa iwo. Adati: “E bambo wathu! Tingafunenso chiyani (kwa munthu waufuluyu)? Ichi chuma chathu chabwezedwa kwa ife; ndipo tikabweretsa chakudya chothandizira mawanja athu; ndipo m’bale wathu tikamsunga; tikapezanso muyeso wangamira imodzi yoonjezera. Umenewu ndi mlingo wochepa (kwa mfumu ya ufuluyo).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ لَنۡ أُرۡسِلَهُۥ مَعَكُمۡ حَتَّىٰ تُؤۡتُونِ مَوۡثِقٗا مِّنَ ٱللَّهِ لَتَأۡتُنَّنِي بِهِۦٓ إِلَّآ أَن يُحَاطَ بِكُمۡۖ فَلَمَّآ ءَاتَوۡهُ مَوۡثِقَهُمۡ قَالَ ٱللَّهُ عَلَىٰ مَا نَقُولُ وَكِيلٞ
(Ya’qub) adati: “Sindingamtumize pamodzi ndi inu pokhapokha mundipatse lonjezo m’dzina la Allah kuti ndithudi mudzambweza kwa ine pokhapokha nonsenu mutazingidwa (ndi zoopsa).” Ndipo pamene adapereka lonjezo lawo, (iye) adati: “Allah ndiye Muyang’aniri (mboni) pa zimene tikunenazi.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَ يَٰبَنِيَّ لَا تَدۡخُلُواْ مِنۢ بَابٖ وَٰحِدٖ وَٱدۡخُلُواْ مِنۡ أَبۡوَٰبٖ مُّتَفَرِّقَةٖۖ وَمَآ أُغۡنِي عَنكُم مِّنَ ٱللَّهِ مِن شَيۡءٍۖ إِنِ ٱلۡحُكۡمُ إِلَّا لِلَّهِۖ عَلَيۡهِ تَوَكَّلۡتُۖ وَعَلَيۡهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُتَوَكِّلُونَ
Adatinso: “E inu ana anga! Musakalowe (mu Iguputo) pachipata chimodzi koma kaloweni pa zipata zosiyanasiyana. Ndipo sindingakuthandizeni chilichonse kwa Allah. Lamulo ndi la Allah basi; kwa Iye ndiko ndatsamira; ndipo otsamira atsamire kwa Iye.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا دَخَلُواْ مِنۡ حَيۡثُ أَمَرَهُمۡ أَبُوهُم مَّا كَانَ يُغۡنِي عَنۡهُم مِّنَ ٱللَّهِ مِن شَيۡءٍ إِلَّا حَاجَةٗ فِي نَفۡسِ يَعۡقُوبَ قَضَىٰهَاۚ وَإِنَّهُۥ لَذُو عِلۡمٖ لِّمَا عَلَّمۡنَٰهُ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo pamene adalowa monga momwe bambo wawo adawalamulira, sikudawathandize chilichonse kwa Allah kupatula khumbo lomwe lidali mu mtima mwa Ya’qub (ndilomwe) adalikwaniritsa, (Ya’qub adali kufuna Yûsuf ndi m’bale wake akumane mwamseri; ndipo adakumanadi). Ndithu iye (Ya’qub) adali wanzeru chifukwa chakuti tidamphunzitsa. Koma anthu ambiri sadziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا دَخَلُواْ عَلَىٰ يُوسُفَ ءَاوَىٰٓ إِلَيۡهِ أَخَاهُۖ قَالَ إِنِّيٓ أَنَا۠ أَخُوكَ فَلَا تَبۡتَئِسۡ بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo pamene adalowa kwa Yûsuf (ndikumuona m’bale wake atalowa payekha), adamkumbatira m’bale wakeyo nati: “Ndithu ine ndine m’bale wako; choncho usadandaule pa zimene (abale athu) akhala akuchita.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا جَهَّزَهُم بِجَهَازِهِمۡ جَعَلَ ٱلسِّقَايَةَ فِي رَحۡلِ أَخِيهِ ثُمَّ أَذَّنَ مُؤَذِّنٌ أَيَّتُهَا ٱلۡعِيرُ إِنَّكُمۡ لَسَٰرِقُونَ
Ndipo pamene adawakonzera chakudya chawo, adaika chikho chomwera madzi mumtolo wa m’bale wakeyo. Kenako woitana adaitana: “E inu a paulendo! Ndithu inu ndinu akuba.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ وَأَقۡبَلُواْ عَلَيۡهِم مَّاذَا تَفۡقِدُونَ
(Onse abale ake a Yûsuf) pamene adawacheukira, adati: “Kodi mukusowa chiyani?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ نَفۡقِدُ صُوَاعَ ٱلۡمَلِكِ وَلِمَن جَآءَ بِهِۦ حِمۡلُ بَعِيرٖ وَأَنَا۠ بِهِۦ زَعِيمٞ
Adati: “Tikusowa muyeso wa Mfumu; ndipo amene aubweretse, alandira mtolo wangamira yathunthu.” (Ndipo Mneneri Yûsuf adati): “Ndipo ine ndine muimiliri pa zimenezi.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ تَٱللَّهِ لَقَدۡ عَلِمۡتُم مَّا جِئۡنَا لِنُفۡسِدَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَمَا كُنَّا سَٰرِقِينَ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Ndithu inu mukudziwa kuti sitidadze kudzaononga m’dziko, ndiponso sitili akuba.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ فَمَا جَزَٰٓؤُهُۥٓ إِن كُنتُمۡ كَٰذِبِينَ
Adati: “Mphoto (chilango) yake ikhala yotani ngati mukunena bodza?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ جَزَٰٓؤُهُۥ مَن وُجِدَ فِي رَحۡلِهِۦ فَهُوَ جَزَٰٓؤُهُۥۚ كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلظَّٰلِمِينَ
Adati: “Mphoto yake ndi yemwe (chikhocho) chapezeka mu mtolo wake, iye ndiye mphoto yake. (Agwidwe monga kapolo kwa chaka chimodzi).” Umu ndi momwe timawalipirira anthu achinyengo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَبَدَأَ بِأَوۡعِيَتِهِمۡ قَبۡلَ وِعَآءِ أَخِيهِ ثُمَّ ٱسۡتَخۡرَجَهَا مِن وِعَآءِ أَخِيهِۚ كَذَٰلِكَ كِدۡنَا لِيُوسُفَۖ مَا كَانَ لِيَأۡخُذَ أَخَاهُ فِي دِينِ ٱلۡمَلِكِ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ نَرۡفَعُ دَرَجَٰتٖ مَّن نَّشَآءُۗ وَفَوۡقَ كُلِّ ذِي عِلۡمٍ عَلِيمٞ
Ndipo (mneneri Yûsuf) adayamba kufufuza m’mitolo mwawo asanafufuze mu mtolo wa m’bale wake; kenako adachitulutsa mu mtolo wa m’bale wake. Umu ndi momwe tidamlinganizira ndale Yûsuf (kuti ampeze m’bale wake). Mwachilamulo cha mfumu (ya m’dzikolo) sakadamutenga m’bale wake (monga kapolo) koma mmene Allah adafunira (powaonetsa abale ake za chilamulo cha kwawo chomuika mu ukapolo munthu wakuba). Timawakwezera pa ulemelero amene tawafuna. Ndipo pa wodziwa aliyense pali wodziwanso kuposa iye.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ قَالُوٓاْ إِن يَسۡرِقۡ فَقَدۡ سَرَقَ أَخٞ لَّهُۥ مِن قَبۡلُۚ فَأَسَرَّهَا يُوسُفُ فِي نَفۡسِهِۦ وَلَمۡ يُبۡدِهَا لَهُمۡۚ قَالَ أَنتُمۡ شَرّٞ مَّكَانٗاۖ وَٱللَّهُ أَعۡلَمُ بِمَا تَصِفُونَ
(Iwo) adati: “Ngati waba, m’bale wakenso adabapo kale.” (Uku kudali kumunamizira Yûsuf bodza pomwe iwo sankadziwa kuti yemwe akuyankhula nayeyo ndiye Yûsuf). Koma Yûsuf adabisa (mawu awa) mu mtima mwake, (chifukwa chowamvera chisoni) ndipo sadawaululire. Adati: “Inu muli ndi chikhalidwe choipa ndipo Allah akudziwa zomwe mukunena!”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡعَزِيزُ إِنَّ لَهُۥٓ أَبٗا شَيۡخٗا كَبِيرٗا فَخُذۡ أَحَدَنَا مَكَانَهُۥٓۖ إِنَّا نَرَىٰكَ مِنَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
(Iwo) adati: “E inu bwana! Uyu ali ndi bambo wake wokalamba kwambiri; choncho tengani mmodzi wa ife mmalo mwake; ndithudi, ife tikuona kuti inu ndinu mmodzi mwa ochita zabwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ مَعَاذَ ٱللَّهِ أَن نَّأۡخُذَ إِلَّا مَن وَجَدۡنَا مَتَٰعَنَا عِندَهُۥٓ إِنَّآ إِذٗا لَّظَٰلِمُونَ
(Yûsuf) adati: “Ha! tikudzitchinjiriza mwa Allah, sitingagwire wina koma yemwe chuma chathu tachipeza ndi iye, kuopa kuti tingakhale ochita zoipa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا ٱسۡتَيۡـَٔسُواْ مِنۡهُ خَلَصُواْ نَجِيّٗاۖ قَالَ كَبِيرُهُمۡ أَلَمۡ تَعۡلَمُوٓاْ أَنَّ أَبَاكُمۡ قَدۡ أَخَذَ عَلَيۡكُم مَّوۡثِقٗا مِّنَ ٱللَّهِ وَمِن قَبۡلُ مَا فَرَّطتُمۡ فِي يُوسُفَۖ فَلَنۡ أَبۡرَحَ ٱلۡأَرۡضَ حَتَّىٰ يَأۡذَنَ لِيٓ أَبِيٓ أَوۡ يَحۡكُمَ ٱللَّهُ لِيۖ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Choncho, pamene adataya mtima za iye, adapita pambali kukanong’onezana. Wamkulu wawo adati: “Kodi simudziwa kuti bambo wanu adatenga lonjezo kuchokera kwa inu m’dzina la Allah (kuti mudzam’bweza iyeyo?) ndiponso kale mudalakwa (pa mapangano anu) pa za Yûsuf. Choncho sindichoka dziko lino kufikira atandilola bambo (kutero) kapena Allah andilamule (zondichotsa kuno pomasulidwa m’bale wangayu); Iye Ngwabwino polamula kuposa olamula.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱرۡجِعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيكُمۡ فَقُولُواْ يَٰٓأَبَانَآ إِنَّ ٱبۡنَكَ سَرَقَ وَمَا شَهِدۡنَآ إِلَّا بِمَا عَلِمۡنَا وَمَا كُنَّا لِلۡغَيۡبِ حَٰفِظِينَ
“Bwererani kwa bambo wanu ndipo mukawauze (kuti): “E bambo wathu! Ndithu mwana wanu waba. Ndipo ife sitidaikire umboni (wakuti wakuba achitidwe ukapolo) koma pa zomwe tidazidziwa (kuti mwa ife mulibe wakuba), ndipo sitidali kudziwa zamseri.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَسۡـَٔلِ ٱلۡقَرۡيَةَ ٱلَّتِي كُنَّا فِيهَا وَٱلۡعِيرَ ٱلَّتِيٓ أَقۡبَلۡنَا فِيهَاۖ وَإِنَّا لَصَٰدِقُونَ
“Ndipo afunseni anthu a m’mudzi momwe tidalimo ndi a pa ulendo omwe tadza nawo, ndipo ndithudi ife tikunena zoona.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ بَلۡ سَوَّلَتۡ لَكُمۡ أَنفُسُكُمۡ أَمۡرٗاۖ فَصَبۡرٞ جَمِيلٌۖ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَأۡتِيَنِي بِهِمۡ جَمِيعًاۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
(Ya’qub) adati: “Koma mitima yanu yakukometserani chinthu. (Kwanga ndi) kupirira kwabwino kokha basi. Mwina Allah adzandibweretsera onse pamodzi. Ndithudi, Iye Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰٓأَسَفَىٰ عَلَىٰ يُوسُفَ وَٱبۡيَضَّتۡ عَيۡنَاهُ مِنَ ٱلۡحُزۡنِ فَهُوَ كَظِيمٞ
Ndipo adawachokera ndikunena (kuti): “Ha! kudandaula kwanga za Yûsuf!” Ndipo maso ake adayera chifukwa cha kudandaula ndipo iye adadzazidwa ndi chisoni.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ تَٱللَّهِ تَفۡتَؤُاْ تَذۡكُرُ يُوسُفَ حَتَّىٰ تَكُونَ حَرَضًا أَوۡ تَكُونَ مِنَ ٱلۡهَٰلِكِينَ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Simusiya kumkumbukira Yûsuf (ndikulira) mpaka mufika podwala, kapena mukhala mwa owonongeka (ndi imfa).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ إِنَّمَآ أَشۡكُواْ بَثِّي وَحُزۡنِيٓ إِلَى ٱللَّهِ وَأَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
(Iye) adati: “Ndithu ine ndikusuma dandaulo langa ndi kukhumata kwanga kwa Allah, ndipo ndikudziwa kupyolera mwa Allah zomwe simukudziwa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰبَنِيَّ ٱذۡهَبُواْ فَتَحَسَّسُواْ مِن يُوسُفَ وَأَخِيهِ وَلَا تَاْيۡـَٔسُواْ مِن رَّوۡحِ ٱللَّهِۖ إِنَّهُۥ لَا يَاْيۡـَٔسُ مِن رَّوۡحِ ٱللَّهِ إِلَّا ٱلۡقَوۡمُ ٱلۡكَٰفِرُونَ
“E ana anga! Pitani mukafufuzefufuze za Yûsuf ndi m’bale wake, ndipo musataye mtima pa chifundo cha Allah. Ndithu palibe amene amataya mtima za chifundo cha Allah koma anthu osakhulupirira.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا دَخَلُواْ عَلَيۡهِ قَالُواْ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡعَزِيزُ مَسَّنَا وَأَهۡلَنَا ٱلضُّرُّ وَجِئۡنَا بِبِضَٰعَةٖ مُّزۡجَىٰةٖ فَأَوۡفِ لَنَا ٱلۡكَيۡلَ وَتَصَدَّقۡ عَلَيۡنَآۖ إِنَّ ٱللَّهَ يَجۡزِي ٱلۡمُتَصَدِّقِينَ
(Ndipo adapita ku Iguputo). Choncho pamene adalowa kwa iye (Yûsuf), adati: “E inu olemekezeka! Masautso atikhudza, ife ndi maanja athu; choncho tabwera ndi chuma chopanda pake. Tidzadzireni mlingo (ngakhale chuma chathucho chili chopanda pake), ndipo tithandizeni mwaulere. Ndithu Allah amawalipira othandiza mwaulere.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ هَلۡ عَلِمۡتُم مَّا فَعَلۡتُم بِيُوسُفَ وَأَخِيهِ إِذۡ أَنتُمۡ جَٰهِلُونَ
(Iye) adati: “Kodi mukudziwa zomwe mudamchitira Yûsuf ndi m’bale wake pamene inu mudali mu umbuli?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُوٓاْ أَءِنَّكَ لَأَنتَ يُوسُفُۖ قَالَ أَنَا۠ يُوسُفُ وَهَٰذَآ أَخِيۖ قَدۡ مَنَّ ٱللَّهُ عَلَيۡنَآۖ إِنَّهُۥ مَن يَتَّقِ وَيَصۡبِرۡ فَإِنَّ ٱللَّهَ لَا يُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
(Iwo) adati: “Kodi iwe ndiwe Yûsuf?” Adati: “Ine ndine Yûsuf, ndipo uyu ndi m’bale wanga; Allah watichitira zabwino. Ndithu amene aopa Allah ndikumapirira, (Allah amulipira). Ndithu Allah sasokoneza malipiro a ochita zabwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ تَٱللَّهِ لَقَدۡ ءَاثَرَكَ ٱللَّهُ عَلَيۡنَا وَإِن كُنَّا لَخَٰطِـِٔينَ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Allah wakusankha pa ife, ndipo ife tidalidi olakwa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ لَا تَثۡرِيبَ عَلَيۡكُمُ ٱلۡيَوۡمَۖ يَغۡفِرُ ٱللَّهُ لَكُمۡۖ وَهُوَ أَرۡحَمُ ٱلرَّٰحِمِينَ
(Iye) adati: “Lero palibe kukudzudzulani; Allah akukhulukirani, ndipo Iye Ngwachifundo chochuluka kuposa achifundo.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱذۡهَبُواْ بِقَمِيصِي هَٰذَا فَأَلۡقُوهُ عَلَىٰ وَجۡهِ أَبِي يَأۡتِ بَصِيرٗا وَأۡتُونِي بِأَهۡلِكُمۡ أَجۡمَعِينَ
“Pitani ndi mkanjo wangawu ndipo mukauponye pamaso pa bambo wanga ndipo iwo akapenya. Kenako nonsenu ndi maanja anu onse mudze kwa ine.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَمَّا فَصَلَتِ ٱلۡعِيرُ قَالَ أَبُوهُمۡ إِنِّي لَأَجِدُ رِيحَ يُوسُفَۖ لَوۡلَآ أَن تُفَنِّدُونِ
Ndipo aulendo pamene adamuka (kubwerera kwawo). Bambo wawo (yemwe adali ku Kenani) adati: “Ndikumva fungo la Yûsuf pakadapanda kuti muli ndi chikhulupiliro choti ndasokonezeka nzeru, (mukadandikhulupirira)”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ تَٱللَّهِ إِنَّكَ لَفِي ضَلَٰلِكَ ٱلۡقَدِيمِ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Ndithu muli mkusokera kwanu kwa kale (pokonda Yûsuf kuposa ife).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّآ أَن جَآءَ ٱلۡبَشِيرُ أَلۡقَىٰهُ عَلَىٰ وَجۡهِهِۦ فَٱرۡتَدَّ بَصِيرٗاۖ قَالَ أَلَمۡ أَقُل لَّكُمۡ إِنِّيٓ أَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Choncho pamene adadza wotenga nkhani yabwino, adauponya (mkanjo wa Yûsuf) pankhope pake, ndipo pompo adapenya. Adati: “Kodi sindinakuuzeni kuti ine ndikudziwa kupyolera mwa Allah zomwe inu simukuzidziwa?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالُواْ يَٰٓأَبَانَا ٱسۡتَغۡفِرۡ لَنَا ذُنُوبَنَآ إِنَّا كُنَّا خَٰطِـِٔينَ
(Iwo) adati: “E bambo wathu! Tipemphereni chikhululuko pa machimo athu. Ndithu ife tidali olakwa.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَالَ سَوۡفَ أَسۡتَغۡفِرُ لَكُمۡ رَبِّيٓۖ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡغَفُورُ ٱلرَّحِيمُ
(Iye) adati: “Posachedwapa (ndikamuona Yûsuf) ndikupempherani chikhululuko kwa Mbuye wanga. Ndithu Iye Ngokhululuka zedi, Ngwachisoni chosatha.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّا دَخَلُواْ عَلَىٰ يُوسُفَ ءَاوَىٰٓ إِلَيۡهِ أَبَوَيۡهِ وَقَالَ ٱدۡخُلُواْ مِصۡرَ إِن شَآءَ ٱللَّهُ ءَامِنِينَ
Ndipo pamene adalowa kwa Yûsuf, adawakumbatira makolo ake ndikunena: “Lowani mu Iguputo, In-shaa-Allah, (Allah akalola) mwamtendere.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَرَفَعَ أَبَوَيۡهِ عَلَى ٱلۡعَرۡشِ وَخَرُّواْ لَهُۥ سُجَّدٗاۖ وَقَالَ يَٰٓأَبَتِ هَٰذَا تَأۡوِيلُ رُءۡيَٰيَ مِن قَبۡلُ قَدۡ جَعَلَهَا رَبِّي حَقّٗاۖ وَقَدۡ أَحۡسَنَ بِيٓ إِذۡ أَخۡرَجَنِي مِنَ ٱلسِّجۡنِ وَجَآءَ بِكُم مِّنَ ٱلۡبَدۡوِ مِنۢ بَعۡدِ أَن نَّزَغَ ٱلشَّيۡطَٰنُ بَيۡنِي وَبَيۡنَ إِخۡوَتِيٓۚ إِنَّ رَبِّي لَطِيفٞ لِّمَا يَشَآءُۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
Ndipo (pamene adafika kwa Yûsuf), (iye) adawakweza makolo ake ndikuwaika pa chimpando (chake) chachifumu, ndipo onse adagwa kumlambira (monga mwachizolowezi chawo nthawi imeneyo). Ndipo (Yûsuf) adati: “E inu bambo wanga! Ili ndilo tanthauzo (lenileni) la maloto anga akale. Palibe chipeneko Mbuye wanga wawatsimikiza (malotowo). Ndipo adandichitira zabwino ponditulutsa kundende ndi pokubweretsani inu kuchokera kumidzi (Kenani), pambuyo pokhwirizira (chidani) satana pakati pa ine ndi abale anga. Ndithudi Mbuye wanga amadziwa kwambiri chinsinsi cha zomwe wakonza kuti zichitike. Ndithu Iye Ngodziwa, Ngwanzeru.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ رَبِّ قَدۡ ءَاتَيۡتَنِي مِنَ ٱلۡمُلۡكِ وَعَلَّمۡتَنِي مِن تَأۡوِيلِ ٱلۡأَحَادِيثِۚ فَاطِرَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ أَنتَ وَلِيِّۦ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۖ تَوَفَّنِي مُسۡلِمٗا وَأَلۡحِقۡنِي بِٱلصَّٰلِحِينَ
(Kenako adathokoza ndi kupempha Allah kuti): “E Mbuye wanga! Ndithu mwandipatsako ufumu ndi kundiphunzitsako kumasulira nkhani (maloto). E Inu Mlengi wa thambo ndi nthaka! Inu ndiye Mtetezi wanga pa dziko lapansi ndi tsiku la chimaliziro. (Ndipo nthawi ya imfa yanga) mudzandipatse imfa ndili Msilamu ndipo kandikumanitseni ndi ochita zabwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
ذَٰلِكَ مِنۡ أَنۢبَآءِ ٱلۡغَيۡبِ نُوحِيهِ إِلَيۡكَۖ وَمَا كُنتَ لَدَيۡهِمۡ إِذۡ أَجۡمَعُوٓاْ أَمۡرَهُمۡ وَهُمۡ يَمۡكُرُونَ
Izi ndi zina mwa nkhani zamseri (zomwe) tikukuululira iwe. Ndipo siudali nawo pamodzi pamene adatsimika chochita chawo (uku) akuchita chiwembu (chawo) choipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَآ أَكۡثَرُ ٱلنَّاسِ وَلَوۡ حَرَصۡتَ بِمُؤۡمِنِينَ
Ndipo ambiri mwa anthu sakhulupirira ngakhale utalimbika chotani.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا تَسۡـَٔلُهُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۚ إِنۡ هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo sukuwapempha malipiro pa zimenezi. Sichina izi (zimene wadza nazo), koma ndi ulaliki kwa zolengedwa zonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَكَأَيِّن مِّنۡ ءَايَةٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ يَمُرُّونَ عَلَيۡهَا وَهُمۡ عَنۡهَا مُعۡرِضُونَ
Ndipo ndi zisonyezo zingati (zosonyeza kuti Allah alipo) kumwamba ndi pansi zomwe akuzidutsa pamene iwo sakuzilabadira.[233]
[233] Apa tanthauzo lake nkuti zilipo zisonyezo zambiri zosonyeza kuti Allah alipo zomwe iwo akuziona ali pamudzi ndiponso akuzidutsa akakhala pa maulendo awo monga thambo, nthaka, dzuwa, mwezi, nyenyezi, mapiri ndi zina zambiri zododometsa zimene zikupezeka kumwamba ndi pansi. Akuziona m’mawa ndi madzulo koma iwo saziganizira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا يُؤۡمِنُ أَكۡثَرُهُم بِٱللَّهِ إِلَّا وَهُم مُّشۡرِكُونَ
Ndipo ambiri a iwo sakhulupirira Allah koma momphatikiza. [234]
[234] Apa akutanthauza kuti ambiri a iwo amamphatikiza Allah ndi milungu yabodza. Iwo amavomereza kuti Allah ndiye Mlengi wopatsa zonse. Koma kuonjezera pachikhulupiliro choterechi, amapembedzanso mafano. Ndipo zoterezi masiku ano zikumachitika ndi Asilamu ena amene amafuulira mizimu ya anthu akufa kuti iwathangate pa mavuto amene awagwera, komwe nkumuphatikiza Allah ndi mizimu ya anthu akufa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَفَأَمِنُوٓاْ أَن تَأۡتِيَهُمۡ غَٰشِيَةٞ مِّنۡ عَذَابِ ٱللَّهِ أَوۡ تَأۡتِيَهُمُ ٱلسَّاعَةُ بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Kodi akudziika pachitetezo kuti silingawadzere tsoka lachilango cha Allah, kapena kuti siingawadzere Qiyâma mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira?
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُلۡ هَٰذِهِۦ سَبِيلِيٓ أَدۡعُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِۚ عَلَىٰ بَصِيرَةٍ أَنَا۠ وَمَنِ ٱتَّبَعَنِيۖ وَسُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ وَمَآ أَنَا۠ مِنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Nena: “Iyi ndi njira yanga. Ndikuitanira kwa Allah mwa nzeru zokwanira, ine ndi omwe akunditsata. Ndithu Allah wapatukana (ndi mbiri zopunguka). Ndipo ine sindili mwa ophatikiza (Allah ndi zinthu zina).”[235]
[235] Apa Mtumiki (s.a.w) akuuzidwa kuti awauze anthu kuti iye pamodzi ndi amene akumutsata kuti amalalikira Chisilamu kwa anthu popereka kwa anthuwo mitsutso yanzeru, ndikuperekanso zisonyezo ndi maumboni amphamvu. Sibwino Msilamu kutsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino. Qur’an ikunenetsa kuti osatsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino pokhapokha chinthucho chitanenedwa ndi Allah kapena Mtumiki Wake.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا مِن قَبۡلِكَ إِلَّا رِجَالٗا نُّوحِيٓ إِلَيۡهِم مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡقُرَىٰٓۗ أَفَلَمۡ يَسِيرُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَيَنظُرُواْ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡۗ وَلَدَارُ ٱلۡأٓخِرَةِ خَيۡرٞ لِّلَّذِينَ ٱتَّقَوۡاْۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Ndipo sitidatume (mtumiki aliyense) patsogolo pako koma adali amuna amene tidawavumbulutsira (chivumbulutso); ochokera mwa anthu a m’mizinda. Kodi sadayende (iwo osakhulupirira) pa dziko nkuona momwe mathero a oipa omwe adalipo patsogolo pawo (momwe adalili)? Ndipo nyumba ya tsiku la chimaliziro njabwino kwa owopa Allah. Kodi mulibe nzeru?
Ang mga Tafsir na Arabe:
حَتَّىٰٓ إِذَا ٱسۡتَيۡـَٔسَ ٱلرُّسُلُ وَظَنُّوٓاْ أَنَّهُمۡ قَدۡ كُذِبُواْ جَآءَهُمۡ نَصۡرُنَا فَنُجِّيَ مَن نَّشَآءُۖ وَلَا يُرَدُّ بَأۡسُنَا عَنِ ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Mpaka pamene atumiki adataya mtima (za anthu awo) nkuganiza kuti ayesedwa onama, chithandizo chathu chidawadzera, ndipo amene tidawafuna adapulumuka. Koma chilango chathu sichibwezedwa kwa anthu oipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَقَدۡ كَانَ فِي قَصَصِهِمۡ عِبۡرَةٞ لِّأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِۗ مَا كَانَ حَدِيثٗا يُفۡتَرَىٰ وَلَٰكِن تَصۡدِيقَ ٱلَّذِي بَيۡنَ يَدَيۡهِ وَتَفۡصِيلَ كُلِّ شَيۡءٖ وَهُدٗى وَرَحۡمَةٗ لِّقَوۡمٖ يُؤۡمِنُونَ
Ndithu m’nkhani zawo izi muli phunziro kwa eni nzeru. (Qur’aniyi) simawu opekedwa, koma (iyi Qur’an) ndi chitsimikizo cha zomwe zidalipo patsogolo pake (m’mabuku ena a Allah), ndi kumasulira kwa tsatanetsatane pa chilichonse ndiponso chiongoko ndi mtendere kwa anthu okhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Yūsuf
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara