Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah   Ayah:

At-Tawbah

بَرَآءَةٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦٓ إِلَى ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّم مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Uku ndikudzipatula kochokera kwa Allah ndi Mtumiki wake ku (mapangano) amene mudapangana nawo (kenako nkuswa mapangano awowo) a m’gulu la Amushirikina.[204]
[204] (Ndime 1-2) Omasulila Qur’an adati Arabu adali kuswa mapangano amene adamanga pamodzi ndi Mtumiki wa Allah. Potero, Allah adalamula Mtumiki Wake kuti awaponyere mapangano awo. Choncho, Mtumiki adatuma Abubakari (r.a) kukhala mtsogoleri wa anthu kumapemphero a Hajj. Ndipo adamtsatanso Ali (r.a) kumeneko ndi nkhani yokhayokhayo kuti akawawerengere anthu kuti Allah ndi Mtumiki Wake atulukamo m’mapangano okhalirana mwa mtendere ndi Amushirikina sadzaloledwa kuyandikira Nyumba Yopatulika chaka chotsatiracho, ndikutinso sadzaloledwa kuzungulira Nyumba yopatulikayo uku ali maliseche.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَسِيحُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ أَرۡبَعَةَ أَشۡهُرٖ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ غَيۡرُ مُعۡجِزِي ٱللَّهِ وَأَنَّ ٱللَّهَ مُخۡزِي ٱلۡكَٰفِرِينَ
(Auze Amushirikina kuti): Yendani pa dziko miyezi inayi basi. (Pambuyo pake sipadzakhala chitetezo pakati pawo ndi ife). Ndipo dziwani kuti inu simungathe kumpambana Allah. Ndipo Allah Ngosambula osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَذَٰنٞ مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦٓ إِلَى ٱلنَّاسِ يَوۡمَ ٱلۡحَجِّ ٱلۡأَكۡبَرِ أَنَّ ٱللَّهَ بَرِيٓءٞ مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ وَرَسُولُهُۥۚ فَإِن تُبۡتُمۡ فَهُوَ خَيۡرٞ لَّكُمۡۖ وَإِن تَوَلَّيۡتُمۡ فَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّكُمۡ غَيۡرُ مُعۡجِزِي ٱللَّهِۗ وَبَشِّرِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِعَذَابٍ أَلِيمٍ
Ndipo uku ndi kulengeza kochokera kwa Allah ndi Mtumiki Wake kwa Anthu pa tsiku la Hajj yaikulu kuti ndithu Allah ndi Mtumiki Wake adzichotsa mmapangano a Amushirikina (omwe ali achinyengo). Choncho, ngati mulapa ndibwino kwa inu; ndipo ngati mutembenuka ndi kunyoza, dziwani kuti inu simungamulepheretse Allah. Ndipo auze za chilango chowawa amene sadakhulupirire.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِلَّا ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّم مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ ثُمَّ لَمۡ يَنقُصُوكُمۡ شَيۡـٔٗا وَلَمۡ يُظَٰهِرُواْ عَلَيۡكُمۡ أَحَدٗا فَأَتِمُّوٓاْ إِلَيۡهِمۡ عَهۡدَهُمۡ إِلَىٰ مُدَّتِهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُتَّقِينَ
Kupatula ena amene mudapangana nawo mapangano mwa Amushirikina, (omwe adasunga mapangano awo), kenako sadapungule chilichonse ndipo sadathandize aliyense pa inu, akwaniritseni mapangano awo mpaka m’nyengo yawo. Ndithu Allah akukonda amene akumuopa (ndi kusunga mapangano).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِذَا ٱنسَلَخَ ٱلۡأَشۡهُرُ ٱلۡحُرُمُ فَٱقۡتُلُواْ ٱلۡمُشۡرِكِينَ حَيۡثُ وَجَدتُّمُوهُمۡ وَخُذُوهُمۡ وَٱحۡصُرُوهُمۡ وَٱقۡعُدُواْ لَهُمۡ كُلَّ مَرۡصَدٖۚ فَإِن تَابُواْ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَوُاْ ٱلزَّكَوٰةَ فَخَلُّواْ سَبِيلَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo miyezi yopatulika ikatha (yomwe njoletsedwa kuchitamo nkhondo), apheni Amushirikina paliponse pamene mwawapeza (menyanani nawo), ndipo agwireni (monga momwe iwo akukuchitirani). Ndipo azungulireni ndi kuwakhalira pa njira zonse. Koma akalapa nayamba kupemphera Swala, ndikupereka chopereka (Zakaat), ilekeni njira yawoyo (asiyeni). Ndithu Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِنۡ أَحَدٞ مِّنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ ٱسۡتَجَارَكَ فَأَجِرۡهُ حَتَّىٰ يَسۡمَعَ كَلَٰمَ ٱللَّهِ ثُمَّ أَبۡلِغۡهُ مَأۡمَنَهُۥۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَعۡلَمُونَ
Ndipo ngati mmodzi wa Amushirikina Atakupempha chitetezo (kuti amvere mawu a Allah), mtetezeni kuti amve mawu a Allah. Kenako (ngati sadakhutitsidwe nawo), mpititseni kumalo kwake mwamtendere (ngati safuna kulowa m’Chisilamu). Izi nchifukwa chakuti iwo ndi anthu osadziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَيۡفَ يَكُونُ لِلۡمُشۡرِكِينَ عَهۡدٌ عِندَ ٱللَّهِ وَعِندَ رَسُولِهِۦٓ إِلَّا ٱلَّذِينَ عَٰهَدتُّمۡ عِندَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِۖ فَمَا ٱسۡتَقَٰمُواْ لَكُمۡ فَٱسۡتَقِيمُواْ لَهُمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ يُحِبُّ ٱلۡمُتَّقِينَ
Chingakhalepo bwanji chipangano pakati pa Amushirikina (oswa mapangano nthawi ndi nthawi) ndi Allah ndi Mthenga Wake, kupatula okhawo amene mudapangana nawo mapangano pa Msikiti Wopatulika? (Amene adakwaniritsa mapangano awo). Ngati iwo akupitiriza kulungama (posunga mapanganowo) kwa inu, nanunso pitirizani kulungama kwa iwo. Ndithu Allah akukonda amene akumuopa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَيۡفَ وَإِن يَظۡهَرُواْ عَلَيۡكُمۡ لَا يَرۡقُبُواْ فِيكُمۡ إِلّٗا وَلَا ذِمَّةٗۚ يُرۡضُونَكُم بِأَفۡوَٰهِهِمۡ وَتَأۡبَىٰ قُلُوبُهُمۡ وَأَكۡثَرُهُمۡ فَٰسِقُونَ
(Kodi inu ndiye osunga malonjezo?) Bwanji? Pomwe iwo akakhala ndi mphamvu pa inu sakusungirani chibale kapena pangano? Amakusangalatsani ndi pakamwa pawo pomwe mitima yawo ikukana (kukukondani). Ndipo ambiri a iwo ngoukira malamulo (a Allah).[205]
[205] Allah akuti kodi mungapangane nawo mapangano anthu oti akapeza mwawi wokugonjetsani inu sasunga chibale chomwe chidali pakati panu ngakhale pangano? Iwo amakunenerani mawu otsekemera ngati uchi pomwe mitima yawo ndi yodzadzidwa ndi mkwiyo ndi inu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱشۡتَرَوۡاْ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ ثَمَنٗا قَلِيلٗا فَصَدُّواْ عَن سَبِيلِهِۦٓۚ إِنَّهُمۡ سَآءَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Asinthanitsa Ayah za Allah (ndi zinthu za dziko lapansi) ndi mtengo wochepa, ndipo atsekereza (anthu) kunjira Yake. Ndithu nzoipa kwabasi zomwe iwo akhala akuchita.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا يَرۡقُبُونَ فِي مُؤۡمِنٍ إِلّٗا وَلَا ذِمَّةٗۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُعۡتَدُونَ
Sasunga chibale pa okhulupirira ngakhale pangano. Awo ndiwo opyola malire.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِن تَابُواْ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَوُاْ ٱلزَّكَوٰةَ فَإِخۡوَٰنُكُمۡ فِي ٱلدِّينِۗ وَنُفَصِّلُ ٱلۡأٓيَٰتِ لِقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
Koma ngati alapa nayamba kupemphera Swala ndikupereka chopereka (Zakaat), ndiye kuti ndi abale anu pa chipembedzo. Ndipo tikuzifotokoza Ayah zi (mwabwino) kwa anthu odziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِن نَّكَثُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُم مِّنۢ بَعۡدِ عَهۡدِهِمۡ وَطَعَنُواْ فِي دِينِكُمۡ فَقَٰتِلُوٓاْ أَئِمَّةَ ٱلۡكُفۡرِ إِنَّهُمۡ لَآ أَيۡمَٰنَ لَهُمۡ لَعَلَّهُمۡ يَنتَهُونَ
Ndipo ngati aswa malumbiro awo pambuyo pomanga chipangano chawo, ndi kuyamba kutukwana chipembedzo chanu, menyanani nawo atsogoleri a kusakhulupirira. Ndithu iwo alibe mapangano, (sasunga mapangano. Menyanani nawo) kuti iwo aleke (machitidwe awo oipa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَا تُقَٰتِلُونَ قَوۡمٗا نَّكَثُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُمۡ وَهَمُّواْ بِإِخۡرَاجِ ٱلرَّسُولِ وَهُم بَدَءُوكُمۡ أَوَّلَ مَرَّةٍۚ أَتَخۡشَوۡنَهُمۡۚ فَٱللَّهُ أَحَقُّ أَن تَخۡشَوۡهُ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
Kodi nchotani kuti musamenyane nawo anthu omwe aswa malonjezo awo, natsimikiza kumtulutsa (kumpirikitsa mu mzinda wa Makka, kapena kumupha) Mtumiki? Iwo ndi amene adayamba kukuputani pachiyambi, nanga mukuwaopa chotani? Allah ndiye wofunika kumuopa, ngati inu mulidi okhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَٰتِلُوهُمۡ يُعَذِّبۡهُمُ ٱللَّهُ بِأَيۡدِيكُمۡ وَيُخۡزِهِمۡ وَيَنصُرۡكُمۡ عَلَيۡهِمۡ وَيَشۡفِ صُدُورَ قَوۡمٖ مُّؤۡمِنِينَ
Menyanani nao; Allah awalanga kupyolera m’manja anu, ndipo awasambula ndi kukupulumutsani kwa iwo ndi kuchiritsa kuwawidwa (komwe kudali) m’mitima mwa anthu okhulupirira (chifukwa cha masautso omwe adawapeza kwa iwo).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَيُذۡهِبۡ غَيۡظَ قُلُوبِهِمۡۗ وَيَتُوبُ ٱللَّهُ عَلَىٰ مَن يَشَآءُۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٌ
Ndi kuchotsa mkwiyo wa m’mitima mwawo (Asilamu). Ndi kuti Allah Alandire kulapa kwa amene wamfuna. Ndipo Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَمۡ حَسِبۡتُمۡ أَن تُتۡرَكُواْ وَلَمَّا يَعۡلَمِ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ جَٰهَدُواْ مِنكُمۡ وَلَمۡ يَتَّخِذُواْ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَلَا رَسُولِهِۦ وَلَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَلِيجَةٗۚ وَٱللَّهُ خَبِيرُۢ بِمَا تَعۡمَلُونَ
Kodi mukuganiza kuti mungosiidwa chabe Allah asanawaonetsere poyera amene amenyera chipembedzo mwa inu ndi amene sachita ubwenzi (ndi wina wake) kupatula Allah ndi Mtumiki wake ndi okhulupirira? Ndipo Allah Ngodziwa zonse zimene muchita.
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَا كَانَ لِلۡمُشۡرِكِينَ أَن يَعۡمُرُواْ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ شَٰهِدِينَ عَلَىٰٓ أَنفُسِهِم بِٱلۡكُفۡرِۚ أُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ وَفِي ٱلنَّارِ هُمۡ خَٰلِدُونَ
Nkosayenera kwa Amushirikina kukhala (ndi udindo) woyang’anira Misikiti ya Allah pomwe iwo akudzichitira okha umboni kuti ngosakhulupirira. Awo (ndi omwe) zochita zawo zabwino zapita pachabe. Ndipo iwo ku Moto adzakhala nthawi yaitali.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّمَا يَعۡمُرُ مَسَٰجِدَ ٱللَّهِ مَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَأَقَامَ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتَى ٱلزَّكَوٰةَ وَلَمۡ يَخۡشَ إِلَّا ٱللَّهَۖ فَعَسَىٰٓ أُوْلَٰٓئِكَ أَن يَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu oyang’anira Misikiti ya Allah ndi kuiyendera ndi amene akhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, ndi kumapemphera Swala ndi kupereka chopereka (Zakaat) ndipo saopa aliyense koma Allah yekha. Choncho, iwowo ndi amene akuyembekezeka kukhala mwa oongoka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ أَجَعَلۡتُمۡ سِقَايَةَ ٱلۡحَآجِّ وَعِمَارَةَ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ كَمَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَجَٰهَدَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۚ لَا يَسۡتَوُۥنَ عِندَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi kumwetsa madzi (anthu) ochita Hajj ndi kusunga Msikiti Wopatulika mukukuyesa kuti nkofanana ndi yemwe wakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, ndi kumenya nkhondo pa njira Ya Allah? Sangakhale ofanana kwa Allah. Ndipo Allah saongola anthu ochita zolakwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَهَاجَرُواْ وَجَٰهَدُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ أَعۡظَمُ دَرَجَةً عِندَ ٱللَّهِۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡفَآئِزُونَ
Amene akhulupirira, ndi kusamuka, ndi kumenya nkhondo pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi matupi awo, ali ndi ulemelero waukulu kwa Allah. Iwowo ndiwo opambana.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يُبَشِّرُهُمۡ رَبُّهُم بِرَحۡمَةٖ مِّنۡهُ وَرِضۡوَٰنٖ وَجَنَّٰتٖ لَّهُمۡ فِيهَا نَعِيمٞ مُّقِيمٌ
Mbuye wawo akuwauza nkhani yabwino ya chifundo chochokera kwa Iye, ndi chiyanjo (Chake) ndi Minda yomwe mkati mwake adzapezamo mtendere wamuyaya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدًاۚ إِنَّ ٱللَّهَ عِندَهُۥٓ أَجۡرٌ عَظِيمٞ
Adzakhala m’menemo muyaya. Ndithu Allah ali nawo malipiro aakulu zedi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَتَّخِذُوٓاْ ءَابَآءَكُمۡ وَإِخۡوَٰنَكُمۡ أَوۡلِيَآءَ إِنِ ٱسۡتَحَبُّواْ ٱلۡكُفۡرَ عَلَى ٱلۡإِيمَٰنِۚ وَمَن يَتَوَلَّهُم مِّنكُمۡ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلظَّٰلِمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Musawachite makolo anu ndi abale anu kukhala atetezi anu ngati (iwo) akukonda kusakhulupirira m’malo mokhulupirira. Ndipo mwa inu amene ati awasankhe kukhala atetezi, otero ndiwo adzichitira okha zoipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُلۡ إِن كَانَ ءَابَآؤُكُمۡ وَأَبۡنَآؤُكُمۡ وَإِخۡوَٰنُكُمۡ وَأَزۡوَٰجُكُمۡ وَعَشِيرَتُكُمۡ وَأَمۡوَٰلٌ ٱقۡتَرَفۡتُمُوهَا وَتِجَٰرَةٞ تَخۡشَوۡنَ كَسَادَهَا وَمَسَٰكِنُ تَرۡضَوۡنَهَآ أَحَبَّ إِلَيۡكُم مِّنَ ٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَجِهَادٖ فِي سَبِيلِهِۦ فَتَرَبَّصُواْ حَتَّىٰ يَأۡتِيَ ٱللَّهُ بِأَمۡرِهِۦۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Nena: “Ngati makolo anu, ana anu, abale anu, akazi anu, ndi anansi anu ndi chuma chimene mwachipata, ndi malonda anu amene mukuopa kuti angaonongeke, ndi nyumba zanu zimene mukuzikonda, (ngati zinthuzi zili) zokondeka kwamhiri kwa inu kuposa Allah ndi Mtumiki Wake ndi kuchita Jihâd pa njira Yake, choncho dikirani kufikira Allah adzabwera ndi lamulo Lake (lokukhaulitsani). Ndipo Allah satsogolera anthu otuluka m’chilamulo (Chake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَقَدۡ نَصَرَكُمُ ٱللَّهُ فِي مَوَاطِنَ كَثِيرَةٖ وَيَوۡمَ حُنَيۡنٍ إِذۡ أَعۡجَبَتۡكُمۡ كَثۡرَتُكُمۡ فَلَمۡ تُغۡنِ عَنكُمۡ شَيۡـٔٗا وَضَاقَتۡ عَلَيۡكُمُ ٱلۡأَرۡضُ بِمَا رَحُبَتۡ ثُمَّ وَلَّيۡتُم مُّدۡبِرِينَ
Ndithu Allah wakhala akukupulumutsani (kwa adani anu) m’malo ambiri omenyanira nkhondo, ndi pa tsiku la Hunaini, pamene kudakunyengani kuchuluka kwanu. Koma sikudakuthandizeni chilichonse. Ndipo dziko lidakupanani ngakhale kuti lidali lotambasuka ndipo kenako mudatembenukira kumbuyo (kuthawa).[206]
[206] Apa Allah akuwakumbutsa Asilamu kuti wakhala akuwapulumutsa m’nkhondo zosiyanasiyana, makamaka pa nkhondo ya Hunaini pamene Asilamu adali kudzitama kuti sangagonjetsedwe chifukwa cha kuchuluka kwawo. Koma kuchulukako sikudawathandize chilichonse. Nthawi zonse chofunika kwa Msilamu nkudalira Allah. Asadalire mphamvu zake, chuma kapena zina zotero.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ أَنزَلَ ٱللَّهُ سَكِينَتَهُۥ عَلَىٰ رَسُولِهِۦ وَعَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَأَنزَلَ جُنُودٗا لَّمۡ تَرَوۡهَا وَعَذَّبَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۚ وَذَٰلِكَ جَزَآءُ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Kenaka Allah adatsitsa mpumulo Wake kwa Mtumiki Wake ndi kwa okhulupirira. Ndipo adatsitsa asilikali ankhondo (angelo) omwe simudawaone. Ndipo adawakhaulitsa osakhulupirira. Imeneyo ndiyo mphoto ya osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ثُمَّ يَتُوبُ ٱللَّهُ مِنۢ بَعۡدِ ذَٰلِكَ عَلَىٰ مَن يَشَآءُۗ وَٱللَّهُ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo pambuyo pa izi, Allah alandira kulapa kwa amene wamfuna (mwa osakhulupirira powalowetsa m’Chisilamu). Ndipo Allah Ngokhululuka Ngwachisoni chosatha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِنَّمَا ٱلۡمُشۡرِكُونَ نَجَسٞ فَلَا يَقۡرَبُواْ ٱلۡمَسۡجِدَ ٱلۡحَرَامَ بَعۡدَ عَامِهِمۡ هَٰذَاۚ وَإِنۡ خِفۡتُمۡ عَيۡلَةٗ فَسَوۡفَ يُغۡنِيكُمُ ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦٓ إِن شَآءَۚ إِنَّ ٱللَّهَ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
E inu amene mwakhulupirira! Ndithu opembedza mafano ndi nyansi, choncho, asayandikire Msikiti Wopatulika chikatha chaka chaochi. Ngati mukuopa umphawi, posachedwa Allah Akulemeretsani ndi zabwino Zake akafuna. Ndithu Allah Ngodziwa zonse, Ngwanzeru zakuya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قَٰتِلُواْ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَلَا بِٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَلَا يُحَرِّمُونَ مَا حَرَّمَ ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥ وَلَا يَدِينُونَ دِينَ ٱلۡحَقِّ مِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ حَتَّىٰ يُعۡطُواْ ٱلۡجِزۡيَةَ عَن يَدٖ وَهُمۡ صَٰغِرُونَ
Menyanani ndi omwe sakhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, omwenso sakusiya zoletsedwa zomwe Allah ndi Mtumiki Wake waletsa; omwenso satsatira chipembedzo choona mwa amene adapatsidwa mabuku. (Menyanani nawo) kufikira apereke msonkho ndi manja awo uku ali odzichepetsa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقَالَتِ ٱلۡيَهُودُ عُزَيۡرٌ ٱبۡنُ ٱللَّهِ وَقَالَتِ ٱلنَّصَٰرَى ٱلۡمَسِيحُ ٱبۡنُ ٱللَّهِۖ ذَٰلِكَ قَوۡلُهُم بِأَفۡوَٰهِهِمۡۖ يُضَٰهِـُٔونَ قَوۡلَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِن قَبۡلُۚ قَٰتَلَهُمُ ٱللَّهُۖ أَنَّىٰ يُؤۡفَكُونَ
Ndipo Ayuda akunena kuti Uzairi ndimwana wa Mulungu, naonso Akhrisitu akunena kuti Mesiya (Isa {Yesu}) ndimwana wa Mulungu. Awa ndi mawu amene akunena ndi pakamwa pawo (popanda umboni wochokera kwa Allah); akutsanzira zonena za omwe sadakhulupirire kale. Allah awaononge; kodi iwo akusokera chotani (kusiya choonadi)?
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱتَّخَذُوٓاْ أَحۡبَارَهُمۡ وَرُهۡبَٰنَهُمۡ أَرۡبَابٗا مِّن دُونِ ٱللَّهِ وَٱلۡمَسِيحَ ٱبۡنَ مَرۡيَمَ وَمَآ أُمِرُوٓاْ إِلَّا لِيَعۡبُدُوٓاْ إِلَٰهٗا وَٰحِدٗاۖ لَّآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۚ سُبۡحَٰنَهُۥ عَمَّا يُشۡرِكُونَ
Awachita ophunzira a za chipembedzo chawo ndi ansembe awo kukhala milungu kusiya Allah (powatsata pa zimene akuwalamula popanda umboni wa Allah). (Amsandutsanso) Mesiya (Isa {Yesu}) mwana wa Mariya (kukhala mulungu); chikhalirecho sadalamulidwe china koma kupembedza Mulungu Mmodzi. Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye, wapatukana ndi zimene akumphatikiza nazozo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يُرِيدُونَ أَن يُطۡفِـُٔواْ نُورَ ٱللَّهِ بِأَفۡوَٰهِهِمۡ وَيَأۡبَى ٱللَّهُ إِلَّآ أَن يُتِمَّ نُورَهُۥ وَلَوۡ كَرِهَ ٱلۡكَٰفِرُونَ
Akufuna kuzimitsa kuunika kwa Allah (Chisilamu) ndi pakamwa pawo; ndipo Allah sadzalola koma kukwaniritsa kuunika kwake ngakhale kuti osakhulupirira zikuwanyansa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
هُوَ ٱلَّذِيٓ أَرۡسَلَ رَسُولَهُۥ بِٱلۡهُدَىٰ وَدِينِ ٱلۡحَقِّ لِيُظۡهِرَهُۥ عَلَى ٱلدِّينِ كُلِّهِۦ وَلَوۡ كَرِهَ ٱلۡمُشۡرِكُونَ
Iye ndi Yemwe adatuma Mtumiki Wake ndi ulangizi ndiponso chipembedzo choona kuti achiwonetsere pa zipembedzo zonse, ngakhale atanyansidwa nazo Amushirikina.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِنَّ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلۡأَحۡبَارِ وَٱلرُّهۡبَانِ لَيَأۡكُلُونَ أَمۡوَٰلَ ٱلنَّاسِ بِٱلۡبَٰطِلِ وَيَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۗ وَٱلَّذِينَ يَكۡنِزُونَ ٱلذَّهَبَ وَٱلۡفِضَّةَ وَلَا يُنفِقُونَهَا فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَبَشِّرۡهُم بِعَذَابٍ أَلِيمٖ
E inu amene mwakhulupirira! Ndithu ambiri ophunzira a za chipembedzo cha Chiyuda ndi cha Chikhristu, akudya chuma cha anthu mwachinyengo ndi kusekeleza anthu ku njira ya Allah. Ndipo amene akusonkhanitsa golide ndi siliva popanda kuzipereka pa njira ya Allah, auze nkhani ya chilango chowawa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَوۡمَ يُحۡمَىٰ عَلَيۡهَا فِي نَارِ جَهَنَّمَ فَتُكۡوَىٰ بِهَا جِبَاهُهُمۡ وَجُنُوبُهُمۡ وَظُهُورُهُمۡۖ هَٰذَا مَا كَنَزۡتُمۡ لِأَنفُسِكُمۡ فَذُوقُواْ مَا كُنتُمۡ تَكۡنِزُونَ
Pa tsiku lomwe (chuma chawo) chidzatenthedwa ku moto wa Jahannam, ndipo ndi chumacho zidzatenthedwa nkhope zawo, nthiti zawo ndi misana yawo (ali kuwuzidwa kuti): “Izi ndi zija zomwe mudadzisungira nokha. Choncho lawani (chilango) cha zomwe mudali kuzisunga.[207]
[207] Mu Ayah iyi, Allah akuchenjeza amene akusonkhanitsa chumacho nkumangochiunjika m’nkhokwe popanda kutulutsamo chopereka (Zakaat). Akawalanga nacho pa tsiku la chimaliziro ndi chilango cha moto. Tero, tulutsamoni Zakaat m’chuma chanu. Musanyozere lamulo la Allah.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ عِدَّةَ ٱلشُّهُورِ عِندَ ٱللَّهِ ٱثۡنَا عَشَرَ شَهۡرٗا فِي كِتَٰبِ ٱللَّهِ يَوۡمَ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ مِنۡهَآ أَرۡبَعَةٌ حُرُمٞۚ ذَٰلِكَ ٱلدِّينُ ٱلۡقَيِّمُۚ فَلَا تَظۡلِمُواْ فِيهِنَّ أَنفُسَكُمۡۚ وَقَٰتِلُواْ ٱلۡمُشۡرِكِينَ كَآفَّةٗ كَمَا يُقَٰتِلُونَكُمۡ كَآفَّةٗۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلۡمُتَّقِينَ
Ndithu chiwerengero cha miyezi kwa Allah (pa chaka), ndi miyezi khumi ndi iwiri m’chilamulo cha Allah kuyambira tsiku lomwe adalenga thambo ndi nthaka. M’menemo muli miyezi inayi yopatulika. Ichi ndicho chipembedzo cha Allah cholunjika, choncho musadzichitire nokha zoipa m’menemo. Ndipo menyanani ndi Amshrikina nonse pamodzi monga momwe akumenyana nanu onse pamodzi. Ndipo dziwani kuti Allah ali pamodzi ndi oopa.[208]
[208] Chiwerengero chamiyezi m’chaka, ndi khumi ndi iwiri monga mwalamulo la Allah. M’miyeziyi muli miyezi inayi yopatulika yomwe ndi Rajabu, Thul Qa’da, Thul Hijja ndi Muharamu. M’miyeziyi nkosaloledwa kuchita nkhondo pokhapokha mutaputidwa ndi adani.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّمَا ٱلنَّسِيٓءُ زِيَادَةٞ فِي ٱلۡكُفۡرِۖ يُضَلُّ بِهِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ يُحِلُّونَهُۥ عَامٗا وَيُحَرِّمُونَهُۥ عَامٗا لِّيُوَاطِـُٔواْ عِدَّةَ مَا حَرَّمَ ٱللَّهُ فَيُحِلُّواْ مَا حَرَّمَ ٱللَّهُۚ زُيِّنَ لَهُمۡ سُوٓءُ أَعۡمَٰلِهِمۡۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndithu kutalikitsa ndi kuchedwetsa (mwezi wopatulika kuti usafike mwamsanga), kumaonjezera kusakhulupirira (mwa Allah), zoterozo akusokerezedwa nazo amene sadakhulupirire. Chaka china amauyesa wosapatulika pomwe chaka china amauyesa wopatulika ndi cholinga chokwaniritsa chiwerengero cholingana ndi miyezi yomwe Allah adaipatula kukhala yopatulika. Choncho, chimene Allah adaletsa, amachiyesa chololedwa. Zakometsedwa kwa iwo zochita zawo zoipa. Ndipo Allah sawatsogolera anthu osakhulupirira.[209]
[209] Kuichedwetsa miyezi yopatulika, kapena ina mwa iyo ndi kuichotsa mu mndondomeko wake umene Allah adaiika monga momwe ankachitira anthu am’nyengo ya umbuli, kumawaonjezera kusakhulupilira anthu osakhulupilira mwa Allah. Arabu m’nyengo ya umbuli amauyesa mwezi wopatulika kukhala wosapatulika akafuna kuti achite nkhondo m’mweziwo. Ndipo mwezi wosapatulika amauyesa wopatulika ncholinga choti akwaniritse chiwerengero cha miyezi yopatulika yomwe Allah adaipatula. Zonsezi zimachitika pofuna kukwaniritsa zilakolako zawo zoipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَا لَكُمۡ إِذَا قِيلَ لَكُمُ ٱنفِرُواْ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ ٱثَّاقَلۡتُمۡ إِلَى ٱلۡأَرۡضِۚ أَرَضِيتُم بِٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا مِنَ ٱلۡأٓخِرَةِۚ فَمَا مَتَٰعُ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا فِي ٱلۡأٓخِرَةِ إِلَّا قَلِيلٌ
E inu amene mwakhulupirira! Mwatani; mukauzidwa (kuti): “Pitani mukachite Jihâd pa njira ya Allah,” mukudziremetsa pa nthaka (polemedwa ndi kutulukako)? Kodi mwasangalatsidwa ndi moyo wa pa dziko lapansi kuposa moyo wa tsiku lachimaliziro? Koma zosangalatsa za m’moyo wa dziko lapansi poyerekeza ndi (moyo wa) tsiku lachimaliziro, ndi zochepa kwambiri.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِلَّا تَنفِرُواْ يُعَذِّبۡكُمۡ عَذَابًا أَلِيمٗا وَيَسۡتَبۡدِلۡ قَوۡمًا غَيۡرَكُمۡ وَلَا تَضُرُّوهُ شَيۡـٔٗاۗ وَٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ
Ngati simupita (ku nkhondoko), (Allah) akulangani ndi chilango chowawa, ndipo abweretsa anthu ena m’malo mwa inu; ndipo simungamuvutitse ndi chilichonse (ngati musiya kupita kukamenyera chipembedzo Chake). Ndipo Allah Ngokhoza chilichonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِلَّا تَنصُرُوهُ فَقَدۡ نَصَرَهُ ٱللَّهُ إِذۡ أَخۡرَجَهُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ ثَانِيَ ٱثۡنَيۡنِ إِذۡ هُمَا فِي ٱلۡغَارِ إِذۡ يَقُولُ لِصَٰحِبِهِۦ لَا تَحۡزَنۡ إِنَّ ٱللَّهَ مَعَنَاۖ فَأَنزَلَ ٱللَّهُ سَكِينَتَهُۥ عَلَيۡهِ وَأَيَّدَهُۥ بِجُنُودٖ لَّمۡ تَرَوۡهَا وَجَعَلَ كَلِمَةَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ ٱلسُّفۡلَىٰۗ وَكَلِمَةُ ٱللَّهِ هِيَ ٱلۡعُلۡيَاۗ وَٱللَّهُ عَزِيزٌ حَكِيمٌ
Ngati simumthandiza (Mtumuki Muhammad {s.a.w} palibe kanthu), ndithu Allah adamthandiza pamene adamtulutsa aja amene sadakhulupirire. Pamene adali awiriwiri kuphanga, pamene ankanena kwa mnzake: “Usadandaule. Ndithu Allah ali nafe pamodzi.” Ndipo Allah adatsitsa mpumulo Wake pa iye, ndipo adaamthangata ndi asilikali a nkhondo omwe simudawaone. Ndipo mawu a amene sadakhulupirire adawachita kukhala apansi ndipo mawu a Allah ndiwo apamwamba. Ndipo Allah Ngopambana, Ngwanzeru zakuya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱنفِرُواْ خِفَافٗا وَثِقَالٗا وَجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِكُمۡ وَأَنفُسِكُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۚ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
Pitani (mukamenyane) muli opepukidwa ndi olemedwa; ndipo menyerani njira ya Allah nchuma chanu ndi inu nomwe. Zimenezi nzabwino kwa inu ngati muli anthu odziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَوۡ كَانَ عَرَضٗا قَرِيبٗا وَسَفَرٗا قَاصِدٗا لَّٱتَّبَعُوكَ وَلَٰكِنۢ بَعُدَتۡ عَلَيۡهِمُ ٱلشُّقَّةُۚ وَسَيَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ لَوِ ٱسۡتَطَعۡنَا لَخَرَجۡنَا مَعَكُمۡ يُهۡلِكُونَ أَنفُسَهُمۡ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ إِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
Ukadakhala ulendo wokafuna za m’dziko zopepuka kuzipeza, ndi ulendo wofupika, ndithu akadakutsata (achiphamaso). Koma ulendo wamavutowu wakhala wautali kwa iwo. Ndipo iwo alumbilira Allah (ponena kuti): “Kukadakhala kotheka kwa ife, tikadapita nanu.” (Pa mawu awa), akudziononga okha. Ndipo Allah akudziwa kuti iwo Ngabodza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
عَفَا ٱللَّهُ عَنكَ لِمَ أَذِنتَ لَهُمۡ حَتَّىٰ يَتَبَيَّنَ لَكَ ٱلَّذِينَ صَدَقُواْ وَتَعۡلَمَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
Allah wakukhululukira. Bwanji wawaloleza kutsalira? (Ukadayembekeza) kufikira adziwike kwa iwe amene akunena zoona, ndikuti uwadziwe abodza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا يَسۡتَـٔۡذِنُكَ ٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ أَن يُجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلۡمُتَّقِينَ
Sangakupemphe chilolezo (chotsala ku nkhondo) amene akhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro kuti asapite kukamenyera (chipembedzo cha Allah) ndi chuma chawo ndi Matupi awo. Ndipo Allah akuwadziwa amene akumuopa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّمَا يَسۡتَـٔۡذِنُكَ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَٱرۡتَابَتۡ قُلُوبُهُمۡ فَهُمۡ فِي رَيۡبِهِمۡ يَتَرَدَّدُونَ
Ndithu amakupempha chilolezo aja amene sakhulupirira Allah ndi tsiku la chimaliziro, ndipo mitima yawo yakaikira, ndipo iwo, chifukwa cha kukaika kwawo akungotekeseka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَلَوۡ أَرَادُواْ ٱلۡخُرُوجَ لَأَعَدُّواْ لَهُۥ عُدَّةٗ وَلَٰكِن كَرِهَ ٱللَّهُ ٱنۢبِعَاثَهُمۡ فَثَبَّطَهُمۡ وَقِيلَ ٱقۡعُدُواْ مَعَ ٱلۡقَٰعِدِينَ
Akadafunadi kuti atuluke (kupita ku nkhondo) akadakonzekera zokonzekera za ku nkhondo; koma Allah sadafune kuti iwo apiteko; choncho adawatsekereza, ndipo kudanenedwa: “Khalani pamodzi ndi Otsalira.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَوۡ خَرَجُواْ فِيكُم مَّا زَادُوكُمۡ إِلَّا خَبَالٗا وَلَأَوۡضَعُواْ خِلَٰلَكُمۡ يَبۡغُونَكُمُ ٱلۡفِتۡنَةَ وَفِيكُمۡ سَمَّٰعُونَ لَهُمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلظَّٰلِمِينَ
Ngati akadatuluka nanu pamodzi, sakadakuonjezerani chilichonse koma chisokonezo ndi kuyenda mwa ukazitape pakati panu ndicholinga chokufunirani chisokonezo, ndipo mwa inu alipo akuwamvelera, ndipo Allah Ngodziwa za oipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَقَدِ ٱبۡتَغَوُاْ ٱلۡفِتۡنَةَ مِن قَبۡلُ وَقَلَّبُواْ لَكَ ٱلۡأُمُورَ حَتَّىٰ جَآءَ ٱلۡحَقُّ وَظَهَرَ أَمۡرُ ٱللَّهِ وَهُمۡ كَٰرِهُونَ
Ndithudi, akhala akukufunirani chisokonezo kuyambira kale, akusanthulirasanthulira zinthu (n’cholinga choti athane nawe) kufikira choonadi chadza ndi kuonekera poyera lamulo la Allah (lowakhaulitsa Ayuda) iwo asakufuna.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِنۡهُم مَّن يَقُولُ ٱئۡذَن لِّي وَلَا تَفۡتِنِّيٓۚ أَلَا فِي ٱلۡفِتۡنَةِ سَقَطُواْۗ وَإِنَّ جَهَنَّمَ لَمُحِيطَةُۢ بِٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo mwa iwo pali yemwe akuti: “Ndiloreni ine (kuti nditsale ku nkhondo) ndipo musandiponye m’mayeso (kuopa kuti ndingalakwe ndikaona akazi akumeneko).” Dziwani kuti iwo agwera kale m’mayesero. Ndipo, ndithu Jahannam ikawazinga mbali zonse osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِن تُصِبۡكَ حَسَنَةٞ تَسُؤۡهُمۡۖ وَإِن تُصِبۡكَ مُصِيبَةٞ يَقُولُواْ قَدۡ أَخَذۡنَآ أَمۡرَنَا مِن قَبۡلُ وَيَتَوَلَّواْ وَّهُمۡ فَرِحُونَ
Chikakupeza chabwino, (iwe Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndi okutsatira) zimawanyansa, ndipo vuto likakupeza amanena: “Tidalingalira zinthu zathu kale. (Nchifukwa chake mavuto atizemba).” Ndipo amatembenuka nkupita uku akukondwa.[210]
[210] Achinyengo sadali kufunira zabwino Asilamu ngakhale kuti adali kudzipachika m’gulu la Asilamu mwachinyengo. Ankati vuto likawagwera Asilamu amasangalala. Koma chikawadzera chabwino amadandaula.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُل لَّن يُصِيبَنَآ إِلَّا مَا كَتَبَ ٱللَّهُ لَنَا هُوَ مَوۡلَىٰنَاۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ
Nena: “Palibe chomwe chitipeze koma chimene Allah watilembera. Iye ndi Mbuye wathu.” Choncho, Asilamu ayadzamire kwa Allah Yekha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُلۡ هَلۡ تَرَبَّصُونَ بِنَآ إِلَّآ إِحۡدَى ٱلۡحُسۡنَيَيۡنِۖ وَنَحۡنُ نَتَرَبَّصُ بِكُمۡ أَن يُصِيبَكُمُ ٱللَّهُ بِعَذَابٖ مِّنۡ عِندِهِۦٓ أَوۡ بِأَيۡدِينَاۖ فَتَرَبَّصُوٓاْ إِنَّا مَعَكُم مُّتَرَبِّصُونَ
Nena: “Kodi chilipo chimene mukuyembekezera mwa ife posakhala chimodzi mwa zinthu ziwiri zabwino, (kupambana pa nkhondo ndi kupeza zotolatola zake, kapena kufa ndikukalowa ku Munda wamtendere)? Ndipo nafe tikukuyembekezerani kuti Allah akupatsani chilango chochokera kwa Iye, kapena kupyolera m’manja mwathu. Choncho bayembekezerani; nafenso tikuyembekezera nanu limodzi.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
قُلۡ أَنفِقُواْ طَوۡعًا أَوۡ كَرۡهٗا لَّن يُتَقَبَّلَ مِنكُمۡ إِنَّكُمۡ كُنتُمۡ قَوۡمٗا فَٰسِقِينَ
Nena (kwa achiphamaso): “Perekani (chuma chanu) mwa chifuniro kapena mosafuna sichizalandiridwa kwa inu. Ndithu inu ndinu anthu otuluka m’chilamulo cha Allah.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا مَنَعَهُمۡ أَن تُقۡبَلَ مِنۡهُمۡ نَفَقَٰتُهُمۡ إِلَّآ أَنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَبِرَسُولِهِۦ وَلَا يَأۡتُونَ ٱلصَّلَوٰةَ إِلَّا وَهُمۡ كُسَالَىٰ وَلَا يُنفِقُونَ إِلَّا وَهُمۡ كَٰرِهُونَ
Palibe chomwe chidaletsa kulandiridwa kwa zopereka zawo koma chifukwa chakuti iwo sadakhulupirire Allah ndi Mtumiki Wake; ndiponso sapita kopemphera koma mwaulesi; ndipo sapereka chopereka koma monyinyirika.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَا تُعۡجِبۡكَ أَمۡوَٰلُهُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُهُمۡۚ إِنَّمَا يُرِيدُ ٱللَّهُ لِيُعَذِّبَهُم بِهَا فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَتَزۡهَقَ أَنفُسُهُمۡ وَهُمۡ كَٰفِرُونَ
Ndipo chisakudolole chuma chawo kapena ana awo. Ndithu Allah akufuna kuwalanga nazo pa moyo wa pa dziko lapansi, ndi kuti mitima yawo ichoke ali osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَيَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ إِنَّهُمۡ لَمِنكُمۡ وَمَا هُم مِّنكُمۡ وَلَٰكِنَّهُمۡ قَوۡمٞ يَفۡرَقُونَ
Ndipo akulumbira (m’dzina la) Allah kuti iwo ali pamodzi ndi inu; pomwe iwo sali pamodzi nanu koma ndithu iwo ndi anthu amantha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَوۡ يَجِدُونَ مَلۡجَـًٔا أَوۡ مَغَٰرَٰتٍ أَوۡ مُدَّخَلٗا لَّوَلَّوۡاْ إِلَيۡهِ وَهُمۡ يَجۡمَحُونَ
Ngati akadapeza linga lothawiramo pena mapanga kapena pamalo pena polowa (ndithu) akadathawira kumeneko mwa liwiro.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِنۡهُم مَّن يَلۡمِزُكَ فِي ٱلصَّدَقَٰتِ فَإِنۡ أُعۡطُواْ مِنۡهَا رَضُواْ وَإِن لَّمۡ يُعۡطَوۡاْ مِنۡهَآ إِذَا هُمۡ يَسۡخَطُونَ
Ndipo alipo ena mwa iwo (achiphamaso) amene akukunyogodola mkugawa kwako sadaka. Akapatsidwa kanthu m’menemo amakondwera koma akapanda kupatsidwa akukwiya nawe.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَوۡ أَنَّهُمۡ رَضُواْ مَآ ءَاتَىٰهُمُ ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥ وَقَالُواْ حَسۡبُنَا ٱللَّهُ سَيُؤۡتِينَا ٱللَّهُ مِن فَضۡلِهِۦ وَرَسُولُهُۥٓ إِنَّآ إِلَى ٱللَّهِ رَٰغِبُونَ
Ndipo ngati iwo akadakondwera ndi chimene Allah ndi Mtumiki Wake wawapatsa, nanena: “Allah watikwanira. Posachedwapa Allah ndi Mtumiki Wake atipatsa zabwino Zake. Ndithu ife tikufunitsitsa kwa Allah.” (Ndiye kuti Allah akadawapatsa zambiri).
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ إِنَّمَا ٱلصَّدَقَٰتُ لِلۡفُقَرَآءِ وَٱلۡمَسَٰكِينِ وَٱلۡعَٰمِلِينَ عَلَيۡهَا وَٱلۡمُؤَلَّفَةِ قُلُوبُهُمۡ وَفِي ٱلرِّقَابِ وَٱلۡغَٰرِمِينَ وَفِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَٱبۡنِ ٱلسَّبِيلِۖ فَرِيضَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
Ndithu sadaka (za Zakaati) ndi za mafukara, masikini, ogwira ntchito yosonkhetsa sadakazo, owalimbitsa mitima yawo (pa Chisilamu amene alowa kumene), kuombolera akapolo (kuti akhale afulu), kuthandizira amene ali m’ngongole; kuzipereka pa njira ya Allah; ndi kuwapatsa a paulendo (omwe alibe choyendera). Ili ndi lamulo lochokera kwa Allah, ndipo Allah Ngodziwa kwabasi, Ngwanzeru zakuya.[211]
[211] M’ndime iyi Allah akutifotokozera magulu a anthu amene ngoyenera kuwagawira chuma cha Zakaat. Iwo ndi awa:- 1. Osauka amene sangagwire ntchito nkudzipezera okha chakudya (mafukara). 2. Osauka amene alibe zokwanira pa zofunikira pa moyo wawo (Masikini). 3. Amene akusonkhetsa chuma cha Zakaat cho omwe ntchito yawo ndiyokhayo. 4. Amene angolowa kumene m’Chisilamu omwe akuyembekezedwa kuti akapatsidwa adzalimbikitsidwa mitima yawo pa chipembedzochi. 5. Amene afuna kudziombola ku ukapolo. 6. Amene akulephera kulipira ngongole ya choonadi. 7. Amene akuchita Jihâd panjira ya Allah. 8. Wapaulendo amene alibe choyendera (ndalama zoyendera).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِنۡهُمُ ٱلَّذِينَ يُؤۡذُونَ ٱلنَّبِيَّ وَيَقُولُونَ هُوَ أُذُنٞۚ قُلۡ أُذُنُ خَيۡرٖ لَّكُمۡ يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَيُؤۡمِنُ لِلۡمُؤۡمِنِينَ وَرَحۡمَةٞ لِّلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنكُمۡۚ وَٱلَّذِينَ يُؤۡذُونَ رَسُولَ ٱللَّهِ لَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo alipo ena mwa iwo amene akuzunza Mneneri ponena kuti: “Uyu ndi khutu (lomvetsera nkhani iliyonse popanda kuiganizira).” Nena: “Ndi khutu labwino kwa inu.” (Mwini khutulo) amakhulupirira Allah, amakhulupirira (zonena) za okhulupirira, ndipo (iye) ndichifundo kwa amene akhulupirira mwa inu. Ndipo amene akuvutitsa Mtumiki wa Allah adzakhala ndi chilango chopweteka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ لَكُمۡ لِيُرۡضُوكُمۡ وَٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥٓ أَحَقُّ أَن يُرۡضُوهُ إِن كَانُواْ مُؤۡمِنِينَ
Akulumbira kwa inu potchula dzina la Allah kuti akukondweretseni (chikhalirecho akunyoza Allah ndi Mtumiki Wake), pomwe Allah ndi Mtumiki Wake ndiye wofunika kuti amkondweretse ngati iwo ngokhulupiriradi (mwachoonadi).
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ يَعۡلَمُوٓاْ أَنَّهُۥ مَن يُحَادِدِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَأَنَّ لَهُۥ نَارَ جَهَنَّمَ خَٰلِدٗا فِيهَاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡخِزۡيُ ٱلۡعَظِيمُ
Kodi sadziwa kuti amene akulimbana ndi Allah ndi Mtumiki Wake, adzapeza moto wa Jahannam ndi kukhalamo nthawi yaitali? Kumeneko ndikuyaluka kwakukulu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَحۡذَرُ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ أَن تُنَزَّلَ عَلَيۡهِمۡ سُورَةٞ تُنَبِّئُهُم بِمَا فِي قُلُوبِهِمۡۚ قُلِ ٱسۡتَهۡزِءُوٓاْ إِنَّ ٱللَّهَ مُخۡرِجٞ مَّا تَحۡذَرُونَ
Achiphamaso akuopa kuwatsikira Sura yomwe ingawafotokozere (zachinyengo chawo) chomwe chili m’mitima mwawo. Nena: “Chitani zachipongwe. Ndithu Allah atulutsira poyera zomwe mukuziopazo (kuti Asilamu asazidziwe).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَئِن سَأَلۡتَهُمۡ لَيَقُولُنَّ إِنَّمَا كُنَّا نَخُوضُ وَنَلۡعَبُۚ قُلۡ أَبِٱللَّهِ وَءَايَٰتِهِۦ وَرَسُولِهِۦ كُنتُمۡ تَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndipo utawafunsa (chifukwa ninji chipembedzo akuchichitira chipongwe)? Anena: “Ife timangosereula ndi kusewera basi (palibe china).” Nena: “Mumachitira Allah ndi Ayah (ndime) Zake ndi Mtumiki Wake zachipongwe?”
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا تَعۡتَذِرُواْ قَدۡ كَفَرۡتُم بَعۡدَ إِيمَٰنِكُمۡۚ إِن نَّعۡفُ عَن طَآئِفَةٖ مِّنكُمۡ نُعَذِّبۡ طَآئِفَةَۢ بِأَنَّهُمۡ كَانُواْ مُجۡرِمِينَ
Musapereke madandaulo (abodza), ndithu mwaonetsera ukafiri wanu poyera, pambuyo pa kukhulupirira kwanu (kwabodza). Ngati gulu lina mwa inu tilikhululukira (litalapa), gulu lina tililanga chifukwa cha kupitiriza kulakwa kwawo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلۡمُنَٰفِقُونَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتُ بَعۡضُهُم مِّنۢ بَعۡضٖۚ يَأۡمُرُونَ بِٱلۡمُنكَرِ وَيَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَقۡبِضُونَ أَيۡدِيَهُمۡۚ نَسُواْ ٱللَّهَ فَنَسِيَهُمۡۚ إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ هُمُ ٱلۡفَٰسِقُونَ
Achiphamaso aamuna ndi achiphamaso aakazi onse khalidwe lawo ndi limodzi. Amalamulira zoipa ndikuletsa zabwino, ndipo amafumbata manja awo (sathandiza pa zabwino). Amuiwala Allah (ponyozera malamulo Ake). Iyenso wawaiwala (powanyozera). Ndithu achiphamaso ngotuluka mchilamulo (cha Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتِ وَٱلۡكُفَّارَ نَارَ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ هِيَ حَسۡبُهُمۡۚ وَلَعَنَهُمُ ٱللَّهُۖ وَلَهُمۡ عَذَابٞ مُّقِيمٞ
Allah walonjeza achiphamaso aamuna ndi achiphamaso aakazi ndi akafiri moto wa Jahannam, akakhala m’menemo nthawi yaitali. Umenewo ukukwanira kwa iwo (kuwalanga). Ndipo Allah wawatembelera, ndipo iwo adzapeza chilango cha nthawi zonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
كَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ كَانُوٓاْ أَشَدَّ مِنكُمۡ قُوَّةٗ وَأَكۡثَرَ أَمۡوَٰلٗا وَأَوۡلَٰدٗا فَٱسۡتَمۡتَعُواْ بِخَلَٰقِهِمۡ فَٱسۡتَمۡتَعۡتُم بِخَلَٰقِكُمۡ كَمَا ٱسۡتَمۡتَعَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُم بِخَلَٰقِهِمۡ وَخُضۡتُمۡ كَٱلَّذِي خَاضُوٓاْۚ أُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
(Inu osakhulupirira) ndinu ofanana ndi amene adalipo patsogolo panu. (Tikuonongani monga tidawaonongera iwo; koma) iwo adali ndi nyonga zambiri kuposa inu; adalinso ndi chuma chambiri ndi ana ambiri kuposa inu. Choncho, adasangalalira gawo lawo, inunso mukusangalalira gawo lanu monga momwe adasangalalira gawo lawo omwe adalipo patsogolo panu, ndipo mwamira m’zoipa monga momwe adamilira iwo. Awo ndi amene zochita zawo zidapita pachabe padziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro. Awo ndi omwe ali otaika (oluza).
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ يَأۡتِهِمۡ نَبَأُ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ قَوۡمِ نُوحٖ وَعَادٖ وَثَمُودَ وَقَوۡمِ إِبۡرَٰهِيمَ وَأَصۡحَٰبِ مَدۡيَنَ وَٱلۡمُؤۡتَفِكَٰتِۚ أَتَتۡهُمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِۖ فَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيَظۡلِمَهُمۡ وَلَٰكِن كَانُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ يَظۡلِمُونَ
Kodi siidawadzere nkhani ya amene adalipo patsogolo pawo anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu; anthu a Ibrahim ndi anthu a ku Madiyan ndi (anthu) a m’midzi imene idatembenuzidwa kumwamba kukhala pansi, pansi kukhala kumwamba? Atumiki awo adawadzera ndi zisonyezo zoonekera (koma adakana kuwatsata. Choncho, Allah adawaononga). Allah sadawachitire choipa, koma ankadzichitira okha zoipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتُ بَعۡضُهُمۡ أَوۡلِيَآءُ بَعۡضٖۚ يَأۡمُرُونَ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلۡمُنكَرِ وَيُقِيمُونَ ٱلصَّلَوٰةَ وَيُؤۡتُونَ ٱلزَّكَوٰةَ وَيُطِيعُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ سَيَرۡحَمُهُمُ ٱللَّهُۗ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Okhulupirira aamuna ndi okhulupirira aakazi, ndiabwenzi omvana pakati pawo. Amalamula zabwino ndikuletsa zoipa ndipo amapemphera Swala ndi kupereka chopereka (zakaat), ndipo amamvera Allah ndi Mtumiki Wake. Awo ndi omwe Allah adzawachitira chifundo. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَا وَمَسَٰكِنَ طَيِّبَةٗ فِي جَنَّٰتِ عَدۡنٖۚ وَرِضۡوَٰنٞ مِّنَ ٱللَّهِ أَكۡبَرُۚ ذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Allah waalonjeza okhulupirira aamuna ndi okhulupirira aakazi Minda yomwe pansi (ndi patsogolo) pake mitsinje ikuyenda, adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Ndi mokhala mwabwino m’Minda ya Edeni. Ndipo chiyanjo chochokera kwa Allah ndichachikulu (omwe ndi mtendere waukulu kwambiri kuposa zonse). Kumeneko ndiko kupambana zedi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ جَٰهِدِ ٱلۡكُفَّارَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱغۡلُظۡ عَلَيۡهِمۡۚ وَمَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
E iwe Mneneri! Limbana ndi osakhulupirira ndi achiphamaso ndipo uwaumire mtima. Mbuto yawo ndi ku Jahannam. Taonani kuipa kwa malo obwerera.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ مَا قَالُواْ وَلَقَدۡ قَالُواْ كَلِمَةَ ٱلۡكُفۡرِ وَكَفَرُواْ بَعۡدَ إِسۡلَٰمِهِمۡ وَهَمُّواْ بِمَا لَمۡ يَنَالُواْۚ وَمَا نَقَمُوٓاْ إِلَّآ أَنۡ أَغۡنَىٰهُمُ ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥ مِن فَضۡلِهِۦۚ فَإِن يَتُوبُواْ يَكُ خَيۡرٗا لَّهُمۡۖ وَإِن يَتَوَلَّوۡاْ يُعَذِّبۡهُمُ ٱللَّهُ عَذَابًا أَلِيمٗا فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۚ وَمَا لَهُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مِن وَلِيّٖ وَلَا نَصِيرٖ
(Achiphamaso pambuyo pomunenera Allah ndi Mtumiki Wake mawu oipa), akulumbira potchula dzina la Allah (kuti) sadanene (zonyoza), pomwe adanenadi mawu aukafiri, ndipo akana chikhulupiliro pambuyo posonyeza Chisilamu chawo (chabodza); ndipo adatsimikiza (kuchita) zomwe sadathe kuzifika. Komatu sadaone choipa (m’kudza kwa Chisilamu), koma kuti Allah ndi Mtumiki Wake adawalemeretsa ndi zabwino zake. Choncho Ngati alapa, zikhala zabwino kwa iwo. Ndipo ngati anyoza, Allah awalanga ndi chilango chowawa pa moyo wa pa dziko lapansi ndi patsiku lachimaliziro. Ndipo sadzakhala ndi mtetezi ngakhale aliyense wowapulumutsa pa dziko.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَمِنۡهُم مَّنۡ عَٰهَدَ ٱللَّهَ لَئِنۡ ءَاتَىٰنَا مِن فَضۡلِهِۦ لَنَصَّدَّقَنَّ وَلَنَكُونَنَّ مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Pakati pawo alipo amene adalonjeza Allah kuti, “Ngati atipatsa zabwino zake (chuma) tidzapereka sadaka ndi kukhala m’gulu la ochita zabwino.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلَمَّآ ءَاتَىٰهُم مِّن فَضۡلِهِۦ بَخِلُواْ بِهِۦ وَتَوَلَّواْ وَّهُم مُّعۡرِضُونَ
Koma pamene adawapatsa zabwino Zakezo, adazichitira umbombo nanyoza, natembenukira kutali (ndi Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَأَعۡقَبَهُمۡ نِفَاقٗا فِي قُلُوبِهِمۡ إِلَىٰ يَوۡمِ يَلۡقَوۡنَهُۥ بِمَآ أَخۡلَفُواْ ٱللَّهَ مَا وَعَدُوهُ وَبِمَا كَانُواْ يَكۡذِبُونَ
Choncho, chotsatira chake adawaika chinyengo m’mitima mwawo kufikira tsiku lokumana naye (Allah), chifukwa cha kuphwanya kwawo zomwe adamulonjeza Allah. Ndiponso chifukwa cha zabodza zomwe ankanena.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ يَعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُ سِرَّهُمۡ وَنَجۡوَىٰهُمۡ وَأَنَّ ٱللَّهَ عَلَّٰمُ ٱلۡغُيُوبِ
Kodi sadziwa kuti Allah akudziwa zobisika zawo ndi manong’onong’o awo ndikuti Allah Ngodziwa zinthu zamseri?
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلَّذِينَ يَلۡمِزُونَ ٱلۡمُطَّوِّعِينَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ فِي ٱلصَّدَقَٰتِ وَٱلَّذِينَ لَا يَجِدُونَ إِلَّا جُهۡدَهُمۡ فَيَسۡخَرُونَ مِنۡهُمۡ سَخِرَ ٱللَّهُ مِنۡهُمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٌ
Amene akuwanyogodola okhulupirira opereka sadaka yambiri, ndiponso (amene akunyoza) amene sapeza (chopereka) koma chinthu chochepa; ndikumawachitira chipongwe, Allah adzawalipira chipongwe chawocho. Iwo adzapeza chilango chopweteka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ أَوۡ لَا تَسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ إِن تَسۡتَغۡفِرۡ لَهُمۡ سَبۡعِينَ مَرَّةٗ فَلَن يَغۡفِرَ ٱللَّهُ لَهُمۡۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡفَٰسِقِينَ
(E iwe Mtumiki!) Uwapemphere chikhululuko (achiphamaso) kapena usawapemphere, (zonsezo nchimodzimodzi). Ngakhale utawapemphera chikhululuko chochuluka kwabasi mokwanira makumi asanu ndi awiri (70) Allah sangawakhululukire. Zimenezo nchifukwa chakuti iwo amkana Allah ndi Mtumiki Wake. Ndipo Allah satsogolera anthu ophwanya malamulo (Ake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَرِحَ ٱلۡمُخَلَّفُونَ بِمَقۡعَدِهِمۡ خِلَٰفَ رَسُولِ ٱللَّهِ وَكَرِهُوٓاْ أَن يُجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَقَالُواْ لَا تَنفِرُواْ فِي ٱلۡحَرِّۗ قُلۡ نَارُ جَهَنَّمَ أَشَدُّ حَرّٗاۚ لَّوۡ كَانُواْ يَفۡقَهُونَ
Akondwa amene adasiidwa m’mbuyo (osapita kunkhondo) chifukwa chakukhala kwawo m’mbuyo polekana ndi Mtumiki wa Allah, nakuda kumenyana pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi miyoyo yawo, nati (kwa anzawo): “Musapite (ku nkhondo) m’nthawi yotenthayi.” Auze: “Moto wa Jahannam ngotentha kwambiri akadakhala akuzindikira.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَلۡيَضۡحَكُواْ قَلِيلٗا وَلۡيَبۡكُواْ كَثِيرٗا جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Choncho, aseke pang’ono (padziko lapansi). Ndipo adzalira kwambiri (patsiku lachimaliziro); (iyo ndi) mphoto ya zomwe adapeza (kuchokera m’zochita zawo zoipa).[212]
[212] Anthu achinyengo (achiphamaso) adakana kupita naye limodzi Mtumiki (s.a.w) ku nkhondo namasangalalira kukhala kwawoko. Ndipo apa Allah akuwauza kuti asangalale ndi kuseka pang’ono. Koma adzalira ndi kukukuta mano nthawi yaitali.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِن رَّجَعَكَ ٱللَّهُ إِلَىٰ طَآئِفَةٖ مِّنۡهُمۡ فَٱسۡتَـٔۡذَنُوكَ لِلۡخُرُوجِ فَقُل لَّن تَخۡرُجُواْ مَعِيَ أَبَدٗا وَلَن تُقَٰتِلُواْ مَعِيَ عَدُوًّاۖ إِنَّكُمۡ رَضِيتُم بِٱلۡقُعُودِ أَوَّلَ مَرَّةٖ فَٱقۡعُدُواْ مَعَ ٱلۡخَٰلِفِينَ
Ngati Allah akubweza (ku nkhondoko) nkufika kugulu lina la mwa iwo ndipo iwo nkukupempha chilolezo chakutuluka (kupita ku nkhondo zomwe zidzapezeke mtsogolo), nena: “Inu simudzatuluka nane mpaka muyaya, ngakhalenso kumenyana ndi adani pamodzi nane; inu mudakonda kukhala nthawi yoyamba; choncho khalani (nthawi zonse) pamodzi ndi otsalira (pambuyo).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا تُصَلِّ عَلَىٰٓ أَحَدٖ مِّنۡهُم مَّاتَ أَبَدٗا وَلَا تَقُمۡ عَلَىٰ قَبۡرِهِۦٓۖ إِنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَمَاتُواْ وَهُمۡ فَٰسِقُونَ
Ndipo usamupemphelere konse aliyense wa iwo yemwe wamwalira, ndipo usaimilire pamanda ake (kumpemphelera); ndithu iwo amukana Allah ndi Mtumiki Wake, ndipo amwalira uku ali opandukira chilamulo (cha Allah).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا تُعۡجِبۡكَ أَمۡوَٰلُهُمۡ وَأَوۡلَٰدُهُمۡۚ إِنَّمَا يُرِيدُ ٱللَّهُ أَن يُعَذِّبَهُم بِهَا فِي ٱلدُّنۡيَا وَتَزۡهَقَ أَنفُسُهُمۡ وَهُمۡ كَٰفِرُونَ
Ndipo chisakudolole chuma chawo kapena ana awo. Ndithu Allah akufuna kuwalanga ndi zimenezo pa dziko lapansi, ndi kuti mizimu yawo ichoke ali osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِذَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٌ أَنۡ ءَامِنُواْ بِٱللَّهِ وَجَٰهِدُواْ مَعَ رَسُولِهِ ٱسۡتَـٔۡذَنَكَ أُوْلُواْ ٱلطَّوۡلِ مِنۡهُمۡ وَقَالُواْ ذَرۡنَا نَكُن مَّعَ ٱلۡقَٰعِدِينَ
Ndipo Sura ikavumbulutsidwa (yonena kuti): “Mkhulupirireni Allah ndi kumenya nkhondo (chifukwa cha chipembedzo Chake) pamodzi ndi Mtumiki Wake,” opeza bwino mwa iwo akukupempha chilolezo (kuti asapite ku nkhondo), ndipo akuti: “Tisiye tikhale pamodzi ndi okhala (otsalira m’mbuyo).”
Ang mga Tafsir na Arabe:
رَضُواْ بِأَن يَكُونُواْ مَعَ ٱلۡخَوَالِفِ وَطُبِعَ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ فَهُمۡ لَا يَفۡقَهُونَ
Akondwera pokhala limodzi ndi otsalira m’mbuyo (akazi ndi ana). Ndipo mitima yawo yadindidwa chidindo (yatsekedwa), choncho iwo sazindikira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَٰكِنِ ٱلرَّسُولُ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مَعَهُۥ جَٰهَدُواْ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡۚ وَأُوْلَٰٓئِكَ لَهُمُ ٱلۡخَيۡرَٰتُۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡمُفۡلِحُونَ
Koma Mtumiki ndi amene akhulupirira pamodzi ndi iye amenya nkhondo ndi chuma chawo ndi matupi awo. Iwowo ndiwo opeza zabwino, ndiponso iwowo ndiwo opambana.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَعَدَّ ٱللَّهُ لَهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Allah wawakonzera minda yoyenda mitsinje pansi (ndi patsogolo) pake; adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَجَآءَ ٱلۡمُعَذِّرُونَ مِنَ ٱلۡأَعۡرَابِ لِيُؤۡذَنَ لَهُمۡ وَقَعَدَ ٱلَّذِينَ كَذَبُواْ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥۚ سَيُصِيبُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٞ
Ndipo adza eni madandaulo (owona) mwa anthu akumidzi (omwe ndi Asilamu) kuti awapatse chilolezo (chosapita ku nkhondo). Koma adakhala (popanda kupempha chilolezo kwa Mtumiki) amene amunamiza Allah ndi Mtumiki Wake. (Amenewa ndi achiphamaso omwe amadzitcha kuti ndi Asilamu pomwe sadali Asilamu). Mwa iwo amene sadakhulupirire Allah chiwapeza chilango chopweteka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَّيۡسَ عَلَى ٱلضُّعَفَآءِ وَلَا عَلَى ٱلۡمَرۡضَىٰ وَلَا عَلَى ٱلَّذِينَ لَا يَجِدُونَ مَا يُنفِقُونَ حَرَجٌ إِذَا نَصَحُواْ لِلَّهِ وَرَسُولِهِۦۚ مَا عَلَى ٱلۡمُحۡسِنِينَ مِن سَبِيلٖۚ وَٱللَّهُ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Palibe tchimo (kusapita kunkhondo) kwa amene ali ofooka (pachilengedwe chawo), ngakhale kwa odwala, ngakhale kwa omwe sapeza chothandiza (pa ulendo ngakhale chosiira akubanja lawo) ngati iwo ali ndi cholinga chabwino pa Allah ndi Mtumiki Wake. Palibe njira (yowadzudzulira) amene akuchita zabwino. Ndipo Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni zedi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا عَلَى ٱلَّذِينَ إِذَا مَآ أَتَوۡكَ لِتَحۡمِلَهُمۡ قُلۡتَ لَآ أَجِدُ مَآ أَحۡمِلُكُمۡ عَلَيۡهِ تَوَلَّواْ وَّأَعۡيُنُهُمۡ تَفِيضُ مِنَ ٱلدَّمۡعِ حَزَنًا أَلَّا يَجِدُواْ مَا يُنفِقُونَ
Ndiponso (palibe tchimo) kwa amene akukudzera kuti uwatenge (kupita ku nkhondo) iwe uunena: “Ndilibe choti ndikunyamulireni,” nabwerera maso awo akutuluka misozi chifukwa cha kudandaula posapeza zimene zingawathandize pa ulendowo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ إِنَّمَا ٱلسَّبِيلُ عَلَى ٱلَّذِينَ يَسۡتَـٔۡذِنُونَكَ وَهُمۡ أَغۡنِيَآءُۚ رَضُواْ بِأَن يَكُونُواْ مَعَ ٱلۡخَوَالِفِ وَطَبَعَ ٱللَّهُ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ فَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
۞ Ndithu njira (yodzudzulidwa) ili pa arnene akukupempha chilolezo (choti asapite ku nkhondo ndi kusiyanso kupereka chuma chawo) pomwe iwo ngolemera. Akonda kukhala pamodzi ndi otsala m’mbuyo. Ndipo Allah wadinda chidindo (cha mantha) m’mitima mwawo, tero sadziwa (chilichonse chowathandiza).
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَعۡتَذِرُونَ إِلَيۡكُمۡ إِذَا رَجَعۡتُمۡ إِلَيۡهِمۡۚ قُل لَّا تَعۡتَذِرُواْ لَن نُّؤۡمِنَ لَكُمۡ قَدۡ نَبَّأَنَا ٱللَّهُ مِنۡ أَخۡبَارِكُمۡۚ وَسَيَرَى ٱللَّهُ عَمَلَكُمۡ وَرَسُولُهُۥ ثُمَّ تُرَدُّونَ إِلَىٰ عَٰلِمِ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِ فَيُنَبِّئُكُم بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Akudandaulirani madandaulo mukabwerera kwa iwo (ndi kukumana nawo). Nena: “Musapereke madandaulo; sitikukhulupirirani. Allah watifotokozera kale nkhani zanu. Posachedwa Allah ndi Mtumiki Wake aona zochita zanu, kenako muzabwezedwa (pambuyo pa imfa) kwa Wodziwa zamseri ndi zoonekera. Choncho, Iye adzakufotokozerani zimene mudali kuchita.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
سَيَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ لَكُمۡ إِذَا ٱنقَلَبۡتُمۡ إِلَيۡهِمۡ لِتُعۡرِضُواْ عَنۡهُمۡۖ فَأَعۡرِضُواْ عَنۡهُمۡۖ إِنَّهُمۡ رِجۡسٞۖ وَمَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُ جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Mukabwerera kwa iwo, adzalumbira m’dzina la Allah kwa inu kuti muwasiye (musawachite kanthu). Choncho, apatukireni. Ndithu iwo ndiuve ndipo malo awo ndi ku Jahannam. Iyi ndi mphoto ya zomwe adali kupeza (kuchokera m’zochita zawo zoipa).
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَحۡلِفُونَ لَكُمۡ لِتَرۡضَوۡاْ عَنۡهُمۡۖ فَإِن تَرۡضَوۡاْ عَنۡهُمۡ فَإِنَّ ٱللَّهَ لَا يَرۡضَىٰ عَنِ ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡفَٰسِقِينَ
Akulumbira kwa inu kuti muwayanje, choncho ngati muwayanja, ndithu Allah sayanja anthu otuluka m’chilamulo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلۡأَعۡرَابُ أَشَدُّ كُفۡرٗا وَنِفَاقٗا وَأَجۡدَرُ أَلَّا يَعۡلَمُواْ حُدُودَ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ عَلَىٰ رَسُولِهِۦۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
Arabu a kumizi ngoyipitsitsa pa kusakhulupirira ndi uchiphamaso ndiponso ngoyenera kusazindikira malire a zomwe Allah wavumbulutsa kwa Mtumiki Wake. Komatu Allah Ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِنَ ٱلۡأَعۡرَابِ مَن يَتَّخِذُ مَا يُنفِقُ مَغۡرَمٗا وَيَتَرَبَّصُ بِكُمُ ٱلدَّوَآئِرَۚ عَلَيۡهِمۡ دَآئِرَةُ ٱلسَّوۡءِۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo alipo ena mwa Arabu a kuchimizi omwe amachichita chimene akupereka pa njira ya Allah ngati dipo (laulere lopanda phindu), ndikumadikira kwa inu kuti miliri ikupezeni. Miliri yoipa ili pa iwo; (iwapeza okha). Ndipo Allah Ngwakumva (nkhani iliyonse), Wodziwa (chilichonse).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِنَ ٱلۡأَعۡرَابِ مَن يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَيَتَّخِذُ مَا يُنفِقُ قُرُبَٰتٍ عِندَ ٱللَّهِ وَصَلَوَٰتِ ٱلرَّسُولِۚ أَلَآ إِنَّهَا قُرۡبَةٞ لَّهُمۡۚ سَيُدۡخِلُهُمُ ٱللَّهُ فِي رَحۡمَتِهِۦٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٞ
Ndipo alipo ena mwa Arabu a kuchimizi omwe akukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro ndipo zomwe akupereka (pa njira ya Allah) amazichita monga chodziyandikitsira nacho kwa Allah, ndi (chowachititsa kuti apeze) mapemphero a Mtumiki. Tamverani! Ndithu zimenezo ndizinthu zowayandikitsa kwa Allah. Allah adzawalowetsa ku Mtendere Wake. Ndithu Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلسَّٰبِقُونَ ٱلۡأَوَّلُونَ مِنَ ٱلۡمُهَٰجِرِينَ وَٱلۡأَنصَارِ وَٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُوهُم بِإِحۡسَٰنٖ رَّضِيَ ٱللَّهُ عَنۡهُمۡ وَرَضُواْ عَنۡهُ وَأَعَدَّ لَهُمۡ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي تَحۡتَهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Ndipo amene adatsogolera poyamba, a m’gulu la Amuhajirina ndi Answari, ndi omwe adawatsatira iwo mwa ubwino, Allah adzakondwa nawo. Naonso adzakondwera Naye (pa zomwe adzapatsidwa ndi Allah). Ndipo wawakonzera minda yomwe mitsinje ikuyenda pansi (ndi pasogolo) pake, adzakhala m’menemo muyaya. Uko ndikupambana kwakukulu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمِمَّنۡ حَوۡلَكُم مِّنَ ٱلۡأَعۡرَابِ مُنَٰفِقُونَۖ وَمِنۡ أَهۡلِ ٱلۡمَدِينَةِ مَرَدُواْ عَلَى ٱلنِّفَاقِ لَا تَعۡلَمُهُمۡۖ نَحۡنُ نَعۡلَمُهُمۡۚ سَنُعَذِّبُهُم مَّرَّتَيۡنِ ثُمَّ يُرَدُّونَ إِلَىٰ عَذَابٍ عَظِيمٖ
Ndipo ena mwa Arabu a kuchimizi omwe akukhala m’mphepete mwanu (m’mphepete mwa mzinda wa Madina) alipo achiphamaso (achinyengo), ndiponso eni mzinda wa Madina aphunzira ukatswiri wachinyengo (kotero kuti) sukuwadziwa, Ife tikuwadziwa. Tiwalanga kawiri (pa dziko lapansi) ndipo kenako adzabwezedwa kuchilango chachikulu (pa tsiku lachimaliziro).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَءَاخَرُونَ ٱعۡتَرَفُواْ بِذُنُوبِهِمۡ خَلَطُواْ عَمَلٗا صَٰلِحٗا وَءَاخَرَ سَيِّئًا عَسَى ٱللَّهُ أَن يَتُوبَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ
Ndipo alipo ena omwe avomereza uchimo wawo (nalapa kwa Allah). Asakaniza zochita zabwino ndi zina zoipa. Ndithu Allah alandira kulapa kwawo. Ndithu Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
خُذۡ مِنۡ أَمۡوَٰلِهِمۡ صَدَقَةٗ تُطَهِّرُهُمۡ وَتُزَكِّيهِم بِهَا وَصَلِّ عَلَيۡهِمۡۖ إِنَّ صَلَوٰتَكَ سَكَنٞ لَّهُمۡۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
Tenga sadaka (Zakaat) m’chuma chawo kuti uwayeretse nayo (kumachimo ndi umbombo) ndi kuti uwatukulire nayo ulemelero wawo kwa Allah; ndipo apemphere (zabwino ndi chiongoko). Ndithu mapemphero ako kwa iwo ndimpumulo. Ndipo Allah Ngwakumva, Wodziwa (chilichonse).
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَلَمۡ يَعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ هُوَ يَقۡبَلُ ٱلتَّوۡبَةَ عَنۡ عِبَادِهِۦ وَيَأۡخُذُ ٱلصَّدَقَٰتِ وَأَنَّ ٱللَّهَ هُوَ ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
Kodi sadziwa kuti Allah ndi Yemwe amalandira kulapa kwa akapolo Ake, ndi kulandira sadaka, ndikuti Allah ndi Mwini kulandira kulapa mochuluka ndiponso Wachisoni chosatha?
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَقُلِ ٱعۡمَلُواْ فَسَيَرَى ٱللَّهُ عَمَلَكُمۡ وَرَسُولُهُۥ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَۖ وَسَتُرَدُّونَ إِلَىٰ عَٰلِمِ ٱلۡغَيۡبِ وَٱلشَّهَٰدَةِ فَيُنَبِّئُكُم بِمَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Ndipo auze: “Gwirani ntchito; Allah ndi Mtumiki Wake ndi okhulupirira aona ntchito yanuyo posachedwa. Ndipo (kenako) mudzabwezedwa kwa Wodziwa zamseri ndi zoonekera poyera. Choncho adzakuuzani zonse (zimene) mudali kuchita.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَءَاخَرُونَ مُرۡجَوۡنَ لِأَمۡرِ ٱللَّهِ إِمَّا يُعَذِّبُهُمۡ وَإِمَّا يَتُوبُ عَلَيۡهِمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٞ
Ndipo aliponso ena amene (adagwa m’machimo omwe) akuyembekezera lamulo la Allah, (kulapa kwawo sikunavomerezekebe), kapena awalanga kapenanso awavomera kulapa kwawo. Ndipo Allah Ngodziwa (khalidwe lawo ndi zomwe zili m’mitima mwawo), Wanzeru zakuya (pa zonse zomwe akuchita kwa anthu Ake popereka mphoto ndi chilango).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَٱلَّذِينَ ٱتَّخَذُواْ مَسۡجِدٗا ضِرَارٗا وَكُفۡرٗا وَتَفۡرِيقَۢا بَيۡنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَإِرۡصَادٗا لِّمَنۡ حَارَبَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ مِن قَبۡلُۚ وَلَيَحۡلِفُنَّ إِنۡ أَرَدۡنَآ إِلَّا ٱلۡحُسۡنَىٰۖ وَٱللَّهُ يَشۡهَدُ إِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
Ndipo (alipo achiphamaso ena) amene adamanga msikiti ndi cholinga chodzetsa masautso ndi (kulimbikitsa) kusakhulupirira Allah ndi kuwagawa okhulupirira (mu umodzi wawo) ndi kuupanga kukhala msasa wa omwe adamthira nkhondo Allah ndi Mtumiki Wake kale. Ndithu alumbira (ndikunena): “Sitidali ncholinga china (pomanga msikitiwo) koma ubwino.” Koma Allah akuikira umboni kuti iwo ngabodza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا تَقُمۡ فِيهِ أَبَدٗاۚ لَّمَسۡجِدٌ أُسِّسَ عَلَى ٱلتَّقۡوَىٰ مِنۡ أَوَّلِ يَوۡمٍ أَحَقُّ أَن تَقُومَ فِيهِۚ فِيهِ رِجَالٞ يُحِبُّونَ أَن يَتَطَهَّرُواْۚ وَٱللَّهُ يُحِبُّ ٱلۡمُطَّهِّرِينَ
Usaimilire (ndi kupemphera) m’menemo mpang’ono pomwe. Ndithu msikiti umene udakhazikitsidwa poyamba ncholinga choopa Allah ndiwo wofunika kuti uimilire m’menemo (ndi kupemphera). M’menemo muli anthu okonda kudziyeretsa (matupi ndi mitima yawo); ndipo Allah amakonda odziyeretsa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَفَمَنۡ أَسَّسَ بُنۡيَٰنَهُۥ عَلَىٰ تَقۡوَىٰ مِنَ ٱللَّهِ وَرِضۡوَٰنٍ خَيۡرٌ أَم مَّنۡ أَسَّسَ بُنۡيَٰنَهُۥ عَلَىٰ شَفَا جُرُفٍ هَارٖ فَٱنۡهَارَ بِهِۦ فِي نَارِ جَهَنَّمَۗ وَٱللَّهُ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Kodi amene wakhazikitsa maziko a chomanga chake chifukwa choopa Allah ndi kufunafuna chiyanjo (Chake), sindiye wabwino, kapena Yemwe wakhazikitsa maziko a chomanga chake m’mphepete mwa dzenje (lakuya) lomwe dothi lake likugumukira (m’dzenjemo) ndipo nkugwa pamodzi naye m’moto wa Jahannam, (ameneyu ndiye wabwino)? Ndithudi, Allah saongolera anthu ochita zoipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا يَزَالُ بُنۡيَٰنُهُمُ ٱلَّذِي بَنَوۡاْ رِيبَةٗ فِي قُلُوبِهِمۡ إِلَّآ أَن تَقَطَّعَ قُلُوبُهُمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمٌ حَكِيمٌ
Chomanga chawo chomwe adachimanga sichileka kudzetsa chikaiko ndi kusakhazikika m’mitima mwawo kufikira mitima yawo itaduka (ndi madandaulo kapena imfa). Ndipo Allah Ngodziwa (chilichonse), Ngwanzeru zakuya (m’zochitachita Zake).
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ إِنَّ ٱللَّهَ ٱشۡتَرَىٰ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ أَنفُسَهُمۡ وَأَمۡوَٰلَهُم بِأَنَّ لَهُمُ ٱلۡجَنَّةَۚ يُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَيَقۡتُلُونَ وَيُقۡتَلُونَۖ وَعۡدًا عَلَيۡهِ حَقّٗا فِي ٱلتَّوۡرَىٰةِ وَٱلۡإِنجِيلِ وَٱلۡقُرۡءَانِۚ وَمَنۡ أَوۡفَىٰ بِعَهۡدِهِۦ مِنَ ٱللَّهِۚ فَٱسۡتَبۡشِرُواْ بِبَيۡعِكُمُ ٱلَّذِي بَايَعۡتُم بِهِۦۚ وَذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Ndithu Allah wagula kwa okhulupirira moyo wawo ndi chuma chawo (kuti apereke moyo wawo ndi chuma chawo pomenya nkhondo pa njira ya Allah) kuti iwo alandire Munda wamtendere. Akumenya nkhondo pa njira ya Allah, ndipo akupha ndi kuphedwa. Ili ndi lonjezo loona lokakamizika pa Iye lomwe likupezeka m’buku la Taurati, Injili ndi Qur’an. Kodi ndani wokwaniritsa lonjezo lake kuposa Allah? Choncho kondwerani ndi kugulitsa kwanu komwe mwagulitsana Naye. Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
Ang mga Tafsir na Arabe:
ٱلتَّٰٓئِبُونَ ٱلۡعَٰبِدُونَ ٱلۡحَٰمِدُونَ ٱلسَّٰٓئِحُونَ ٱلرَّٰكِعُونَ ٱلسَّٰجِدُونَ ٱلۡأٓمِرُونَ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَٱلنَّاهُونَ عَنِ ٱلۡمُنكَرِ وَٱلۡحَٰفِظُونَ لِحُدُودِ ٱللَّهِۗ وَبَشِّرِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
(Awo amene alonjezedwa kupeza izi, ndi) omwe amalapa (akalakwa); ochita mapemphero (awo m’njira yoyenera); otamanda Allah kwambiri; ochulukitsa kusala (Swaumu kapena oyendayenda padziko ncholinga chochitira zabwino anthu), owerama, ogwetsa nkhope zawo pansi; olamula zabwino; oletsa zoipa ndi osunga malire a Allah (malamulo Ake). Choncho, auze nkhani yabwino awo amene akhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَا كَانَ لِلنَّبِيِّ وَٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَن يَسۡتَغۡفِرُواْ لِلۡمُشۡرِكِينَ وَلَوۡ كَانُوٓاْ أُوْلِي قُرۡبَىٰ مِنۢ بَعۡدِ مَا تَبَيَّنَ لَهُمۡ أَنَّهُمۡ أَصۡحَٰبُ ٱلۡجَحِيمِ
Nkosayenera kwa Mneneri ndi amene akhulupirira kuwapemphera chikhululuko opembedza mafano ngakhale atakhala abale awo, pambuyo poonekera kwa iwo kuti iwowo ndi anthu a ku Moto.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا كَانَ ٱسۡتِغۡفَارُ إِبۡرَٰهِيمَ لِأَبِيهِ إِلَّا عَن مَّوۡعِدَةٖ وَعَدَهَآ إِيَّاهُ فَلَمَّا تَبَيَّنَ لَهُۥٓ أَنَّهُۥ عَدُوّٞ لِّلَّهِ تَبَرَّأَ مِنۡهُۚ إِنَّ إِبۡرَٰهِيمَ لَأَوَّٰهٌ حَلِيمٞ
Ndipo sikudali kupempha chikhululuko kwa Ibrahim kuwapemphera bambo wake koma chifukwa cha lonjezo lomwe adamulonjeza. Koma pamene zidaonekera kwa iye poyera kuti iwo (bambo wake) ndi mdani wa Allah, adadzipatula kwa iwo. Ndithudi, Ibrahim adali wochulukitsa kupempha Allah modzichepetsa, woleza mtima.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيُضِلَّ قَوۡمَۢا بَعۡدَ إِذۡ هَدَىٰهُمۡ حَتَّىٰ يُبَيِّنَ لَهُم مَّا يَتَّقُونَۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٌ
Ndipo Allah sangasokeretse anthu (ndi kupititsa chilango pa iwo) pambuyo powaongolera ku Chisilamu; koma pokhapokha atawonetsa poyera kwa iwo zimene zingafunike kuzipewa. Ndithu Allah Ngodziwa chilichonse.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ ٱللَّهَ لَهُۥ مُلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۖ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُۚ وَمَا لَكُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ مِن وَلِيّٖ وَلَا نَصِيرٖ
Ndithudi, Allah ndi Wake ufumu wakumwamba Ndi pansi. Amapereka moyo ndi imfa. Inu mulibe mtetezi ngakhale mthandizi koma Allah basi.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَّقَد تَّابَ ٱللَّهُ عَلَى ٱلنَّبِيِّ وَٱلۡمُهَٰجِرِينَ وَٱلۡأَنصَارِ ٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُوهُ فِي سَاعَةِ ٱلۡعُسۡرَةِ مِنۢ بَعۡدِ مَا كَادَ يَزِيغُ قُلُوبُ فَرِيقٖ مِّنۡهُمۡ ثُمَّ تَابَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّهُۥ بِهِمۡ رَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndithu Allah wafunira zabwino Mtumiki Wake ndi Amuhajirina ndi Answari amene adamtsatira iye (Muhammad {s.a.w}) m’nthawi yamasautso (pokamenyana ndi Aroma pankhondo ya Tabuk), nthawi yomwe mitima ya ena a iwo idatsala pang’ono kupotoka (kutsata machitidwe achikafiri); kenako Allah adawatembenukira ndi chifundo. Ndithu Iye (Allah) kwa iwo Ngodekha, Ngwachisoni chosatha.[213]
[213] Nkhondo ya Tabuk idachitika m’mwezi wa Rajab m’chaka cha chisanu nchinayi chakusamuka. Idali pakati pa Asilamu ndi Aroma. Gulu lankhondo la Chisilamu lomwe lidapita kunkhondo linkatchedwa “Gulu la Masautso” chifukwa kukonzekera kwa nkhondoyi kudachitika m’nyengo ya masautso kwa anthu. Ndipo pamene Mtumiki adafika ku Tabuk, adadza msogoleri wa gulu lankhondo la Aroma wotchedwa Yohane namvana kuti pasakhale nkhondo. M’malo mwake iye adzapereka “Jiziya” (msonkho), motero Mtumiki adabwerera ku Madina. lyi idali nkhondo yake yomaliza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَعَلَى ٱلثَّلَٰثَةِ ٱلَّذِينَ خُلِّفُواْ حَتَّىٰٓ إِذَا ضَاقَتۡ عَلَيۡهِمُ ٱلۡأَرۡضُ بِمَا رَحُبَتۡ وَضَاقَتۡ عَلَيۡهِمۡ أَنفُسُهُمۡ وَظَنُّوٓاْ أَن لَّا مَلۡجَأَ مِنَ ٱللَّهِ إِلَّآ إِلَيۡهِ ثُمَّ تَابَ عَلَيۡهِمۡ لِيَتُوبُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ هُوَ ٱلتَّوَّابُ ٱلرَّحِيمُ
Ndiponso (adawatembenukira mwachifundo) aja atatu amene adawadikiritsa (pakusavomera msanga kulapa kwawo), kufikira pamene dziko lidawapana ngakhale lidali lophanuka, nabanika m’mitima mwawo natsimikiza kuti palibe komuthawira Allah (kwina) koma kwa Iye (Allah polapa). Kenako (Allah) adawatsogolera kulapa kuti alape. Ndithu Allah Ngolandira kulapa, Ngwachisoni chosatha.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَكُونُواْ مَعَ ٱلصَّٰدِقِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah, ndipo khalani pamodzi ndi owona (amene akuchitsimikiza Chisilamu chawo ndi zochita zawo, osati kungoyankhula pakamwa pokha).
Ang mga Tafsir na Arabe:
مَا كَانَ لِأَهۡلِ ٱلۡمَدِينَةِ وَمَنۡ حَوۡلَهُم مِّنَ ٱلۡأَعۡرَابِ أَن يَتَخَلَّفُواْ عَن رَّسُولِ ٱللَّهِ وَلَا يَرۡغَبُواْ بِأَنفُسِهِمۡ عَن نَّفۡسِهِۦۚ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ لَا يُصِيبُهُمۡ ظَمَأٞ وَلَا نَصَبٞ وَلَا مَخۡمَصَةٞ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ وَلَا يَطَـُٔونَ مَوۡطِئٗا يَغِيظُ ٱلۡكُفَّارَ وَلَا يَنَالُونَ مِنۡ عَدُوّٖ نَّيۡلًا إِلَّا كُتِبَ لَهُم بِهِۦ عَمَلٞ صَٰلِحٌۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُضِيعُ أَجۡرَ ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Nkosayenera kwa anthu a mu mzinda wa Madina ndi amene ali m’mphepete mwawo, mwa Arabu a kuchimizi, kutsalira m’mbuyo mwa Mtumiki wa Allah (poleka kutsagana naye ku nkhondo), ndiponso nkosayenera kwa iwo kudzikonda okha kuposa iye (Mtumiki). Zimenezo nchifukwa chakuti iwo silingaapeze ludzu kapena mavuto kapena njala pa njira ya Allah, ndipo sangaponde malo owakwiitsa osakhulupirira, ndipo sangampatse mdani chompatsa chilichonse chopweteka koma kulembedwa kwa iwo pa zimenezo (kuti achita) ntchito yabwino. Ndithu Allah sawononga malipiro a ochita zabwino.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَلَا يُنفِقُونَ نَفَقَةٗ صَغِيرَةٗ وَلَا كَبِيرَةٗ وَلَا يَقۡطَعُونَ وَادِيًا إِلَّا كُتِبَ لَهُمۡ لِيَجۡزِيَهُمُ ٱللَّهُ أَحۡسَنَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo sangapereke chopereka chaching’ono kapena chachikulu, ndipo sangadutse ntunda wachigwa; koma kulembedwa kwa iwo kuti Allah adzawalipira malipiro abwino pa zomwe adali kuchita.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَمَا كَانَ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ لِيَنفِرُواْ كَآفَّةٗۚ فَلَوۡلَا نَفَرَ مِن كُلِّ فِرۡقَةٖ مِّنۡهُمۡ طَآئِفَةٞ لِّيَتَفَقَّهُواْ فِي ٱلدِّينِ وَلِيُنذِرُواْ قَوۡمَهُمۡ إِذَا رَجَعُوٓاْ إِلَيۡهِمۡ لَعَلَّهُمۡ يَحۡذَرُونَ
Nkosafunika kwa okhulupirira kutuluka onse (m’midzi yawo kupita ku Madina ndi kusiya midzi yopanda anthu). Nchifukwa ninji silituluka gulu m’fuko lililonse mwa iwo (ndikupita ku Madina kwa Mtumiki) kukaphunzira bwino za Chipembedzo, ndipo akawachenjeze anthu awo akazabwerera kwa iwo kuti aope.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ قَٰتِلُواْ ٱلَّذِينَ يَلُونَكُم مِّنَ ٱلۡكُفَّارِ وَلۡيَجِدُواْ فِيكُمۡ غِلۡظَةٗۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلۡمُتَّقِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Menyani nkhondo ndi awo osakhulupirira amene ali pafupi nanu, ndipo apeze kuuma mtima mwa inu. Ndipo dziwani kuti ndithu Allah ali pamodzi ndi oopa (Iye).
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِذَا مَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٞ فَمِنۡهُم مَّن يَقُولُ أَيُّكُمۡ زَادَتۡهُ هَٰذِهِۦٓ إِيمَٰنٗاۚ فَأَمَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ فَزَادَتۡهُمۡ إِيمَٰنٗا وَهُمۡ يَسۡتَبۡشِرُونَ
Ndipo nthawi zonse sura (yatsopano) ikavumbulutsidwa, alipo mwa iwo (achiphamaso) amene akunena: “Ndani mwa inu sura iyi yamuonjezera chikhulupiliro?” Koma amene akhulupirira yawaonjezera chikhulupiliro ndipo iwo akukondwera.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَأَمَّا ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ فَزَادَتۡهُمۡ رِجۡسًا إِلَىٰ رِجۡسِهِمۡ وَمَاتُواْ وَهُمۡ كَٰفِرُونَ
Koma amene ali ndi matenda m’mitima mwawo, yawaonjezera zoipa pamwamba pa zoipa zomwe adali nazo, ndipo akufa ali osakhulupirira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
أَوَلَا يَرَوۡنَ أَنَّهُمۡ يُفۡتَنُونَ فِي كُلِّ عَامٖ مَّرَّةً أَوۡ مَرَّتَيۡنِ ثُمَّ لَا يَتُوبُونَ وَلَا هُمۡ يَذَّكَّرُونَ
Kodi saona kuti iwo akuyesedwa mayeso chaka chilichonse kamodzi, kapena kawiri, (kapena kochulukirapo)? Koma salapa (kwa Allah) ndiponso iwo sakumbukira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
وَإِذَا مَآ أُنزِلَتۡ سُورَةٞ نَّظَرَ بَعۡضُهُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٍ هَلۡ يَرَىٰكُم مِّنۡ أَحَدٖ ثُمَّ ٱنصَرَفُواْۚ صَرَفَ ٱللَّهُ قُلُوبَهُم بِأَنَّهُمۡ قَوۡمٞ لَّا يَفۡقَهُونَ
Ndipo nthawi iliyonse sura yatsopano ikavumbulutsidwa amayang’anana (iwo achiphamaso kuti athawe, asamvere mawu ake, uku akuuzana pakati pawo): “Kodi alipo amene akukuonani?” Kenako amatembenuka nkuthawa. Tero, Allah waikhotetsa mitima yawo chifukwa chakuti iwo ndi anthu osazindikira.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَقَدۡ جَآءَكُمۡ رَسُولٞ مِّنۡ أَنفُسِكُمۡ عَزِيزٌ عَلَيۡهِ مَا عَنِتُّمۡ حَرِيصٌ عَلَيۡكُم بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ رَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndithu wakudzerani Mtumiki wochokera mwa inu. Zimamudandaulitsa iye zomwe zikukuvutitsani; iye ngoikira mtima pa inu pokufunirani zabwino; ndipo pa okhulupirira ngodekha ndiponso ngwachisoni.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَإِن تَوَلَّوۡاْ فَقُلۡ حَسۡبِيَ ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ عَلَيۡهِ تَوَكَّلۡتُۖ وَهُوَ رَبُّ ٱلۡعَرۡشِ ٱلۡعَظِيمِ
Koma ngati (iwo osakhulupirira) apitiriza kunyoza, nena: “Allah wandikwanira (palibe vuto lingapezeke kuchokera kwa inu) palibe woti nkupembedzedwa koma Iye basi. Ndatsamira kwa Iye. Ndipo Iye, ndi Bwana wa Arsh (mpando wachifumu) yaikulu!”
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara