Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Fajr   Ayah:

Al-Fajr

وَٱلۡفَجۡرِ
Ndikulumbilira kuyera kwa m’bandakucha; (pamene usiku uthawa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَيَالٍ عَشۡرٖ
Ndi masiku khumi (a mwezi wa Dhul-Hijjah omwe ngopatulika kwa Allah).[430]
[430] Tanthauzo la Ayah iyi ndi masiku khumi olemekezeka omwe ali mkhumi loyamba la mwezi wa Thul-Hijjah umene ndi mwezi wa 12 pa kalendala ya Chisilamu. Amenewa ndi masiku olemekezeka kuposa masiku onse ngakhale masiku a Ramadan kupatula usiku wa LAILA-TUL-QADR, ndi masiku khumi omaliza a mwezi wa Ramadan. Choncho ndi bwino kuchulukitsa mapemphero m’masiku amenewa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلشَّفۡعِ وَٱلۡوَتۡرِ
Ndi Shaf’i ndi Witri: (nambala yogawika ndi yosagawika).[431]
[431] Shafi ndi nambala yotheka kugawa ndi 2 (even number) Witri ndi nambala yosatheka kuigawa ndi 2 (odd number). Cholinga cha Allah pamenepa ndi kuzilumbilira zinthu zonse zimene adazilenga, zowerengedwa mnjira zonse ziwiri.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَسۡرِ
Ndi usiku pamene ukupita (chifukwa cha kuyenda kwa dziko kodabwitsa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
هَلۡ فِي ذَٰلِكَ قَسَمٞ لِّذِي حِجۡرٍ
Kodi m’zimene zatchulidwazi simuli kulumbira kokwanira, kwa munthu wa nzeru?
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ تَرَ كَيۡفَ فَعَلَ رَبُّكَ بِعَادٍ
Kodi sudadziwe momwe Mbuye wako adawalangira Âdi (anthu a mneneri Hûd).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِرَمَ ذَاتِ ٱلۡعِمَادِ
Aku Irama; ataliatali ngati zipilala.[432]
[432] (Ndime 7-9) Âdi aku Irama ndi mtundu wa Mneneri Hud. Adali akuluakulu matupi a mphamvu kwambiri mwakuti ankanena kuti: “Ndani wamphamvu kuposa ife!” Thamudu (Samudu) ndi mtundu wa Mneneri Swaleh. Iwowa adali kukhala ku mpoto kwa chilumba cha Arabia.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلَّتِي لَمۡ يُخۡلَقۡ مِثۡلُهَا فِي ٱلۡبِلَٰدِ
Omwe onga iwo sadalengedwe m’maiko ena?
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَثَمُودَ ٱلَّذِينَ جَابُواْ ٱلصَّخۡرَ بِٱلۡوَادِ
Ndi Asamudu, (anthu a mneneri Swaleh) amene adali kudula matanthwe ku chigwa (chotchedwa Wadi Qura ndi kumamanga nyumba zikuluzikulu)?
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَفِرۡعَوۡنَ ذِي ٱلۡأَوۡتَادِ
Komanso Firiauna (Farawo) mwini magulu ankhondo (omwe amalimbikitsa ufumu wake monga momwe zichiri zimalimbikitsira tenti)?
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلَّذِينَ طَغَوۡاْ فِي ٱلۡبِلَٰدِ
Amene adaipitsa m’maiko mopyola malire?
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَكۡثَرُواْ فِيهَا ٱلۡفَسَادَ
Ndipo adachulukitsa m’menemo kuononga (pamwamba pa kuononga).[433]
[433] Mzinthu zoipa zimene Farawo adachita, ndi kudzitcha kuti iye ndi mulungu, kupha ana achimuna popanda chilungamo, ndi kuwazunza Aisraeli.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَصَبَّ عَلَيۡهِمۡ رَبُّكَ سَوۡطَ عَذَابٍ
Choncho Mbuye wako adawathira ndi mitundu ya zilango (zoopsa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ رَبَّكَ لَبِٱلۡمِرۡصَادِ
Ndithu Mbuye wako ali tcheru (ndi zochita za anthu. Ndipo akuwasungira kuti adzawalipire).[434]
[434] Apa ndikuti Allah akuwaona anthu Ake nthawi ili yonse. Palibe chimene iwo achita popanda Iye kuchiona ndi kuchilemba.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَمَّا ٱلۡإِنسَٰنُ إِذَا مَا ٱبۡتَلَىٰهُ رَبُّهُۥ فَأَكۡرَمَهُۥ وَنَعَّمَهُۥ فَيَقُولُ رَبِّيٓ أَكۡرَمَنِ
Pamene munthu Mbuye wake akumuyesa (mayeso) ndikumulemekeza ndi kumpatsa mtendere (wachuma, ulemelero ndi mphamvu) amanena monyada: Mbuye wanga wandilemekeza (chifukwa zimenezi nzondiyenera ine).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَمَّآ إِذَا مَا ٱبۡتَلَىٰهُ فَقَدَرَ عَلَيۡهِ رِزۡقَهُۥ فَيَقُولُ رَبِّيٓ أَهَٰنَنِ
Koma akamuyesa mayeso ndi kumchepetsera rizq lake, (chuma) amanena (motaya rntima): Mbuye wanga wandinyoza!
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّاۖ بَل لَّا تُكۡرِمُونَ ٱلۡيَتِيمَ
Sichoncho ayi, (monga momwe mukuganizira) koma inu simuchitira za ufulu ana amasiye!
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا تَحَٰٓضُّونَ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo simulimbikitsana za kudyetsa osauka,
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَتَأۡكُلُونَ ٱلتُّرَاثَ أَكۡلٗا لَّمّٗا
Ndipo mukudya chuma cha masiye; kudya kosusuka.[435]
[435] Arabu asadalowe m’Chisilamu akazi sadali kugawiridwa chuma cha masiye kudzanso ana aang’onoang’ono a masiye sadali kuchiona chumacho.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَتُحِبُّونَ ٱلۡمَالَ حُبّٗا جَمّٗا
Ndiponso mukukonda chuma; kukonda kopyola muyeso.
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَلَّآۖ إِذَا دُكَّتِ ٱلۡأَرۡضُ دَكّٗا دَكّٗا
Sichoncho! (Siyani machitidwe amenewa); nthaka ikadzapondedwa (ndikuifafaniza).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءَ رَبُّكَ وَٱلۡمَلَكُ صَفّٗا صَفّٗا
Ndikubwera Mbuye wako (mmabweredwe omwe akuwadziwa Iye Mwini) ndi angelo ali mmizeremizere.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجِاْيٓءَ يَوۡمَئِذِۭ بِجَهَنَّمَۚ يَوۡمَئِذٖ يَتَذَكَّرُ ٱلۡإِنسَٰنُ وَأَنَّىٰ لَهُ ٱلذِّكۡرَىٰ
Ndi kubweretsedwa Jahannam pa tsikulo, basi tsiku limenelo munthu adzakumbukira, koma kukumbuka kumeneko kudzamthandiza chiyani?
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَقُولُ يَٰلَيۡتَنِي قَدَّمۡتُ لِحَيَاتِي
Adzanena: Kalanga ine! Ndikadatsogoza zabwino pa za moyo wanga uno!
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَيَوۡمَئِذٖ لَّا يُعَذِّبُ عَذَابَهُۥٓ أَحَدٞ
Motero patsikuli, palibe wina amene adzalange monga momwe (Allah) adzalangire.[436]
[436] (Ndime 25-26) Tanthauzo lake ndikuti palibe chofanizira chilango cha Allah chomwe chidzaperekedwe kwa akafiri ndiponso ndi kunjata komwe akafiri adzanjatidwe.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا يُوثِقُ وَثَاقَهُۥٓ أَحَدٞ
Ndiponso sanganjate aliyense monga kunjata kwa iye (Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيَّتُهَا ٱلنَّفۡسُ ٱلۡمُطۡمَئِنَّةُ
E iwe mzimu wokhazikika (ndi choona)![437]
[437] “Mzimu wokhazikika” ndi mzimu wa munthu wokhulupilira amene akuchita zomwe walamulidwa ndi kusiya zimene waletsedwa. Umenewo ndiwo mzimu umene udzakhale wodekha pa tsiku lachimaliziro chifukwa chakuti pa tsikulo sudzakhala ndi mantha kapena kudandaula.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱرۡجِعِيٓ إِلَىٰ رَبِّكِ رَاضِيَةٗ مَّرۡضِيَّةٗ
Bwerera kwa Mbuye wako uli wokondwera (ndi zomwe wapatsidwa), ndipo uli woyanjidwa (ndi Allah pa zomwe udatsogoza).[438]
[438] Tanthauzo lake nkuti mzimu wokhazikika udzakondwera ndi zimene udzalandira kwa Allah tsiku limenelo ndipo naye Allah adzakondwera nawo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَٱدۡخُلِي فِي عِبَٰدِي
Lowa mgulu la akapolo anga abwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱدۡخُلِي جَنَّتِي
Ndipo lowa m’munda Wanga (mnyumba ya mtendere wa muyaya).
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Fajr
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara