Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: ‘Abasa   Ayah:

‘Abasa

عَبَسَ وَتَوَلَّىٰٓ
Adachita tsinya (Mneneri) ndi kuyang’ana kumbali.[384]
[384] Tsiku lina Mneneri (s.a.w) atakhala ndi akuluakulu a Aquraishi. Adali kuwalalikira za chipembedzo mwachidwi, ndipo adali kuyembekezera kuti akavomereza Chisilamu iwo, ndiye kuti anthu owatsatira naonso avomereza. Chifukwa anthu ambiri sadalowe Chisilamu poopa atsogoleri awo. Pa nthawi imeneyi adatulukira wakhungu wina yemwe ankatchedwa Ibn Ummu Maktum. Sadadziwe kuti Mneneri (s.a.w) ali wotanganidwa. Adamukuwira: “E Iwe Mneneri wa Allah! Ndiphunzitse inenso zimene wakuphunzitsa Allah.” Ndipo ankangomubwerezera-bwerezera mawu amenewa. Mneneri (s.a.w) pakuti adali ndi chidwi ndi kulalikira akuluakulu aja, adamchitira tsinya wakhungu uja chifukwa chomuonongera ntchito yake; sadamumvere. Basi pamenepa Allah akumdzudzula Mneneri Wake pa zomwe adachita posiya kumumvera amene adamubwerera kudzafuna chiongoko.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَن جَآءَهُ ٱلۡأَعۡمَىٰ
Chifukwa chakuti adamdzera wakhungu (kudzamfunsa zokhudzana ndi chipembedzo chake pamene iye adali kuyankhula ndi atsogoleri Achiquraishi).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّهُۥ يَزَّكَّىٰٓ
Nanga chingakudziwitse nchiyani kuti mwina iye angadziyeretse (pomvera ulaliki wako watsopano)?
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَوۡ يَذَّكَّرُ فَتَنفَعَهُ ٱلذِّكۡرَىٰٓ
Kapena akumbukira, ndipo kukumbukirako kumthandiza?
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَمَّا مَنِ ٱسۡتَغۡنَىٰ
Koma amene wadzikwaniritsa (ndi chuma chake ndi mphamvu zake),
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَنتَ لَهُۥ تَصَدَّىٰ
Ameneyo ndi yemwe ukumchitira chidwi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا عَلَيۡكَ أَلَّا يَزَّكَّىٰ
Palibe chilichonse pa iwe ngati sadziyeretsa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَمَّا مَن جَآءَكَ يَسۡعَىٰ
Koma amene wakudzera uku akuthamanga (kufuna maphunziro ndi chiongoko),
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَهُوَ يَخۡشَىٰ
Ndipo iye akuopa (Allah mu mtima mwake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَنتَ عَنۡهُ تَلَهَّىٰ
Za iye, iwe sukusamala, (ukuyikira chidwi kwa wina).
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّآ إِنَّهَا تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithudi iyi (Qur’an) ndi chikumbutso (chenjezo).[385]
[385] (Ndime 11-16) Apa Allah akumuletsa Mtumiki Wake kuti asachitenso zonga adachitazo ndi kumuuza kuti Qur’an ndi ulaliki chabe, amene afuna kulingalira za ulalikiwo, umuthandiza, ndipo amene safuna, kutaika ndi kwake. Ndiponso adamufotokozera kuti Qur’an idachokera m’mabuku olemekezeka; idachokera ku “Lauhil-Mahfudh” mabuku omwe ali m’manja mwa Angelo olemba, olemekezeka, ochita zabwino omwe ndi abwino kuposa Aquraishi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Basi, amene wafuna alangizika (ndi Qur’an, ndipo amene sakufuna msiye).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فِي صُحُفٖ مُّكَرَّمَةٖ
(Malangizowa akuchokera) mmakalata olemekezeka (kwa Allah);
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَّرۡفُوعَةٖ مُّطَهَّرَةِۭ
Apamwamba ndiponso oyeretsedwa (kumbiri iliyonse yopunguka);
Ang mga Tafsir na Arabe:
بِأَيۡدِي سَفَرَةٖ
Omwe ali m’manja mwa Alembi (Angelo).
Ang mga Tafsir na Arabe:
كِرَامِۭ بَرَرَةٖ
Olemekezeka, omvera.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُتِلَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَآ أَكۡفَرَهُۥ
Waonongeka (watembeleredwa) munthu. Nkotani kusayamika kwake kotereku.
Ang mga Tafsir na Arabe:
مِنۡ أَيِّ شَيۡءٍ خَلَقَهُۥ
Kuchokera mchinthu chanji chimene iye adamulenga.
Ang mga Tafsir na Arabe:
مِن نُّطۡفَةٍ خَلَقَهُۥ فَقَدَّرَهُۥ
Kuchokera ku dontho lamadzi (onyozeka) adamulenga, namkonzeratu mkalengedwe kosiyanasiyana.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ ٱلسَّبِيلَ يَسَّرَهُۥ
Kenako adamfewetsera njira (yotulukira m’mimba mwa mai ake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ أَمَاتَهُۥ فَأَقۡبَرَهُۥ
Ndipo amamchititsa kuti amwalire namukumbula m’manda,
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ إِذَا شَآءَ أَنشَرَهُۥ
Kenako akadzafuna adzamuukitsa (pambuyo pa imfa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّا لَمَّا يَقۡضِ مَآ أَمَرَهُۥ
Ayi ndithu (munthu) sanakwaniritsebe zimene adamulamula Mbuye wake (Allah chingakhale wakhala nthawi yaitali pa dziko lapansi).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلۡيَنظُرِ ٱلۡإِنسَٰنُ إِلَىٰ طَعَامِهِۦٓ
Alingalire munthu (mmene chilili) chakudya chake;[386]
[386] Ngati munthu sakumbuka chilengedwe chake, ayang’ane chakudya chimene akudya momwe chimapezekera. Azindikira mphamvu za Allah.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَنَّا صَبَبۡنَا ٱلۡمَآءَ صَبّٗا
Ndithu Ife timagwetsa mvula yambiri (kuchokera ku mitambo).
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ شَقَقۡنَا ٱلۡأَرۡضَ شَقّٗا
Kenako timaing’amba nthaka kuti mmera utuluke;
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَنۢبَتۡنَا فِيهَا حَبّٗا
Ndipo timameretsa m’menemo njere (ya chakudya cha anthu ndi zina zimene amasunga mnkhokwe),
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَعِنَبٗا وَقَضۡبٗا
Ndi mphesa ndi msipu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَزَيۡتُونٗا وَنَخۡلٗا
Ndi mzitona (wabwino) ndi (zipatso za) kanjedza,
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَحَدَآئِقَ غُلۡبٗا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo,
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَفَٰكِهَةٗ وَأَبّٗا
Ndi zipatso (zodyedwa ndi anthu) ndi msipu (wodyedwa ndi nyama);
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَّتَٰعٗا لَّكُمۡ وَلِأَنۡعَٰمِكُمۡ
(Tazimeretsa zimenezo kuti) zikondweretse inu ndi ziweto zanu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِذَا جَآءَتِ ٱلصَّآخَّةُ
Choncho likadzafika lipenga logonthetsa mkhutu (ndi kuumitsa makosi).
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَوۡمَ يَفِرُّ ٱلۡمَرۡءُ مِنۡ أَخِيهِ
Patsikuli munthu adzathawa m’bale wake,
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأُمِّهِۦ وَأَبِيهِ
Mayi wake ndi bambo wake,
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَبَنِيهِ
Mkazi wake ndi ana ake.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لِكُلِّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ يَوۡمَئِذٖ شَأۡنٞ يُغۡنِيهِ
Munthu aliyense mwa iwo, tsiku limenelo adzakhala ndi zakezake zotangwanika nazo. (Sadzalabadira za anzake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ مُّسۡفِرَةٞ
Tsiku limenelo nkhope zina zidzakhala zowala;[387]
[387] (Ndime 38-39) Tsiku limenelo anthu adzakhala kakhalidwe ka mitundu iwiri: amene adakhulupilira ndi kuchita ntchito zabwino nkhope zawo zidzawala ndi chimwemwe, ndipo amene adakanira ndikumachita zoipa, nkhope zawo zidzakhala zafumbi ndi zakuda monga momwe anenera ma Ayah 40 ndi 42.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ضَاحِكَةٞ مُّسۡتَبۡشِرَةٞ
Zosekelera ndi zachimwemwe (chifukwa cha nkhani yabwino ya ku Munda wamtendere.)
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَوُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ عَلَيۡهَا غَبَرَةٞ
Ndipo nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zokutidwa ndi fumbi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
تَرۡهَقُهَا قَتَرَةٌ
Mdima udzazikuta.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡكَفَرَةُ ٱلۡفَجَرَةُ
Iwo ndi anthu osakhulupirira oipa (olakwira Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: ‘Abasa
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara